< Jeremias 18 >
1 Det Ord, som kom til Jeremias fra Herren, saalydende:
Yehova anawuza Yeremiya kuti,
2 Staa op og gaa ned til Pottemagerens Hus, og der vil jeg lade dig høre mine Ord.
“Pita ku nyumba ya munthu wowumba mbiya, ndipo kumeneko ndikakuwuza mawu anga.”
3 Og jeg gik ned til Pottemagerens Hus, og se, han gjorde et Arbejde paa Skiven.
Choncho ndinatsikira ku nyumba ya wowumba mbiya, ndipo ndinamuona akuwumba mbiya pa mkombero.
4 Og naar det Kar, som han gjorde, mislykkedes, som det kan gaa med Leret i Pottemagerens Haand, saa begyndte han igen og gjorde et andet Kar deraf, saaledes som det var ret for Pottemagerens Øjne at gøre.
Tsono amati ngati mbiya imene waumba ikhala yosawumbika bwino ankayiphwanya nʼkuwumbanso ina monga mmene afunira ndi dothi lake lomwe lija.
5 Da kom Herrens Ord til mig saaledes:
Kenaka Yehova anandiwuza kuti,
6 Mon jeg ikke kan gøre ved eder, Israels Hus, ligesom denne Pottemager? siger Herren; se, ligesom Leret er i Pottemagerens Haand, saaledes ere I, Israels Hus, i min Haand.
“Inu Aisraeli, kodi Ine sindingathe kuchita nanu monga amachitira wowumba mbiya?” akutero Yehova. “Inu muli mʼmanja mwanga ngati mtapo mʼmanja mwa wowumba mbiya.
7 I eet Øjeblik taler jeg imod et Folk og imod et Rige, til at oprykke og til at ødelægge det;
Ngati nditalengeza kuti mtundu wina wa anthu kapena ufumu wina ndiwuzula, kuwugwetsa ndi kuwuwononga,
8 men naar dette Folk, imod hvilket jeg har talt, omvender sig fra sin Ondskab, da skal jeg angre det onde, som jeg havde tænkt at gøre ved det.
ndipo ngati mtundu wa anthu umene ndawuchenjezawo ulapa zoyipa zawo, ndiye kuti Ine ndidzaleka ndipo sindidzabweretsa pa anthuwo mavuto amene ndinakonzekera kuwachitira.
9 Og i eet Øjeblik taler jeg om et Folk og om et Rige til at bygge og til at plante det;
Ndipo ngati ndilengeza kuti ndikufuna kumanga ndi kukhazikitsa mtundu wa anthu kapena ufumu.
10 men naar det gør, hvad der er ondt for mine Øjne, saa at det ikke hører min Røst, da skal jeg angre det gode, med hvilket jeg havde sagt at ville gøre vel imod det.
Koma mtunduwo ukachita choyipa pamaso panga nʼkusandimvera, ndiye kuti sindidzawuchitiranso zabwino zimene ndimafuna ndiwuchitire.
11 Og nu, sig dog til Judas Mænd og til Jerusalems Indbyggere: Saa siger Herren: Se, jeg bereder Ulykke over eder og udtænker et Anslag imod eder; vender dog om, hver fra sin onde Vej, og bedrer eders Veje og eders Idrætter!
“Ndipo tsopano kawawuze anthu a ku Yuda ndi amene akukhala mu Yerusalemu kuti, ‘Yehova akuti, Taonani! Ndikukukonzerani mavuto, ndi kuganizira zoti ndikulangeni. Kotero siyani makhalidwe anu oyipa aliyense wa inu, ndipo mukonzenso makhalidwe anu ndi zochita zanu.’
12 Men de sige: Det er forgæves! thi vi ville vandre efter vore egne Tanker og gøre hver efter sit onde Hjertes Stivhed.
Koma iwo adzayankha kuti, ‘Zimenezo nʼzosathandiza. Ife tidzapitiriza kuchita zomwe takonzekera; aliyense wa ife adzatsatira zoyipa za mtima wake wokanika.’”
13 Derfor, saa siger Herren: Spørger dog iblandt Hedningerne: „Hvo har hørt saadanne Ting?” Noget saare grueligt har Israels Jomfru begaaet.
Yehova akuti, “Uwafunse anthu a mitundu ina kuti: Kodi ndani anamvapo zinthu zofanana ndi zimenezi? Israeli amene anali ngati namwali wanga wachita chinthu choopsa kwambiri.
14 Mon Libanons Sne gaar bort fra Klippen paa Marken? eller mon de fremtrængende, friske, rindende Vande standse?
Kodi chisanu chimatha pa matanthwe otsetsereka a phiri la Lebanoni? Kodi madzi ozizira amitsinje ochokera ku phiri la Lebanoni adzamphwa?
15 Dog mit Folk har glemt mig, de gøre Røgelse for, hvad der er Forfængelighed, og de bragtes til at snuble paa deres Veje og de evige Baner, saa at de gik ind paa Stier, paa en Vej, som ikke var banet,
Komatu anthu anga andiyiwala; akufukiza lubani kwa mafano achabechabe. Amapunthwa mʼnjira zawo zakale. Amayenda mʼnjira zachidule ndi kusiya njira zabwino.
16 til at gøre deres Land til en Gru, til en evig Spot; hver som gaar derover, gruer og ryster med sit Hoved.
Dziko lawo amalisandutsa chipululu, chinthu chochititsa manyazi nthawi zonse; onse odutsapo adzadabwa kwambiri ndipo adzapukusa mitu yawo.
17 Som Østenvejret vil jeg adsprede dem for Fjendens Ansigt; jeg vil vende Ryggen og ikke Ansigtet til dem paa deres Trængsels Dag.
Ngati mphepo yochokera kummawa, ndidzawabalalitsa pamaso pa adani awo; ndidzawafulatira osawathandiza pa tsiku la mavuto awo.”
18 Men de sagde: Kommer og lader os optænke Anslag imod Jeremias; thi Loven gaar ikke tabt for Præsten, eller Raadet for den vise, eller Ordet for Profeten; kommer og lader os slaa ham med Tungen, og lader os ikke give Agt paa noget af hans Ord!
Anthuwo anati, “Tiyeni, tipangane zoti timuchitire Yeremiya; pakuti ansembe otiphunzitsa malamulo tidzakhala nawobe. Anthu anzeru otilangiza tidzakhala nawo, ndiponso aneneri otilalikira mawu. Choncho tiyeni timupezere chifukwa ndipo tisamvere chilichonse chimene akunena.”
19 Herre! giv Agt paa mig, og hør deres Røst, som trætte imod mig.
Ndipo ndinapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova, ndimvereni; imvani zimene adani anga akunena za ine!
20 Mon man skulde betale ondt for godt? thi de have gravet en Grav for min Sjæl; kom i Hu, hvorledes jeg har staaet for dit Ansigt for at tale godt for dem, for at bortvende din Vrede fra dem.
Kodi chinthu choyipa nʼkukhala dipo la chinthu chabwino? Komabe iwo andikumbira dzenje. Kumbukirani kuti ndinadzayima pamaso panu kudzawapempherera kuti muwachotsere mkwiyo wanu.
21 Derfor giv deres Børn hen til Hungeren, og overlad dem i Sværdets Vold, og lad deres Hustruer blive barnløse og Enker og deres Mænd ihjelslagne ved Døden; lad deres unge Karle blive dræbte med Sværd i Krigen!
Choncho langani ana awo ndi njala; aperekeni kuti aphedwe ndi lupanga. Akazi awo asanduke opanda ana ndi amasiye; amuna awo aphedwe ndi mliri, anyamata awo aphedwe ndi lupanga ku nkhondo.
22 Lad der høres Skrig fra deres Huse, naar du lader en Trop pludselig komme over dem; thi de grove en Grav for at fange mig og skjulte Snarer for mine Fødder.
Kulira kumveke kuchokera mʼnyumba zawo mutawatumizira gulu lankhondo mwadzidzidzi kuti liwakanthe. Iwo andikumbira dzenje kuti ndigweremo ndipo atchera msampha mapazi anga.
23 Men du, Herre! du ved alt deres Raad imod mig til Døden, son ikke deres Misgerning, og udslet ikke deres Synd for dit Ansigt; lad dem være nedstyrtede for dit Ansigt, handle med dem i din Vredes Tid!
Koma Inu Yehova, mukudziwa ziwembu zawo zonse zofuna kundipha. Musawakhululukire zolakwa zawo kapena kufafaniza machimo awo pamaso panu. Agonjetsedwe pamaso panu; muwalange muli wokwiya.”