< Esajas 9 >

1 Thi der skal ej være Mørke for det Land, hvor der nu er Trængsel; som han i den første Tid bragte Vanære over Sebulons Land og Nafthalis Land, saa skal han gøre det herligt paa det sidste, Landet ad Vejen ved Havet, paa hin Side Jordan, Hedningernes Galilæa.
Anthu amene anali ndi nkhawa, sadzakhalanso otaya mtima. Masiku amakedzana Mulungu ananyozetsa dziko la Zebuloni ndi dziko la Nafutali, koma kutsogolo kuno dera lonse la Galileya, limene lili dziko la anthu a mitundu ina, kuyambira ku nyanja yayikulu, mʼmbali mwa Yorodani, adzalisandutsa laulemu.
2 Det Folk, som vandrede i Mørket, ser et stort Lys; over dem, som boede i Dødens Skygges Land, skinner et Lys.
Anthu oyenda mu mdima awona kuwala kwakukulu; kwa iwo okhala mʼdziko la mdima wandiweyani kuwunika kwawafikira.
3 Du formerer Folket, hvis Glæde du ikke havde gjort stor; de glæde sig for dit Ansigt, ligesom Glæden er om Høsten, ligesom man fryder sig, naar man uddeler Bytte.
Inu mwauchulukitsa mtundu wanu ndipo mwawonjezera chimwemwe chawo. Iwo akukondwa pamaso panu, ngati mmene anthu amakondwera nthawi yokolola, ngatinso mmene anthu amakondwera pamene akugawana zolanda ku nkhondo.
4 Thi dets Byrdes Aag og Kæppen over dets Ryg, dets Drivers Stav, har du sønderbrudt som paa Midians Dag;
Monga munachitira pogonjetsa Amidiyani, inu mwathyola goli limene limawalemera, ndodo zimene amamenyera mapewa awo, ndiponso mikwapulo ya anthu owazunza.
5 thi hver Krigsstøvle, som blev baaren i Stridstummelen, og Klæderne, som vare sølede i Blod, skulle opbrændes og blive Ildens Næring.
Nsapato iliyonse ya munthu wankhondo, ndiponso chovala chilichonse chodonthekera magazi zidzatenthedwa pa moto ngati nkhuni.
6 Thi et Barn er os født, en Søn er os given, og Fyrstendømmet skal være paa hans Skulder, og hans Navn kaldes Under, Raadgiver, vældige Gud, Evigheds Fader, Fredsfyrste;
Chifukwa mwana watibadwira, mwana wamwamuna wapatsidwa kwa ife, ndipo ulamuliro udzakhala pa phewa lake. Ndipo adzamutcha dzina lake lakuti Phungu Wodabwitsa, Mulungu Wamphamvu, Atate Amuyaya, ndi Mfumu ya Mtendere.
7 for at Fyrstendømmet maa blive stort, og at der maa blive Fred uden Ende over Davids Trone og over hans Rige til at befæste det og til at opholde det ved Ret og Retfærdighed fra nu og indtil evig Tid; den Herre Zebaoths Nidkærhed skal gøre dette.
Ulamuliro ndi mtendere wake zidzakhala zopanda malire. Iye adzalamulira ufumu wake ali pa mpando waufumu wa Davide, ndipo adzawukhazikitsa ndi kuwuchirikiza mwa chiweruzo cholungama ndi pochita zachilungamo kuyambira nthawi imeneyo mpaka muyaya. Ndi mtima wake wonse, Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza kuchita zimenezi.
8 Herren har sendt et Ord i Jakob, og det er faldet i Israel.
Ambuye atumiza mawu otsutsa Yakobo; ndipo mawuwo agwera pa Israeli.
9 Og det hele Folk skal fornemme det, Efraim og Indbyggerne i Samaria, med deres Hovmodighed og Hjerters Stolthed; de sige:
Anthu onse okhala mu Efereimu ndi okhala mu Samariya, adzadziwa zimenezi. Iwo amayankhula modzikuza kuti,
10 Teglstenene ere faldne, men vi ville bygge med hugne Sten; Morbærtræerne ere afhugne, men vi ville sætte Cedertræer i Stedet.
“Ngakhale njerwa zagumuka, koma ife tidzamanga ndi miyala yosema. Mitanda ya mkuyu yagwetsedwa, koma ife tidzayika mitanda ya mkungudza mʼmalo mwake.”
11 Og Herren skal ophøje Rezins Modstandere over ham, og han vil væbne hans Fjender.
Koma Yehova wadzutsa adani kuti alimbane nawo ndipo wawafulumiza adani awo kuti amenyane nawo.
12 Syrerne forfra og Filisterne bagfra fortærede Israel med fuld Mund. Med alt dette har hans Vrede ikke lagt sig, men hans Haand er endnu udrakt.
Asiriya ochokera kummawa ndi Afilisti ochokera kumadzulo ndipo ayasama pakamwa kuti adye a Israeli. Komabe, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
13 Og Folket har ikke omvendt sig til den, som slog det, og har ikke søgt den Herre Zebaoth.
Koma anthu sanabwerere kwa amene anawakantha uja, ngakhale kufunafuna Yehova Wamphamvuzonse.
14 Derfor vil Herren afhugge af Israel Hoved og Hale, Palmegren og Siv, paa een Dag.
Choncho Yehova adzadula mutu wa Israeli pamodzi ndi mchira womwe, nthambi ya kanjedza ndi bango lomwe tsiku limodzi;
15 Den gamle og den ansete, han er Hovedet; men en Profet, som lærer Løgn, han er Halen.
mutuwo ndiye akuluakulu ndi olemekezeka, mchira ndiye aneneri ophunzitsa zabodza.
16 Og dette Folks Førere forføre det, og de iblandt det, som lade sig føre, opsluges.
Amene amatsogolera anthuwa ndiwo amawasocheretsa, ndipo otsogoleredwa amatayika.
17 Derfor kan Herren ikke glæde sig over dets unge Karle og ej forbarme sig over dets faderløse og over dets Enker; thi hver af dem er vanhellig og handler ondt, og hver Mund taler Daarskab. Med alt dette har hans Vrede ikke lagt sig, men hans Haand er endnu udrakt.
Nʼchifukwa chake Ambuye adzakondwera nawo achinyamata, ngakhale kuwachitira chifundo ana amasiye ndi akazi amasiye, pakuti aliyense ndi wosapembedza Mulungu ndiponso ndi wochimwa ndipo aliyense amayankhula zopusa. Komabe, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
18 Thi Ugudelighed brænder som en Ild, der fortærer Torn og Tidsler og sætter Ild paa Skovens Tykninger, og de skulle hvirvle højt op i Røg.
Ndithu kuyipa kwa anthuwo kumayaka ngati moto; moto wake umanyeketsa mkandankhuku ndi minga, umayatsa nkhalango yowirira, ndipo utsi wake umachita kuti toloo ngati mtambo.
19 Landet er sat i Brand i den Herre Zebaoths Vrede; og Folket er som det, der fortæres af Ild, de spare ikke den ene den anden.
Dziko lidzatenthedwa ndi ukali wa Yehova Wamphamvuzonse, dziko lidzatenthedwa ndipo anthu adzakhala ngati nkhuni zosonkhera moto; palibe munthu amene adzachitire chifundo mʼbale wake.
20 Og man snapper til højre og hungrer endda, og man æder om sig til venstre og mættes ej; de fortære hver sin Arms Kød:
Kudzanja lamanja adzapeza chakudya nʼkudya, koma adzakhalabe ndi njala; kudzanja lamanzere adzapeza chakudya nʼkudya, koma sadzakhuta. Aliyense azidzadya ana ake omwe.
21 Manasse er imod Efraim og Efraim imod Manasse, begge med hverandre imod Juda. Med alt dette har hans Vrede ikke lagt sig, men hans Haand er endnu udrakt.
Manase adzadya Efereimu ndipo Efereimu adzadya Manase; onsewa pamodzi adzadya Yuda. Komabe pa zonsezi, mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.

< Esajas 9 >