< Esajas 65 >
1 Jeg er søgt af dem, som ikke spurgte efter mig, jeg er funden af dem, som ikke ledte; jeg sagde til et Folk, som ikke er kaldet efter mit Navn: Se, her er jeg, se, her er jeg.
“Ndinali wokonzeka kumva mapemphero a amene sankandipempha kanthu; ndipo ndinalola kuti anthu amene ankandifunafuna kuti andipeze. Kwa mtundu wa anthu umene sunkapempha chithandizo kwa Ine, ndinati, ‘Ine ndili pano, Ine ndili pano.’
2 Jeg udbredte mine Hænder den ganske Dag til et genstridigt Folk, som vandrer ad en Vej, som ikke er god, og efter deres egne Tanker;
Tsiku lonse ndatambasulira manja anga anthu owukira aja, amene amachita zoyipa, natsatira zokhumba zawo.
3 til det Folk, som opirrer mig altid for mit Ansigt, og som ofrer i Haverne, og som gør Røgelse paa Teglstenene;
Ndatambasulira manja anga anthu aja amene nthawi zonse amandikwiyitsa mopanda manyazi. Iwo amapereka nsembe mʼminda ndi kufukiza lubani pa maguwa ansembe a njerwa.
4 til dem, som bo i Gravene og blive om Natten i Afkrogene, dem, som æde Svinekød og have vederstyggelig Suppe i deres Kar;
Amakatandala ku manda ndipo amakachezera usiku wonse kumalo obisika. Amadya nyama ya nkhumba, ndipo mʼmiphika mwawo muli msunzi wa nyama yodetsedwa.
5 til dem, som sige: Hold dig hos dig selv, kom ikke nær til mig, thi jeg er hellig over for dig; disse ere en Røg i min Næse, en Ild, som brænder den ganske Dag.
Amawuza ena kuti, ‘Khala patali usandiyandikire, chifukwa ungatengere kupatulika kwanga!’ Ukali wanga pa anthu otere uli ngati utsi mphuno zanga, ngati moto umene umayaka tsiku lonse.
6 Se, det er skrevet for mit Ansigt: Jeg vil ikke tie, før jeg faar betalt, ja, faar betalt det i deres Skød.
“Taonani, ndatsimikiza kale mlandu ndi chilango chawo; sindidzakhala chete koma ndidzawalanga kwathunthu chifukwa cha machimo awo
7 Eders Misgerninger og eders Fædres Misgerninger til Hobe vil jeg betale, siger Herren, deres, som gjorde Røgelse paa Bjergene og forhaanede mig paa Højene; deres Løn vil jeg forinden tilmaale dem i deres Skød.
ndi a makolo awo,” akutero Yehova. “Chifukwa anapereka nsembe zopsereza pa mapiri ndi kundinyoza Ine pa zitunda zawo, Ine ndidzawalanga kwathunthu potsata zimene anachita kale.”
8 Saa siger Herren: Som der findes Most i Vinklasen, og man siger: Fordærv den ikke; thi der er Velsignelse udi den, saa vil jeg gøre for mine Tjeneres Skyld og ikke fordærve alt.
Yehova akuti, “Pamene madzi akanapezeka mu phava la mphesa ndipo anthu amati, ‘Musawononge phavalo, popeza madzi ena abwino akanalimobe mʼphavalo,’ Inenso chifukwa cha mtumiki wanga; sindidzawononga onse.
9 Men af Jakob vil jeg lade udgaa en Sæd og af Juda den, som skal arve mine Bjerge; og mine udvalgte skulle arve dem og mine Tjenere bo der.
Ndidzatulutsa zidzukulu mʼbanja la Yakobo, ndipo a banja la Yuda adzalandira mapiri anga ngati cholowa chawo. Anthu anga osankhidwa adzalandira zimenezi, ndipo atumiki anga adzakhala kumeneko.
10 Og Saron skal blive til en Græsgang for Faar og Akors Dal til et Leje for Øksne, for mit Folk, for dem, som søge mig.
Chigwa cha Saroni chidzakhala kodyetserako nkhosa, ndipo chigwa cha Akori chidzakhala malo opumirako ngʼombe kwa anthu anga ondifunafuna Ine.
11 Men I, som forlade Herren, I, som glemme mit hellige Bjerg, I, som dække Bord for Gad, og I, som skænke fuldt i af blandet Drik for Meni:
“Koma inu amene mumasiya Yehova ndi kuyiwala phiri langa lopatulika, amene munamukonzera Gadi chakudya ndi kuthirira Meni chakumwa,
12 Eder vil jeg give hen til Sværdet, og I skulle alle bøje eder ned til at slagtes, efterdi jeg kaldte, og I svarede ikke, efterdi jeg talte, og I hørte ikke; men I gjorde det, som var ondt for mine Øjne, og udvalgte det, som jeg ikke havde Lyst til.
ndidzakuperekani ku lupanga ngati nsembe, ndipo nonse mudzaphedwa; chifukwa simunayankhe pamene ndinakuyitanani, ndinayankhula koma simunamvere. Munachita zoyipa pamaso panga ndipo munasankha kuchita zoyipa zomwe sindikondwera nazo.”
13 Derfor, saa siger den Herre, Herre: Se, mine Tjenere skulle æde, men I skulle hungre; se, mine Tjenere skulle drikke, men I skulle tørste; se, mine Tjenere skulle glædes, men I skulle beskæmmes;
Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, “Atumiki anga adzadya, koma inu mudzakhala ndi njala; atumiki anga adzamwa, koma inu mudzakhala ndi ludzu; atumiki anga adzakondwa, koma inu mudzakhala ndi manyazi.
14 se, mine Tjenere skulle synge af Hjertens Glæde, men I skulle skrige af Hjertekvide og hyle af Aands Fortvivlelse.
Atumiki anga adzayimba mosangalala, koma inu mudzalira kwambiri chifukwa chovutika mu mtima ndipo mudzalira mofuwula chifukwa mudzamva kuwawa mu mtima.
15 Og I skulle efterlade mine udvalgte eders Navn til at sværge ved, og den Herre, Herre skal dræbe eder; men sine Tjenere skal han give et nyt Navn.
Anthu anga osankhidwa adzatchula dzina lanu potemberera. Ambuye Yehova adzakuphani, koma atumiki ake adzawapatsa dzina lina.
16 Hver den, som velsigner sig i Landet, skal velsigne sig i den trofaste Gud, og hver den, som sværger i Landet, skal sværge ved den trofaste Gud; thi de forrige Trængsler ere glemte, og de ere borte for mine Øjne.
Aliyense wopempha dalitso mʼdzikomo adzachita zimenezo kwa Mulungu woona; ndipo aliyense wochita malumbiro mʼdzikomo adzalumbira mwa Mulungu woona. Pakuti mavuto akale adzayiwalika ndipo adzachotsedwa pamaso panga.
17 Thi se, jeg skaber nye Himle og en ny Jord; og det første skal ikke ihukommes, ej heller rinde nogen i Sinde.
“Taonani, ndikulenga mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano. Zinthu zakale sizidzakumbukika, zidzayiwalika kotheratu.
18 Men glæder eder og fryder eder indtil evig Tid ved det, som jeg skaber; thi se, jeg skaber Jerusalem til Fryd og dets Folk til Glæde.
Koma inu mukhale osangalala ndi okondwa mpaka muyaya chifukwa cha zimene ndikulenga, pakuti ndikulenga Yerusalemu kukhala malo wosangalatsa ndipo anthu ake adzakhala achimwemwe.
19 Og jeg vil fryde mig over Jerusalem og glæde mig over mit Folk, og der skal ikke ydermere høres Graads Røst eller Skrigs Røst deri.
Ine ndidzakondwa chifuwa cha Yerusalemu ndipo ndidzasangalala chifukwa cha anthu anga. Kumeneko sikudzamvekanso kulira ndi mfuwu wodandaula.
20 Derfra skal ikke ydermere komme noget Barn, som lever faa Dage, eller nogen gammel, som ikke naar sine Dages Tal; thi Drengen skal dø hundrede Aar gammel, og Synderen, som er hundrede Aar gammel, skal kaldes forbandet.
“Ana sadzafa ali akhanda ndipo nkhalamba zonse zidzakwaniritsa zaka zawo zonse. Wamngʼono mwa iwo adzafa ali ndi zaka 100. Amene adzalephere kufika zaka 100 adzatengedwa kukhala wotembereredwa.
21 Og de skulle bygge Huse og bo deri og plante Vingaarde og æde deres Frugt.
Anthu adzamanga nyumba ndi kukhalamo, adzadzala mpesa ndipo adzadya zipatso zake.
22 De skulle ikke bygge, at en anden skal bo deri, og ikke plante, at en anden skal æde det; thi som Træets Dage skulle mit Folks Dage være, og mine udvalgte skulle til fulde nyde deres Hænders Gerning.
Sadzamanganso nyumba anthu ena nʼkukhalamo, kapena kudzala ndi ena nʼkudya. Pakuti anthu anga adzakhala ndi moyo wautali ngati mitengo. Osankhidwa anga adzakondwera ndi ntchito ya manja awo nthawi yayitali.
23 De skulle ikke have Møje forgæves og ej føde Børn til brat Død; thi de ere den Sæd, som er velsignet af Herren, og deres Afkom skal blive hos dem.
Sadzagwira ntchito pachabe kapena kubereka ana kuti aone tsoka; chifukwa adzakhala anthu odalitsidwa ndi Yehova, iwowo pamodzi ndi adzukulu awo omwe.
24 Og det sker, førend de raabe, da vil jeg svare; naar de endnu tale, da vil jeg høre.
Ndidzawayankha ngakhale asanathe nʼkupempha komwe. Pamene akuyankhula kumene Ine ndidzakhala nditamva kale.
25 En Ulv og et Lam skulle græsse sammen, og en Løve skal æde Halm som en Okse, og en Slanges Spise skal være Støv, de skulle ikke gøre ondt, ej heller handle fordærveligt paa hele mit hellige Bjerg, siger Herren.
Mʼmbulu ndi mwana wankhosa wamkazi zidzadyera pamodzi. Mkango udzadya udzu monga ngʼombe, koma fumbi ndiye chidzakhale chakudya cha njoka. Pa phiri langa lopatulika sipadzakhala chinthu chopweteka kapena chowononga,” akutero Yehova.