< Esajas 64 >
1 gid du vilde sønderrive Himlene og fare ned, saa at Bjergene fløde bort for dit Ansigt!
Inu Yehova, bwanji mukanangongʼamba mlengalenga ndi kutsika pansi, kuti mapiri agwedezeke pamaso panu!
2 Ligesom Ild antænder Kviste, ligesom Ild kommer Vand til at syde, saa lade du dine Fjender kende dit Navn, saa at Hedningerne bæve for dit Ansigt.
Monga momwe moto umatenthera tchire ndiponso kuwiritsa madzi, tsikani kuti adani anu adziwe dzina lanu, ndiponso kuti mitundu ya anthu injenjemere pamaso panu.
3 Da du har gjort underlige Ting, skulde vi da ikke vente? du nedfor, Bjerge fløde bort for dit Ansigt.
Pakuti nthawi ina pamene munatsika munachita zinthu zoopsa zimene sitinaziyembekezere, ndipo mapiri anagwedezeka pamaso panu.
4 Og fra gammel Tid har man ikke hørt, har man ikke fornummet, intet Øje set, at nogen Gud uden du gjorde saadanne Ting for den, som bier efter ham.
Chikhalire palibe ndi mmodzi yemwe anamvapo kapena kuona Mulungu wina wonga Inu, amene amachitira zinthu zotere amene amadikira pa Iye.
5 Du møder den, som er glad ved at gøre Retfærdighed, de skulle komme dig i Hu paa dine Veje; se, du var vred, og vi bleve ved at synde; vare vi evindelig blevne paa dem, da vare vi nu frelste.
Inu mumabwera kudzathandiza onse amene amakondwera pochita zolungama, amene amakumbukira njira zanu. Koma Inu munakwiya, ife tinapitiriza kuchimwa. Kodi nanga tingapulumutsidwe bwanji?
6 Men vi bleve alle som de urene og al vor Retfærdighed som et besmittet Klædebon; og vi faldt alle, af som et Blad, og vor Misgerning førte os bort som et Vejr.
Tonsefe takhala ngati anthu amene ndi odetsedwa, ndipo ntchito zathu zili ngati sanza za msambo; tonse tafota ngati tsamba, ndipo machimo athu akutiwuluzira kutali ngati mphepo.
7 Og der er ingen, som paakalder dit Navn, ingen, som rejser sig for at holde fast ved dig; thi du har skjult dit Ansigt for os og smeltet os for vore Misgerningers Skyld.
Palibe amene amapemphera kwa Inu kutekeseka kuti apemphe chithandizo kwa Inu; pakuti mwatifulatira ndi kutisiya chifukwa cha machimo athu.
8 Men nu, Herre! du er vor Fader; vi ere Leret, og du er den, som har dannet os, og vi ere alle din Haands Gerning.
Komabe, Inu Yehova ndinu Atate athu. Ife ndife chowumba, Inu ndinu wowumba; ife tonse ndi ntchito ya manja anu.
9 Herre! vær ikke saa saare vred, og kom ikke Misgerninger evindelig i Hu; se, sku dog, vi ere alle dit Folk!
Inu Yehova, musatikwiyire kopitirira muyeso musakumbukire machimo athu mpaka muyaya. Chonde, mutiganizire, ife tikupempha, pakuti tonsefe ndi anthu anu.
10 Dine Helligdoms Stæder ere blevne til en Ørk; Zion er bleven til en Ørk, Jerusalem en Ødelæggelse.
Mizinda yanu yopatulika yasanduka chipululu; ngakhaletu Ziyoni wasanduka chipululu, Yerusalemu ndi wamasiye.
11 Vor Helligheds og vor Herligheds Hus, i hvilket vore Fædre lovede dig, er opbrændt med Ild, og alle vore lystelige Ting ere ødelagte.
Nyumba yanu yopatulika ndi yaulemu, kumene makolo athu ankakutamandani, yatenthedwa ndi moto ndipo malo onse amene tinkawakonda asanduka bwinja.
12 Vil du over for disse Ting holde dig tilbage, Herre? vil du tie og nedtrykke os saa saare?
Inu Yehova, zonse zachitikazi, kodi mungokhala osatithandiza? Kodi mudzapitirizabe kukhala chete ndi kutilangabe mopitirira muyeso?