< Esajas 63 >
1 Hvo er denne, som kommer fra Edom, i højrøde Klæder fra Bozra, han, som er saa prægtig i sit Klædebon, han, som skrider frem i sin store Kraft? Det er mig, som taler Retfærdighed, mig, som er mægtig til at frelse!
Kodi ndani uyo akubwera kuchokera ku Edomu, atavala zovala za ku Bozira za madontho ofiira? Kodi uyu ndani, amene wavala zovala zokongola, akuyenda mwa mphamvu zake? “Ndi Ineyo, woyankhula zachilungamo ndiponso wamphamvu zopulumutsa.”
2 Hvorfor er der rødt paa dit Klædebon og dine Klæder som dens, der træder Vinpersen?
Nanga bwanji zovala zanu zili psuu, ngati za munthu wofinya mphesa?
3 Jeg traadte Persekarret, jeg alene, og der var intet af Folkene med mig; saa traadte jeg dem i min Vrede og stampede dem ned i min Harme; da sprudlede deres Blod op paa mine Klæder, og jeg fik alle mine Klæder besudlede.
“Ndapondereza ndekha anthu a mitundu ina ngati mphesa, palibe ndi mmodzi yemwe anali nane. Ndinawapondereza ndili wokwiya ndipo ndinawapondereza ndili ndi ukali; magazi awo anadothera pa zovala zanga, ndipo zovala zanga zonse zinathimbirira.
4 Thi Hævnens Dag var besluttet i mit Hjerte, og mit Genløsningsaar var kommet.
Pakuti ndinatsimikiza mu mtima mwanga kuti lafika tsiku lolipsira anthu anga; ndipo chaka cha kuwomboledwa kwanga chafika.
5 Og jeg saa mig om, og der var ingen Hjælper, og jeg undrede mig over, at der ingen var, som holdt med mig; men min Arm hjalp mig, og min Harme stod mig bi.
Ndinayangʼana ndipo panalibe munthu wondithandiza. Ndinadabwa kwambiri kuti panalibe wondichirikiza; choncho ndinapambana ndi mphamvu zanga, ndipo mkwiyo wanga unandilimbitsa.
6 Og jeg nedtraadte Folkene i min Vrede og gjorde dem drukne i min Harme og lod deres Blod rinde til Jorden.
Ndinapondereza mitundu ya anthu ndili wokwiya; ndipo ndinawasakaza ndipo ndinathira magazi awo pansi.”
7 Jeg vil forkynde Herrens Miskundhed, Herrens Pris, efter alt det, som Herren har gjort imod os, ja, den megen Godhed imod Israels Hus, som han gjorde imod dem, efter sin Barmhjertighed og efter sin store Miskundhed.
Ndidzafotokoza za kukoma mtima kwa Yehova, ntchito zimene Iye ayenera kutamandidwa. Ndidzatamanda Yehova chifukwa cha zonse zimene watichitira. Inde, mwa chifundo ndi kukoma mtima kwake Yehova wachitira nyumba ya Israeli zinthu zabwino zambiri.
8 Og han sagde: Kun de ere mit Folk, de ere Børn, som ikke ville handle falskelig; og han blev dem en Frelser.
Yehova anati, “Ndithu awa ndi anthu anga, ana anga amene sadzandinyenga Ine.” Choncho anawapulumutsa.
9 I al deres Trængsel var der ikke Trængsel, men hans Ansigts Engel frelste dem; han genløste dem for sin Kærligheds og for sin Overbærelses Skyld, og han lagde dem paa sig og bar dem igennem alle Fortidens Dage.
Iyenso anasautsidwa mʼmasautso awo onse, ndipo mngelo wochokera kwa Iye anawapulumutsa. Mwa chikondi ndi chifundo chake iye anawapulumutsa, anawanyamula ndikuwatenga kuyambira kale lomwe.
10 Men de, de vare genstridige og bedrøvede hans Helligaand; derfor omskiftede han sig til deres Modstander, han stred imod dem.
Komabe iwo anawukira ndi kumvetsa chisoni Mzimu Woyera. Motero Yehova anatembenuka nakhala mdani wawo ndipo Iye mwini anamenyana nawo.
11 Da ihukom hans Folk de gamle Dage under Mose: Hvor er han, som opførte dem af Havet tillige med sin Hjords Hyrde? hvor er han, som gav sin Helligaand midt iblandt dem?
Pamenepo anthu ake anakumbukira masiku amakedzana, masiku a Mose mtumiki wake; ndipo anafunsa kuti, “Ali kuti Yehova amene anawawolotsa pa nyanja, pamodzi ndi Mose mʼbusa wawo? Ali kuti Iye amene anayika Mzimu Woyera pakati pawo?
12 han, som lod sin Herligheds Arm føre Moses højre Haand, han, som kløvede Vandene for deres Ansigt for at gøre sig et evigt Navn?
Ali kuti amene anachita zinthu zodabwitsa ndi mphamvu zake zazikulu kudzera mwa Mose? Ali kuti amene anagawa madzi pa nyanja anthu ake akuona, kuti dzina lake limveke mpaka muyaya,
13 han, som førte dem igennem Afgrundene som en Hest igennem Ørken, saa at de ikke stødte sig?
amene anawayendetsa pa nyanja yozama? Monga kavalo woyendayenda mʼchipululu, iwo sanapunthwe;
14 Ligesom Kvæget gaar ned i Dalen, har Herrens Aand ladet dem komme til Hvile; saaledes førte du dit Folk for at gøre dig et herligt Navn.
Mzimu Woyera unawapumulitsa ngati mmene ngʼombe zimapumulira. Umu ndi mmene Inu munatsogolera anthu anu kuti dzina lanu lilemekezeke.”
15 Sku ned fra Himlene, og se til fra din Helligheds og Herligheds Bolig! hvor er din Nidkærhed og din Vælde, din dybe Medlidenhed og din Barmhjertighed, der holder sig tilbage fra mig?
Inu Yehova amene muli kumwambako, pa mpando wanu wolemekezeka, wopatulika ndi waulemerero, tiyangʼaneni ife. Kodi changu chanu ndi mphamvu zanu zili kuti? Simukutionetsanso kukoma mtima kwanu ndi chifundo chanu.
16 Thi du er vor Fader; thi Abraham ved intet af os, og Israel kender os ikke; men du, Herre! er vor Fader, vor Genløser, fra Evighed af er dit Navn.
Koma Inu ndinu Atate athu, ngakhale Abrahamu satidziwa kapena Israeli kutivomereza ife; Inu Yehova, ndinu Atate athu, kuyambira kale dzina lanu ndinu Mpulumutsi wathu.
17 Herre! hvorfor lader du os fare vild fra dine Veje? hvorfor lader du vort Hjerte blive haardt, at det ikke frygter dig? vend om for dine Tjeneres Skyld, for din Arvs Stammers Skyld!
Chifukwa chiyani, Inu Yehova, mukutisocheretsa pa njira zanu? Bwanji mukutilola kuti tikhale owuma mitima kotero kuti sitikukuopaninso? Bwererani chifukwa cha atumiki anu; mafuko a anthu amene ali cholowa chanu.
18 En liden Tid har dit hellige Folk ejet Landet; men vore Modstandere have nedtraadt din Helligdom.
Anthu anu atangokhala pa malo anu opatulika pa kanthawi kochepa, adani athu anasakaza malo anu opatulika.
19 Vi ere, som om du ikke havde regeret over os fra gammel Tid, og som om vi ikke vare kaldede efter dit Navn;
Ife tili ngati anthu amene simunawalamulirepo ngati iwo amene sanakhalepo anthu anu.