< Esajas 60 >

1 Gør dig rede, bliv Lys; thi dit Lys er kommet, og Herrens Herlighed er opgangen over dig.
“Dzuka, wala, pakuti kuwala kwako kwafika, ndipo ulemerero wa Yehova wakuwalira.
2 Thi se, Mørke skjuler Jorden og Dunkelhed Folkene; men over dig skal Herren oprinde, og over dig skal hans Herlighed ses.
Taona, mdima waphimba dziko lapansi ndipo mdima wandiweyani wagwa pa anthu a mitundu ina, koma Yehova adzakuwalira iwe, ndipo ulemerero wake udzaoneka pa iwe.
3 Og Hedningerne skulle vandre hen til dit Lys, og Kongerne hen til det Skin, som er opgangen for dig.
Mitundu ya anthu idzatsata kuwunika kwako ndipo mafumu adzalondola kunyezimira kwa mʼbandakucha wako.
4 Kast dine Øjne trindt omkring og se, de samle sig alle, de komme til dig, dine Sønner komme langvejs fra, og dine Døtre bæres paa Arm.
“Tukula maso ako, yangʼanayangʼana ndipo ona zimene zikuchitika. Onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe; ana ako a amuna akubwera kuchokera kutali ndipo ana ako aakazi anyamulidwa mʼmanja.
5 Da skal du se det og straale af Glæde, og dit Hjerte skal banke og udvide sig; thi Rigdommen fra Havet skal vende sig til dig, Hedningernes Magt skal komme til dig.
Ukadzaona zimenezi udzasangalala kwambiri, mtima wako udzalumpha ndi kudzaza ndi chimwemwe; chuma chakunyanja chidzabwera kwa iwe chuma cha mitundu ya anthu chidzabwera kwa iwe.
6 Kamelernes Mangfoldighed skal skjule dig, Midians og Efas Dromedarer, alle de af Skeba skulle komme; de skulle bringe Guld og Røgelse og forkynde Herrens Pris.
Gulu la ngamira lidzaphimba dziko lako, ngamira zingʼonozingʼono zidzachokera ku Midiyani ndi ku Efai. Ndipo onse a ku Seba adzabwera atanyamula golide ndi lubani uku akutamanda Yehova.
7 Alle Kedars Faar skulle samles til dig, Nebajots Vædre skulle tjene dig; de skulle ofres paa mit Alter til mit Velbehag, og min Herligheds Hus vil jeg forherlige.
Ziweto zonse za ku Kedara adzazisonkhanitsa kwa inu, nkhosa zazimuna za ku Nabayoti zidzakutumikirani; zidzalandiridwa monga chopereka pa guwa langa la nsembe, ndipo ndidzakongoletsa Nyumba yanga.
8 Hvo ere disse, der komme flyvende som en Sky og som Duer til deres Dueslag?
“Kodi ndi zayani izo zikuwuluka ngati mitambo, ngati kapena nkhunda zobwerera ku zisa zawo?
9 Thi paa mig vente Øer, og Tharsis's Skibe ere foran for at føre dine Børn hid langvejs fra, og med dem deres Sølv og deres Guld, til Herren din Guds Navn og til Israels Hellige; thi han har forherliget dig.
Ndithu, izi ndi sitima za pa madzi zochokera ku mayiko akutali; patsogolo pali sitima zapamadzi za ku Tarisisi, zikubweretsa ana ako ochokera kutali, pamodzi ndi siliva wawo ndi golide wawo, kudzalemekeza Yehova Mulungu wako, Woyerayo wa Israeli, pakuti Iye wakuvekani inu ulemerero.
10 Og de fremmede skulle bygge dine Mure og deres Konger tjene dig; thi i min Vrede slog jeg dig, men i min Naade forbarmede jeg mig over dig.
“Alendo adzamanganso malinga ako, ndipo mafumu awo adzakutumikira. Ngakhale ndinakukantha ndili wokwiya, koma tsopano ndidzakukomera mtima ndikukuchitira chifundo.
11 Og dine Porte skal man altid holde aabne, hverken Dag eller Nat skulle de lukkes, for at lade Hedningernes Magt og deres Konger, som føres hid, komme til dig.
Zipata zako zidzakhala zotsekula nthawi zonse, sadzazitseka nthawi zonse, usana ndi usiku, kotero anthu adzabwera kwa iwe ndi chuma chawo, akuyenda pa mdipiti mafumu awo ali patsogolo.
12 Thi det Folk og det Rige, som ikke vil tjene dig, skal ødelægges, og Hedningerne skulle gaa aldeles til Grunde.
Pakuti mtundu wa anthu ndi mafumu amene sakutumikira iwe; adzawonongeka kotheratu.
13 Libanons Herlighed skal komme til dig, baade Fyrretræ og Kintræ og Buksbom, for at pryde min Helligdoms Sted og gøre mine Fødders Sted herligt.
“Adzabwera nayo kwa iwe mitengo ya payini, mkuyu ndi naphini imene ili mʼnkhalango ya Lebanoni kuti adzakongoletsere malo a nyumba yanga yopatulika; ndipo ndidzalemekeza malo amene Ine ndimapondapo.
14 Og Børnene af dem, som trængte dig, skulle gaa bøjede til dig, og alle de, som spottede dig, skulle kaste sig ned for dine Fødder, og de skulle kalde dig Herrens Stad, Zion, den Helliges i Israel.
Ana aja amene anakuzunzani adzabwera ndipo adzakugwadirani; onse amene anakunyozani adzagwada pansi pa mapazi anu. Ndipo adzakutchani kuti Mzinda wa Yehova; Ziyoni mzinda wa Woyerayo wa Israeli.
15 I Stedet for at du var forladt og forhadt, saa at ingen gik der igennem, vil jeg gøre dig til en evig Herlighed, til en Fryd fra Slægt til Slægt.
“Ngakhale anthu anakusiya nadana nawe, koma Ine ndidzakukuza mpaka muyaya, ndipo udzakhala malo a chimwemwe cha anthu amibado yonse.
16 Og du skal die Hedningers Mælk og die Kongers Bryst, og du skal fornemme, at jeg Herren er din Frelser og Jakobs Mægtige din Genløser.
Udzamwa mkaka wa mitundu ya anthu ndi kuleredwa pa maere aufumu, motero udzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wako, Momboli wako ndiye Wamphamvu wa Yakobo.
17 Jeg vil sætte Guld i Stedet for Kobber og sætte Sølv i Stedet for Jern og Kobber i Stedet for Træ og Jern i Stedet for Sten; og jeg vil give dig Øverster til Fred og Herskere til Retfærdighed.
Ndidzakupatsa golide mʼmalo mwa mkuwa, ndi siliva mʼmalo mwa chitsulo. Ndidzakupatsa mkuwa mʼmalo mwa thabwa ndi chitsulo mʼmalo mwa miyala. Olamulira ako adzakhala a mtendere. Ndidzasandutsa okulamulira kuti akhale achilungamo.
18 Der skal ikke ydermere høres om Vold i dit Land eller om Ødelæggelse og Forstyrrelse inden dine Landemærker; men du skal kalde Frelsen dine Mure og Lovsangen dine Porte.
Ziwawa sizidzamvekanso mʼdziko lako, bwinja kapena chiwonongeko sizidzapezeka mʼdziko lako, ndidzakhala malinga ako okuteteza ndipo udzanditamanda.
19 Solen skal ikke ydermere være dig til Lys om Dagen, og Maanen skal ikke lyse for dig til Glans; men Herren skal være dig et evigt Lys og din Gud din Herlighed.
Sipadzakhala dzuwa kuti likuwunikire, kapena mwezi kuti uwunikire usiku, pakuti Yehova ndiye adzakhale kuwunika kwako kwa muyaya, ndipo Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.
20 Din Sol skal ikke mere gaa ned og din Maane ikke miste sit Skin; thi Herren skal være dig et evigt Lys og din Sorrigs Dage være endte.
Dzuwa lako silidzalowanso, ndipo mwezi wako sudzazimiriranso; Yehova adzakhala kuwunika kwako kwamuyaya, ndipo masiku a mavuto ako adzatha.
21 Og dit Folk, de skulle alle være retfærdige, de skulle eje Landet evindelig som de, der ere en Kvist af min Plantning, et Værk af mine Hænder, mig til Herlighed.
Ndipo anthu ako onse adzakhala olungama ndipo dzikolo lidzakhala lawo mpaka muyaya. Iwo ndi mphukira imene Ine ndayidzala, ntchito ya manja anga, kuti aonetse ulemerero wanga.
22 Den lille skal blive til tusinde, og den ringe til et stærkt Folk; jeg Herren, jeg vil lade det hastelig ske i sin Tid.
Kabanja kakangʼono kadzasanduka fuko, kafuko kakangʼono kudzasanduka mtundu wamphamvu. Ine ndine Yehova, nthawi yake ikafika ndidzazichita zimenezi mofulumira.”

< Esajas 60 >