< Esajas 57 >

1 Den retfærdige omkommer, og der er ingen, som lægger det paa Hjerte; og fromme Folk kaldes bort, men der er ingen, som giver Agt derpaa; thi den retfærdige kaldes bort, før det onde kommer.
Anthu olungama amafa, ndipo palibe amene amalingalira mu mtima mwake; anthu odzipereka amatengedwa, ndipo palibe amene amamvetsa chifukwa chake. Anthu olungama amatengedwa kuti tsoka lisawagwere.
2 De gaa ind til Fred, de hvile i deres Sovekamre, hver den, som vandrer ret for sig.
Iwo amene amakhala moyo wolungama amafa mwamtendere; amapeza mpumulo pamene agona mu imfa.
3 Men I, kommer hid, I Troldkvindens Børn, du Horkarlens og Horkvindens Yngel!
“Bwerani kuno, anthu ochita zoyipa, inu muli ngati zidzukulu za mkazi wachigololo ndi wadama!
4 Over hvem gøre I eder lystige? ad hvem vrænge I Mund og række Tungen langt ud? ere I ikke Overtrædelsens Børn, Løgnens Sæd?
Kodi inu mukuseka yani? Kodi mukumunena ndani ndi kupotoza pakamwa panu? Kodi inu si ana owukira, zidzukulu za anthu abodza?
5 I, som ere optændte af Brynde for Afguderne, under hvert grønt Træ, I, som slagte Børnene i Dalene, i Kløfterne under Stenklipperne!
Inu mumapembedza mafano pamene mumalobodoka ndi zilakolako zanu pakati pa mitengo ya thundu, ndiponso pa tsinde pa mtengo uliwonse wa nthambi zambiri. Mumapereka ana anu ngati nsembe mu zigwa ndiponso mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.
6 Din Del er Dalens glatte Stene, de, de ere i din Lod, ja, for dem udgød du Drikofre, du ofrede dem Madoffer; skulde jeg berolige mig over disse Ting?
Mafano a pakati pa miyala yosalala ya mu zigwa ndiye chuma chanu. Inde, ndiye gawo lanu. Mumapereka chopereka cha chakumwa kwa mafanowo, ndipo mumaperekanso chopereka cha chakudya. Kodi zimenezi zingandichititse kuti ndikukomereni mtima?
7 Du redte dit Leje paa et højt og ophøjet Bjerg; ogsaa der gik du op til at slagte Slagtoffer?
Inu munayiwala bedi lanu pa phiri lalitali ndi looneka kutali. Mumapita kumeneko kukapereka nsembe zanu.
8 Og du satte dit Mindetegn bag Døren og Dørstolpen; thi bortvendt fra mig blottede du dig og gik op; du udvidede dit Leje og indlod dig i Pagt med dem; du elskede deres Leje paa hver Plads, du saa dem.
Mʼnyumba mwanu mwayika mafano kuseri kwa zitseko ndiponso pa mphuthu. Mwandisiya Ine, mwavula zovala zanu. Bedi lanu mwalikulitsa ndipo mwakwera ndi zibwenzi zanu, ndiye mwazilipira kuti mugone nazo. Kumene mwakwaniritsa zilakolako zanu zoyipa.
9 Og salvet med Olie saa du hen til Kongen og formerede dine vellugtende Salver; og du sendte dine Bud langvejs hen og steg dybt ned indtil Dødsriget. (Sheol h7585)
Mumapita kukapembedza fano la Moleki mutatenga mafuta ndi zonunkhira zochuluka. Munachita kutumiza akazembe anu kutali; inu ngakhale munapita ku manda kwenikweniko! (Sheol h7585)
10 Formedelst din lange Vej er du bleven træt; dog sagde du ikke: „Jeg giver tabt!” du fandt Liv i din Haand, derfor blev du ikke syg.
Inu mumatopa ndi maulendo anu, koma simunathe kunena kuti, ‘Nʼzopanda phindu.’ Munapezako kumeneko zokhumba zanu nʼchifukwa chake simunalefuke.
11 Og for hvem har du været bange og frygtet, saa at du vil lyve? men mig kommer du ikke i Hu og lægger det ikke paa dit Hjerte! mon ikke jeg har tiet og det fra fordums Tid af? men mig vil du ikke frygte!
“Kodi ndani amene mwachita naye mantha ndi kumuopa, kotero kuti mwakhala mukundinamiza, ndipo Ine simundikumbukira nʼkomwe, kapena kuganizirapo mʼmitima yanu za Ine? Kodi mwaleka kundiopa chifukwa choti ndakhala chete nthawi yayitali?
12 Jeg vil kundgøre din Retfærdighed og dine Gerninger, og de skulle ikke gavne dig.
Koma ndaonetsa poyera ntchito zanu zomwe mumati nʼzolungama, ndi mafano anu kuti nʼzosathandiza.
13 Naar du raaber, da lad dine Skarer redde dig! men Vejret skal løfte dem alle sammen op, et Vindpust skal tage dem bort; men den, som forlader sig paa mig, skal arve Landet og eje mit hellige Bjerg.
Pamene mufuwula kupempha thandizo, mafano anu amene munasonkhanitsawo ndiyetu akupulumutseni! Mphepo idzanyamula mafano anu onsewo, mpweya chabe udzawulutsa mafanowo. Koma munthu amene amadalira ine adzalandira dziko lokhalamo. Phiri langa lopatulika lidzakhala lakelake.”
14 Og man skal sige: Baner, baner, rydder Vejen, tager Stød bort af mit Folks Vej!
Ndipo panamveka mawu akuti, “Undani, undani, konzani msewu! Chotsani zotchinga pa njira yoyendamo anthu anga.”
15 Thi saa siger den Høje og Ophøjede, som bor i Evigheden, og hvis Navn er helligt: Jeg bor i det høje og hellige, og hos den sønderknuste og i Aanden nedbøjede for at gøre de nedbøjedes Aand levende og at gøre de sønderknustes Hjerter levende.
Pakuti Iye amene ali Wamkulu ndi Wopambanazonse, amene alipo nthawi zonse, amene dzina lake ndi Woyerayo, akunena kuti, “Ndimakhala pamalo aulemu ndi opatulika, koma ndimakhalanso ndi munthu wodzichepetsa ndi wosweka mtima kuti odzichepetsawo ndiwalimbitse ndi kuwachotsa mantha osweka mtima.
16 Thi jeg vil ikke trætte evindelig og ikke være vred i Evighed; thi ellers maatte Aanden og de Sjæle, som jeg har skabt, forsmægte for mit Ansigt.
Sindidzawatsutsa anthu mpaka muyaya kapena kuwapsera mtima nthawi zonse, popeza kuti ndinalenga anthu anga ndi kuwapatsa mpweya wamoyo.
17 For hans Gerrigheds Synd var jeg vred og slog ham, jeg skjulte mig i Vrede; men han vendte sig bort og gik sit Hjertes Vej.
Ine ndinakwiya kwambiri chifukwa cha tchimo lawo ladyera; ndinawalanga ndi kuwafulatira mokwiya, koma iwo anapitirirabe kuchita ntchito zawo zoyipa.
18 Hans Veje saa jeg, og jeg vil læge ham; og jeg vil lede ham og give ham og dem, som sørgede med ham, Trøst.
Ndaona zochita zawo, komabe ndidzawachiritsa; kuwapumulitsa ndi kuwapatsa mtendere,
19 Jeg skaber Læbers Frugt: Fred, Fred for fjern og nær, siger Herren, og jeg læger ham.
anthu olira a mu Israeli adzanditamanda ndi milomo yawo. Anthu amene ali kutali ndi apafupi pomwe ndidzawapatsa mtendere,” “Ndipo ndidzawachiritsa.” Akutero Yehova.
20 Men de ugudelige ere som Havet, der er oprørt; thi det kan ikke være roligt, men dets Vande udkaste Skarn og Dynd.
Koma anthu oyipa ali ngati nyanja yowinduka, yosatha kukhala bata, mafunde ake amaponya matope ndi ndere.
21 De ugudelige, siger min Gud, have ingen Fred.
“Palibe mtendere kwa oyipa,” akutero Mulungu wanga.

< Esajas 57 >