< Esajas 35 >
1 Ørken og de tørre Steder skulle glæde sig, og den øde Mark skal fryde sig og blomstre som en Rose.
Chipululu ndi dziko lopanda madzi zidzasangalala; dziko lowuma lidzakondwa ndi kuchita maluwa.
2 Den skal blomstre frodigt, den skal juble og synge med Fryd, Libanons Herlighed er given den, Karmels og Sarons Pragt; de skulle se Herrens Herlighed, vor Guds Pragt.
Dzikolo lidzakhala ndi maluwa ochuluka lidzasangalala kwambiri ndi kufuwula mwachimwemwe. Lidzakhala ndi ulemerero monga wa ku mapiri a ku Lebanoni, maonekedwe ake wokongola adzakhala ngati a ku Karimeli ndi a ku Saroni. Aliyense adzaona ulemerero wa Yehova, ukulu wa Mulungu wathu.
3 Styrker de afmægtige Hænder, og giver de snublende Knæ Kraft!
Limbitsani manja ofowoka, limbitsani mawondo agwedegwede;
4 Siger til de mistrøstige af Hjerte: Værer frimodige, frygter ikke! se, eders Gud! Hævn kommer, Gengældelse fra Gud, han skal komme og frelse eder.
nenani kwa a mitima yamantha kuti; “Limbani mtima, musachite mantha; Mulungu wanu akubwera, akubwera kudzalipsira; ndi kudzabwezera chilango adani anu; akubwera kudzakupulumutsani.”
5 Da skulle de blindes Øjne aabnes og de døves Øren oplades.
Pamenepo maso a anthu osaona adzapenyanso ndipo makutu a anthu osamva adzatsekuka.
6 Da skal den halte springe som en Hjort og den stummes Tunge synge med Fryd; thi Vande bryde frem i Ørken og Bække paa den øde Mark.
Anthu olumala adzalumpha ngati mbawala, ndipo osayankhula adzayimba mokondwera. Akasupe adzatumphuka mʼchipululu ndipo mitsinje idzayenda mʼdziko lowuma,
7 Og den glødende Sandørk skal blive til Sø og det tørstige Sted til Vandkilder; i den Bolig, hvor Drager laa, skal være Sted for Rør og Siv.
mchenga wotentha udzasanduka dziwe, nthaka yowuma idzasanduka ya akasupe. Pamene panali mbuto ya ankhandwe padzamera udzu ndi bango.
8 Og en banet Sti og Vej skal være der, en Vej, som kaldes Helligdommens; ingen uren skal gaa ad den, men den skal være for dem selv; de, som vandre paa denne Vej, endog enfoldige, skulle ikke fare vild.
Ndipo kumeneko kudzakhala msewu waukulu; ndipo udzatchedwa Msewu Wopatulika. Anthu odetsedwa sadzayendamo mʼmenemo; zitsiru sizidzasochera mʼmenemo.
9 Ingen Løve skal være der, og intet Rovdyr kommer derop eller findes der; men de igenløste skulle vandre der.
Kumeneko sikudzakhala mkango, ngakhale nyama yolusa sidzafikako; sidzapezeka konse kumeneko. Koma okhawo amene Yehova anawapulumutsa adzayenda mu msewu umenewu.
10 Og Herrens forløste skulle komme tilbage og komme til Zion med Frydesang, og evig Glæde skal være over deres Hoved; Fryd og Glæde skulle de naa, og Sorrig og Suk skal fly.
Iwo amene Yehova anawawombola adzabwerera. Adzalowa mu mzinda wa Ziyoni akuyimba; kumeneko adzakondwa mpaka muyaya. Adzakutidwa ndi chisangalalo ndi chimwemwe, ndipo chisoni ndi kudandaula zidzatheratu.