< Esajas 28 >

1 Ve de druknes stolte Krone i Efraim og deres dejlige Prydelses falmede Blomst, som staar oven over den fede Dal, der hvor de rave af Vin!
Tsoka ufumu wonyada wa zidakwa za ku Efereimu. Tsoka kwa ulemerero wake wokongola umene ukufota ngati duwa limene lili pa mutu pa anthu oledzera a mʼchigwa chachonde.
2 Se, Herren har en stærk og mægtig, der er som et Regnskyl med Hagel, som en ødelæggende Storm; som et Skyl af mægtige Vande, der strømme over, skal han slaa ned til Jorden med Magt.
Taonani, ambuye ali naye wina wamphamvu ndi nyonga. Iye adzabwera ngati mkuntho wamatalala ndi namondwe wowononga, ngati madzi amphamvu osefukira a mvula yamkuntho; ndipo adzawagwetsa pansi mwankhanza.
3 Med Fødder skal den trædes ned, de druknes stolte Krone i Efraim.
Ulamuliro wa atsogoleri oledzera a ku Efereimu adzawuthetsa.
4 Og deres dejlige Prydelses falmede Blomst, som er oven over den fede Dal, skal blive som en Figen, der er tidligt moden før Sommeren, hvilken en faar at se og opsluger, saa snart han faar den i sin Haand.
Ndipo ulemerero wokongola wa mzinda umene uli ngati duwa lofota pamutu pa anthu oledzera a mʼchigwa chachonde uja, udzakhala ngati nkhuyu yoyambirira kupsa imene munthu akangoyiona amayithyola nthawi yokolola isanakwane.
5 Paa den Dag skal den Herre Zebaoth være til en dejlig Krone og en herlig Krans for sit Folks overblevne
Tsiku limenelo Yehova Wamphamvuzonse adzakhala ngati nkhata yaufumu, chipewa chokongola kwa anthu ake otsala.
6 og til Rettens Aand for den, som sidder i Retten, og til Styrke for dem, som drive Krigen tilbage til Porten.
Iye adzapereka mtima wachilungamo kwa oweruza, adzakhala chilimbikitso kwa amene amabweza adani pa zipata za mzinda.
7 Men ogsaa disse rave af Vin og ere forvildede af stærk Drik; Præst og Profet rave af stærk Drik, de ere overvældede af Vin, forvildede af stærk Drik, de fare vild under Synet, de vakle under Dommen.
Nawonso awa ali dzandidzandi chifukwa cha vinyo ndipo akusochera chifukwa cha mowa: ansembe ndi aneneri akudzandira chifukwa cha mowa ndipo akusokonezeka chifukwa cha vinyo; akusochera chifukwa cha mowa, akudzandira pamene akuona masomphenya, kupunthwa pamene akupereka chigamulo.
8 Thi alle Borde ere fulde af væmmeligt Spy; der er ikke en ren Plet.
Pa matebulo onse pali masanzi okhaokha ndipo palibenso malo wopanda zonyansa.
9 Hvem skal han lære Kundskab? og hvem skal han bringe til at forstaa det, som høres? er det dem, som ere afvante fra Mælk, dem, som ere tagne fra Bryst?
Iwo akuti, “Kodi munthu ameneyu akufuna aphunzitse ndani? Uthengawu akufuna kufotokozera yani? Ndi kwa ana amene aleka kuyamwa, kwa makanda ongowachotsa kumene ku bere?
10 Thi der er Bud paa Bud, Bud paa Bud, Regel paa Regel, Regel paa Regel, lidet her, lidet der.
Akuyesa kumatiphunzitsa pangʼonopangʼono lemba ndi lemba, mzere ndi mzere, phunziro ndi phunziro. Zonsezi akungoti apa pangʼono apa pangʼono.”
11 Men ved Folk med stammende Læber og med fremmed Tungemaal skal han tale til dette Folk,
Mulungu adzayankhula kwa anthu ake kudzera mwa anthu aziyankhulo zachilendo, ziyankhulo zosamveka bwino. Mulungu adzayankhula kwa anthu awa, amene
12 til hvilket han sagde: Her er Rolighed, lader den trætte hvile, her er Vederkvægelse, men de vilde ikke høre.
anakuwuzani kuti, “Malo opumulira ndi ano, otopa apumule, malo owusira ndi ano.” Koma inu simunamvere.
13 Saa skal Herrens Ord da vorde dem Bud paa Bud, Bud paa Bud, Regel paa Regel, Regel paa Regel, lidet her, lidet der; paa det de skulle gaa bort og falde baglæns og sønderbrydes og besnæres og fanges.
Choncho Yehova adzakuphunzitsani pangʼonopangʼono lemba ndi lemba, mzere ndi mzere, phunziro ndi phunziro. Kotero mudzayenda ndi kugwa chambuyo, adzapweteka ndi kukodwa mu msampha ndipo adzakutengani ku ukapolo.
14 Derfor hører Herrens Ord, I Bespottere! der herske over dette Folk, som er i Jerusalem.
Nʼchifukwa chake imvani mawu a Yehova, inu anthu achipongwe amene mumalamulira anthu awa mu Yerusalemu.
15 Fordi I sagde: Vi have gjort en Pagt med Døden og gjort et Forbund med Dødsriget; naar den svungne Svøbe farer forbi, da skal den ikke komme til os; thi vi have sat Løgn til vor Tilflugt og Falskhed til vort Skjul. (Sheol h7585)
Inu mumayankhula monyada kuti, “Ife tinachita pangano ndi imfa, ife tachita mgwirizano ndi manda. Pamene mliri woopsa ukadzafika sudzatikhudza ife, chifukwa timadalira bodza ngati pothawirapo pathu ndi chinyengo ngati malo anthu obisalapo.” (Sheol h7585)
16 Derfor, saa sagde den Herre, Herre: Se, jeg lægger til Grundvold i Zion en Sten, en prøvet Sten, en kostelig Hjørnesten, fast grundlagt; hvo, som tror, haster ikke.
Tsono zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi: “Taonani, ndikuyika mwala wovomerezeka ndi amisiri ngati maziko mu Ziyoni, mwala wapangodya, wamtengowapatali wopanga maziko amphamvu; munthu amene awukhulupirira sadzagwedezeka.
17 Og jeg vil sætte Ret til Maalesnor og Retfærdighed til Vægt, og Hagel skal bortdrive den falske Tilflugt, og Vandene overskylle Skjulet.
Ntchito zolungama zidzakhala ngati chingwe choyezera maziko ake, ndipo chilungamo chidzakhala chowongolera mzere; matalala adzawononga malo anu othawirapo, amene ndi mabodza, ndipo madzi adzamiza malo anu obisalako.
18 Og eders Pagt med Døden skal blive til intet, og eders Forbund med Dødsriget skal ikke bestaa; naar den svungne Svøbe farer forbi, da skal den slaa eder ned. (Sheol h7585)
Pangano limene munachita ndi imfa lidzathetsedwa; mgwirizano wanu ndi manda udzachotsedwa. Pakuti mliri woopsa udzafika, ndipo udzakugonjetsani. (Sheol h7585)
19 Saa ofte den farer forbi, skal den rive eder bort; thi den skal fare forbi hver Morgen, om Dagen og om Natten; og det skal allerede være en Skræk at høre Rygtet.
Ndipo ukadzangofika udzakutengani. Udzafika mmawa uliwonse, usiku ndi usana.” Anthu akadzamvetsetsa uthenga umenewu adzaopsedwa kwambiri.
20 Thi Sengen er for kort, saa at man ikke kan strække; sig ud, og Dækket er: fer smalt, naar man vil (Jække sig dermed.
Mudzakhala ngati munthu wogona pa bedi lalifupi kwambiri kuti sangathe kutambalitsapo miyendo; ndiponso mudzakhala ngati munthu amene wafunda bulangeti lochepa kwambiri kuti sangathe nʼkufunda komwe.
21 Thi Herren skal gøre sig rede som ved Perazims Bjerg, han skal fortørnes som i Gibeons Dal, til at gøre sin Gerning — paafaldende er hans Gerning! og fuldkomme sit Værk — uhørt er hans Værk!
Yehova adzamenya nkhondo monga anachitira ku phiri la Perazimu adzakalipa monga anachitira ku chigwa cha Gibiyoni; adzagwira ntchito yake yooneka ngati yachilendo, ndipo zimene ati adzachite zidzakhala ngati zodabwitsa.
22 Og nu, spotter ikke, at eders Baand ikke skulle blive haardere; thi jeg har hørt om Ødelæggelse og om en fast Beskikkelse fra Herren, den Herre Zebaoth, over al Jorden,
Tsopano lekani kunyoza, mukapanda kutero maunyolo anu adzakuthinani kwambiri; Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse wandiwuza kuti, “Ndagamula kuti ndidzawononga dziko lapansi.”
23 Vender Ørene hid og hører min Røst, mærker og hører min Tale!
Tcherani khutu ndipo mumve mawu anga; mvetserani ndipo mumve zimene ndikunena.
24 Mon Plovmanden pløjer til alle Tider for at saa, fælder og harver sin Jord?
Kodi mlimi wofuna kudzala mbewu amangokhalira kutipula kokhakokha? Kodi amangokhalira kugawula ndi kugalawuza kokhakokha?
25 Er det ej saa, at naar han har jævnet dens Overflade, da udspreder han Dild og strør Kommen og saar Hvede i Rader og Byg paa det afmærkede Sted og Spelt i Kanten deraf?
Pamene iye wasalaza mundawo, kodi samafesa mawere ndi chitowe? Kodi suja samadzala tirigu ndi barele mʼmizere yake, nadzala mchewere mʼphepete mwa mundawo?
26 Thi Gud underviser ham om den rette Maade, hans Gud lærer ham den.
Mulungu wake amamulangiza ndi kumuphunzitsa njira yabwino.
27 Thi Dild tærskes ikke med Tærskevogn, og Vognhjul gaa ikke hen over Kommen; men Dild afslaas med Stav og Kommen med Kæp.
Mawere sapunthira chopunthira cha galeta lopanda mikombero, kapena chitowe sapuntha popondetsapo mikombero ya galeta; mawere amapuntha ndi ndodo ndipo chitowe amapuntha ndi kamtengo.
28 Brødkorn stødes smaat; thi man tærsker det ej evindelig; og driver man sine Vognhjul og sine Heste derover, knuser man det ikke.
Tirigu ayenera kusinjidwa kuti apangire buledi, komabe munthu samangokhalira kupuntha tiriguyo osalekeza, kuopa kuti angatekedzeke. Ngakhale kuti amapuntha tiriguyo poyendetsapo mikombero ya galeta, koma akavalo ake satekedza tiriguyo.
29 Ogsaa dette udgaar fra den Herre Zebaoth, han er underlig i Raad og stor i Visdom.
Izinso zimachokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, wa uphungu wodabwitsa ndi wa nzeru zopambana.

< Esajas 28 >