< Hoseas 5 >

1 Hører dette I Præster! og giver Agt, Israels Hus! og du, Kongehus, laan Øre! thi Dommen angaar eder, fordi I vare en Snare for Mizpa og et udbredt Garn over Tabor.
“Ansembe inu, imvani izi! Inu Aisraeli, tcherani khutu! Inu nyumba yaufumu, mvetserani! Chiweruzo ichi ndi chotsutsa inu: Inu munali ngati msampha ku Mizipa, munali ngati ukonde woyalidwa pa phiri la Tabori.
2 Og de afvegne ere dybt fordærvede; men jeg er den, som tugter dem alle sammen.
Owukira azama mʼmoyo wakupha, Ine ndidzawalanga onsewo.
3 Jeg kender Efraim, og Israel er ikke skjult for mig; thi nu har du, Efraim, bedrevet Hor, Israel er besmittet.
Ndimadziwa zonse za Efereimu; Aisraeli ndi osabisika kwa Ine. Efereimu wayamba tsopano kuchita zachiwerewere; Israeli wadziyipitsa.
4 Deres Idrætter tillade dem ikke at vende om til deres Gud; thi der er en Horeriets Aand i deres Indre, og Herren kende de ikke.
“Ntchito zawo siziwalola kubwerera kwa Mulungu wawo. Mʼmitima mwawo muli mzimu wachiwerewere; Iwo sadziwa Yehova.
5 Og Israels Stolthed vidner imod det; og Israel og Efraim skulle falde for deres Misgerning, Juda skal ogsaa falde med dem.
Kudzikuza kwa Israeli kwakhala umboni womutsutsa; Aisraeli, ngakhale Aefereimu, anagwa mʼmachimo awo; Yudanso anagwa nawo pamodzi.
6 Med deres Faar og med deres Øksne skulle de gaa hen for at søge Herren, men ikke finde ham; han har draget sig bort fra dem.
Pamene adzapita ndi nkhosa zawo ndi ngʼombe zawo kukapereka nsembe kwa Yehova, iwo sadzamupeza; Iye wawachokera.
7 Imod Herren have de handlet troløst, thi de fødte fremmede Børn; nu skal Nymaaneden fortære dem med deres Agre.
Iwo ndi osakhulupirika kwa Yehova; amabereka ana amʼchigololo ndipo chikondwerero chawo cha mwezi watsopano chidzawawononga pamodzi ndi minda yawo.
8 Blæser i Trompeten i Gibea, i Basunen i Rama! raaber højt i Beth-Aven: Bag dig, Benjamin!
“Womba lipenga mu Gibeya, liza mbetete mu Rama. Fuwulani mfuwu wankhondo mu Beti-Aveni; iwe Benjamini tsogolera.
9 Efraim skal blive øde paa Straffens Dag; iblandt Israels Stammer har jeg kundgjort, hvad der staar fast.
Efereimu adzasanduka bwinja pa tsiku la chilango. Ine ndikulengeza zomwe zidzachitikadi pakati pa mafuko a Israeli.
10 Judas Fyrster ere blevne som de, der flytter Grænseskel; over dem vil jeg udøse min Harme som Vand.
Atsogoleri a Yuda ali ngati anthu amene amasuntha miyala ya mʼmalire. Ndidzawakhutulira ukali wanga ngati madzi a chigumula.
11 Undertrykt er Efraim og knust i sin Ret; thi det tog sig for at vandre efter selvgjorte Bud.
Efereimu waponderezedwa, akulangidwa chifukwa chotsatira mafano.
12 Og jeg er som Møl for Efraim og som Kræft for Judas Hus.
Ine ndili ngati njenjete kwa Efereimu, ngati chinthu chowola kwa anthu a ku Yuda.
13 Der Efraim saa sin Sygdom og Juda sin Byld, da gik Efraim til Assyrien og sendte Bud til en stridbar Konge; men han skal ikke kunne læge eder, og Bylden skal ikke gaa bort fra eder.
“Efereimu ataona nthenda yake, ndi Yuda ataona zilonda zake, pamenepo Efereimu anatembenukira kwa Asiriya, ndipo anawatumizira mfumu yayikulu kudzawathandiza. Koma mfumuyo singathe kukuchizani, singathe kuchiritsa mabala anu.
14 Thi jeg er som en Løve for Efraim og som en ung Løve for Judas Hus, jeg, jeg sønderriver og gaar bort, jeg tager det med, og ingen skal redde.
Pakuti Ine ndidzakhala ngati mkango kwa Efereimu. Ngati mkango wamphamvu kwa Yuda. Ndidzawakhadzula nʼkuchokapo; ndidzawatenga ndipo palibe amene adzawalanditse.
15 Jeg vil gaa bort, jeg vil vende tilbage til mit Sted, indtil de kende deres Skyld og søge mit Ansigt; naar de ere i Trængsel, ville de søge mig.
Ndipo ndidzabwerera ku malo anga mpaka anthu anga atavomereza kulakwa kwawo. Ndipo iwo adzafunafuna nkhope yanga; mʼmasautso awo adzandifunitsitsa Ine.”

< Hoseas 5 >