< Habakkuk 1 >

1 Profetien, som Habakuk, Profeten, har skuet.
Uthenga umene mneneri Habakuku analandira mʼmasomphenya.
2 Hvor længe, Herre! har jeg dog raabt, og du vil ikke høre! jeg raaber til dig over Vold, og du vil ikke frelse.
Kodi inu Yehova, ndidzakhala ndikukupemphani thandizo kwa nthawi yayitali motani, koma wosayankha? Kapena kufuwulira kwa inu kuti, “Chiwawa kuno!” koma wosatipulumutsa?
3 Hvorfor lader du mig skue Uret og ser selv paa Jammer? Ødelæggelse og Vold er for mit Ansigt, og der kom Trætte, og Kiv rejser sig.
Chifukwa chiyani mukundionetsa zinthu zoyipa? Chifukwa chiyani mukundionetsa mavutowa? Ndikuona chiwonongeko ndi chiwawa; pali ndewu ndi kukangana kwambiri.
4 Derfor er Lov magtesløs, og Ret kommer aldrig frem; thi de ugudelige omringe den retfærdige, derfor kommer Retten forvendt ud.
Kotero malamulo anu atha mphamvu, ndipo chilungamo sichikugwira ntchito. Anthu oyipa aposa olungama, kotero apotoza chilungamo.
5 Ser ud iblandt Hedningerne, og skuer; forundrer eder, og vorder forundrede; thi jeg gør en Gerning i eders Dage, I vilde ikke tro den, naar den fortaltes.
“Yangʼanani pakati pa mitundu ya anthu, ndipo penyetsetsani, ndipo muthedwe nazo nzeru. Pakuti ndidzachitadi zinthu pa nthawi yanu zimene inu simudzazikhulupirira, ngakhale wina atakufotokozerani.
6 Thi se, jeg opvækker Kaldæerne, et barsk og hastigt Folk, som farer frem, saa vidt som Jorden naar, for at tage Boliger til Eje, som ikke høre det til.
Pakuti taonani, Ine ndikuwutsa Ababuloni, anthu ankhanza ndiponso amphamvu, amene amapita pa dziko lonse lapansi kukalanda malo amene si awo.
7 Frygteligt og forfærdeligt er det; fra det gaar dets Ret og Overhøjhed ud.
Iwowa ndi anthu ochititsa mantha, ndipo ndi owopsa; amadzipangira okha malamulo ndi kudzipezera okha ulemu.
8 Og dets Heste ere lettere end Pardere og hidsigere end Ulve om Aftenen, og dets Ryttere brede sig ud, ja, dets Ryttere komme langt borte fra, de flyve som en Ørn, der haster efter Æde.
Akavalo awo ndi aliwiro kwambiri kupambana akambuku ndi owopsa kupambana mimbulu yolusa nthawi ya madzulo. Okwerapo awo akuthamanga molunjika; a pa akavalo awo ndi ochokera kutali, akuwuluka ngati chiwombankhanga chofuna kugwira nyama;
9 Alle til Hobe komme de til Voldsdaad, deres Ansigters Higen er fremad, og det samler Fanger som Sand.
onse akubwera atakonzekera zachiwawa. Gulu la ankhondo likubwera ngati mphepo ya mʼchipululu ndi kugwira akapolo ochuluka ngati mchenga.
10 Og det spotter Konger, og Fyrster ere til Latter for det; det ler ad hver Befæstning, saa det dynger Støv op og indtager den.
Akunyoza mafumu ndiponso kuchitira chipongwe olamulira. Akupeputsa mizinda yonse yotetezedwa; akumanga mitumbira ndi kulanda mizindayo.
11 Da farer det frem som en Stormvind og drager videre, saa at det paadrager sig Skyld; denne dets Kraft bliver til dets Gud.
Kenaka amasesa mofulumira ngati mphepo nʼkumangopitirirabe, anthu ochimwa, amene mphamvu zawo ndiye mulungu wawo.”
12 Er du ikke fra fordums Tid Herren, min Gud, min Hellige! vi skulle ikke dø; Herre! du har sat det til Dom; o Klippe! du har grundfæstet det til at straffe os.
Inu Yehova, kodi sindinu wachikhalire? Mulungu wanga, Woyera wanga, ife sitidzafa. Inu Yehova, munawasankha anthuwo kuti abweretse chiweruzo; Inu Thanthwe, munawayika iwowo kuti atilange.
13 Du, som er ren af Øjne, saa at du ikke kan se paa ondt og ikke formaar at skue Jammer, hvorfor skuer du hen til de troløse, hvorfor tier du, naar den ugudelige opsluger den, som er retfærdigere end han?
Maso anu ndi oyera kwambiri safuna kuona choyipa; Inu simulekerera cholakwa. Chifukwa chiyani nanga mukulekerera anthu ochita zachinyengowa? Chifukwa chiyani muli chete pamene anthu oyipa akuwononga anthu olungama kupambana iwowo?
14 Du gjorde da Menneskene som Fiske i Havet, som Krybet, der ingen Herre har.
Mwasandutsa anthu kukhala ngati nsomba zamʼnyanja, ngati zolengedwa zamʼnyanja zimene zilibe wolamulira.
15 Han drager dem alle sammen op med Krog, samler dem i sin Vod og sanker dem i sit Garn; derover glæder og fryder han sig.
Mdani wawo woyipa amakoka anthu onse ndi mbedza, amawakola mu ukonde wake, amawasonkhanitsa mu khoka lake; kotero iyeyo amakondwa ndi kusangalala.
16 Derfor ofrer han til sin Vod og bringer Røgoffer til sit Garn; thi ved dem er hans Del fed, og hans Mad er det fede.
Choncho iye amaperekera nsembe ukonde wake ndiponso kufukizira lubani khoka lake, popeza ukonde wakewo ndiye umamubweretsera moyo wapamwamba ndipo amadya chakudya chabwino kwambiri.
17 Mon han derfor skal tømme sin Vod og altid slaa Folk ihjel uden Skaansel?
Kodi iye azipitirabe kugwiritsa ntchito makoka akewo, kuwononga mitundu ya anthu mopanda chifundo?

< Habakkuk 1 >