< 1 Mosebog 7 >

1 Og Herren sagde til Noa: Gak ind, du og dit ganske Hus, i Arken; thi dig har jeg set retfærdig for mig i denne Slægt.
Ndipo Yehova anati kwa Nowa, “Lowa mu chombo iwe ndi banja lako lonse, chifukwa ndaona kuti ndiwe wolungama mu mʼbado uwu.
2 Tag dig af alle Haande rent Kvæg syv og syv, Han og Hun; men af det Kvæg, som er urent, et Par, Han og Hun;
Pa mtundu uliwonse wa nyama zoti nʼkudya utengepo zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi zazikazi zisanu ndi ziwirinso. Koma pa mtundu wa nyama iliyonse yosati nʼkudya utengepo zazimuna ziwiri ndi zazikazi ziwirinso.
3 ogsaa af Fuglene under Himmelen, syv og syv, Han og Hun, at holde Sæd paa al Jorden i Live.
Chimodzimodzinso mbalame, utenge zisanu ndi ziwiri zazimuna ndi zisanu ndi ziwiri zazikazi za mtundu uliwonse kuti mitundu yawo isungike ndi moyo pa dziko lonse lapansi.
4 Thi end om syv Dage vil jeg lade regne paa Jorden fyrretyve Dage og fyrretyve Nætter og udslette af Jorden alle levende Væsener, som jeg har gjort.
Pakapita masiku asanu ndi awiri ndidzagwetsa mvula pa dziko lapansi kwa masiku makumi anayi usana ndi usiku ndipo ndidzawononga cha moyo chilichonse chimene ndinachipanga pa dziko lapansi.”
5 Og Noa gjorde efter alt, hvad Herren bød ham.
Ndipo Nowa anachita zonse zimene Yehova anamulamulira.
6 Og der Noa var seks Hundrede Aar gammel, da kom Floden med Vande over Jorden.
Pamene chigumula chinabwera pa dziko lapansi Nowa anali ndi zaka 600.
7 Og Noa gik ind og hans Sønner og hans Hustru og hans Sønners Hustruer med ham i Arken for Flodens Vande.
Ndipo Nowa, ana ake aamuna, mkazi wake, pamodzi ndi ana ake aakazi analowa mu chombo chija kuthawa madzi a chigumula.
8 Af rent Kvæg og af det Kvæg, som ikke er rent, og af Fuglene og alt det, som kryber paa Jorden,
Nyama zoti nʼkudya ndi nyama zosadyedwa, mbalame, pamodzi ndi nyama zokwawa zonse zinadza kwa Nowa ziwiriziwiri ndi kulowa mʼchombomo.
9 gik Par og Par til Noa til Arken, Han og Hun, ligesom Gud havde befalet Noa.
Ndipo Nowa anatenga ziwiriziwiri, yayimuna ndi yayikazi monga anamulamulira Mulungu.
10 Og det skete paa den syvende Dag, da kom Flodens Vande over Jorden.
Patapita masiku asanu ndi awiri chigumula chinabwera pa dziko lapansi.
11 I det Aar, der Noa var seks Hundrede Aar gammel, i den anden Maaned, paa den syttende Dag i Maaneden, paa den Dag opbrast alle Kilder i den store Afgrund, og Himmelens Sluser oplodes.
Pa tsiku la 17 la mwezi wachiwiri, Nowa ali ndi zaka 600, akasupe onse akuya kwambiri anasefuka ndiponso zitseko za madzi akumwamba zinatsekuka.
12 Og der var Regn paa Jorden fyrretyve Dage og fyrretyve Nætter.
Ndipo mvula inagwa pa dziko lapansi masiku makumi anayi usana ndi usiku.
13 Paa den selvsamme Dag gik Noa og Sem og Kam og Jafet, Noas Sønner, og Noas Hustru og hans Sønners tre Hustruer med dem i Arken;
Linali tsiku lomwelo pamene Nowa ndi ana ake aamuna, Semu, Hamu ndi Yafeti, pamodzi ndi mkazi wake ndi akazi a ana ake atatu aja analowa mu chombo.
14 de og alle Haande vilde Dyr efter deres Slags og alle Haande Kvæg efter deres Slags og alle Haande Kryb, som krybe paa Jorden, efter deres Slags, og alle Haande Fugle efter deres Slags, alt det, som kan flyve, alt det, som har Vinger.
Iwowa analowa mʼchombomo pamodzi ndi nyama iliyonse ya kutchire monga mwa mtundu wake, ziweto zonse monga mwa mitundu yawo, nyama yokwawa iliyonse monga mwa mtundu wake ndi mbalame iliyonse monga mwa mtundu wake.
15 Og de gik i Arken til Noa, Par og Par af alt Kød, i hvilket der var Livs Aande.
Nowa analowa mu chombo muja pamodzi ndi zamoyo zonse.
16 Og de, som kom, kom Han og Hun af alle Haande Kød, ligesom Gud havde budet ham; og Herren lukkede til efter ham.
Iye analowa nazo zazimuna ndi zazikazi monga mmene Mulungu anamulamulira. Kenaka Yehova anatseka pa khomo.
17 Da kom Floden fyrretyve Dage over Jorden; og Vandet formeredes og opløftede Arken, og den hævedes op over Jorden.
Chigumula chinagwa pa dziko la pansi kwa masiku makumi anayi. Madzi anayamba kuchuluka ndipo ananyamula chombo chija ndi kuchiyandamitsa pamwamba pa dziko.
18 Og Vandet fik Overhaand og formeredes saare over Jorden; og Arken flød oven paa Vandet.
Madzi anafika mwamphamvu ndipo anachulukirachulukira pa dziko lapansi moti chombo chinayandama pamwamba pa madziwo.
19 Og Vandet fik Overhaand saare meget over Jorden; og alle høje Bjerge bleve skjulte, som vare under den ganske Himmel.
Madzi a chigumula anabwerabe molimbika motero kuti mapiri ataliatali onse a pa dziko anamizidwa.
20 Femten Alen oventil fik Vandet Overhaand, og Bjergene bleve skjulte.
Madzi anakwera namiza mapiri kwa mamita pafupifupi asanu ndi awiri.
21 Saa udaandede alt Kød, som rørte sig paa Jorden, af Fugle og af Kvæg og af vilde Dyr og af al den Vrimmel, som vrimlede paa Jorden, og hvert Menneske.
Chamoyo chilichonse choyenda pa dziko lapansi chinafa: mbalame, ziweto, nyama zakuthengo, miyandamiyanda ya zonse zolengedwa za pa dziko lapansi pamodzi ndi anthu.
22 Alt det, som havde Livs Aande i sin Næse, alt det, som var paa det tørre, døde.
Chilichonse chamoyo, chokhala pa mtunda chinafa.
23 Og hvert Væsen udslettedes, som var paa Jorden, fra Mennesket indtil Kvæg, indtil Kryb og indtil Fugle under Himmelen, og de bleve udslettede af Jorden; og Noa blev alene igen, og hvad der var med ham i Arken.
Chamoyo chilichonse pa dziko lapansi chinawonongedwa, kuyambira munthu, nyama, zokwawa ndi mbalame. Nowa yekha ndiye anatsala pamodzi ndi onse amene anali naye.
24 Og Vandet havde Overhaand over Jorden hundrede og halvtredsindstyve Dage.
Madziwo anadzaza dziko lonse lapansi kwa masiku 150.

< 1 Mosebog 7 >

The Great Flood
The Great Flood