< 1 Mosebog 48 >

1 Og det skete derefter, at der sagdes til Josef: Se, din Fader er syg; og han tog begge sine Sønner med sig, Manasse og Efraim.
Patapita kanthawi Yosefe anawuzidwa kuti, “Abambo ako akudwala.” Choncho anatenga ana ake awiri aja Manase ndi Efereimu ndi kupita nawo kwa Yakobo.
2 Og det gaves Jakob til Kende, og der sagdes: Se, din Søn Josef kommer til dig; saa gjorde Israel sig stærk og sad paa Sengen.
Yakobo atawuzidwa kuti, “Mwana wanu Yosefe wabwera,” Israeli anadzilimbitsa nadzuka kukhala tsonga pa bedi pake.
3 Og Jakob sagde til Josef: Den almægtige Gud aabenbaredes for mig i Lus, udi Kanaans Land, og velsignede mig,
Yakobo anati kwa Yosefe, “Mulungu Wamphamvuzonse anandionekera ku Luzi mʼdziko la Kanaani, ndipo anandidalitsa,
4 og han sagde til mig: Se, jeg vil gøre dig frugtbar og formere dig og gøre dig til en Hob Folk og give din Sæd efter dig dette Land til Ejendom evindelig.
nati kwa ine, ‘Ndidzakupatsa ana ambiri ndipo zidzukulu zako zidzasanduka mitundu yambiri ya anthu. Ndidzapereka dziko ili kwa zidzukulu zako zobwera pambuyo pako kuti likhale lawo mpaka muyaya.’
5 Og nu, dine to Sønner, som ere fødte dig i Ægyptens Land, før jeg kom til dig i Ægypten, de skulle høre mig til; Efraim og Manasse skulle høre mig til, som Ruben og Simeon.
“Tsopano ana ako aamuna awiri amene anabadwa ine ndisanabwere kuno adzakhala ana anga. Efereimu ndi Manase adzakhala anga monga mmene alili Rubeni ndi Simeoni.
6 Men dit Afkom, som du avler efter dem, skal høre dig til; de skulle kaldes efter deres Brødres Navn i deres Arv.
Koma amene ati adzabadwe pambuyo pa iwowa adzakhala ako ndipo cholowa chawo chidzadziwika ndi mayina a abale awo.
7 Og der jeg kom fra Paddan, døde Rakel for mig i Kanaans Land paa Vejen, der jeg havde endnu et Stykke Vej for at komme til Efrath, og jeg begrov hende der paa Vejen til Efrath, det er Bethlehem.
Pamene ndimabwerera kuchoka ku Parani, mwachisoni Rakele, amayi ako anamwalira mʼdziko la Kanaani, tikanali mʼnjira, mtunda wokafika ku Efurata ukanalipo. Ndipo ndinawayika kumeneko mʼmphepete mwa msewu wa ku Efurata” (amene ndi Betelehemu).
8 Og Israel saa Josefs Sønner og sagde: Hvo ere disse?
Israeli ataona ana a Yosefe anafunsa kuti, “Anyamatawa ndi a yani?”
9 Og Josef sagde til sin Fader: Det er mine Sønner, som Gad har givet mig her, og han sagde: Kære, led dem til mig, og jeg vil velsigne dem.
Yosefe anati kwa abambo ake, “Awa ndi ana anga amene Mulungu wandipatsa kuno.” Ndipo Israeli anati, “Bwera nawo kuno kuti ndiwadalitse.”
10 Og Israels Øjne vare matte af Alder, han kunde ikke se; og han lod dem komme til ham, og han kyssede dem og tog dem i Favn.
Koma maso a Israeli anali ofowoka chifukwa cha kukalamba moti sankaona nʼkomwe. Tsono Yosefe anabwera nawo ana ake aja pafupi ndi abambo ake ndipo abambo ake anawapsompsona nawakumbatira.
11 Og Israel sagde til Josef: Jeg havde ikke tænkt at se dit Ansigt, og se, Gud har endog ladet mig se din Sæd.
Israeli anati kwa Yosefe, “Ine sindinali kuyembekeza kuti nʼkudzaonanso nkhope yako, ndipo tsopano Mulungu wandilola kuti ndionenso ngakhale ana ako.”
12 Og Josef førte dem ud fra hans Knæ og bøjede sig med sit Ansigt til Jorden.
Tsono Yosefe anawachotsa ana aja pa mawondo a Israeli ndipo anamuweramira nkhope pansi.
13 Og Josef tog dem begge, Efraim i sin højre Haand, for Israels venstre Haand, og Manasse i sin venstre Haand, for Israels højre Haand, og lod dem komme nær til ham.
Yosefe anawagwira ana onse awiri padzanja, Efereimu ku dzanja lake lamanja kulunjika dzanja lamanzere la Israeli ndipo Manase ku dzanja lamanzere kulunjikitsa dzanja lamanja la Israeli, ndipo anawayandikiza kwa Yakobo.
14 Og Israel rakte sin højre Haand ud og lagde den paa Efraims Hoved, enddog han var den yngste, og sin venstre Haand paa Manasses Hoved; vidende gjorde han saaledes med sine Hænder, thi Manasse var den førstefødte.
Koma Israeli anapinganitsa mikono motero kuti anayika dzanja lake lamanja pamutu pa Efereimu ngakhale kuti iyeyo anali wamngʼono ndi dzanja lake lakumanzere analisanjika pamutu pa Manase ngakhale kuti iyeyu ndiye anali mwana woyamba.
15 Og han velsignede Josef og sagde: Den Gud, for hvis Ansigt mine Fædre, Abraham og Isak, vandrede, den Gud, som vogtede mig, fra jeg blev til, indtil denne Dag,
Kenaka anadalitsa Yosefe nati, “Mulungu amene makolo anga Abrahamu ndi Isake anamutumikira, Mulungu amene wakhala ali mʼbusa wanga moyo wanga wonse kufikira lero,
16 den Engel, som udløste mig fra alt ondt, velsigne Drengene, at de maa kaldes efter mit Navn og efter mine Fædres, Abrahams og Isaks, Navn, og at de maa blive saare mange midt i Landet.
mngelo amene wandipulumutsa ine ku zovuta zonse, ameneyo adalitse anyamata awa. Kudzera mwa iwowa dzina langa ndi mayina a makolo anga, Abrahamu ndi Isake, adzamveka. Iwowa adzakhala ndi ana ambiri nadzasanduka mtundu waukulu pa dziko lapansi.”
17 Der Josef saa, at hans Fader lagde sin højre Haand paa Efraims Hoved, da mishagede det ham; og han tog fat paa sin Faders Haand for at føre den fra Efraims Hoved paa Manasses Hoved.
Yosefe ataona kuti abambo ake ayika dzanja lamanja pa Efereimu, sanakondwere. Choncho anagwira dzanja la abambo ake kuti alichotse pamutu pa Efereimu ndi kuliyika pamutu pa Manase,
18 Og Josef sagde til sin Fader: Ikke saa, min Fader! thi denne er den førstefødte, læg din højre Haand paa hans Hoved.
nati kwa abambo ake, “Ayi, abambo anga, uyu ndiye woyamba kubadwa, ikani dzanja lanu lamanja pamutu pake.”
19 Men hans Fader vægrede sig og sagde: Jeg ved det, min Søn, jeg ved det; han skal ogsaa blive til Folk, og han skal ogsaa blive stor; men hans yngste Broder skal blive større end han, og hans Sæd skal være en stor Hob Folk.
Koma abambo ake anakana nati, “Ndikudziwa, mwana wanga, ndikudziwa. Adzukulu a iyeyunso adzakhala mtundu waukulu. Komabe mʼbale wake wamngʼonoyu adzakhala wamkulu kuposa iye, ndipo zidzukulu zake zidzakhala mitundu yayikulu ya anthu.”
20 Saa velsignede han dem paa den samme Dag og sagde: Ved dig skal Israel velsigne og sige: Gud sætte dig som Efraim og som Manasse! og han satte Efraim foran Manasse.
Tsono iye anawadalitsa tsiku limenelo nati, “Aisraeli adzagwiritsa ntchito dzina lanu podalitsa nadzati: Mulungu akudalitseni monga Efereimu ndi Manase.” Choncho anayika Efereimu patsogolo pa Manase.
21 Og Israel sagde til Josef: Se, jeg dør, og Gud skal være med eder og føre eder til eders Fædres Land igen.
Kenaka Israeli anati kwa Yosefe, “Ine ndatsala pangʼono kufa, koma Mulungu adzakhala ndipo adzakutenganinso kubwerera nanu ku dziko la makolo anu.
22 Og jeg har givet dig fremfor dine Brødre et Stykke Land, som jeg har taget af Amoriternes Haand med mit Sværd og med min Bue.
Ndiponso iwe wekha ndikupatsa moposera abale ako, malo woonjezera, Sekemu, malo amene ndinalanda kwa Aamori ndi lupanga ndi uta wanga.”

< 1 Mosebog 48 >