< 1 Mosebog 45 >

1 Og Josef kunde ikke holde sig for alle dem, som stode hos ham, og han raabte: Lader hver Mand gaa ud fra mig; og ikke een Mand stod hos ham, der Josef lod sig kende for sine Brødre.
Tsono Yosefe sanathenso kuwugwira mtima kuti asalire pamaso pa antchito ake ndipo anafuwula kuti, “Aliyense achoke pamaso panga!” Motero panalibe wina aliyense pamene Yosefe anadziwulula kwa abale ake.
2 Og han opløftede sin Røst med Graad, og Ægypterne hørte det, og Faraos Hus hørte det.
Ndipo analira mokweza mwakuti Aigupto anamva. Onse a ku nyumba kwa Farao anamvanso za zimenezi.
3 Og Josef sagde til sine Brødre: Jeg er Josef; lever min Fader endnu? og hans Brødre kunde ikke svare ham; thi de forfærdedes for hans Ansigt.
Yosefe anati kwa abale ake, “Ine ndine Yosefe! Kodi abambo anga akanali ndi moyo?” Koma abale ake sanathe kumuyankha chifukwa anali ndi mantha kwambiri pamaso pake.
4 Da sagde Josef til sine Brødre: Kommer dog hid til mig; og de gik frem; og han sagde: Jeg er Josef, eders Broder, som I solgte til Ægypten.
Ndipo Yosefe anati kwa abale ake, “Senderani pafupi nane.” Atasendera iye anati, “Ine ndine mʼbale wanu Yosefe amene munamugulitsa ku Igupto!
5 Men værer nu ikke bekymrede, og lader det ikke være mishageligt for eders Øjne, at I solgte mig hid; thi for at I skulde blive holdte ved Live, har Gud sendt mig hid foran eder.
Ndipo tsopano, musawawidwe mtima kapena kudzipsera mtima chifukwa choti munandigulitsa ine kuno, popeza Mulungu ananditsogoza ine kuti adzapulumutse miyoyo yanu.
6 Thi nu har der været to Aar Hunger i Landet, og endnu er der fem Aar, i hvilke der ikke skal være Pløjning eller Høst.
Kwa zaka ziwiri tsopano, kwakhala kuli njala mʼdziko muno, ndipo kwa zaka zisanu zikubwerazi, anthu sadzalima kapena kukolola.
7 Men Gud har sendt mig foran eder, at lade eder blive tilovers i Landet og at lade eder leve, til en stor Befrielse.
Koma Mulungu ananditsogoza kuti adzakusungeni ndi moyo ndi kuti mudzakhale ndi zidzukulu pa dziko lapansi.
8 Og nu, ikke I have sendt mig hid, men Gud; og han har sat mig til en Fader for Farao og til en Herre over alt hans Hus og til en Hersker i alt Ægyptens Land.
“Motero, si inu amene munanditumiza kuno koma Mulungu. Iye anandisandutsa kukhala nduna yayikulu ya Farao, ndipo zonse za mʼnyumba mwake zili mʼmanja mwangamu. Komanso amene akulamulira dziko lonse la Igupto ndi ine.
9 Skynder eder og drager op til min Fader, og I skulle sige til ham: Saa siger din Søn Josef: Gud har sat mig til en Herre over al Ægypten; kom ned til mig, tøv ikke!
Tsono fulumirani mubwerere kwa abambo anga ndi kuwawuza kuti, ‘Mwana wanu Yosefe akuti, Mulungu anandisandutsa kukhala mbuye wa dziko lonse la Igupto. Ndiye bwerani kuno musachedwe.
10 Og du skal bo i Gosen Land og være nær hos mig, du og dine Børn og dine Børnebørn og dit Kvæg og dine Øksen og alt det, du har.
Ndipo inu, ana anu, zidzukulu zanu, pamodzi ndi nkhosa ndi ngʼombe zanu ndi antchito anu amene muli nawo muzidzakhala mʼdziko la Goseni pafupi ndi ine.
11 Og jeg vil opholde dig der; thi endnu er der fem Aar Hunger; paa det du ikke skal forarmes, du og dit Hus og alt det, som tilhører dig.
Ine ndizidzakupatsani zakudya kumeneko chifukwa zaka zisanu za njala zikubwera ndithu. Kupanda kutero, inu ndi mabanja anu pamodzi ndi anthu anu onse mudzasowa chakudya.’
12 Og se, eders Øjne og min Broder Benjamins Øjne se, at jeg taler mundtligen til eder.
“Tsono inu nonse pamodzi ndi mʼbale wangayu Benjamini, mukuona kuti ndi inedi amene ndikuyankhula nanu.
13 Og I skulle forkynde min Fader al min Herlighed i Ægypten, og alt det, som I have set; og skynder eder og lader min Fader komme hid ned.
Mukawawuze abambo anga kuti ndili pa ulemerero ku dziko la Igupto kuno ndi zonse zimene mwaziona. Tsopano fulumirani kuti mukabwere nawo kuno abambo anga.”
14 Saa faldt han om Benjamins, sin Broders, Hals og græd, og Benjamin græd om hans Hals.
Kenaka Yosefe anakhumbatira Benjamini, mngʼono wake uja nayamba kulira. Nayenso Benjamini anayamba kulira atamukumbatira.
15 Og han kyssede alle sine Brødre og græd over dem, og derefter talede hans Brødre med ham.
Atatero, Yosefe anapsompsona abale ake onse aja, akulira. Pambuyo pake abale ake aja anacheza ndi Yosefe.
16 Og det rygtedes i Faraos Hus, og der sagdes: Josefs Brødre ere komne; det var godt baade i Faraos Øjne og i hans Tjeneres Øjne.
Akunyumba kwa Farao atamva kuti abale ake a Yosefe abwera, Farao pamodzi ndi nduna zake zonse anakondwera.
17 Og Farao sagde til Josef: Sig til dine Brødre: gører dette, belæsser eders Dyr og gaar, at I maa komme til Kanaans Land.
Farao anati kwa Yosefe, “Uwawuze abale ako kuti, ‘Senzetsani nyama zanu katundu ndi kubwerera ku dziko la Kanaani.
18 Og tager eders Fader og eders Husfolk og kommer til mig, og jeg vil give eder det bedste i Ægyptens Land, at I skulle æde af Landets Fedme.
Mukabwere nawo abambo anu ndi mabanja anu kuno, ndipo ine ndidzakupatsani dera lachonde kwambiri mʼdziko la Igupto. Mudzadya zokoma za mʼdzikoli.’”
19 Og det er dig befalet: gører dette; tager eder Vogne af Ægyptens Land til eders Børn og til eders Hustruer, og fører eders Fader der paa og kommer.
“Uwawuzenso kuti, ‘Tengani ngolo zingapo za kuno ku Igupto kuti mukakwezepo ana anu, akazi anu pamodzi ndi abambo ako ndi kubwera nawo kuno.
20 Og lader eders Øjne ikke se hen til eders Boskab; thi det bedste, som er i alt Ægyptens Land, er eders.
Musadandaule zosiya katundu komweko chifukwa dziko lachonde la kuno ku Igupto lidzakhala lanu.’”
21 Og Israels Sønner gjorde saa, og Josef gav dem Vogne efter Faraos Ord og gav dem Tæring paa Vejen.
Choncho ana a Israeli anachita zimenezo. Yosefe anawapatsa ngolo monga Farao analamulira, ndipo anawapatsanso chakudya cha paulendo wawo.
22 Han gav alle, hver især, Klædninger til at skifte med; men Benjamin gav han tre Hundrede Sekel Sølv og fem Klædninger til at skifte med.
Anaperekanso kwa aliyense zovala zatsopano, koma kwa Benjamini anapereka siliva wolemera pafupifupi makilogalamu anayi ndi zovala zisanu.
23 Og han sendte sin Fader ligervis ti Asener, som bare af Ægyptens bedste Gods, og ti Aseninder, som bare Korn og Brød og Føde, til hans Fader paa Vejen.
Ndipo abambo ake anawatumizira izi: abulu khumi osenza zinthu zabwino kwambiri za ku Igupto, ndi abulu aakazi khumi osenza tirigu, buledi ndi zakudya zina za pa ulendo wake.
24 Og han lod sine Brødre fare, og de gik; og han sagde til dem: Kives ikke paa Vejen!
Kenaka anawalola abale ake aja kuti azipita, ndipo akunyamuka, iye anawawuza kuti, “Osakangana mʼnjira!”
25 Saa droge de op af Ægypten, og de kom til det Land Kanaan, til Jakob, deres Fader.
Ndipo anachoka ku Igupto nafika kwa abambo awo Yakobo mʼdziko la Kanaani.
26 Og de forkyndte ham, sigende: Josef lever endnu, og han er en Hersker over alt Ægyptens Land; men hans Hjerte blev koldt, thi han troede dem ikke.
Iwo anawuza abambo awo kuti, “Yosefe akanali ndi moyo! Ndiponsotu, ndiye akulamulira dziko la Igupto.” Yakobo anangoti kakasi osankhulupirira.
27 Da sagde de ham alle Josefs Ord, som han havde sagt til dem, og han saa Vognene, som Josef havde sendt til at føre ham paa; og Jakobs, deres Faders, Aand blev levende.
Komabe atamufotokozera zonse zimene Yosefe anawawuza ndipo ataona ngolo zimene Yosefe anatumiza kuti adzakweremo popita ku Igupto, mtima wa Yakobo, abambo awo unatsitsimuka.
28 Og Israel sagde: Det er meget, Josef min Søn lever endnu; jeg vil fare hen og se ham, før jeg dør.
Ndipo Israeli anati, “Ndatsimikizadi! Mwana wanga Yosefe akanali ndi moyodi. Ndipita ndikamuone ndisanafe.”

< 1 Mosebog 45 >