< 1 Mosebog 42 >
1 Der Jakob saa, at Korn var til fals i Ægypten, da sagde Jakob til sine Sønner: Hvi se I paa hverandre?
Yakobo atamva kuti ku Igupto kuli tirigu, anati kwa ana ake, “Nʼchifukwa chiyani mukungoyangʼanana wina ndi mnzake?
2 Og han sagde: Se, jeg hører, at der er Korn til føls i Ægypten, farer did ned og køber til os derfra, at vi maa leve og ikke dø.
Ine ndamva kuti ku Igupto kuli tirigu. Pitani kumeneko mukatigulireko kuti tisafe ndi njala.”
3 Saa droge Josefs ti Brødre ned at købe Korn i Ægypten.
Choncho abale ake khumi a Yosefe anapita kukagula tirigu ku Igupto.
4 Men Jakob lod ikke Benjamin, Josefs Broder, fare med sine Brødre; thi han sagde: Der kunde vederfares ham nogen Ulykke.
Koma Yakobo sanamulole Benjamini mngʼono wake wa Yosefe kuti apite nawo chifukwa anaopa kuti choyipa chingamuchitikire.
5 Saa kom Israels Sønner at købe iblandt dem, som kom; thi der var Hunger i Landet Kanaan.
Choncho ana a Israeli aja anapita pamodzi ndi gulu la anzawo kukagula tirigu pakuti ku Kanaani kunalinso njala.
6 Og Josef var Regent over Landet, han var den, som solgte til alt Folket i Landet; og Josefs Brødre kom, og de faldt ned for ham paa deres Ansigt til Jorden.
Pakuti Yosefe anali nduna yayikulu yolamulira dziko la Igupto, ndiye kuti analinso amene ankagulitsa tirigu kwa anthu onse. Choncho abale ake a Yosefe nawonso anabwera, ndipo anamugwadira pansi.
7 Og Josef saa sine Brødre og kendte dem og holdt sig fremmed mod dem og talede haarde Ting med dem og sagde til dem: Hvorfra komme I? og de sagde: Fra det Land Kanaan for at købe Spise.
Yosefe atangowaona abale ake anawazindikira, koma ananamizira kukhala ngati mlendo nawayankhula mwaukali kuwafunsa kuti, “Mwachokera kuti?” Iwo anayankha, “Ku dziko la Kanaani, tikudzagula chakudya.”
8 Og Josef kendte sine Brødre; men de kendte ikke ham.
Ngakhale Yosefe anawazindikira abale ake, koma iwo sanamuzindikire.
9 Og Josef kom de Drømme i Hu, som han havde drømt om dem, og sagde til dem: I ere Spejdere, I ere komne at bese, hvor Landet er blot.
Pamenepo anakumbukira maloto aja amene analota za iwo ndipo anati, “Inu ndinu akazitape! Mwabwera kudzazonda dziko lathu kuti muone pamene palibe chitetezo.”
10 Og de sagde til ham: Nej, min Herre! men dine Tjenere ere komne for at købe Spise.
Iwo anayankha, “Ayi mbuye wathu, antchito anufe tabwera kudzagula chakudya.
11 Vi ere alle een Mands Sønner, vi ere redelige, dine Tjenere ere ikke Spejdere.
Tonse ndife ana a munthu mmodzi. Ndife antchito anu okhulupirika osati akazitape.”
12 Og han sagde til dem: Nej, men I ere komne for at bese, hvor Landet er blot.
Iye anawawuza kuti, “Ayi! Inu mwabwera kudzaona pamene palibe chitetezo mʼdziko muno.”
13 De svarede: Vi, dine Tjenere, vare tolv Brødre, een Mands Sønner i Kanaans Land; og se, den yngste er endnu hos vor Fader, men den ene er ikke til.
Koma iwo anayankha, “Tinalipo ana aamuna khumi ndi awiri. Abambo athu ndi mmodzi, ndipo kwathu ndi ku Kanaani. Panopo wotsiriza ali ndi abambo athu ndipo wina anamwalira.”
14 Og Josef sagde til dem: Det er det, som jeg har talet til eder, der jeg sagde: I ere Spejdere.
Yosefe anawawuza kuti, “Ndi momwe ndaneneramo: Inu ndinu akazitape.
15 Derpaa skulle I prøves: saa sandt Farao lever, skulle I ikke komme herfra, uden eders yngste Broder kommer hid.
Ndiye ndikuyesani motere: Ine ndikulumbira pali Farao ndithu, inuyo simudzachoka malo ano mpaka wotsirizayo atabwera kuno.
16 Sender een af eder bort, at han skal hente eders Broder; men I skulle være fangne, og eders Ord skulle prøves, om I fare med Sandhed; thi hvis ikke, da ere I, saa sandt Farao lever, Spejdere.
Tumizani mmodzi wa inu akamutenge mʼbale wanuyo ndipo ena nonsenu musungidwa mʼndende, kuti titsimikize ngati zimene mukunenazi ndi zoona. Apo ayi, pali Farao ndithu, inu ndinu akazitape!”
17 Og han satte dem tilsammen i Forvaring i tre Dage.
Ndipo onse anawayika mʼndende kwa masiku atatu.
18 Men den tredje Dag sagde Josef til dem: Gører dette, saa skulle I leve; jeg frygter Gud.
Pa tsiku lachitatu Yosefe anawawuza kuti, “Popeza ine ndimaopa Mulungu, ndipo inuyo ngati mukufuna kukhala ndi moyo muchite izi:
19 Dersom I ere redelige, da lader een af eders Brødre blive som Fange i eders Forvaringshus; men farer I andre hen og fører det hjem, som I have købt mod Hungeren, for eders Huse,
Ngati muli anthu achilungamo, mmodzi wa inu atsale mʼndende, pamene ena nonse mupite kwanu kuti muwatengere chakudya anthu akwanu kuli njalako.
20 og henter eders yngste Broder til mig, saa skulle eders Ord tros, og I skulle ikke dø; og de gjorde saaledes.
Mukabwere naye kuno mngʼono wanu wotsirizayo kuti titsimikizire zimene munanena kuti musafe.” Ndipo anachita zomwezo.
21 Men de sagde den ene til den anden: Vi have sandelig forskyldt dette for vor Broder, da vi saa hans Sjæls Angest, idet han bad os, og vi vilde ikke høre, derfor kommer denne Angest over os.
Iwo anati kwa wina ndi mnzake, “Ndithu ife tinalakwira mʼbale wathu uja popeza kuti ngakhale tinaona kuvutika kwake ndi kumva kulira kwake pamene ankatidandaulira kuti timuchitire chifundo, koma ife sitinamvere. Nʼchifukwa chake masautso awa atigwera.”
22 Og Ruben svarede dem og sagde: Talede jeg det ikke til eder, der jeg sagde: synder ikke mod Drengen, og I hørte ikke? og se, nu kræves ogsaa hans Blod.
Rubeni anayankha, “Kodi sindinakuwuzeni kuti musamuchite kanthu mnyamata uja? Koma inu simunamvere! Tsopano tikulandira malipiro a magazi ake.”
23 Men de vidste ikke, at Josef forstod det; thi der var en Tolk imellem dem.
Koma sanadziwe kuti Yosefe ankawamva popeza kuti ankagwiritsa ntchito wotanthauzira poyankhula naye.
24 Og han vendte sig fra dem og græd, og han vendte sig til dem igen og talede med dem og tog Simeon fra dem og lod ham binde for deres Øjne.
Yosefe anapita pambali payekha kukalira. Kenaka anabweranso nadzayankhula nawo. Iye anatenga Simeoni namumanga iwo akuona.
25 Og Josef befalede, at man skulde fylde deres Poser med Korn og give dem deres Penge igen, hver i sin Sæk, og give dem Tæring paa Vejen; og han gjorde saa mod dem.
Yosefe analamula kuti awadzazire matumba awo ndi tirigu, awayikiremo ndalama zawo momwemo ndiponso awapatse chakudya cha panjira. Izi anawachitiradi.
26 Og de lagde deres Korn paa deres Asener og fore derfra.
Abale a Yosefe aja anasenzetsa abulu awo tirigu amene anagula uja ndipo ananyamuka ulendo wawo.
27 Men der den ene lod sin Sæk op for at give sit Asen Foder i Herberget, da saa han sine Penge, og se, de laa oven i hans Pose.
Atafika pamalo pena poti agone, mmodzi mwa iwo anatsekula thumba lake kuti atapemo chakudya cha bulu wake. Atangomasula anaona kuti ndalama zake zili pakamwa pa thumba.
28 Og han sagde til sine Brødre: Mine Penge ere komne igen, og se, de ere her i min Pose; da faldt deres Mod, og de forskrækkedes den ene med den anden og sagde: Hvorfor har Gud gjort os dette?
Iye anati kwa abale akewo, “Ndalama zanga andibwezera, izi zili mʼthumba mwangamu.” Mitima yawo inachita ngati yachokamo ndipo anali ndi mantha ambiri, nati, “Ndi chiyani chimene Mulungu watichitira?”
29 Og de kom til Jakob, deres Fader, til Kanaans Land; og de gave ham til Kende alt det, som var dem vederfaret, og sagde:
Atafika kwa abambo awo Yakobo mʼdziko la Kanaani anafotokoza zonse zimene zinawachitikira nati,
30 Den Mand, som er Herre i Landet, talte os haardelig til og holdt os for Landets Spejdere.
“Nduna yayikulu ya mʼdzikomo inatiyankhula mwa ukali kwambiri ndipo inkatiyesa kuti ndife akazitape.
31 Og vi svarede ham: vi ere redelige, vi ere ikke Spejdere.
Koma tinamuwuza kuti, ‘Ndife anthu woona mtima osati akazitape.
32 Vi vare tolv Brødre, vor Faders Sønner, den ene er ikke til, og den yngste er endnu hos vor Fader i Kanaans Land.
Ife tonse tinalipo ana aamuna khumi ndi awiri, abambo mmodzi. Mmodzi anamwalira, ndipo wamngʼono ali ndi abambo athu ku Kanaani.’”
33 Da sagde Manden, Landets Herre, til os: derpaa vil jeg kende, om I ere redelige: lader den ene af eders Brødre blive hos mig, og tager, hvad I behøve mod Hungeren for eders Huse, og farer hen
Ndipo nduna ija inati kwa ife, “Kuti ndidziwedi kuti ndinu anthu owona mtima muchite izi: Mmodzi mwa inu atsale ndi ine kuno, ndipo enanu mutenge chakudya ndi kubwerera kwanu kumene kuli njalako.
34 og henter eders yngste Broder til mig, saa kan jeg kende, at I ikke ere Spejdere, men at I ere redelige; saa vil jeg give eder eders Broder igen, og I maa handle i Landet.
Koma mundibweretsere wotsirizayo kuti ndidziwedi kuti sindinu akazitape koma anthu achilungamo. Kenaka ndidzakubwezerani mʼbale wanuyu ndipo mukhoza kuchita malonda mʼdzikoli.”
35 Og det skete, der de tømte deres Sække, se, da var hvers Pengeknude i hans Sæk; og de saa deres Pengeknuder, de og deres Fader, og frygtede.
Pamene amakhuthula matumba awo a tirigu aliyense anapeza kuti kathumba kake ka ndalama kali momwemo. Ataona zimenezi, iwo pamodzi ndi abambo awo anachita mantha kwambiri.
36 Da sagde Jakob, deres Fader, til dem: I berøve mig mine Børn; Josef er ikke til, og Simeon er ikke til, og Benjamin ville I tage hen; over mig kommer det altsammen.
Abambo awo Yakobo anawawuza kuti, “Mwandilanda ana anga ine. Yosefe anamwalira ndipo Simeoni palibenso, ndiye tsopano mukufuna mutengenso Benjamini. Zonsezi zandigwera ine!”
37 Og Ruben talede til sin Fader og sagde: Du maa slaa begge mine Sønner ihjel, om jeg ikke fører ham til dig igen; giv ham i min Haand, og jeg vil føre ham til dig igen.
Koma Rubeni anati kwa abambo ake, “Ngati sindidzabwera naye kwa inu, mudzaphe ana anga aamuna awiri. Muperekeni mʼmanja mwangamu ndipo ndidzamusamala ndi kubwera naye kwa inu.”
38 Og han sagde: Min Søn skal ikke fare ned med eder; thi hans Broder er død, og han alene er bleven tilbage, og møder ham nogen Ulykke paa Vejen, som I drage hen paa, da skulle I føre mine graa Haar med Sorg til Graven. (Sheol )
Koma Yakobo anati, “Mwana wanga sapita nanu kumeneko; mkulu wake anamwalira ndipo watsala yekha. Ngati choyipa chitamuchitikira pa ulendo mukupitawu, ndiye kuti ndi mmene ndakalambiramu inu mudzandipha ndi chisoni chotere.” (Sheol )