< 1 Mosebog 4 >

1 Og Adam kendte sin Hustru Eva; og hun undfik og fødte Kain og sagde: Jeg har faaet en Mand, som er Herren.
Adamu anagona malo amodzi ndi Hava mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Kaini, ndipo anati, “Ndi thandizo la Yehova ndapeza mwana wamwamuna.”
2 Og hun blev ved at føde, nemlig hans Broder Abel; og Abel blev en Faarehyrde, og Kain dyrkede Jorden.
Kenaka anabereka mʼbale wake Abele. Abele anali woweta nkhosa ndipo Kaini anali mlimi.
3 Og det hændte sig, der en Tid var forløben, og Kain frembar et Offer til Herren af Jordens Frugt.
Patapita nthawi, Kaini anatenga zipatso za ku munda nakazipereka kwa Yehova monga nsembe.
4 Og Abel, ogsaa han bar frem af sin Hjords første Affødning og af deres Fedme; og Herren saa til Abel og til hans Offer.
Nayenso Abele anatenga ana ankhosa oyamba kubadwa pamodzi ndi mafuta ake nakazipereka ngati nsembe kwa Yehova. Yehova anakondwera ndi Abele ndi nsembe yake.
5 Men til Kain og til hans Offer saa han ikke; da blev Kain meget vred, og hans Ansigt falmede.
Koma sanakondwere ndi Kaini ndi nsembe yake. Kotero Kaini anakwiya kwambiri ndipo nkhope yake inagwa.
6 Og Herren sagde til Kain: Hvi er du vred, og hvi er dit Ansigt falmet?
Choncho Yehova anati kwa Kaini, “Chifukwa chiyani wakwiya ndipo bwanji nkhope yako yagwa?
7 Er det ikke saa, at dersom du gør godt, da er du behagelig, og dersom du ikke gør godt, da ligger Synden for Døren, og til dig er dens Attraa? men du skal herske over den.
Ukanachita zabwino sindikanakulandira kodi? Koma tsopano wachita zoyipa ndipo tchimo likukudikira pa khomo pako, likufuna kukugwira; koma iwe uyenera kugonjetsa tchimolo.”
8 Og Kain talede med Abel sin Broder; og det hændte sig, der de vare paa Marken, da stod Kain op imod Abel sin Broder og ihjelslog ham.
Tsiku lina Kaini anati kwa mʼbale wake Abele, “Tiye tipite ku munda.” Ndipo ali ku mundako, Kaini anawukira mʼbale wake namupha.
9 Og Herren sagde til Kain: Hvor er Abel, din Broder? Og han sagde: Jeg ved ikke, mon jeg være min Broders Vogter?
Ndipo Yehova anamufunsa Kaini kuti, “Ali kuti mʼbale wako Abele?” Iye anayankha kuti, “Sindikudziwa. Kodi ine ndine wosunga mʼbale wanga?”
10 Og han sagde: Hvad har du gjort? din Broders Blods Røst raaber til mig af Jorden.
Yehova anati, “Kodi wachita chiyani? Tamvera! Magazi a mʼbale wako akulirira kwa Ine kuchokera mʼnthaka.
11 Og nu være du forbandet fra Jorden, som oplod sin Mund til at tage din Broders Blod af din Haand.
Ndipo tsopano ndiwe wotembereredwa ndipo wachotsedwa mʼdziko limene nthaka yake inatsekula pakamwa pake kulandira magazi a mʼbale wako amene unakhetsa.
12 Naar du dyrker Jorden, skal den ikke ydermere give dig sin Kraft; ustadig og flygtig skal du være paa Jorden.
Udzalima munda koma nthakayo sidzakupatsanso zokolola zake. Udzakhala wosakhazikika; womangoyendayenda pa dziko lapansi.”
13 Da sagde Kain til Herren: Min Misgerning er større, end jeg kan bære.
Kaini anati kwa Yehova, “Chilango changa ndi chachikulu kuposera mphamvu zanga.
14 Se, du har i Dag drevet mig fra Jordens Kreds, og jeg maa skjule mig for dit Ansigt; og jeg bliver ustadig og flygtig paa Jorden, og det vil ske, hvo som finder mig, slaar mig ihjel.
Lero mukundipirikitsa pa dziko ndi pamaso panu; ndidzakhala wosakhazikika, woyendayenda, ndipo aliyense amene adzandipeze adzandipha.”
15 Men Herren sagde til ham: Derfor, hvo som ihjelslaar Kain, paa ham skal det hævnes syvfold; saa satte Herren for Kain et Tegn, at ingen, som fandt ham, skulde slaa ham ihjel.
Koma Yehova anamuwuza kuti, “Sizidzatero ayi; aliyense amene adzaphe Kaini adzalangidwa ndi kulipiritsidwa kasanu ndi kawiri.” Pamenepo Yehova anayika chizindikiro pa Kaini kuti aliyense womupeza asamuphe.
16 Saa gik Kain ud fra Herrens Ansigt og blev i det Land Nod Østen for Eden.
Ndipo Kaini anachoka pamaso pa Yehova nakakhala ku dziko la Nodi, kummawa kwa Edeni.
17 Og Kain kendte sin Hustru, og hun undfik og fødte Hanok; og han byggede en Stad og kaldte Stadens Navn efter sin Søns Navn, Hanok.
Kaini anagona malo amodzi ndi mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Enoki. Kaini nthawi imeneyo nʼkuti akumanga mzinda ndipo anawutcha dzina la mwana wake Enoki.
18 Og for Hanok blev født Irad, og Irad avlede Mehujael, og Mehujael avlede Mathusael, og Mathusael avlede Lamek.
Enoki anabereka Iradi; Iradi anabereka Mehuyaeli, ndipo Mehuyaeli anabereka Metusela, ndipo Metusela anabereka Lameki.
19 Og Lamek tog sig to Hustruer, den enes Navn var Ada, og den andens Navn Zilla.
Lameki anakwatira akazi awiri, wina dzina lake linali Ada ndi winayo dzina lake linali Zila.
20 Og Ada fødte Jabal; han var Fader til dem, som boede i Telte og vogtede Kvæg.
Ada anabereka Yabala; iyeyu anali kholo la onse okhala mʼmatenti ndi oweta ziweto.
21 Og hans Broders Navn var Jubal; han var Fader til alle dem, der legede paa Harpe og Fløjte.
Dzina la mʼbale wake linali Yubala; iyeyu anali kholo la onse oyimba zeze ndi chitoliro.
22 Og Zilla, ogsaa hun fødte, nemlig Thubalkain, som kunstigen gjorde alle Haande skarpt Kobber- og Jerntøj; og Thubalkains Søster var Naama.
Zila nayenso anali ndi mwana wamwamuna, dzina lake Tubala-Kaini. Iyeyu anali kholo la amisiri onse osula zida za mkuwa ndi chitsulo. Mlongo wake wa Tubala-Kaini anali Naama.
23 Og Lamek sagde til sine Hustruer: Ada og Zilla, hører min Røst, Lameks Hustruer, mærker min Tale! Om jeg har slagen en Mand ihjel, mig til et Saar, og en Dreng, mig til en Byld:
Lameki anawuza akazi akewo kuti, “Ada ndi Zila, ndimvereni; inu akazi anga imvani mawu anga. Ine ndinapha munthu chifukwa anandipweteka. Ndinapha mnyamatayo chifukwa anandimenya.
24 da skal Kain hævnes syvfold, og Lamek halvfjerdsindstyve Gange og syv Gange.
Ngati wopha Kaini amulipsira kasanu nʼkawiri, ndiye kuti wopha ine Lameki adzamulipsira kokwanira 77.”
25 Og Adam kendte ydermere sin Hustru, og hun fødte en Søn og kaldte hans Navn Seth; thi Gud har sat mig, sagde hun, en anden Sæd i Abels Sted; thi Kain slog ham ihjel.
Adamu anagonanso malo amodzi ndi mkazi wake, ndipo anabereka mwana wamwamuna namutcha Seti, kutanthauza kuti, “Mulungu wandipatsa mwana wina mʼmalo mwa Abele, popeza Kaini anamupha.”
26 Og for Seth blev og født en Søn, og han kaldte hans Navn Enos; da begyndte man at paakalde Herrens Navn.
Seti naye anali ndi mwana wa mwamuna, ndipo anamutcha Enosi. Pa nthawi imeneyi anthu anayamba kupemphera mʼdzina la Yehova.

< 1 Mosebog 4 >