< Ezekiel 46 >

1 Saa siger den Herre, Herre: Den indre Forgaards Port, som vender imod Østen, skal være tillukket de seks Arbejdsdage; men paa Sabbatens Dag skal den oplades, og paa Nymaanedens Dag skal den oplades.
“Ambuye Yehova akuti, Chipata chakummawa cha bwalo lamʼkati chizikhala chotseka pa masiku asanu ndi limodzi ogwira ntchito, koma chizitsekulidwa pa tsiku la sabata ndi pa tsiku la chikondwerero cha mwezi watsopano.
2 Og Fyrsten skal gaa ind ad Vejen til Portens Forhal udenfra og staa ved Portens Dørstolper; og Præsterne skulle tilberede hans Brændoffer og hans Takofre, og han skal tilbede paa Dørtærskelen, i Porten, og saa gaa ud; og Porten skal ikke tillukkes inden Aftenen.
Mfumu izilowa podzera mʼkhonde la mʼkati la chipata pochokera kunja, nʼkudzayima pafupi ndi nsanamira yapakhomo. Ansembe apereke nsembe yake yopsereza ndi nsembe yake yachiyanjano. Mfumuyo ipembedze pa chiwundo cha pa chipatacho kenaka nʼkutuluka. Koma chipatacho asachitseke mpaka madzulo.
3 Og Landets Folk skal tilbede ved Indgangen til samme Port, paa Sabbaterne og paa Nymaanederne, for Herrens Ansigt.
Anthu a mʼdziko azipembedza pamaso pa Yehova pa khomo la chipata chimenechi pa masiku a sabata ndi pa tsiku la mwezi watsopano.
4 Og Brændofferet, som Fyrsten skal bringe Herren paa Sabbatens Dag, skal bestaa i seks lydefrie Lam og een lydefri Væder.
Nsembe yopsereza imene mfumu iyenera kupereka kwa Yehova ikhale motere: pa tsiku la Sabata izipereka ana ankhosa aamuna asanu ndi mmodzi wopanda chilema, ndiponso nkhosa yayima yopanda chilema.
5 Og Madofferet skal være en Efa med Væderen, og med Lammene et Madoffer, som hans Haand maatte give; og en Hin Olie til hver Efa.
Pamodzi ndi nkhosa yayimuna, mfumu izipereka nsembe ya chakudya yokwanira efa imodzi. Pamodzi ndi ana ankhosa, mfumu izipereka monga ikufunira kutero. Iperekenso hini imodzi ya mafuta pa efa iliyonse ya tirigu.
6 Men paa Nymaanedens Dag skal det være en lydefri ung Okse og seks Lam og en Væder, de skulle være lydefrie.
Pa tsiku la mwezi watsopano mfumuyo ipereke mwana wangʼombe wamwamuna, ana ankhosa asanu ndi mmodzi ndiponso nkhosa yayimuna, zonsezi zopanda chilema.
7 Og som Madoffer skal han ofre en Efa med Oksen og en Efa med Væderen, men med Lammene saa meget, som hans Haand formaar; og at Olie en Hin til hver Efa.
Ipereke efa imodzi ya tirigu pa ngʼombe yayimuna iliyonse ndiponso efa ina pa nkhosa yayimuna iliyonse. Pa ana ankhosa ipereke tirigu monga ikufunira kutero. Pamodzi ndi efa ya tirigu, ipereke hini imodzi ya mafuta.
8 Og naar Fyrsten gaar ind, skal han gaa ind ad Vejen til Portens Forhal og gaa ud ad samme Vej.
Pamene mfumu ikulowa, izidzera mʼkhonde lamʼkati la chipata chakummawa, izitulukiranso pomwepo.
9 Og naar Folket i Landet gaar ind for Herrens Ansigt paa Højtiderne, skal den, som gaar ind ad den nordre Ports Vej for at tilbede, gaa ud ad den søndre Ports Vej; og den, som gaar ind ad den søndre Ports Vej, skal gaa ud ad den nordre Ports Vej; man skal ikke gaa tilbage ad den Ports Vej, som man gik ind ad, men de skulle gaa ud hver lige frem for sig.
“Anthu a mʼdzikomo akabwera kudzapembedza Yehova pa masiku a chikondwerero, ngati munthu alowera pa chipata chakumpoto atulukire chipata chakummwera. Munthu wolowera chipata chakummwera, atulukire chipata chakumpoto. Munthu asatulukire pomwe walowera, koma atulukire pa chipata choyangʼanana nacho.
10 Og Fyrsten, han skal gaa ind midt iblandt dem, naar de gaa ind, og naar de gaa ud, skulle de gaa ud sammen.
Mfumu izidzakhala pakati pawo. Anthu akamadzalowa mfumu idzalowa nawo. Anthu akamadzatuluka mfumu idzatuluka nawo.
11 Men paa Festerne og paa Højtiderne skal Madofferet være en Efa med Oksen og en Efa med Væderen, men med Lammene, hvad hans Haand maatte give; og af Olie en Hin til hver Efa.
“Pa masiku achikondwerero ndi pa masiku ena osankhidwa, zopereka za chakudya zikhale zokwanira efa imodzi pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, efa imodzinso ndi nkhosa yayimuna, koma pa mwana wankhosa apereke monga angathere. Iperekenso hini imodzi ya mafuta pa efa iliyonse.
12 Og naar Fyrsten vil gøre et frivilligt Offer, Brændoffer eller Takofre, frivilligt for Herren, da skal man oplade ham Porten, som vender imod Østen, og han skal bringe sit Brændoffer og sine Takofre, ligesom han gør paa Sabbatens Dag; og han skal gaa ud, og man skal lukke Porten, efter at han er udgangen.
Pamene mfumu ikufuna kupereka chopereka chaufulu kwa Yehova, kaya ndi nsembe yopsereza kapena zopereka za chiyanjano, ayitsekulire chipata chakummawa. Iyo ipereke nsembe yopsereza kapena zopereka zake za chiyanjano monga imachitira pa tsiku la Sabata. Kenaka ituluke ndipo mfumuyo itatuluka, atseke chitsekocho.
13 Og du skal ofre et lydefrit Lam, eet Aar gammelt, til Brændoffer dagligt for Herren; hver Morgen skal du ofre det.
“Tsiku lililonse nthawi ya mmawa azipereka kwa Yehova mwana wankhosa wa chaka chimodzi.
14 Og du skal ofre som Madoffer dertil hver Morgen en Sjettedel af en Efa, og en Tredjedel af en Hin Olie til at væde det fine Mel med; det er et Madoffer for Herren, evige Bestemmelser for bestandigt.
Pamodzi ndi nyamayo aziperekanso mmawa uliwonse chopereka cha chakudya chokwanira chimodzi mwa zigawo zisanu ndi chimodzi za efa. Aziperekanso chimodzi mwa zigawo zitatu za hini ya mafuta okandira ufa wosalala. Chopereka cha chakudya chimenechi chiziperekedwa kwa Yehova nthawi zonse mwa lamulo.
15 Og de skulle tilberede Lammet og Madofferet og Olien hver Morgen til et bestandigt Brændoffer.
Motero azipereka mwana wankhosa ndi chopereka cha chakudya ndi mafuta mmawa uliwonse kuti zikhale nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku.
16 Saa siger den Herre, Herre: Naar Fyrsten giver nogen af sine Sønner en Gave, saa er det dennes Arv, hans Sønner skal det tilhøre; det er deres Ejendom til Arv.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ngati kalonga apereka mphatso chigawo cha cholowa chake kwa mmodzi mwa ana ake, mphatsoyo idzakhala ya ana akewo. Idzakhala yawo chifukwa ndi cholowa chawo.
17 Men naar han giver en af sine Tjenere en Gave af sin Arv, da skal det høre denne til indtil Frihedsaaret og da komme til Fyrsten igen; kun hans Sønner skal den Arv, enhver faar, tilhøre.
Koma ngati ipereka mphatso yotere kuchokera pa cholowa chake kwa mmodzi mwa antchito ake, mphatsoyo idzakhala ya wantchitoyo mpaka chaka chaufulu. Pambuyo pake idzabwereranso kwa kalongayo chifukwa cholowa chake ndi cha ana ake.
18 Og Fyrsten skal ikke tage af Folkets Arv, saa at han fortrænger dem fra deres Ejendom; af sin egen Ejendom skal han lade sine Sønner arve, for at ikke mit Folk skal adspredes og nogen komme bort fra sin Ejendom.
Kalonga asalande cholowa chilichonse cha anthu, kuwachotsa mʼdera lawo la dziko. Iye apereke kwa ana ake cholowa chawo chochokera pa chuma chakechake, kuti pasapezeke ndi mmodzi yemwe mwa anthu anga wolandidwa chuma chake.’”
19 Og han førte mig ad Indgangen, som var ved Siden af Porten, hen til de hellige Celler, som vare for Præsterne, og som vendte imod Nord; og se, der var en Plads ved den yderste Ende, imod Vesten.
Kenaka munthu uja anandidzeretsa pa khomo la pambali pa chipata nandilowetsa ku zipinda za ansembe zoyangʼana kumpoto. Ndipo ndinaona kumeneko malo chakumadzulo kwa zipindazo.
20 Og han sagde til mig: Dette er den Plads, hvor Præsterne skulle koge Skyldofferet og Syndofferet, hvor de skulle bage Madofferet for ikke at bære det ud til den ydre Forgaard, saa at de hellige Folket.
Munthuyo anandiwuza kuti, “Awa ndi malo amene ansembe adzaphikirapo nsembe yopepesera kupalamula ndi nsembe yopepesera machimo. Kumenekonso azidzawotcherako chopereka cha chakudya. Sadzatuluka nazo zoyerazi mʼbwalo lakunja kuopa kuti angapatsireko kuyera anthu ena.”
21 Og han førte mig ud i den ydre Forgaard og lod mig gaa forbi de fire Hjørner i Forgaarden, og se, der var en Indhegning i hvert Hjørne af Forgaarden.
Pambuyo pake anandilowetsa mʼbwalo lakunja napita nane ku ngodya zinayi za bwalolo. Ndipo ndinaona mʼkati mwa ngodya iliyonse bwalo lina.
22 I de fire Hjørner af Forgaarden var der lukkede Indhegninger, fyrretyve Alen i Længden og tredive Alen i Bredden; alle fire Hjørneindhegninger havde samme Maal.
Motero pa ngodya zinayi za bwalo panalinso mabwalo ena angʼonoangʼono. Mabwalo amenewa anali ofanana. Mulitali mwake munali mamita makumi awiri ndipo mulifupi mwake munali mamita khumi ndi asanu.
23 Og der var en muret Ring trindt omkring i dem, trindt omkring for dem alle fire; og der var Kogesteder gjorte neden under de murede Ringe trindt omkring.
Kuzungulira mabwalo anayi angʼonoangʼono aja panali mpanda wamiyala, ndi malo asonkhapo moto omangidwa mʼmunsi mwa mpandawo mozungulira.
24 Og han sagde til mig: Dette er Kokkenes Hus, hvor Husets Tjenere skulle koge Folkets Slagtoffer.
Munthuyo anandiwuza kuti, “Izi ndi zipinda zophikiramo. Mʼmenemu anthu otumikira ku Nyumba ya Mulungu adzaphikiramo nyama za nsembe za anthu.”

< Ezekiel 46 >