< Ezekiel 39 >

1 Og du Menneskesøn! spaa imod Gog, og sig: Saa siger den Herre, Herre: Se, jeg kommer imod dig, Gog, du Fyrste over Rosk, Mesek og Tubal.
“Iwe mwana wa munthu, nenera modzudzula Gogi ndi kumuwuza kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa Mesaki ndi Tubala.
2 Og jeg vil vende dig om og drive dig frem og føre dig op fra det yderste Nord og lade dig komme over Israels Bjerge.
Ine ndidzakuzunguza ndi kukupirikitsira kutsogolo. Ndidzakutenga kuchokera kutali kumpoto ndi kukutumiza kuti ukalimbane ndi anthu a ku mapiri a Israeli.
3 Og jeg vil slaa din Bue ud af din venstre Haand og lade dine Pile falde ud af din højre Haand.
Kenaka Ine ndidzathyola uta wa mʼdzanja lako lamanzere ndipo ndidzagwetsa mivi ya mʼdzanja lako lamanja.
4 Paa Israels Bjerge skal du falde, du og alle dine Hære og de Folk, som ere med dig; jeg vil give dig til Føde for Rovfuglene, Smaafuglene, alt det bevingede og de vilde Dyr paa Marken.
Udzagwa ku mapiri a ku Israeli, iwe ndi magulu ako onse ankhondo ndiponso mitundu ya anthu imene ili nawe. Ndidzakusandutsa chakudya cha mitundu yonse ya mbalame zodya nyama, ndiponso cha zirombo zakuthengo.
5 Paa den vide Mark skal du falde; thi jeg har talt det, siger den Herre, Herre.
Udzafera pa mtetete kuthengo, pakuti Ine ndayankhula. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
6 Og jeg vil sende en Ild paa Magog og paa dem, som bo tryggelig Paa Øerne, og de skulle fornemme, at jeg er Herren.
Ndidzatumiza moto pa Magogi ndi pa onse amene amakhala mwamtendere mʼmbali mwa nyanja. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
7 Og jeg vil kundgøre mit hellige Navn midt iblandt mit Folk Israel og ikke ydermere lade mit hellige Navn vanhelliges, og Hedningerne skulle fornemme, at jeg er Herren, den Hellige i Israel.
“Ndidzachititsa kuti dzina langa loyera lidziwike pakati pa anthu anga Israeli. Sindidzalola kuti dzina langa liyipitsidwenso, ndipo mitundu ya anthu idzadziwa kuti Ine Yehova ndine Woyera mu Israeli.
8 Se, det kommer, og det skal ske, siger den Herre, Herre; det er den Dag, som jeg har talt om.
Zikubwera! Ndipo zidzachitikadi, ndikutero Ine Ambuye Yehova. Ndiye tsiku limene ndinanena lija.
9 Og Indbyggerne i Israels Stæder skulle gaa ud og gøre Ild paa og hede med Rustninger og smaa Skjolde og store Skjolde, med Bue og med Pile og med Haandstav og med Spyd, og de skulle gøre Ild dermed i syv Aar.
“Pamenepo okhala mʼmizinda ya Israeli adzatuluka ndipo adzasonkhanitsa zida zankhondo kuti zikhale nkhuni ndipo adzazitentha; zishango ndi lihawo, mauta ndi mivi, zibonga za nkhondo ndi mikondo. Adzazisonkhera moto kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
10 Og de skulle ikke hente Træ fra Marken eller hugge af Skovene; thi de skulle gøre Ild med Rustninger; og de skulle røve fra dem, for hvilke de vare et Rov, og plyndre dem, af hvilke de bleve plyndrede, siger den Herre, Herre.
Iwo sadzatolera nkhuni kuthengo kapena kukadula ku nkhalango, chifukwa adzasonkhera moto zidazo. Ndipo iwo adzafunkha amene anawafunkhawo, ndi kulanda chuma cha amene anawalanda, ndikutero Ine Ambuye Yehova.
11 Og det skal ske paa denne Dag, at jeg vil give Gog et Sted der til Begravelse i Israel, de vejfarendes Dal Østen for Havet, og den skal bringe de vejfarende til at holde sig for Næsen; og der skulle de begrave Gog og al hans Mangfoldighed og kalde den Gogs Mangfoldigheds Dal.
“Pa tsiku limenelo ndidzamupatsa Gogi manda mu Israeli, mʼchigwa cha apaulendo, kummawa kwa Nyanja Yakufa. Mandawo adzatseka njira ya apaulendo, chifukwa Gogi ndi gulu lake lankhondo adzayikidwa kumeneko. Ndipo chigwacho chidzatchedwa chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
12 Og Israels Hus skal begrave dem, for at rense Landet, i syv Maaneder;
“Nyumba ya Israeli idzakhala ikukwirira mitembo kwa miyezi isanu ndi iwiri ndi cholinga choyeretsa dziko.
13 ja, alt Folket i Landet skal begrave dem, og det skal vorde dem til et Navn, paa den Dag, jeg forherliger mig, siger den Herre, Herre.
Anthu onse a mʼdzikomo adzakwirira nawo mitembo. Ntchito imeneyo adzatchuka nayo pa tsiku limene ndidzaonetsa ulemerero wanga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
14 Og de skulle udnævne faste Mænd, nogle, som skulle gaa igennem Landene, og nogle, som tillige med dem, der gaa igennem Landet, skulle begrave dem, der maatte være blevne tilbage oven paa Jorden, for at rense det; naar syv Maaneder ere til Ende, skulle de gennemsøge det.
“Patapita miyezi isanu ndi iwiri adzalemba ntchito anthu ena odzayenda mʼdziko lonse kufunafuna mitembo imene inatsalira nʼkumayikwirira. Choncho adzayeretseratu dzikolo.
15 Og de, som gaa igennem Landene, skulle gaa omkring, og naar nogen ser et Menneskes Ben, da skal han sætte et Mærke derved, indtil de, som begrave, begrave det i Gogs Mangfoldigheds Dal.
Poyenda mʼdzikomo azidzati akaona fupa la munthu azidzayikapo chizindikiro pambali pake mpaka okumba manda atakalikwirira fupalo ku chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
16 Og der skal ogsaa en Stad kaldes Hamona; saa skulle de rense Landet.
(Komwekonso kudzakhala mzinda wotchedwa Gulu la nkhondo). Ndipo potero adzayeretsa dziko.
17 Og du Menneskesøn! saa siger den Herre, Herre: Sig til Fuglene, alt det bevingede, og til alle vilde Dyr paa Marken: Samler eder og kommer, sanker eder trindt omkring fra til mit Slagtoffer, som jeg slagter for eder, et stort Slagtoffer paa Israels Bjerge, og I skulle æde Kød og drikke Blod.
“Tsono iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Itana mbalame za mitundu yonse ndi zirombo zonse zakuthengo ndipo uziwuze kuti, ‘Sonkhanani ndipo bwerani kuchokera ku mbali zonse ku nsembe imene ndikukonzerani inu, nsembe yayikulu pa mapiri a Israeli. Kumeneko inu mudzadya mnofu ndi kumwa magazi.
18 I skulle æde de vældiges Kød og drikke Jordens Fyrsters Blod: Vædres, Lams og Bukkes, Øksnes, som alle ere fedede i Basan.
Mudzadya mnofu wa anthu ankhondo amphamvu ndi kumwa magazi a akalonga a dziko lapansi. Onsewo anaphedwa ngati nkhosa zazimuna, ana ankhosa onenepa, mbuzi ndiponso ngati ngʼombe zazimuna zonenepa za ku Basani.
19 Og I skulle æde det fede, til I blive mætte, og drikke Blod, til I blive drukne, af mit Slagtoffer, som jeg slagter til eder.
Ku phwando lansembe limene ndikukonzera inulo, mudzadya zonona mpaka kukhuta ndi kumwa magazi mpaka kuledzera.
20 Og I skulle mætte eder ved mit Bord af Heste og Rytteri, at de vældige og alle Haande Krigsmænd, siger den Herre, Herre.
Pa tebulo langa mudzakhuta pakudya akavalo ndi okwerapo ake, anthu amphamvu ndi asilikali amitundumitundu,’ ndikutero Ine Ambuye Yehova.
21 Og jeg vil vise min Herlighed iblandt Hedningerne, og alle Hedningerne skulle se min Dom, som jeg har holdt, og min Haand, som jeg har lagt paa dem.
“Ine ndidzaonetsa ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina, ndipo adzaona mmene ndidzawalangire ndikadzayika dzanja langa pa iwo.
22 Og Israels Hus skal fornemme, at jeg er Herren deres Gud, fra den samme Dag af og fremdeles.
Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo Aisraeli adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.
23 Og Hedningerne skulle kende, at Israels Hus blev bortført for deres Misgerning, fordi de havde været troløse imod mig, saa at jeg skjulte mit Ansigt for dem og gav dem i deres Fjenders Haand, og de alle faldt for Sværdet.
Ndipo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti anthu a Israeli anatengedwa ukapolo chifukwa cha tchimo lawo, chifukwa anali osakhulupirika kwa Ine. Choncho Ine ndinawabisira nkhope yanga ndi kuwapereka kwa adani awo. Motero anaphedwa pa nkhondo.
24 Efter deres Urenhed og efter deres Overtrædelser handlede jeg imod dem, og jeg skjulte mit Ansigt for dem.
Ndinawachita zimenezi chifukwa cha kunyansa kwawo ndi zolakwa zawo, ndipo ndinawabisira nkhope yanga.
25 Derfor, saa siger den Herre, Herre: Nu vil jeg vende Jakobs Fangenskab og forbarme mig over Israels hele Hus og være nidkær for mit hellige Navn.
“Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsopano ndidzakhazikanso pa bwino banja la Yakobo. Ndidzachitira chifundo Aisraeli onse, ndipo ndidzateteza dzina langa loyera.
26 Og de skulle bære deres Skam og al Jeres Troløshed, som de begik imod mig, naar de bo tryggelig i deres Land, og der ingen er, som forfærder dem,
Anthuwo akadzakhala mwamtendere mʼdziko lawo popanda wina wowaopseza, pamenepo adzayiwala zamanyazi zawo zimene zinawachitikira chifukwa chosandikhulupirira Ine.
27 naar jeg fører dem tilbage fra Folkene og sanker dem fra deres Fjenders Lande, og naar jeg helliggør mig paa dem for mange Hedningers Øjne.
Ndidzawabwezeranso kwawo kuchokera pakati pa anthu a mitundu ina ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko a adani awo. Poteropo ndidzaonetsa pamaso pa anthu a mitundu yambiri kuti ndine Woyera.
28 Og de skulle fornemme, at jeg er Herren deres Gud, idet jeg har bortført dem til Hedningerne og nu samler dem til deres Land og ikke ydermere lader nogen af dem blive tilbage hist.
Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo, ngakhale kuti ndinawapereka ku ukapolo pakati pa anthu a mitundu ina. Ine ndidzawasonkhanitsanso ku dziko lawo osasiyako wina mʼmbuyo.
29 Jeg vil og ikke mere skjule mit Ansigt for dem; thi jeg har udgydt min Aand over Israels Hus, siger den Herre, Herre.
Ine sindidzawabisiranso nkhope yanga, pakuti ndidzathira Mzimu wanga pa Aisraeli. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”

< Ezekiel 39 >