< Ezekiel 32 >

1 Og det skete i det tolvte Aar, i den tolvte Maaned, paa den første Dag i Maaneden, at Herrens Ord kom til mig saaledes:
Pa tsiku loyamba la mwezi wa khumi ndi chiwiri, chaka chakhumi ndi chiwiri, Yehova anandiyankhula kuti:
2 Du Menneskesøn! opløft et Klagemaal over Farao, Kongen af Ægypten, og sig til ham: Du blev lignet med en ung Løve iblandt Folkene, men du var som en Drage i Havet, du brød frem i dine Strømme, og plumrede Vandene med dine Fødder og trampede i deres Strømme.
“Iwe mwana wa munthu imba nyimbo ya maliro a Farao mfumu ya Igupto ndipo uyiwuze kuti, “Iwe umadziyesa ngati mkango pakati pa mitundu ya anthu. Koma iwe uli ngati ngʼona mʼnyanja. Umakhuvula mʼmitsinje yako, kuvundula madzi ndi mapazi ako ndi kudetsa madzi mʼmitsinje.
3 Saa siger den Herre, Herre: Derfor vil jeg udbrede mit Garn over dig ved en Forsamling af mange Folkeslag, og de skulle trække dig op i mit Vod.
“Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Pogwiritsa ntchito gulu la anthu a mitundu yambiri, ndidzakuponyera khoka langa ndi kukugwira mu ukonde wanga.
4 Og jeg vil kaste dig op paa Landet og slænge dig hen oven paa Marken; og jeg vil lade alle Himmelens Fugle sætte sig paa dig og mætte de vride Dyr paa hele Jorden af dig.
Ndidzakuponya ku mtunda ndi kukutayira pansi. Ndidzabweretsa mbalame zamumlengalenga kuti zidzatere pa iwe, ndipo zirombo zonse za dziko lapansi zidzakudya.
5 Og jeg vil kaste dit Kød paa Bjergene og fylde Dalene med din store Krop.
Ndidzayanika mnofu wako pa mapiri ndipo zigwa zidzadzaza ndi zotsalira zako.
6 Og jeg vil væde Landet med, hvad der udstrømmer af dig, med dit Blod, indtil Bjergene, og Flodsengene skulle blive fulde af dig.
Ndidzanyowetsa dziko ndi magazi ako, mpaka kumapiri komwe, ndipo mitsinje idzadzaza ndi mnofu wako.
7 Og naar jeg udslukker dig, vil jeg bedække Himmelen og formørke dens Stjerner; Solen vil jeg bedække med en Sky, og Maanen skal ikke lade sit Lys skinne.
Ndikadzakuwononga, ndidzaphimba miyamba ndikudetsa nyenyezi zake. Ndidzaphimba dzuwa ndi mtambo, ndipo mwezi sudzawala.
8 Jeg vil lade alle klare Lys paa Himmelen formørkes for din Skyld, og jeg vil lægge Mørke over dit Land, siger den Herre, Herre.
Zowala zonse zamumlengalenga ndidzazizimitsa; ndidzachititsa mdima pa dziko lako, akutero Ambuye Yehova.
9 Og jeg vil bedrøve mange Folks Hjerter, naar jeg bringer dit Fald ud iblandt Folkene, i de Lande, som du ikke har kendt.
Ndidzasautsa mitima ya anthu a mitundu yambiri pamene ndidzakupititsa ku ukapolo pakati pa mitundu ya anthu, ku mayiko amene iwe sunawadziwe.
10 Og jeg vil gøre, at mange Folk skulle forfærdes over dig, og deres Konger skulle gyse saare over dig, naar jeg lader mit Sværd blinke for deres Ansigt; og de skulle bæve alle Øjeblikke, hver for sit Liv, paa dit Falds Dag.
Ine ndidzachititsa kuti anthu a mitundu yambiri adabwe nawe, ndipo mafumu awo adzanjenjemera ndi mantha aakulu chifukwa cha iwe pamene ndidzaonetsa lupanga langa pamaso pawo. Pa nthawi ya kugwa kwako, aliyense wa iwo adzanjenjemera moyo wake wonse.
11 Thi saa siger den Herre, Herre: Kongen af Babels Sværd skal komme over dig.
“‘Pakuti ndikunena Ine Ambuye Yehova kuti, “‘Lupanga la mfumu ya ku Babuloni lidzabwera kudzalimbana nawe.
12 Jeg vil lade din Hob falde for de vældiges Sværd, for dem, som alle sammen ere de forfærdelige iblandt Folkene; og de skulle ødelægge Ægyptens Stolthed, at al dets Hob skal gaa til Grunde.
Ndidzachititsa gulu lako lankhondo kuti ligwe ndi lupanga la anthu amphamvu, anthu ankhanza kwambiri pakati pa mitundu yonse ya anthu. Adzathetsa kunyada kwa Igupto, ndipo gulu lake lonse la nkhondo lidzagonjetsedwa.
13 Og jeg vil ødelægge alt dets Kvæg, at det ej bliver ved de mange Vande, og dem skal intet Menneskes Fod mere plumre; og heller intet Dyrs Klove skulle plumre dem.
Ndidzawononga ziweto zake zonse zokhala mʼmbali mwa madzi ambiri. Ku madziko sikudzaonekanso phazi la munthu kapena kudetsedwa ndi phazi la ziweto.
14 Da vil jeg lade deres Vande klare sig og lade deres Floder flyde som Olie, siger den Herre, Herre,
Pambuyo pake ndidzayeretsa madzi ake ndipo mitsinje yake idzayenda mokometsera ngati mafuta, akutero Ambuye Yehova.
15 naar jeg gør Ægyptens Land til en Ødelæggelse, og Landet bliver øde for det, som det er fuldt af, naar jeg slaar alle dets Indbyggere; og de skulle fornemme, at jeg er Herren.
Ndikadzasandutsa dziko la Igupto kukhala bwinja; ndikadzawononga dziko lonse ndi kukantha onse okhala kumeneko, adzadziwa kuti ndine Yehova.’
16 Det er et Klagemaal, og man skal synge det, Hedningernes Døtre skulle synge det; over Ægypten og over al dets Hob skulle de synge det, siger den Herre, Herre.
“Mawu angawa adzakhala nyimbo ya maliro. Ana a akazi amitundu ya anthu adzayimba, kuyimbira Igupto ndi gulu lake lonse la nkhondo, akutero Ambuye Yehova.”
17 Og det skete i det tolvte Aar, paa den femtende Dag i Maaneden, da kom Herrens Ord til mig, saaledes:
Pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, chaka cha khumi ndi chiwiri, Yehova anayankhula kuti:
18 Du Menneskesøn! istem en Sørgesang over Ægyptens Hob, og lad den fare ned, den og Døtrene af herlige Folkefærd, til Underverdenens Land, til dem, som nedfare i Hulen.
“Iwe mwana wa munthu, lirira gulu lankhondo la Igupto ndipo uwalowetse pamodzi ndi anthu ena amphamvu a mayiko ena ku dziko la anthu akufa.
19 Hvem overgaar du i Dejlighed? far ned, læg dig ved de uomskaarne!
Ufunse kuti, ‘Ndani amene akukuposa kukongola? Tsikirani ku manda ndi kukhala pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe.’
20 Midt iblandt dem, som ere ihjelslagne ved Sværd, skulle de falde; Sværdet er givet, trækker det ned med alle dets Hobe!
Aigupto adzagwa pakati pa amene akuphedwa ndi lupanga. Lupanga ndi losololedwa kale. Iye adzaphedwa pamodzi ndi gulu lake lankhondo.
21 De vældiges Fyrster tale om ham midt fra Dødsriget, med hans Hjælpere; de ere nedfarne, de ligge der, de uomskaarne, ihjelslagne med Sværd. (Sheol h7585)
Mʼkati mwa manda atsogoleri amphamvu pamodzi ndi ogwirizana nawo azidzakambirana za Igupto nʼkumati, ‘Afika kuno anthu osachita mdulidwe aja! Ndi awa agona apawa, ophedwa pa nkhondo.’ (Sheol h7585)
22 Der er Assur og al dets Forsamling, trindt omkring ham ere deres Grave, alle sammen ere de ihjelslagne, de, som faldt ved Sværd;
“Asiriya ali komweko ndipo ankhondo ake onse ali mʼmanda omuzungulira. Onsewo anaphedwa pa nkhondo.
23 dets Grave ere lagte i Hulens nederste Dyb, og dets Forsamling er trindt omkring dets Grav; de ere alle ihjelslagne, faldne ved Sværd, de, som voldte Forskrækkelse i de levendes Land.
Manda awo ali kumalo ozama a dzenje, ndipo ankhondo ake azungulira manda ake. Onse amene anaopseza dziko la anthu amoyo aphedwa, agwa ndi lupanga.
24 Der er Elam og al dets Hob trindt omkring i dets Grav; alle sammen ere de ihjelslagne, de, som faldt ved Sværd, hvilke som uomskaarne fore ned til Underverdenens Land og havde voldt Forskrækkelse for sig i de levendes Land, og de bære deres Skændsel iblandt dem, som fare ned i Hulen.
“Elamu ali komweko ndipo ankhondo ake ali mʼmanda omuzungulira. Onsewa anaphedwa pa nkhondo, natsikira ku manda ali osachita mdulidwe. Iwowa kale ankaopseza anthu pa dziko lapansi. Tsopano akuchita manyazi pamodzi ndi amene ali mʼmanda.
25 Man har givet det Leje midt iblandt de ihjelslagne, iblandt al dets Hob, trindt omkring ham ere deres Grave; alle ere de uomskaarne, ihjelslagne ved Sværd; thi Forskrækkelse for dem var udbredt i de levendes Land, og de bære deres Skændsel iblandt dem, som fare ned i Hulen, midt iblandt de ihjelslagne er han lagt.
Amukonzera pogona pakati pa anthu ophedwa, pamodzi ndi gulu lake lonse la nkhondo litazungulira manda ake. Onsewo ndi anthu osachita mdulidwe ophedwa ndi lupanga. Paja anthuwa ankaopsa mʼdziko la anthu a moyo. Koma tsopano akuchita manyazi pamodzi ndi amene ali mʼmanda. Iwo ayikidwa pakati pa anthu ophedwa.
26 Der er Mesek, Tubal og al dets Hob, trindt omkring ham ere deres Grave; alle ere de uomskaarne, ihjelslagne med Sværd, thi de have voldet Forskrækkelse for sig i de levendes Land.
“Mesaki ndi Tubala ali komweko, pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo litazungulira manda awo. Onsewo ndi anthu osachita mdulidwe, ophedwa ndi lupanga. Paja ankaopsa mʼdziko la anthu amoyo.
27 Men de ligge ikke ved de Helte, som ere faldne af de uomskaarne, hvilke nedfore til Dødsriget med deres Krigsvaaben og fik deres Sværd lagte under deres Hoveder; deres Misgerninger ere komne over deres Ben; thi de vare en Forskrækkelse for Heltene i de levendes Land. (Sheol h7585)
Iwo sanayikidwe mwaulemu ngati ankhondo amphamvu amakedzana, amene anatsikira ku dziko la anthu akufa ndi zida zawo zomwe za nkhondo. Malupanga awo anawayika ku mitu yawo, ndipo zishango zawo anaphimba mafupa awo. Kale anthu amphamvu amenewa ankaopsa dziko la anthu amoyo. (Sheol h7585)
28 Og du! du skal sønderknuses midt iblandt de uomskaarne og ligge ved dem, som ere ihjelslagne ved Sværd.
“Iwenso Farao, udzaphwanyidwa ndi kuyikidwa pakati pa anthu osachita mdulidwe, amene anaphedwa ndi lupanga.
29 Derhen kom Edom, dets Konger og alle dets Fyrster, som trods deres Styrke ere lagte hos dem, som ere ihjelslagne med Sværd; de ligge ved de uomskaarne og ved dem, som nedfare i Hulen.
“Edomu ali kumeneko pamodzi ndi mafumu ake ndi akalonga ake onse. Ngakhale anali amphamvu, koma anayikidwa. Ayikidwa pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje.
30 Derhen kom alle de ypperste Mænd af Norden og alle Zidonier, som fore ned til de ihjelslagne og bleve beskæmmede, uagtet de havde voldet Forskrækkelse formedelst deres Styrke, og de ligge som uomskaarne ved dem, som ere ihjelslagne ved Sværd, og bære deres Skændsel iblandt dem, som nedfare i Hulen.
“Akalonga onse akumpoto pamodzi ndi anthu onse a ku Sidoni ali kumeneko. Anatsikira ku dziko la anthu akufa mwamanyazi ngakhale anali owopsa ndi mphamvu zawo. Iwo akugona osachita mdulidwe pamodzi ndi amene anaphedwa ndi lupanga ndipo akuchita manyazi pamodzi ndi iwo amene anatsikira kale ku manda.
31 Dem skal Farao se og trøste sig over hele sin Hob; ihjelslagen med Sværd er Farao og al hans Hær, siger den Herre, Herre.
“Farao ndi gulu lake lankhondo akadzawaona iwowa adzathunza mtima pokumbukira kuchuluka kwa gulu lake lankhondo limene linaphedwa pa nkhondo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
32 Thi jeg har ladet ham volde Forskrækkelse i de levendes Land; saa skal Farao og al hans Hob lægges midt iblandt de uomskaarne, iblandt dem, som ere ihjelslagne med Sværd, siger den Herre, Herre.
Paja ankaopsa mʼdziko la anthu amoyo. Koma Faraoyo pamodzi ndi ankhondo ake onse adzayikidwa pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, pamodzi ndi amene anaphedwa pa nkhondo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”

< Ezekiel 32 >