< Ezekiel 27 >

1 Og Herrens Ord kom til mig saaledes:
Yehova anandiyankhula kuti:
2 Og du Menneskesøn! opløft et Klagemaal over Tyrus,
“Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira Turo.
3 og sig til Tyrus, som bor ved Havets Havne, og som handler med Folkene paa mange Øer: Saa siger den Herre, Herre: O Tyrus! du sagde: Jeg er fuldkommen i Skønhed.
Uza Turo, mzinda wokhala pa dooko la nyanja, wochita malonda ndi anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja kuti: Ambuye Yehova akuti, “Iwe Turo, umanena kuti, ‘Ndine wokongola kwambiri.’
4 Dine Landemærker ere midt i Havet, dine Bygningsmænd have gjort din Skønhed fuldendt.
Malire ako anali mʼkati mwenimweni mwa nyanja; amisiri ako anakukongoletsa kwambiri.
5 De byggede dig hele Opklædningen af Fyrretræ fra Senir; de hentede Geder fra Libanon til at gøre en Mast paa dig.
Anakupanga ndi matabwa a payini ochokera ku Seniri; anatenga mikungudza ya ku Lebanoni kupangira mlongoti wako.
6 De gjorde dine Aarer af Eg fra Basan; dit Dæk gjorde de af Elfenben, indlagt i Buksbom fra Kithims Øer.
Ndi mitengo ya thundu ya ku Basani anapanga zopalasira zako; ndi matabwa a mitengo ya payini yochokera ku zilumba za Kitimu. Pakuti anapanga thandala lako pakati pa matabwawo panali minyanga ya njovu.
7 Dit Sejl var af hvidt Linned med stukket Arbejde fra Ægypten, for at det skulde være dig til Mærke; af blaat Purpur og rødt Purpur fra Elisas Øer var dit Solsejl.
Nsalu yabafuta yopeta yochokera ku Igupto inali thanga yako, ndipo inakhala ngati mbendera. Nsalu zophimba matenti ako zinali za mtundu wamtambo ndi pepo zochokera ku zilumba za Elisa.
8 Indbyggerne i Zidon og Arvad vare dine Rorkarle; dine vise, o Tyrus! som vare i dig, de vare dine Styrmænd.
Anthu a ku Sidoni ndi Arivadi ndi amene anali opalasa ako. Anthu aluso ako, iwe Turo, anali mwa iwe ndiwo amene ankakuyendetsa.
9 Gebals Ældste og dens vise vare hos dig for at stoppe din Læk; alle Skibe i Havet og deres Skibsfolk vare hos dig for at drive Handel med dig.
Akuluakulu ndi eni luso a ku Gebala anali mʼkati mwako, ngati okonza zibowo zako. Sitima za pa nyanja zonse, ndi oyendetsa ake ankabwera pamodzi ndi katundu kudzachita nawe malonda.
10 Folk fra Persien og Lydien og fra Put vare i din Hær som dine Krigsfolk, de ophængte Skjold og Hjelm i dig, de gave dig Glans.
“Anthu a ku Perisiya, a ku Ludi ndi Puti anali asilikali mʼgulu lako la nkhondo. Iwo ankapachika zishango ndi zipewa zawo zankhondo pa makoma ako, kubweretsa kwa iwe ulemerero.
11 Arvads Børn og din Hær vare paa dine Mure trindt omkring, og tapre Mænd vare paa dine Taarne; de hængte deres Skjolde paa dine Mure trindt omkring, de gjorde din Skønhed fuldendt.
Anthu a ku Arivadi ndi Heleki ankalondera mbali zonse za mpanda wako; anthu a ku Gamadi anali mu nsanja zako, Iwo ankapachika zishango zawo pa makoma ako onse. Amenewo ndiwo anakukongoletsa kwambiri.
12 Tharsis handlede med dig, fordi du havde Mangfoldighed af alle Haande Gods; med Sølv, Jern, Tin og, Bly betalte de dine Varer.
“Dziko la Tarisisi linachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa katundu wako wamtundumtundu. Iwo ankapereka siliva, chitsulo, chitini ndi mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.
13 Javan, Tubal og Mesek, de vare dine Kræmmere; Menneskesjæle og Kobberkar gave de dig i Tusk.
“Yavani, Tubala ndi Mesaki ankachita nawe malonda; iwo ankapereka akapolo ndi ziwiya za mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.
14 De af Thogarmas Hus betalte dine Varer med Køreheste og Rideheste og Mulæsler.
“Anthu a ku Beti Togarima ankapereka akavalo antchito, akavalo ankhondo ndi abulu mosinthanitsa ndi katundu wako.
15 Dedans Børn vare dine Kræmmere; mange Kyster stode i Handelsforhold med dig; de gave dig Elfenben og Ebentræ til Betaling.
“Anthu a ku Dedani ankachita nawe malonda, ndipo anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja anali ogula malonda ako. Ankakupatsa minyanga ya njovu ndi phingo.
16 Syrien handlede med dig, fordi du havde en Mangfoldighed af Arbejder; med Karbunkel, Purpur og stukket Arbejde jog hvidt Linned og Koraller og Rubiner betalte de dine Varer.
“Anthu a ku Aramu ankachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa zinthu zako. Iwo ankapereka miyala ya emeradi, nsalu zapepo, nsalu zopetapeta, nsalu zabafuta, korali ndi miyala ya rubi mosinthanitsa ndi katundu wako.
17 Judas og Israels Lande, de vare dine Kræmmere; Hvede fra Minnit og søde Sager og Honning og Olie og Balsam gave de dig i Tusk.
“Yuda ndi Israeli ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka tirigu ochokera ku Miniti ndi zokometsera zakudya, uchi, mafuta ndi mankhwala mosinthanitsa ndi katundu wako.
18 Damaskus handlede med dig, fordi du havde en Mangfoldighed af Arbejder, for Mangfoldigheden af alle Haande Gods, med Vin af Helbon og hvid Uld.
“Anthu a ku Damasiko, chifukwa cha zinthu zako za malonda zambiri ndi katundu wako wosiyanasiyana, ankachita nawe malonda a vinyo wochokera ku Heliboni ndi ubweya wankhosa ochokera ku Zahari.
19 Vedan og Javan gave Sager fra Uzzal for dine Varer; skinnende Jern, Kasia og Kalmus gaves dig i Tusk.
Adani ndi Agriki ochokera ku Uzala ankagula katundu wako. Iwo ankapereka chitsulo chosalala, kasiya ndi bango lonunkhira mosinthanitsa ndi katundu wako.
20 Dedan handlede med dig med Dækkener til at ride paa.
“Anthu a ku Dedani ankakugulitsa nsalu zoyika pa zishalo za akavalo.
21 Arabien og alle Kedars Fyrster, de stode i Handelsforhold med dig; med Lam og Vædre og Bukke, med dem handlede de med dig.
“Arabiya ndi mafumu onse a ku Kedara anali ogula malonda ako. Iwo ankachita nawe malonda a ana ankhosa onenepa, nkhosa zazimuna ndi mbuzi.
22 Kræmmere fra Seba og Raema, de vare dine Kræmmere; med det ypperste af alle Haande Urter og med alje Haande kostbare Stene og Guld betalte de dine Varer.
“Anthu amalonda a ku Seba ndi Raama ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka zonunkhira zosiyanasiyana zabwino kwambiri, miyala yokongola ndi golide mosinthanitsa ndi katundu wako.
23 Haran og Karma og Eden, Kræmmere fra Seba, Assur og Kilmad handlede med dig.
“Amalonda a ku Harani, Kane, Edeni, Seba, Asuri ndi Kilimadi ankachita nawe malonda.
24 De vare dine Kræmmere med Kostbarheder, bestaaende i Kapper af blaat Purpur og stukket Arbejde, og med værdifuldt Garn, i tvundne og faste Snore, paa dit Marked.
Iwowa ankasinthanitsana nawe zovala zokongola, nsalu zopetapeta, zoyala pansi za mawangamawanga, atazimanga bwino ndi zingwe zolimba.
25 Tharsis's Skibe droge omkring for dig, de dreve din Handel, og du blev fyldt og saare rig midt i Havet.
“Sitima za pa madzi za ku Tarisisi zinali zonyamula malonda ako. Motero iwe uli ngati sitima yapamadzi yodzaza ndi katundu wolemera.
26 Dine Rorkarle førte dig paa de store Vande, Østenvejret sønderslog dig midt i Havet.
Anthu opalasa ako amakupititsa pa nyanja yozama. Koma mphepo yakummawa idzakuthyolathyola pakati pa nyanja.
27 Dit Gods og dine Varer, hvad du handlede med, dine Skibsfolk og dine Styrmænd, de, som stoppede din Læk, og de, som dreve din Handel, og alle dine Krigsmænd, som vare i dig, med hele din Skare, som var i din Midte, faldt midt i Havet paa dit Falds Dag.
Chuma chako, katundu wako, malonda ako, okuyendetsa ako, okuwongolera ako ndi opanga sitima za pa madzi, anthu ako amalonda ndi asilikali ako onse ndiponso aliyense amene ali mʼmenemo adzamira mʼnyanja tsiku limene udzawonongeka.
28 Ved Lyden af dine Styrmænds Skrig bæve Strandmarkerne.
Madera a mʼmbali mwa nyanja adzagwedezeka chifukwa cha kufuwula kwa oyendetsa sitimawo.
29 Og alle de, som føre Aarer, stige ud af deres Skibe; Skibsfolk, alle Styrmænd paa Havet, de træde i Land.
Onse amene amapalasa sitima zapamadzi, adzatuluka mʼsitima zawo; oyendetsa ndi onse owongolera sitima zapamadzi adzayimirira mʼmbali mwa nyanja.
30 Og de lade deres Røst høre over dig og raabe bitterlig; og de kaste Støv paa deres Hoved, de vælte sig i Asken.
Iwo akufuwula, kukulira iwe kwambiri; akudzithira fumbi kumutu, ndi kudzigubuduza pa phulusa.
31 Og de rage sig helt skaldede for din Skyld og iføre sig Sæk; og de græde over dig i Sjælens Bitterhed med en bitter Sorg.
Akumeta mpala mitu yawo chifukwa cha iwe ndipo akuvala ziguduli. Akukulira iweyo ndi mitima yowawa kwambiri.
32 Og de opløfte et Klagemaal over dig i deres Jamren og beklage dig: „Hvo er som Tyrus, som den, der er bleven tavs midt paa Havet?”
Akuyimba nyimbo yokudandaulira nʼkumati: ‘Ndani anawonongedwapo ngati Turo pakati pa nyanja?’
33 Der dine Varer kom frem af Havene, mættede du mange Folk; med Mangfoldigheden af dit Gods, og hvad du handlede med, gjorde du Konger rige paa Jorden.
Pamene malonda ako ankawoloka nyanja unakhutitsa mitundu yambiri ya anthu. Mafumu a dziko lapansi analemera ndi chuma chako komanso ndi malonda ako.
34 Nu, da du knust er forsvunden af Havene i de dybe Vandeler din Handel og hele din Skare midt i dig falden.
Koma tsopano wathyokera mʼnyanja, pansi penipeni pa nyanja. Katundu wako ndi onse amene anali nawe amira pamodzi nawe.
35 Alle Øernes Indbyggere gyse over dig, og deres Konger forfærdes saare, de se bedrøvelige ud i Ansigtet.
Onse amene amakhala mʼmbali mwa nyanja aopsedwa ndi zimene zakuchitikira. Mafumu awo akuchita mantha ndipo nkhope zangoti khululu.
36 Købmændene iblandt Folkene pibe ad dig; du er bleven til Gru og er til evig Tid ikke mere.
Anthu amalonda a mitundu ina akukunyogodola. Watha mochititsa mantha ndipo sudzakhalaponso mpaka muyaya.”

< Ezekiel 27 >