< Ezekiel 22 >

1 Og Herrens Ord kom til mig saaledes:
Yehova anandiyankhula nati:
2 Og du Menneskesøn! vil du dømme, vil du dømme den blodskyldige Stad? ja, kundgør den alle dens Vederstyggeligheder!
“Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza mzinda uwo wa anthu akupha anzawo? Tsono uwudzudzule chifukwa cha machitidwe ake onse onyansa
3 Og du skal sige: Saa siger den Herre, Herre: Det er en Stad, som udøser Blod i sin Midte, for at dens Tid skal komme, og som gør sig Afguder til at besmitte sig ved.
ndipo unene kuti, ‘Ambuye akuti: Iwe mzinda umene wadzigwetsa wekha mʼtsoka pa kukhetsa magazi pakati pako ndi kudziyipitsa popanga mafano,
4 Du er bleven skyldig ved dit Blod, som du har udøst, og har besmittet dig med de Afguder, som du har gjort, saa at du bragte dine Dage til at nærme sig og naaede dine Aar: Derfor har jeg gjort dig til Forhaanelse iblandt Hedningerne og til Spot for alle Landene.
wapezekatu wolakwa chifukwa cha magazi amene wakhetsa, ndipo wadziyipitsa chifukwa cha mafano amene wapanga. Choncho wachepetsa masiku ako, ndipo zaka zako zafika kumapeto. Nʼchifukwa chake ndalola kuti anthu a mitundu ina akunyoze ndiponso kuti anthu a mayiko onse akuseke.
5 Baade de, som ere nær, og de, som ere langt fra dig, skulle spotte dig, du med det besmittede Navn og med den store Forstyrrelse!
Mayiko amene ali pafupi ndi mayiko omwe ali kutali adzakunyoza, iwe mzinda wa mbiri yoyipa, wodzaza ndi chiwawa.
6 Se, Israels Fyrster, hver efter sin Arms Styrke, vare hos dig for at udøse Blod.
“‘Taona momwe aliyense wa atsogoleri a Israeli amagwiritsira mphamvu zake kupha anthu.
7 Man ringeagtede Fader og Moder hos dig, man handlede med Vold imod den fremmede i din Midte, man forfordelte den faderløse og Enken hos dig.
Mu mzindamo anthu amanyoza abambo ndi amayi awo. Iwo amapondereza alendo ndi kuzunza ana amasiye ndi akazi amasiye.
8 Du foragtede mine Helligdomme og vanhelligede mine Sabbater.
Wanyoza zinthu zanga zopatulika ndi kuyipitsa Masabata anga.
9 Bagvadskere var der hos dig, paa det de kunde udøse Blod; og man holdt Maaltid paa Bjergene hos dig, man gjorde skændige Ting i din Midte.
Mwa iwe muli anthu onenera anzawo zabodza kuti aphedwe. Mwa iwe mulinso amene amadyera zansembe pa mapiri a chipembedzo. Enanso amachita zonyansa.
10 Man har blottet en Faders Blusel hos dig; man har krænket Kvinden i hendes Svaghed hos dig.
Mwa iwe muli ena ogonana ndi akazi a abambo awo, muli enanso amene amavuta akazi pamene ali woyipitsidwa ndi msambo.
11 Og man har bedrevet Vederstyggelighed med sin Næstes Hustru, og man har vanæret sin Sønnekone med Skændsel, og man har krænket sin Søster, sin Faders Datter, hos dig.
Ena amachita chigololo ndi akazi a anzawo, ndipo ena, mopanda manyazi, amayipitsa mkazi wa mwana wawo. Palinso ena amene amayipitsa alongo awo, ana aakazi a abambo awo.
12 De toge Skænk hos dig for at udøse Blod; du tog Aager og Overgivt og forfordelte din Næste ved Undertrykkelse, men mig glemte du, siger den Herre, Herre.
Mwa iwe muli anthu amene amalandira ziphuphu kuti aphe anzawo; ena amachita katapira ndi kupeza phindu loposera muyeso; enanso amapeza phindu mwachinyengo poopseza anzawo. Ndipo mwandiyiwala Ine, akutero Ambuye Yehova.
13 Og se, jeg har slaaet mine Hænder sammen over din Vinding, som du har gjort dig, og for din Blodskyld, som er i din Midte.
“‘Koma Ine ndachita kuwomba mʼmanja kuti phuu nʼkudabwa chifukwa cha phindu lachinyengo limene mwapeza ndiponso chifukwa cha kuphana kumene kumachitika pakati panu.
14 Mon dit Hjerte skal kunne holde Stand? mon dine Hænder skulle beholde Styrke paa de Dage, naar jeg vil handle med dig? jeg, Herren, jeg har talt det og vil gøre det.
Kodi mtima wako udzakhala wolimbabe kapena manja ako adzakhalabe amphamvu ndikadzatsiriza kukulanga iwe? Ine Yehova ndayankhula, ndipo ndidzazichitadi.
15 Og jeg vil adsprede dig iblandt Hedningerne og strø dig over Landene og bortskaffe din Urenhed fra dig,
Ndidzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukumwazirani ku mayiko onse. Umu ndi mmene ndidzachotsere zoyipa zako.
16 Og du skal være vanhelliget ved dig selv for Hedningernes Øjne og fornemme, at jeg er Herren.
Udzanyozedwa pamaso pa anthu a mitundu ina. Pambuyo pake udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
17 Og Herrens Ord kom til mig saaledes:
Yehova anandiyankhula nati:
18 Du Menneskesøn! Israels Hus er blevet mig til Slagger; de ere alle Kobber og Tin og Jern og Bly midt i en Ovn, Sølvslagger ere de blevne.
“Iwe mwana wa munthu, Aisraeli asanduka chinthu cha chabechabe kwa Ine. Onse ali ngati mkuwa, chitini, chitsulo ndi mtovu zotsala mʼngʼanjo atayeretsa siliva.
19 Derfor, saa siger den Herre, Herre, fordi I alle ere blevne til Slagger, derfor se, jeg vil samle eder midt i Jerusalem.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Pakuti nonse mwasanduka chinthu cha chabechabe, Ine ndidzakusonkhanitsani mu Yerusalemu.
20 Ligesom man samler Sølv og Kobber og Jern og Bly og Tin midt i en Ovn for at oppuste Ild derover, til at smelte det: Saaledes vil jeg samle eder i min Vrede og i min Harme og lægge eder ind og smelte eder.
Monga momwe anthu amasonkhanitsira siliva, mkuwa, chitsulo, mtovu ndi chitini mʼngʼanjo ndi kusonkhetsa moto kuti azisungunule, motero Inenso ndidzakusonkhanitsani ndili wokwiya ndi waukali, ndipo ndidzakuyikani mʼkati mwa mzinda, ndikukusungunurani.
21 Ja, jeg vil samle eder og oppuste min Vredes Ild over eder, og I skulle smeltes derinde.
Ndidzakusonkhanitsani mu mzindamo ndi kukoleza moto wa mkwiyo wanga, ndipo inu mudzasungunuka mu mzindamo.
22 Ligesom Sølv smeltes midt i en Ovn, saa skulle I smeltes i dens Midte, og I skulle fornemme, at jeg, Herren, jeg har udøst min Harme over eder.
Monga siliva amasungunulidwa mʼngʼanjo, kotero inunso mudzasungunuka mʼkati mwa mzinda ndipo Inu mudzadziwa kuti Ine Yehova ndakukwiyirani.’”
23 Og Herrens Ord kom til mig saalunde:
Yehova anandiyankhulanso nati,
24 Du Menneskesøn! sig til det: Du er et Land, som ikke er renset, som ikke har faaet Regn paa Vredens Dag.
“Iwe mwana wa munthu, uza dziko la Israeli kuti, ‘Iwe ndiwe dziko losayeretsedwa, ndiponso losavumbidwa ndi mvula chifukwa cha mkwiyo wanga.’
25 Dets Profeter have sammensvoret sig i dets Midte, de ere som en brølende Løve, der røver Rov; de fortære Sjæle, tage Gods og dyrebare Ting, gøre mange til Enker derudi.
Atsogoleri ake mu mzindamo ali ngati mkango wobangula pogwira nyama. Apha anthu, alanda chuma ndi zinthu za mtengowapatali, ndiponso asandutsa amayi ambiri kukhala amasiye.
26 Dets Præster forgribe sig paa min Lov og vanhellige mine Helligdomme, de gøre ingen Forskel imellem helligt og vanhelligt, og Forskellen imellem rent og urent gøre de ikke bekendt; og de lukke deres Øjne for mine Sabbater, og jeg vanhelliges midt iblandt dem.
Ansembe ake amaphwanya lamulo langa ndi kuyipitsa zinthu zanga zopatulika. Sasiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba. Saphunzitsa anthu kusiyana kwa zinthu zoyenera pa chipembedzo ndi zinthu zosayenera. Sasamalira za kusunga masabata anga. Motero Ine ndimanyozedwa pakati pawo.
27 Dets Fyrster i dets Midte ere som Ulve, der røve Rov, saa at de udøse Blod, ødelægge Sjæle for at gøre sig Vinding.
Atsogoleri ake ali ngati mimbulu yokhadzula nyama; amakhetsa magazi ndi kupha anthu kuti apeze phindu loyipa.
28 Og dets Profeter anstryge dem med løs Kalk, idet de bringe dem forfængelige Syner og spaa Løgn for dem, sigende: „Saa siger den Herre, Herre‟; skønt Herren ikke har talt.
Aneneri ake amabisa zonsezi monga muja amachitira anthu popaka njereza. Amazimphimba ndi zabodza zimene aona mʼmasomphenya awo ndi zonama za mʼmawula awo. Iwo amati, ‘Ambuye Yehova akuti,’ pamene Ine Yehova sindinayankhule.
29 Folket i Landet undertrykke de ved Vold, de røve Rov og forfordele den elendige og fattige og undertrykke den fremmede tværtimod Ret.
Anthu a mʼdzikomo amasautsa anzawo ndi kulanda anthu osowa. Amazunza anthu osauka ndi amphawi. Amavutitsa alendo posawachitira zinthu mwachilungamo.
30 Og jeg ledte efter en Mand iblandt dem, som vilde gærde et Gærde og staa i Gabet for mit Ansigt til Værn for Landet, at jeg ikke skulde ødelægge det; men jeg fandt ingen.
“Ndinafunafuna munthu pakati pawo woti amange linga, woti ayimirire dziko pamaso panga kundipepesa kuti ndisaliwononge, koma sindinamupeze.
31 Derfor udøser jeg min Vrede over dem, jeg gør Ende paa dem i min Fortørnelses Ild; jeg lader deres Vej falde tilbage paa deres Hoved, siger den Herre, Herre.
Nʼchifukwa chake ndawakwiyira kwambiri. Ndawawonongeratu ndi mkwiyo wanga woyaka ngati moto. Ndawalanga molingana ndi zimene anachita. Akutero Ambuye Yehova.”

< Ezekiel 22 >