< 2 Mosebog 23 >

1 Du skal ikke antage falsk Rygte; du skal ikke række den ugudelige Haanden til at være et uretfærdigt Vidne.
“Usafalitse mbiri yabodza. Usathandize munthu wolakwa pomuchitira umboni wonama.
2 Du skal ikke følge Mængden til det onde, og du skal ikke svare i en Trætte, saa at du bøjer Retten efter Mængden.
“Usatsate gulu la anthu ndi kuchita choyipa. Pamene ukupereka umboni mʼbwalo lamilandu, usakhotetse mlandu chifukwa chofuna kukondweretsa anthu ambiri.
3 Og du skal ikke besmykke den ringe i hans Trætte.
Ndipo poweruza mlandu wa munthu wosauka usamukondere.
4 Naar du møder din Fjendes Okse eller hans Asen, som farer vild, da skal du føre dem til ham igen.
“Ngati ukumana ndi ngʼombe kapena bulu wa mdani wako zitasochera, uwonetsetse kuti wazitenga kupita nazo kwa mwini wakeyo.
5 Naar du ser din Uvens Asen ligge under sin Byrde, da vogt dig, at du ikke overlader det til ham; du skal løse Byrden af tillige med ham.
Ngati uwona bulu wa munthu wina amene amakuda atagwa ndi katundu, usamusiye pomwepo, uwonetsetse kuti wamuthandiza.
6 Du skal ikke bøje Retten for den fattige hos dig i hans Trætte.
“Usakhotetse milandu ya anthu osauka.
7 Du skal holde dig langt fra falsk Sag, og du skal ikke ihjelslaa den uskyldige og retfærdige; thi jeg lader ikke den skyldige have Ret.
Upewe zabodza ndipo usaphetse munthu wosalakwa ndi wolungama, chifukwa Ine sindidzakhululukira wochimwa.
8 Og du skal ikke tage Gave; thi Gaven kan forblinde de seende og forvende de retfærdiges Sager.
“Musamalandire chiphuphu, pakuti chiphuphu chimadetsa mʼmaso anthu oweruza ndi kusintha mawu awo kuti mlandu uyipire osalakwa.
9 Og du skal ikke fortrykke den fremmede; thi I vide selv, hvorledes den fremmede er til Mode, thi I vare selv fremmede i Ægyptens Land.
“Usamuzunze mlendo, pakuti inu nomwe mukudziwa mmene amamvera mlendo chifukwa nanunso munali alendo mʼdziko la Igupto.
10 Og seks Aar skal du besaa dit Land og sanke dets Grøde;
“Muzidzala mbewu zanu mʼmunda ndi kumakolola mbewuzo kwa zaka zisanu ndi chimodzi.
11 men i det syvende skal du lade det ligge og hvile, at de fattige iblandt dit Folk maa æde deraf, og hvad deraf bliver tilovers, maa vilde Dyr paa Marken æde; saa skal du gøre med din Vingaard og med din Oliegaard.
Koma chaka chachisanu ndi chiwiri muzisiya osalima mindayo kuti anthu osauka pakati panu azipezamo chakudya, ndipo nyama zakuthengo zizidya zotsalazo. Muzichita chimodzimodzi ndi minda ya mpesa ndi mitengo ya olivi.
12 Seks Dage skal du gøre din Gerning, men paa den syvende Dag skal du hvile, paa det at din Okse og dit Asen maa hvile, og din Tjenestekvindes Søn og den fremmede maa vederkvæges.
“Muzigwira ntchito masiku asanu ndi limodzi koma tsiku lachisanu ndi chiwiri musagwire ntchito kuti ngʼombe yanu ndi bulu wanu apume ndiponso kuti kapolo wobadwira mʼnyumba yanu ndi mlendo yemwe apezenso mphamvu.
13 Og alt det, som jeg har sagt til eder, skulle I holde; og I skulle ikke ihukomme andre Guders Navn, det skal ikke høres af din Mund.
“Samalani pochita zonse zimene ine ndanena. Musamapemphere kwa milungu ina ndipo mayina awo musamawatchule.
14 Du skal holde mig tre Gange Højtid om Aaret.
“Muzichita zikondwerero zolemekeza Ine katatu pa chaka.
15 Du skal holde de usyrede Brøds Højtid; du skal æde usyrede Brød syv Dage, saasom jeg befalede dig, til den bestemte Tid i Abib Maaned, thi i den drog du ud af Ægypten; og for mit Ansigt skal ingen lade sig se tomhændet;
“Muzichita Chikondwerero cha Buledi wopanda Yisiti. Kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti monga ndinakulamulirani. Muzichita zimenezi mwezi wa Abibu pa nthawi yomwe ndayika, pakuti mʼmwezi umenewu munatuluka mʼdziko la Igupto. “Pasapezeke munthu wobwera pamaso panga wopanda kanthu mʼmanja.
16 og den Højtid naar du høster dit Arbejdes Førstegrøde af det, som du har saaet paa Marken; og Indsamlingens Højtid naar Aaret gaar ud, naar du har samlet dit Arbejdes Frugt af Marken.
“Muzichita Chikondwerero cha Masika pogwiritsa ntchito zipatso zoyambirira kucha zimene munadzala mʼmunda. “Muzichitanso Chikondwerero cha Zokolola pakutha pa chaka, pamene mukututa zokolola zanu mʼmunda.
17 Tre Gange om Aaret skal alt dit Mandkøn ses for den Herres, Herres Ansigt.
“Amuna onse azionekera pamaso pa Ambuye Yehova katatu pa chaka.
18 Du skal ikke ofre mit Slagtoffers Blod, hvor der er syret Brød, og det fede fra min Højtid skal ikke blive liggende Natten over til om Morgenen.
“Musapereke magazi anyama ngati nsembe kwa Ine pamodzi ndi chilichonse chimene chili ndi yisiti. “Ndipo musasunge mafuta anyama yansembe ya pa chikondwerero mpaka mmawa.
19 Det første, din Jords Førstegrøde, skal du føre til Herren din Guds Hus; du skal ikke koge et Kid i dets Moders Mælk.
“Muzibwera ndi zipatso zoyambirira kucha zabwino kwambiri ku Nyumba ya Yehova Mulungu wanu. “Musamaphike kamwana kambuzi mu mkaka wa mayi wake.
20 Se, jeg sender en Engel for dit Ansigt at bevare dig paa Vejen og føre dig til det Sted, som jeg har beredt.
“Taona Ine ndikutuma mngelo wanga patsogolo panu kuti akutetezeni mʼnjiramo ndi kukakufikitsani ku malo amene ndakonza.
21 Forvar dig for hans Ansigt og lyd hans Røst, fortørn ham ikke; thi han skal ikke forlade eder eders Overtrædelser, thi mit Navn er i ham.
Muzimumvera ndi kumvetsetsa zimene akunena. Musamuwukire chifukwa sadzakhululuka kuwukira kwanu, pakuti akuchita zimenezi mʼdzina langa.
22 Thi dersom du hører hans Røst og gør alt det, som jeg vil sige, da vil jeg og være dine Fjenders Fjende, og jeg vil trænge dem, som trænge dig.
Ngati mudzamvera iyeyu ndi kuchita zonse zimene Ine ndikunena, Ine ndidzakhala mdani wa adani anu ndipo ndidzatsutsana ndi onse otsutsana nanu.
23 Thi min Engel skal gaa for dit Ansigt, og føre dig til de Amoriter og Hethiter og Feresiter og Kananiter og Heviter og Jebusiter; og jeg vil udslette dem.
Mngelo wanga adzakhala patsogolo panu ndipo adzakufikitsani mʼdziko la Aamori, Ahiti, Aperezi, Akanaani, Ahivi ndi Ayebusi, ndipo ndidzawapheratu onsewo.
24 Du skal ikke tilbede deres Guder og ej tjene dem og ikke gøre, som de gøre; men du skal nedbryde dem og sønderslaa deres Billeder.
Musagwadire milungu yawo kapena kuyipembedza. Ndipo musatsatire zinthu zomwe amachita. Koma inu mukawononge milungu yawo ndi kuphwasula malo amene amapembedzerapo.
25 Men I skulle tjene Herren, eders Gud, og han skal velsigne Brødet og Vandet for dig; og jeg vil borttage Sygdom fra dig.
Muzipembedza Yehova Mulungu wanu ndipo adzakudalitsani ndi chakudya ndi madzi ndiponso ndidzachotsa nthenda pakati panu.
26 Der skal ingen være, som føder i Utide eller er ufrugtbar i dit Land; jeg vil lade dig fylde dine Dages Tal.
Palibe mkazi amene adzapite padera kapena kukhala wosabereka mʼdziko mwanu. Ndidzakupatsani moyo wautali.
27 Jeg vil sende Forfærdelse for mig for dit Ansigt og forvirre hvert Folk, som du kommer til; og jeg vil lade alle dine Fjender fly for dig.
“Ine ndidzawachititsa mantha ndi kusokoneza anthu onse amene adzalimbana ndi inu ndipo adani anu onse adzakuthawani.
28 Og jeg vil sende Gedehamse for dit Ansigt, som skulle udjage Heviterne, Kananiterne og Hethiterne for dig.
Ahivi, Akanaani ndi Ahiti adzathawa ngati kuti ndawatumizira mavu.
29 Jeg vil ikke udjage dem fra dit Ansigt paa eet Aar, at Landet ikke skal blive øde, og vilde Dyr paa Marken ikke skulle formeres mod dig.
Komabe sindidzawachotseratu onse mʼchaka chimodzi chifukwa dziko lingadzakhale lopanda anthu ndipo nyama zakuthengo zidzakuchulukirani.
30 Jeg vil uddrive dem for dit Ansigt lidt efter lidt, indtil at du bliver mangfoldig og besidder Landet.
Ndidzawathamangitsa pangʼonopangʼono mpaka inu mutachuluka kokwanira mwakuti nʼkutenga dzikolo.
31 Og jeg vil sætte dit Landemærke fra det røde Hav indtil Filistrenes Hav og fra Ørken indtil Floden; thi jeg vil give Landets Indbyggere i eders Haand, og du skal uddrive dem fra dit Ansigt.
“Malire a dziko lanu adzakhala kuyambira ku Nyanja Yofiira mpaka ku nyanja ya Afilisti, ndiponso kuyambira ku chipululu mpaka ku mtsinje wa Yufurate. Anthu onse okhala mʼdziko limeneli ndidzawapereka mʼmanja mwanu ndipo mudzawathamangitsa.
32 Du skal ikke gøre Pagt med dem eller med deres Guder.
Musachite pangano ndi iwo kapena ndi milungu yawo.
33 Lad dem ikke bo i dit Land, at de ikke skulle komme dig til at synde imod mig; thi du kunde tjene deres Guder, og det vilde blive dig til en Snare.
Asadzakhale mʼdziko lanu chifukwa angadzakuchimwitseni ndi kuyamba kupembedza milungu yawo. Mukadzatero ndiye kuti mwakodwa mu msampha.”

< 2 Mosebog 23 >