< 2 Mosebog 21 >

1 Og disse ere de Love, som du skal forelægge dem.
“Uwawuze Aisraeli malamulo awa:
2 Naar du køber en hebraisk Tjener, da skal han tjene seks Aar, og i det syvende skal han udgaa fri for intet.
“Mukagula kapolo wa Chihebri, azikugwirirani ntchito zaka zisanu ndi chimodzi. Koma mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri muzimumasula, ndipo asalipire kanthu.
3 Dersom han kom enlig, da skal han udgaa enlig; dersom han var en Hustrus Mand, da skal hans Hustru udgaa med ham.
Ngati anabwera yekha, amasulidwenso yekha. Koma ngati anali ndi mkazi pamene ankabwera, mkaziyo apite nayenso.
4 Dersom hans Herre har givet ham en Hustru, og hun har født ham Sønner eller Døtre, da skal Kvinden og hendes Børn høre hendes Herre til, og han selv skal udgaa enlig.
Ngati bwana wake amupatsa mkazi ndipo mkaziyo anabereka ana aamuna kapena aakazi, mkazi ndi anawo adzakhala a bwanayo ndipo mwamuna yekhayo ndiye adzamasulidwe.
5 Men dersom Tjeneren siger saa: Jeg elsker, min Herre, min Hustru og mine Børn, jeg vil ikke gaa ud som fri:
“Koma ngati kapoloyo alengeza kuti, ‘Ine sindikufuna kumasulidwa chifukwa ndimakonda mbuye wanga, mkazi wanga ndi ana,’
6 Da skal hans Herre føre ham frem for Gud og holde ham op til Døren eller til Dørstolpen, og hans Herre skal gennemstikke hans Øre med en Syl; saa skal han tjene ham bestandig.
mbuye wakeyo abwere naye kwa Yehova. Abwere naye pa chitseko kapena pa mphuthu zachitseko ndipo abowole khutu lake ndi chitsulo. Ndipo iye adzakhala kapolo wake moyo wake wonse.
7 Og naar nogen sælger sin Datter til at være en Tjenestepige, da skal hun ikke udgaa, som Tjenere udgaa.
“Ngati munthu agulitsa mwana wake wamkazi kukhala mdzakazi, mwanayo asamasulidwe monga achitira ndi akapolo aamuna.
8 Dersom hun er mishagelig for hendes Herres Øjne, som har trolovet sig med hende, da skal han tillade, at hun løses; han skal ikke have Magt til at sælge hende til et fremmed Folk, efterdi han har handlet troløst mod hende.
Koma ngati mkaziyo sakukondweretsa bwana wake amene wamusankha kuti amukwatire, amulole kuti awomboledwe. Bwanayo alibe mphamvu zomugulitsa kwa anthu achilendo, chifukwa iyeyo waphwanya pangano lake lomukwatira iye.
9 Men dersom han trolover hende med sin Søn, skal han gøre mod hende efter Døtrenes Ret.
Ngati anamusankha kuti akhale mkazi wa mwana wake, ayenera kumusunga ngati mwana wake wamkazi.
10 Dersom han tager ham en anden, da skal han ikke formindske hendes Livs Ophold, hendes Klædning og Ægteskabspligten mod hende.
Ngati akwatira mkazi wina, asamumane woyambayo chakudya ngakhale chovala ndipo apiritirize kugona naye ngati mkazi wake.
11 Men dersom han ikke gør disse tre Ting imod hende, da skal hun udgaa for intet, uden Betaling.
Koma ngati sangathe kumuchitira zonsezi, ndiye amuleke apite popanda kulipira kanthu.
12 Hvo som slaar et Menneske, saa at det dør, han skal visselig dødes.
“Munthu aliyense amene amenya mnzake namupha, iyenso ayenera kuphedwa.
13 Men har han ikke luret efter ham, men Gud har ladet ham falde i hans Haand, da vil jeg bestemme dig et Sted, hvor han skal fly hen.
Koma ngati sanachite dala, ndipo Mulungu analola kuti zichitike, iyeyo athawire ku malo kumene ndidzakupatsani.
14 Og naar nogen hovmodelig sætter sig op imod sin Næste og slaar ham ihjel med Svig, da skal du tage ham endog fra mit Alter til at dø.
Koma ngati munthu akonza chiwembu ndi kupha mnzake mwadala, ameneyo muchotseni ngakhale ku guwa langa lansembe ndipo aphedwe.
15 Og hvo som slaar sin Fader eller Moder, skal visselig dødes.
“Munthu aliyense amene amenya abambo ake kapena mayi ake ayenera kuphedwa.
16 Og hvo som stjæler et Menneske og sælger det, eller det bliver fundet i hans Vold, han skal visselig dødes.
“Munthu aliyense amene aba munthu mnzake, ndi kukamugulitsa, kapena kumangomusunga, ayenera kuphedwa.
17 Og hvo som bander sin Fader eller sin Moder, skal visselig dødes.
“Aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa.
18 Og naar Mænd trættes, og den ene slaar den anden med en Sten eller med Næve, og han ikke dør, men maa ligge til Sengs,
“Ngati anthu awiri akangana ndipo wina amenya mnzake ndi mwala kapena nkhonya koma wosamupha, womenyedwayo akadwala nagona pa bedi,
19 og han kommer op igen og gaar om paa Gaden ved sin Stav, da skal den, som slog, være uskyldig; dog skal han betale hans Tidsspilde og lade ham fuldkomment læge.
kenaka nachira ndi kuyamba kuyenda ndi ndodo kutuluka kunja kwa nyumba yake, ndiye kuti womenya mnzakeyo sadzayimbidwa mlandu. Komabe adzayenera kulipira womenyedwayo chifukwa cha nthawi imene anagona pa bedi ija, ndiponso ayenera kumusala mpaka atachiritsitsa.
20 Og naar nogen slaar sin Tjener eller sin Tjenestepige med en Kæp, saa at de dø under hans Haand, da skal det visselig hævnes.
“Ngati munthu amenya kapolo wake wamwamuna kapena mdzakazi ndi ndodo, kapolo uja ndikufa chifukwa cha kumenyedwako, munthuyo ayenera kulangidwa.
21 Dog dersom de blive ved Live een eller to Dage, da skal det ikke hævnes; thi det er hans Penge.
Koma ngati kapolo uja akhala ndi moyo tsiku lonse kapena masiku awiri, ndiye kuti mbuye uja asalangidwe chifukwa kapolo ndi chuma chake.
22 Og naar Mænd trættes tilsammen og slaa en frugtsommelig Kvinde, og hendes Foster fødes, og der ikke sker Ulykke, da skal der gives Bøde, eftersom Kvindens Husbonde paalægger ham, og han skal give efter Dommeres Tykke.
“Ngati anthu akumenyana ndi kupweteka mayi woyembekezera, mayiyo napita padera, koma osavulala, wolakwayo ayenera kulipira chilichonse chimene mwamuna wake wa mkaziyo adzalamula ndipo bwalo lamilandu lavomereza.
23 Men dersom der sker Ulykke, da skal du give Liv for Liv.
Koma ngati wavulazidwa kwambiri, ndiye malipiro ake adzakhala motere: moyo kulipa moyo,
24 Øje for Øje, Tand for Tand, Haand for Haand, Fod for Fod,
diso kulipira diso, dzino kulipira dzino, mkono kulipa mkono, phazi kulipa phazi.
25 brændt for brændt, Saar for Saar, blaatslaget for blaatslaget.
Kutentha ndi moto kulipa kutentha ndi moto, bala kulipa bala, mkwingwirima kulipa mkwingwirima.
26 Og naar nogen slaar sin Tjeners Øje eller sin Tjenestepiges Øje og fordærver det, da skal han lade dem fare fri for deres Øjes Skyld.
“Ngati munthu amenya wantchito wake wa mwamuna kapena mdzakazi wake pa diso ndi kuliwononga, wantchitoyo amasulidwe ngati malipiro a diso lake.
27 Og dersom han slaar sin Tjeners Tand eller Tjenestepiges Tand ud, skal han lade dem fare fri for deres Tands Skyld.
Ndipo ngati agulula dzino la wantchito wamwamuna kapena mdzakazi, wantchitoyo amasulidwe ngati malipiro a dzino lake.
28 Og om en Okse stanger en Mand eller Kvinde, saa at de dø, da skal Oksen visselig stenes, og dens Kød skal ikke ædes; men Oksens Herre skal være uskyldig.
“Ngati ngʼombe ipha munthu wamwamuna kapena wamkazi ndi nyanga yake, iponyedwe miyala ndipo nyama yake isadyedwe. Ndipo mwini ngʼombeyo asayimbidwe mlandu.
29 Men dersom den Okse tilforn var vant at stange, og det var vitterliggjort for dens Ejermand, og han ikke passede paa den, og den dræber Mand eller Kvinde, da skal Oksen stenes, og dens Ejermand skal ogsaa dødes.
Koma ngati ngʼombeyo inali ndi chizolowezi chogunda anthu ndipo mwini wakeyo anachenjezedwa koma iye sanayimange ndipo yapha mwamuna kapena mkazi, ngʼombeyo iponyedwe miyala ndipo mwini wakeyo aphedwenso.
30 Men dersom der bliver paalagt ham en Bod, da skal han give Løsepenge for sit Liv efter alt det, som paalægges ham.
Koma ngati wauzidwa kuti alipire, iye apereke zimene wauzidwazo kuti awombole moyo wake.
31 Enten den stanger en Søn, eller den stanger en Datter, da skal ham ske efter denne Vis.
Lamulo ili ligwirenso ntchito ngati ngʼombeyo yagunda mwana wamwamuna kapena wamkazi.
32 Dersom en Okse stanger en Tjener eller Tjenestepige, da skal der gives deres Husbonde tredive Sekel Sølv, og Oksen skal stenes.
Ngati ngʼombeyo yagunda kapolo wamwamuna kapena mdzakazi, mwini ngʼombeyo apereke masekeli makumi atatu a siliva kwa mwini kapoloyo, ndipo ngʼombeyo iponyedwe miyala.
33 Og naar nogen aabner en Brønd, eller naar nogen graver en Brønd og dækker den ikke til, og der falder en Okse eller et Asen i den,
“Munthu akasiya dzenje lapululu kapena akakumba dzenje koma wosaphimbapo, ndipo ngʼombe kapena bulu nʼkugweramo,
34 da skal Brøndens Ejermand betale derfor, han skal give Penge derfor til deres Herre, og det døde Dyr skal han have.
mwini dzenjelo amulipire mwini chiweto chakufacho koma iye atenge chiwetocho.
35 Og naar en Mands Okse stanger en anden Mands Okse, saa at den dør, da skulle de sælge den levende Okse og halvdele dens Værd, og den døde skulle de og halvdele.
“Ngati ngʼombe ya munthu wina ipha ngʼombe ya mnzake, ngʼombe yamoyo ija igulitsidwe ndipo anthu awiriwo agawane pakati ndalama yake. Achite chimodzimodzi ndi ngʼombe yakufa ija.
36 Eller var det vitterligt, at den Okse plejede tilforn at stange, og dens Ejermand ikke vilde passe paa den, da skal han visselig betale Okse for Okse, og den døde skal han have.
Koma zikadziwika kuti ngʼombeyo inali ndi khalidwe logunda, ndipo mwini wake samayitsekera mʼkhola, mwini ngʼombeyo alipire ngʼombe ina yamoyo koma atenge yakufayo.”

< 2 Mosebog 21 >