< Prædikeren 4 >

1 Og jeg vendte tilbage og saa alle de undertrykte, som ilde medhandles under Solen; og se, de undertryktes Taarer, og der var ingen, som trøstede dem, og fra deres Undertrykkeres Haand udgik Vold; derimod havde de ingen, som trøstede dem.
Ndinayangʼananso ndi kuona chipsinjo chimene chimachitika pansi pano: ndinaona misozi ya anthu opsinjika, ndipo iwo alibe owatonthoza; mphamvu zinali ndi anthu owapsinjawo ndipo iwonso analibe owatonthoza.
2 Da prisede jeg de døde, som alt vare døde, fremfor de levende, som endnu ere i Live;
Ndipo ndinanena kuti akufa, amene anafa kale, ndi osangalala kuposa amoyo, amene akanalibe ndi moyo.
3 men lykkelig fremfor begge dog den, som endnu ikke har været til, som ikke har set den onde Gerning, der gøres under Solen.
Koma wopambana onsewa ndi amene sanabadwe, amene sanaone zoyipa zimene chimachitika pansi pano.
4 Og jeg saa alt Arbejde og al Dygtighed i Gerningen, at det paadrog en Mand Misundelse af hans Næste; ogsaa dette er Forfængelighed og Aandsfortærelse.
Ndipo ndinazindikira kuti ntchito zonse zolemetsa ndiponso ntchito zonse zaluso zimachitika chifukwa choti wina akuchitira nsanje mnzake. Izinso ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
5 Daaren lægger sine Hænder sammen og fortærer sit eget Kød.
Chitsiru chimangoti manja ake lobodo ndi kudzipha chokha ndi njala.
6 En Haandfuld med Ro er bedre end begge Næver fulde med Møje og Aandsfortærelse.
Nʼkwabwino kukhala ndi dzanja limodzi lodzaza uli pa mtendere, kuposa kukhala ndi manja awiri odzaza uli pa mavuto, ndipo uku nʼkungodzivuta chabe.
7 Og jeg vendte tilbage og saa Forfængelighed under Solen:
Ndinaonanso chinthu china chopanda phindu pansi pano:
8 Der er den, som er ene og ikke har nogen anden og har hverken Søn eller Broder; dog er der ingen Ende paa alt hans Arbejde, og hans Øjne mættes ikke af Rigdom; — og: „For hvem arbejder jeg og lader min Sjæl fattes det gode”? ogsaa dette er Forfængelighed og en slem Møje.
Panali munthu amene anali yekhayekha; analibe mwana kapena mʼbale. Ntchito yake yolemetsa sinkatha, ndipo maso ake sankakhutitsidwa ndi chuma chake. Iye anadzifunsa kuti, “Kodi ntchito yosautsayi ndikuyigwirira yani? Nanga nʼchifukwa chiyani ndikudzimana chisangalalo?” Izinso ndi zopandapake, zosasangalatsa!
9 Bedre to end een; thi de have en god Løn for deres Arbejde.
Kukhala awiri nʼkwabwino kuposa kukhala wekha, chifukwa ntchito ya anthu awiri ili ndi phindu:
10 Thi dersom de falde, kan den ene oprejse sin Stalbroder, men ve den, som er ene; naar han falder, er der ingen anden til at oprejse ham.
Ngati winayo agwa, mnzakeyo adzamudzutsa. Koma tsoka kwa munthu amene agwa ndipo alibe wina woti amudzutse!
11 Ogsaa naar to ligge sammen, da have de Varme; men hvorledes kan en alene blive varm?
Komanso ngati anthu awiri agona malo amodzi, adzafunditsana. Koma nanga mmodzi angadzifunditse yekha?
12 Og om nogen vilde overvælde ham, som er ene, kunde to staa ham imod; og den tredobbelte Traad sønderrives ikke saa snart.
Munthu mmodzi angathe kugonjetsedwa, koma anthu awiri akhoza kudziteteza. Chingwe cha maulusi atatu sichidukirapo.
13 Bedre faren er et ungt Menneske, som er viist, end en gammel Konge, som er en Daare, og som endnu ikke ved at lade sig advare.
Wachinyamata wosauka koma wanzeru aposa mfumu yokalamba koma yopusa imene simvanso malangizo.
14 Thi af Fangehuset udgik hin for at blive Konge, medens den, som var født i sit Kongerige, blev fattig.
Wachinyamatayo angathe kuchokera ku ndende ndi kudzakhala mfumu, kapena angathe kubadwa wosauka mʼdziko la mfumuyo.
15 Jeg saa alle dem, som leve, som vandre under Solen, at holde sig til det andet unge Menneske, der indtager hans Sted.
Ndipo ndinaona kuti iwo onse amene anakhala ndi moyo ndi kuyenda pansi pano anatsatira wachinyamatayo, amene anatenga malo a mfumu.
16 Der var ikke Ende paa alt det Folk, paa alt det, som han gik i Spidsen for, dog skulle Efterkommerne ikke glædes over ham: Thi ogsaa dette er Forfængelighed og Aandsfortærelse.
Mfumu ikhoza kulamulira anthu osawerengeka, komabe itamwalira, palibe amene adzayamikire zomwe mfumuyo inachita. Izinso ndi zopandapake, nʼkungozivuta chabe.

< Prædikeren 4 >