< 5 Mosebog 34 >

1 Og Mose gik op fra Moabs slette Marker paa Nebo Bjerg, paa Pisgas Top, som er lige over for Jeriko; og Herren lod ham se hele Landet: Gilead indtil Dan
Ndipo Mose anakwera Phiri la Nebo kuchokera ku chigwa cha Mowabu ndi kukafika pamwamba pa Phiri la Pisiga, kummawa kwa Yeriko. Kumeneko Yehova anamuonetsa dziko lonse; kuchokera ku Giliyadi mpaka ku Dani.
2 og hele Nafthali og Efraims og Manasse Land og hele Judas Land indtil det yderste Hav
Dera lonse la Nafutali, dziko lonse la Efereimu ndi Manase, dziko lonse la Yuda mpaka kukafika kumadzulo kwa nyanja,
3 og Sydlandet og Sletten, Dalen ved Jeriko, Palmestaden, indtil Zoar.
Negevi ndi chigawo chonse kuchokera ku Chigwa cha Yeriko, Mzinda wa mitengo ya migwalangwa, mpaka ku Zowari.
4 Og Herren sagde til ham: Dette er det Land, som jeg har tilsvoret Abraham, Isak og Jakob og sagt: Din Sæd vil jeg give det; jeg har ladet dig se det med dine Øjne, men du skal ikke drage derover.
Kenaka Yehova anawuza Mose kuti, “Limenelo ndi dziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo pamene ndinanena kuti, ‘Ndidzalipereka kwa zidzukulu zanu.’ Ndakulola kuti ulione, koma sudzawoloka kuti ukalowemo.”
5 Og Mose, Herrens Tjener, døde der i Moabs Land, efter Herrens Mund.
Choncho Mose mtumiki wa Yehova anamwalira kumeneko ku Mowabu, monga momwe ananenera Yehova.
6 Og han begrov ham i Dalen i Moabiternes Land, tværs over for Beth-Peor; og ingen ved hans Grav indtil denne Dag.
Yehova anamuyika mʼmanda ku Mowabu, mʼchigwa choyangʼanana ndi Beti-Peori, koma mpaka lero palibe amene amadziwa pamene pali manda ake.
7 Og Mose var hundrede og tyve Aar gammel, der han døde; hans Øje var ikke sløvet, og hans Kraft var ikke veget fra ham.
Mose anamwalira ali ndi zaka 120, koma maso ake ankaonabe ndipo anali amphamvu.
8 Og Israels Børn begræd Mose paa Moabiternes slette Marker tredive Dage; og Graadens Dage endtes, Sorgen over Mose.
Aisraeli analira maliro a Mose mʼchikhwawa cha Mowabu kwa masiku makumi atatu mpaka nthawi ya kulira maliro ndi kukhuza inatha.
9 Og Josva, Nuns Søn, blev fyldt med Visdomsaand, thi Mose havde lagt sine Hænder paa ham; og Israels Børn hørte ham og gjorde, som Herren havde befalet Mose.
Tsono Yoswa, mwana wa Nuni anadzazidwa ndi mzimu wanzeru chifukwa nʼkuti Mose atamusanjika manja. Choncho Aisraeli anamumvera ndipo anachita zomwe Yehova analamula Mose.
10 Men der opstod ikke en Profet ydermere i Israel som Mose, hvem Herren kendte Ansigt til Ansigt,
Kuyambira nthawi imeneyi, mu Israeli simunakhalepo mneneri wina aliyense wofanana ndi Mose, amene Yehova amayankhula naye maso ndi maso.
11 naar man ser hen til alle de Tegn og de underlige Ting, som Herren sendte ham til at gøre i Ægyptens Land, paa Farao og paa alle hans Tjenere og paa alt hans Land,
Amene anachita zizindikiro zozizwitsa zonsezi ndi zozizwitsa zimene Yehova anamutuma kuti achite mu Igupto, kwa Farao ndi kwa nduna zake zonse ndiponso mʼdziko lake lonse.
12 og til den vældige Haand og til alle de forfærdelige og store Gerninger, som Mose gjorde for al Israels Øjne.
Ndithudi palibe mneneri wina aliyense amene anachita zinthu zazikulu ndi zoopsa zofanana ndi zomwe Mose anachita pamaso pa Aisraeli onse.

< 5 Mosebog 34 >