< Daniel 2 >
1 Og i Nebukadnezars andet Regeringsaar drømte Nebukadnezar Drømme, og hans Aand blev bekymret, og det var forbi for ham med hans Søvn.
Chaka chachiwiri cha ulamuliro wake, Nebukadinezara analota maloto; anavutika mu mtima mwake ndipo analephera kugona.
2 Da sagde Kongen, at de skulde kalde Spaamændene og Besværgerne og Troldkarlene og Kaldæerne for at forkynde Kongen hans Drømme; og de kom og stode for Kongens Ansigt.
Tsono mfumu inayitana amatsenga, owombeza, amawula ndi oyangʼana nyenyezi kuti amufotokozere zomwe analota. Pamene iwo analowa ndi kuyima pamaso pa mfumu,
3 Og Kongen sagde til dem: Jeg drømte en Drøm, og min Aand blev bekymret, saa at jeg maa vide Drømmen.
mfumuyo inawawuza kuti, “Ndalota loto lomwe likundisautsa ndipo ndikufuna kudziwa tanthauzo lake.”
4 Da talte Kaldæerne til Kongen paa Syrisk: Kongen leve evindelig! sig dine Tjenere Drømmen, og vi skulle kundgøre Udtydningen.
Pamenepa alawuli anati kwa mfumu mʼChiaramu, “Mukhale ndi moyo wautali mfumu! Tiwuzeni ife atumiki anu zimene mwalota, ndipo tidzakuwuzani tanthauzo lake.”
5 Kongen svarede og sagde til Kaldæerne: Ordet fra mig staar fast: Dersom I ikke kundgøre mig Drømmen og Udtydningen derpaa, skulle I blive huggede i Stykker og eders Huse blive gjorte til en Møgdynge.
Mfumu inayankha alawuliwo kuti, “Zimene ndatsimikiza kuchita ndi izi: Ngati inu simundifotokozera zimene ndalota ndi tanthauzo lake, mudzadulidwa nthulinthuli ndipo nyumba zanu ndidzazisandutsa bwinja.
6 Men dersom I kundgøre Drømmen og Udtydningen derpaa, da skulle I bekomme Skænk og Gave og stor Ære af mig; derfor kundgører mig Drømmen og Udtydningen derpaa!
Koma ngati mundiwuza zimene ndalota ndi tanthauzo lake, ndidzakupatsani mphatso ndi mphotho ndi ulemu waukulu. Choncho mundiwuze zimene ndalota ndi tanthauzo lake.”
7 De svarede anden Gang og sagde: Kongen sige sine Tjenere Drømmen, saa ville vi kundgøre Udtydningen.
Iwo anayankhanso kachiwiri kuti, “Mfumu iwuze atumiki ake chimene yalota, ndipo ife tidzatanthauzira.”
8 Kongen svarede og sagde: Sandelig, jeg mærker, at I ville vinde Tid, efterdi I se, at Ordet fra mig staar fast;
Ndipo mfumu inayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti mukungozengereza kufuna kutaya nthawi chabe chifukwa mukuzindikira kuti izi ndi zimene ndatsimikiza kuchita.
9 dersom I ikke kundgøre mig Drømmen, da er der een Dom over eder, og I ere komne overens om at sige løgnagtig og fordærvelig Tale for mig, indtil Tiden forandrer sig; derfor siger mig Drømmen, saa kan jeg vide, at I kunne kundgøre mig Udtydningen derpaa.
Ngati simundiwuza zimene ndalota, chilango chake ndi chimodzi. Inu mwagwirizana kuti mundiwuze ine bodza ndi chinyengo ndi kuyembekeza kuti ine ndisintha. Tsono mundiwuze zimene ndalota, ndipo ine ndidzadziwa kuti mukhoza kunditanthauzira.”
10 Kaldæerne svarede Kongen og sagde: Der er intet Menneske paa Jorden, som kan kundgøre det, som Kongen forlanger, efterdi ingen stor og mægtig Konge har begæret saadan Ting af nogen Spaamand eller Besværger eller Kaldæer.
Alawuli anayankha mfumu kuti, “Palibe munthu pa dziko lapansi amene akhoza kuchita chimene mfumu ikufunsa! Palibe mfumu, kaya yayikulu kapena yamphamvu bwanji imene inafunsapo amatsenga, owombeza kapena alawuli aliwonse zimenezi.
11 Og den Ting, som Kongen begærer, er svar, og der er ingen anden, som kan kundgøre den for Kongen, uden Guderne, hvis Bolig ikke er hos Menneskene.
Zimene mfumu yafunsa ndi zapatali. Palibe wina amene angathe kuwulula izi kwa mfumu kupatula milungu, ndipo sikhala pakati pa anthu.”
12 Over dette blev Kongen fortørnet og meget vred, og han befalede, at man skulde udrydde alle vise i Babel.
Zimenezi zinapsetsa mtima mfumu ndipo inakwiya kwambiri kotero inalamula kuti anzeru onse a ku Babuloni aphedwe.
13 Og Befalingen udgik, og de vise bleve ihjelslagne; og man ledte efter Daniel og hans Medbrødre, for at de kunde blive ihjelslagne.
Choncho lamulo linaperekedwa kuti anthu anzeru aphedwe, ndipo anatuma anthu kukafunafuna Danieli ndi anzake kuti iwonso aphedwe.
14 Da gav Daniel et klogt og forstandigt Svar til Ariok, Øversten for Kongens Livvagt, som var gaaet ud for at ihjelslaa de vise i Babel.
Danieli anayankhula mwanzeru ndi mwaulemu kwa Ariyoki, mkulu wa asilikali olondera mfumu amene anatumidwa kukapha anthu anzeru a ku Babuloni.
15 Han svarede og sagde til Ariok, Kongens mægtige Mand: Hvorfor kommer denne strenge Befaling fra Kongen? Saa gav Ariok Sagen til Kende for Daniel.
Danieli anafunsa Ariyoki kapitawo wa mfumu kuti, “Chifukwa chiyani mfumu yapereka lamulo lankhanza lotere?” Kenaka Ariyoki anafotokoza nkhaniyi kwa Danieli.
16 Og Daniel gik ind og begærede af Kongen, at han vilde give ham Tid, og at han maatte kundgøre Kongen Udtydningen.
Danieli anapita mofulumira kwa mfumu ndipo anamupempha kuti amupatse nthawi kuti amuwuze zimene walota ndi tanthauzo lake.
17 Da gik Daniel til sit Hus og kundgjorde Hanania, Misael og Asaria, sine Medbrødre, Sagen,
Kenaka Danieli anabwerera ku nyumba kwake ndi kukafotokozera anzake aja zimenezi: Hananiya, Misaeli ndi Azariya.
18 og det, for at de skulde begære Barmhjertighed af Gud i Himmelen angaaende denne Hemmelighed, for at de ikke skulde udrydde Daniel og hans Medbrødre tillige med Resten af de vise i Babel.
Danieli anadandaulira anzake kuti apemphe kwa Mulungu wakumwamba kuti awachitire chifundo ndi kumuwululira chinsinsi, kuti iye ndi anzakewo asanyongedwe pamodzi ndi anzeru ena onse a ku Babuloni.
19 Da blev Hemmeligheden aabenbaret for Daniel i et Syn om Natten; da velsignede Daniel Himmelens Gud.
Usiku Yehova anamuwululira Danieli chinsinsi chija mʼmasomphenya. Pamenepo Danieli anatamanda Mulungu wakumwamba,
20 Daniel svarede og sagde: Velsignet være Guds Navn fra Evighed og indtil Evighed; thi Visdommen og Kraften er hans.
ndipo anati: “Litamandike dzina la Mulungu ku nthawi za nthawi; nzeru ndi mphamvu zonse ndi zake.
21 Og han forandrer Tider og Timer, han afsætter Konger og indsætter Konger; han giver de vise Visdom og de forstandige Kundskab.
Amasintha nthawi ndi nyengo; amakweza mafumu ndipo amawatsitsanso. Amapatsa nzeru kwa anzeru ndi chidziwitso kwa ozindikira zinthu.
22 Han aabenbarer de dybe og skjulte Ting; han ved, hvad der er i Mørket, og Lyset bor hos ham.
Amavumbulutsa zinthu zozama ndi zobisika; amadziwa zimene zili mu mdima, ndipo kuwunika kumakhala ndi Iye.
23 Dig, mine Fædres Gud! lover og priser jeg, thi du har givet mig Visdom og Styrke; og du har nu kundgjort mig det, vi begærede af dig, thi du har kundgjort os Kongens Sag.
Ndikuyamika ndi kutamanda Inu Mulungu wa makolo anga: mwandipatsa nzeru ndi mphamvu, mwandiwululira zomwe tinakupemphani, mwatiwululira maloto a mfumu.”
24 Derfor gik Daniel ind til Ariok, som Kongen havde befalet at udrydde de vise i Babel; han gik hen og sagde saaledes til ham: Udryd ikke de vise i Babel; før mig ind for Kongen, saa vil jeg kundgøre Kongen Udtydningen.
Motero Danieli anapita kwa Ariyoki, amene mfumu inamusankha kuti akaphe anthu anzeru a ku Babuloni, ndipo anati kwa iye, “Musaphe anthu anzeru a ku Babuloni. Ndiperekezeni kwa mfumu, ndipo ndidzayimasulira maloto ake.”
25 Da førte Ariok Daniel hastelig: ind for Kongen og sagde saaledes til ham: Jeg har fundet iblandt det bortførte Folk af Juda en Mand, som vil kundgøre Kongen Udtydningen.
Ariyoki anapita naye Danieli kwa mfumu nthawi yomweyo ndipo anati, “Ndapeza munthu pakati pa akapolo ochokera ku Yuda amene akhoza kuwuza mfumu zimene maloto ake akutanthauza.”
26 Kongen svarede og sagde til Daniel, hvis Navn var Beltsazar: Er du i Stand til at kundgøre mig den Drøm, som jeg saa, og Udtydningen derpaa?
Mfumu inafunsa Danieli (wotchedwanso Belitesezara) kuti, “Kodi ukhoza kundiwuza zomwe ine ndinaona mʼmaloto anga ndi tanthauzo lake?”
27 Daniel svarede Kongen og sagde: Hemmeligheden som Kongen begærer, kunne de vise, Besværgerne, Spaamændene og Sandsigerne ikke kundgøre Kongen.
Danieli anayankha kuti, “Palibe munthu wanzeru, wowombeza, wamatsenga kapena wamawula amene akhoza kufotokozera mfumu chinsinsi chimene mwafuna kudziwa,
28 Men der er en Gud i Himmelen, som aabenbarer hemmelige Ting, han har kundgjort Kong Nebukadnezar, hvad der skal ske i de sidste Dage; din Drøm og dit Hoveds Syner paa dit Leje ere disse:
koma kuli Mulungu kumwamba amene amawulula zinsinsi. Iye waonetsera mfumu Nebukadinezara zimene zidzachitika mʼmasiku akutsogolo. Maloto ndi masomphenya anu amene munawaona mukugona pa bedi lanu ndi awa:
29 Du Konge! dine Tanker opstege paa dit Leje om, hvad der skulde ske herefter; og han, som aabenbarer hemmelige Ting, har kundgjort dig, hvad der skal ske.
“Mukugona pa bedi, inu Mfumu, maganizo anakufikirani a zinthu zakutsogolo, ndipo Yehova wowulula zinsinsi anakuonetserani zimene zidzachitika.
30 Og mig er denne Hemmelighed aabenbaret, ikke af den Visdom, som er i mig, fremfor alle dem, der leve; men for at Udtydningen skulde gives Kongen til Kende, og du maatte komme til at vide dit Hjertes Tanker.
Koma chinsinsi ichi chavumbulutsidwa kwa ine, si chifukwa chakuti ndili ndi nzeru zochuluka kuposa anthu ena onse, koma kuti mfumu mudziwe tanthauzo la maloto anu ndi kuti muzindikire maganizo amene anali mu mtima mwanu.
31 Du, Konge! saa, og se, der var et højt Billede, samme Billede var stort, og dets Glans var herlig; det stod foran dig, og dets Udseende var forfærdeligt.
“Inu mfumu, munaona chinthu chowumba chachikulu chimene chinayima pamaso panu. Chowumbachi chinali chonyezimira mʼmaonekedwe.
32 Dette Billedes Hoved var af fint Guld, dets Bryst og dets Arme af Sølv, dets Bug og dets Lænder af Kobber,
Mutu wa chowumbacho unali wagolide wabwino kwambiri. Chifuwa ndi manja ake zinali zasiliva. Mimba ndi ntchafu zake zinali zamkuwa.
33 dets Ben vare af Jern, dets Fødder til Dels af Jern og til Dels af Ler.
Miyendo yake inali yachitsulo, mapazi ake anali achitsulo chosakaniza ndi dongo.
34 Du saa, indtil der blev en Sten løsreven, og det ikke ved Hænder, og den slog Billedet paa dets Fødder, som vare af Jern og Ler, og knuste dem.
Inu mukuona, mwala unagamuka, koma osati ndi manja a munthu. Unagwera fanolo pa mapazi ake achitsulo chosakaniza ndi dongo aja ndi kuwaphwanya.
35 Da blev Jernet, Leret, Kobberet, Sølvet og Guldet knuste paa een Gang og bleve ligesom Avner fra Tærskepladserne om Sommeren, og Vinden borttog dem, og intet Sted blev fundet for dem; men den Sten, som sønderslog Billedet, blev til et stort Bjerg og opfyldte hele Jorden.
Tsono chitsulo, dongo, mkuwa, siliva ndi golide zonse zinaphwanyika pamodzi ndikukhala tizidutswa towuluka ndi mphepo ngati mungu wa mowombera tirigu nthawi ya chilimwe. Zonse zinawuluka ndi mphepo osasiyako chilichonse. Koma mwala umene unagwera pa chowumba chija unasanduka phiri lalikulu ndi kudzaza dziko lonse lapansi.
36 Det er Drømmen, og Udtydningen derpaa skulle vi sige Kongen.
“Maloto aja ndi amenewa; tidzafotokoza tanthauzo lake kwa mfumu.
37 Du, Konge, Kongernes Konge, hvem Himmelens Gud har givet Riget, Magten og Styrken og Æren,
Inu mfumu, ndinu mfumu ya mafumu. Mulungu wakumwamba wakupatsani ufumu, ulamuliro ndi mphamvu ndi ulemerero;
38 og har allesteds, hvor Mennesker bo, Dyrene paa Marken og Fuglene under Himmelen, givet dem i din Haand og ladet dig herske over dem alle: Du selv er Guldholdet
Iye anayika mʼmanja mwanu anthu ndi nyama zakuthengo ndi mbalame zamlengalenga. Kulikonse kumene zikhala, iye anakuyikani wolamulira wa zonse. Inu ndinu mutu wagolidewo.
39 Og efter dig skal opkomme et andet Rige, ringere end dit, og et tredje Rige endnu, af Kobber, som skal herske over hele Jorden.
“Pambuyo pa inu, ufumu wina udzadzuka, wochepa mphamvu poyerekeza ndi wanuwu. Padzabweranso ufumu wachitatu, wamkuwa, udzalamulira dziko lonse lapansi.
40 Og et fjerde Rige skal være stærkt som Jernet; eftersom Jernet knuser og sønderslaar alt, skal det som Jernet der sønderslaar, knuse og sønderslaa alle hine.
Pomaliza, padzakhala ufumu wachinayi, wolimba ngati chitsulo popeza chitsulo chimaphwanya ndi kutikita chilichonse. Ndipo monga chitsulo chimaphwanya zinthu ndikuteketeratu, choncho udzawononga ndi kuphwanya maufumu ena onse.
41 Men at du saa Fødderne og Tæerne til Dels at være af Pottemagerler og til Dels af Jern, betyder, at det skal blive et delt Rige, og at der skal blive noget af Jernets Styrke derudi, efterdi du saa, at Jernet var blandet med Leret.
Ndipo monga munaonera kuti mapazi ndi zala zake zinali za chitsulo chosakaniza ndi dongo, choncho uwu udzakhala ufumu wogawikana; komabe udzakhala ndi mphamvu zina zachitsulo zotikita.
42 Og at Tæerne paa Fødderne vare til Dels af Jem og til Dels af Ler, betyder, at Riget for en Del skal være stærkt og for en Del skrøbeligt.
Monga zala zinali za chitsulo chosakaniza ndi dongo, choncho ufumu uwu udzakhala pangʼono wolimba ndi pangʼono wofowoka.
43 At du saa Jernet blandet med Leret, betyder, at de skulle blande sig ved Slægtskabsforbindelser, men dog ikke indbyrdes holde sammen; se, ligesom Jernet ikke kan blandes med Leret.
Ndipo monga munaona chitsulo chosakanizidwa ndi dongo, choncho anthu adzakhala wosakanizana ndipo sadzagwirizana, monga muja chitsulo sichingasakanizike ndi dongo.
44 Men i disse Kongers Dage skal Himmelens Gud oprette et Rige, som i al Evighed ikke skal forgaa, og hvis Regering ikke skal overlades til noget andet Folk; det skal knuse og tilintetgøre alle hine Riger; men selv skal det bestaa evindelig,
“Pa nthawi ya mafumu amenewo, Mulungu wakumwamba adzakhazikitsa ufumu umene sudzawonongedwa, kapenanso kuperekedwa kwa anthu ena. Udzawononga maufumu onse aja ndi kuwatheratu, koma iwo wokha udzakhalapobe mpaka muyaya.
45 efterdi du saa, at en Sten blev løsrevet fra Bjerget, og det ikke ved Hænder, og at den knuste Jernet, Kobberet, Leret, Sølvet og Guldet. Den store Gud har ladet Kongen vide, hvad der skal ske herefter, og Drømmen staar fast, og Udtydningen derpaa er vis.
Limeneli ndilo tanthauzo la masomphenya a mwala umene unagamuka pa phiri, koma osati ndi manja a anthu; mwala umene unaphwanya chitsulo, mkuwa, dongo, siliva ndi golide mʼtizidutswa. “Mulungu wamkulu wakuonetsani mfumu chimene chidzachitika kutsogolo. Malotowo ndi woona ndipo tanthauzo lake ndi lodalirika.”
46 Da faldt Kong Nebukadnezar paa sit Ansigt og nedbøjede sig for Daniel, og han befalede, at man skulde ofre ham Madofre og Røgelse.
Pamenepo mfumu Nebukadinezara inadzigwetsa chafufumimba pamaso pa Danieli ndi kumupatsa ulemu. Ndipo inalamula kuti anthu onse amuthirire Danieli nsembe ndi kumufukizira lubani.
47 Kongen svarede Daniel og sagde: Sandt er det, at eders Gud, han er en Gud over Guder og en Herre ovør Konger, og Hemmeligheders Aabenbarer, efterdi du har kunnet aabenbare denne Hemmelighed.
Mfumu inati kwa Danieli, “Zoonadi, Mulungu wako ndi Mulungu wa milungu ndi Ambuye wa mafumu ndi wowulula zinsinsi, pakuti iwe wathadi kuwulula chinsinsi ichi.”
48 Da gjorde Kongen Daniel stor og gav ham mange store Gaver og gjorde ham til Fyrste over hele Landskabet Babel og til øverste Forstander for alle de vise i Babel.
Ndipo mfumu inamukweza Danieli ndi kumupatsa mphatso zambiri. Anamuyika kuti akhale wolamulira chigawo chonse cha Babuloni ndi kutinso akhale woyangʼanira anthu ake onse anzeru.
49 Og Daniel begærede af Kongen, at han til Bestyrelsen over Landskabet Babel vilde beskikke Sadrak, Mesak og Abed-Nego; men Daniel blev ved Kongens Hof.
Komanso, monga mwa pempho la Danieli, mfumu inayika Sadirake, Mesaki ndi Abedenego, kuti akhale oyangʼanira chigawo cha Babuloni, pamene Danieliyo ankakhazikika mʼbwalo la mfumu.