< Daniel 12 >
1 Og paa den Tid skal Mikael, den store Fyrste, der staar som Værn for dit Folks Børn, staa frem, og der skal være en Trængsels Tid, som aldrig har været, siden Folk blev til og indtil den Tid; og paa samme Tid skal dit Folk undkomme, hver den, som findes skreven i Bogen.
“Pa nthawi imeneyo Mikayeli, mngelo wamkulu amene amateteza anthu a mtundu wako, adzabwera. Imeneyi idzakhala nthawi ya mavuto aakulu omwe sanaonekepo kuyambira pachiyambi cha mitundu ya anthu mpaka nthawi ikudzayo. Komatu pa nthawiyi anthu a mtundu wako, aliyense amene dzina lake lidzapezeke lolembedwa mʼbuku adzapulumutsidwa.
2 Og mange af dem, som sove i Støvets Jord, skulle opvaagne, somme til et evigt Liv, og somme til Skam, til evig Afsky.
Ambiri mwa amene akugona mʼnthaka adzadzuka: ena adzapita ku moyo wosatha, ena ku malo amanyazi ndi chilango chosatha.
3 Men de forstandige skulle skinne som den udstrakte Befæstnings Skin; og de, der førte de mange til Retfærdighed, som Stjernerne evindelig og altid.
Amene ali anzeru mʼnjira ya chilungamo adzawala ngati kuwala kwa mlengalenga, ndipo amene alondolera ambiri ku njira yolungama, adzawala ngati nyenyezi ku nthawi zosatha.
4 Og du, Daniel, luk til for Ordene, og forsegl Bogen indtil Endens Tid; mange skulle søge ivrigt i den, og Kundskab skal blive mangfoldig.
Koma iweyo, Danieli, sungitsa mawuwa, umate bukuli kufikira nthawi ya chimaliziro. Anthu ambiri adzapita uku ndi uko ndipo nzeru zidzanka zikukulirakulira.”
5 Og jeg, Daniel, jeg saa, og se, der stod to andre, een her paa Bredden af Floden, og een der paa Bredden af Floden.
Kenaka ine Danieli poyangʼana ndinaona anthu ena awiri atayima, wina tsidya lino la mtsinje, wina tsidya linalo.
6 Og der blev sagt til den Mand, som var iført de linnede Klæder, og som stod oven over Flodens Vande: Hvor længe skal det vare med Enden paa disse underfulde Ting?
Mmodzi mwa awiriwo anafunsa munthu wovala chovala chosalala amene anali mʼmbali mwa madzi a mu mtsinje uja kuti, “Kodi padzapita nthawi yayitali bwanji kuti zodabwitsazi zidzakwaniritsidwe?”
7 Og jeg hørte Manden, som var iført de linnede Klæder, og som stod oven over Flodens Vande, og han opløftede sin højre Haand og sin venstre Haand imod Himlene og svor ved ham, som lever evindelig: Igennem een Tid, Tider og en halv Tid, og naar det hellige Folks Magt fuldstændigt er knust, skulle alle disse Ting fuldendes.
Munthu wovala chovala chosalala, amene anali mʼmbali mwa madzi a mu mtsinje uja, anakweza dzanja lake lamanja ndi lamanzere kumwamba, ndipo ndinamumva akulumbira mʼdzina la Wamoyo ku nthawi zonse uja kuti, “Zidzachitika patapita zaka zitatu ndi theka. Zinthu zonsezi zidzachitika akadzatha masautso amene agwera anthu olungama.”
8 Og jeg hørte det, men forstod det ikke; og jeg sagde: Min Herre! hvad er det sidste af dette?
Ndinamva, koma sindinamvetsetse. Choncho ndinafunsa kuti, “Mbuye wanga, nanga matsiriziro a zonsezi adzakhala chiyani?”
9 Og han sagde: Gak bort, Daniel! thi Ordene skulle være tillukkede og forseglede indtil Endens Tid.
Ndipo anandiyankha kuti, “Pita iwe Danieli, pakuti mawuwa ndi osungidwa ndi omatidwa kufikira nthawi ya chimaliziro.
10 Mange skulle rense sig og to sig hvide og lutre sig, men de ugudelige skulle handle ugudeligt, og ingen af de ugudelige skal forstaa det; men de forstandige skulle forstaa det.
Anthu ambiri adzayeretsedwa nakhala olungama wopanda chodetsa, koma oyipa adzakhala chiyipire. Palibe mmodzi wa anthu oyipa amene adzamvetsetsa koma okhawo amene ali anzeru adzamvetsetsa.
11 Og fra den Tid, da den stadige Tjeneste bliver borttagen, og det for at opstille Ødelæggelsens Vederstyggelighed, er der Tusinde to Hundrede og halvfemsindstyve Dage.
“Kuyambira pamene nsembe ya tsiku ndi tsiku idzathetsedwa ndi kukhazikitsa kwa chonyansa chobweretsa chisokonezo chija, padzapita masiku 1,290.
12 Salig er den, som bier og naar til Tusinde tre Hundrede fem og tredive Dage.
Wodala munthu amene adikirabe nadzafika pa mapeto a masiku 1,335.
13 Men gak du dit Endeligt i Møde, og hvil, og staa frem til din Lod ved Dagenes Ende!
“Koma iweyo Danieli, pitiriza ndipo ulimbikire mpaka matsiriziro. Kenaka udzamwalira. Koma mʼmasiku otsiriza udzauka kuti ulandire gawo lako.”