< Amos 8 >
1 Saaledes lod den Herre, Herre mig se et Syn: Og se, en Kurv med Sommerfrugt;
Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: dengu la zipatso zakupsa.
2 Og han sagde: Hvad ser du, Amos? og jeg sagde: En Kurv med Sommerfrugt; da sagde Herren til mig: Enden er kommen for mit Folk Israel, jeg vil ikke ydermere blive ved at skaane det.
Iye anandifunsa kuti, “Amosi nʼchiyani ukuona?” Ine ndinayankha kuti, “Dengu la zipatso zakupsa.” Ndipo Yehova anati kwa ine, “Nthawi yachimaliziro yawakwanira anthu anga Aisraeli; sindidzawakhululukiranso.
3 Men Sangene i Paladset skulle blive til Hyl paia denne Dag, siger den Herre, Herre; der er mange døde Kroppe, paa alle Steder har man kastet dem hen — tys!
“Tsiku limenelo,” Ambuye Yehova akulengeza kuti, “Nyimbo za mʼNyumba ya Mulungu zidzasanduka kulira kofuwula. Mitembo ya anthu idzachuluka, ndipo adzayiponya ponseponse! Kudzangoti zii!”
4 Hører dette, I, som hige efter den fattige og efter at gøre Ende paa de ringe i Landet;
Imvani izi, inu amene mumapondereza anthu osowa ndipo simulabadira anthu osauka a mʼdzikomu.
5 idet I sige: Naar vil Nymaanen gaa forbi, for at vi kunne sælge Korn, og Sabbaten, for at vi kunne lade op for Kornforraadet; at vi kunne gøre Efaen liden, og Sekelen stor og forvende Vægtskaalene med Svig?
Mumanena kuti, “Kodi chikondwerero cha mwezi watsopano chidzatha liti kuti tigulitse zinthu? Ndipo tsiku la Sabata litha liti kuti tigulitse tirigu, kuti tichepetse miyeso, kukweza mitengo kuti tibere anthu ndi miyeso ya chinyengo,
6 at vi kunne købe de ringe for Penge og den fattige formedelst et Par Sko, og at vi kunne sælge Affald af Korn?
tigule osauka ndi ndalama zasiliva ndi osowa powapatsa nsapato, tigulitse ngakhale mungu wa tirigu?”
7 Herren har svoret ved Jakobs Stolthed: Alle deres Gerninger vil jeg ikke glemme evindelig.
Yehova amene Yakobo amamunyadira, walumbira kuti: Ine sindidzayiwala chilichonse chimene anachita.
8 Skal ikke for dette Jorden ryste, saa at hver, som bor derpaa, sørger, og den helt hæver sig som Floden, drives hid og did og sænker sig som Ægyptens Flod?
“Kodi dziko silidzagwedezeka chifukwa cha zimenezi, ndi onse okhala mʼmenemo kulira mwachisoni? Dziko lonse lidzavunduka ngati mtsinje wa Nailo; lidzagwedezeka kenaka nʼkukhala bata ngati mtsinje wa ku Igupto.
9 Og det skal ske paa denne Dag, siger den Herre, Herre, da vil jeg lade Solen gaa ned om Middagen og lade det blive mørkt for Jorden ved højlys Dag.
“Tsiku limenelo,” Ambuye Yehova akunena kuti, “Ndidzadetsa dzuwa masana ndi kugwetsa mdima pa dziko lapansi dzuwa likuswa mtengo.
10 Og jeg vil omvende eders Fester til Sorg og alle eders Sange til Klagemaal og bringe Sæk om alle Lænder og gøre hvert Hoved skaldet; og jeg vil give Sorg der som over en eneste Søn, og det sidste der skal være som en bitter Dag.
Maphwando anu achipembedzo ndidzawasandutsa kulira kwa chisoni ndipo kuyimba kwanu konse ndidzakusandutsa maliro. Ndidzakuvekani chiguduli nonsenu ndi kumeta mipala mitu yanu. Nthawi imeneyo idzakhala ngati yolira mwana wamwamuna mmodzi yekhayo, ndipo tsikulo lidzakhala lowawa mpaka kutha kwake.
11 Se, de Dage komme, siger den Herre, Herre, da jeg vil sende Hugger i Landet, ikke Hunger efter Brød og ikke Tørst efter Vand, men efter at høre Herrens Ord.
“Nthawi ikubwera,” Ambuye Yehova akunena kuti, “Ndidzagwetsa njala mʼdziko lonse; osati njala ya chakudya kapena ludzu la madzi, koma njala yofuna kumva mawu a Yehova.
12 Og de skulle vanke hid og did, fra Hav indtil Hav og fra Norden og indtil Østen; de skulle løbe omkring for at søge efter Herrens Ord, og de skulle ikke finde det.
Anthu azidzangoyendayenda kuchoka ku nyanja ina kupita ku nyanja ina. Azidzangoyendayenda kuchoka kumpoto kupita kummawa, kufunafuna mawu a Yehova, koma sadzawapeza.
13 Paa denne Dag skulle de dej lige Jomfruer og de unge Karle forsmægte af Tørst,
“Tsiku limenelo “anamwali okongola ndi anyamata amphamvu adzakomoka ndi ludzu.
14 de, som sværge ved Samarias Skyld, og sige: Saa sandt din Gud lever, Dan! og saa sandt Beersabas Skik bestaar! Og de skulle falde og ikke rejse sig mere.
Onse amene amalumbira pa tchimo la Samariya, kapena kumanena kuti, ‘Iwe Dani, pali mulungu wako wamoyo,’ kapena, ‘Pali mulungu wamoyo wa ku Beeriseba.’ Iwowo adzagwa ndipo sadzadzukanso.”