< Amos 7 >

1 Saaledes lod den Herre, Herre mig se et Syn: Og se, han dannede Græshopper, da Græsset til anden Slæt begyndte at komme frem; og se der kom Græs til anden Slæt efter Kongens Høslæt.
Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Yehova ankasonkhanitsa gulu la dzombe nthawi imene gawo la zokolola za mfumu linali litakololedwa kale ndipo mbewu zachiwiri zinali zitangoyamba kumera kumene.
2 Og det skete, der de vare færdige med at æde Urterne i Landet, at jeg sagde: Herre, Herre, tilgiv dog! hvorledes skal Jakob kunne bestaa? thi liden er han.
Dzombelo litadya zomera zonse za mʼdzikomo, Ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, khululukani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
3 Herren angrede dette; det skal ikke ske, sagde Herren.
Kotero Yehova anakhululuka. Yehovayo anati, “Izi sizidzachitika.”
4 Saaledes lod den Herre, Herre mig se et Syn: Og se, den Herre, Herre kaldte for at holde Ret ved Ild; og den fortærede det store Dyb, og den fortærede Ageren.
Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Ambuye Yehova ankayitana malawi a moto kuti alange anthu. Motowo unawumitsa nyanja yakuya ndi kupsereza dziko.
5 Og jeg sagde: Herre, Herre, lad dog af! hvorledes skal Jakob kunne bestaa? thi liden er han.
Tsono ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, chonde ndikukupemphani, lekani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
6 Herren angrede dette; heller ikke det skal ske, sagde den Herre, Herre.
Kotero Yehova anakhululuka. Ambuye Yehova anati, “Izinso sizidzachitika.”
7 Saaledes lod han mig se et Syn: Og se, Herren stod paa en lodret Mur, og han havde et Blylod i sin Haand.
Zimene Iye anandionetsa ndi izi: Ambuye anayima pambali pa khoma lomangamanga, mʼmanja mwake muli chingwe chowongolera khoma.
8 Og Herren sagde til mig: Hvad ser du, Amos? og jeg sagde: Et Blylod; da sagde Herren: Se, jeg vil bruge et Blylod midt iblandt mit Folk Israel; jeg vil ikke ydermere blive ved at skaane det.
Ndipo Ambuye anandifunsa kuti, “Amosi, nʼchiyani ukuonachi?” Ine ndinayankha kuti, “Chingwe chowongolera khoma.” Ndipo Yehova anati, “Taona, Ine ndikuyika chingwe chowongolerachi pakati pa anthu anga, Aisraeli; sindidzawalekereranso.
9 Men Isaks Høje skulle ødelægges, og Israels Helligdomme skulle blive øde, og jeg vil rejse mig imod Jeroboams Hus med Sværdet.
“Malo achipembedzo a Isake adzawonongedwa ndipo malo opatulika a Israeli adzasanduka bwinja; ndidzagwetsa nyumba ya Yeroboamu ndi lupanga langa.”
10 Da sendte Amazia, Præsten i Bethel, Bud til Jeroboam, Israels Konge, og lod sige: Amos har stiftet Sammensværgelse imod dig, midt i Israels Hus, Landet kan ikke udholde alle hans Ord.
Pamenepo Amaziya wansembe wa ku Beteli anatumiza uthenga kwa Yeroboamu mfumu ya Israeli kuti, “Amosi akukuutsirani chiwembu pakati pa Aisraeli. Dziko silingalekerere zonena zake zonsezo.
11 Thi saa har Amos sagt: Jeroboam skal dø ved Sværdet, og Israel skal visselig bortføres fra sit Land.
Pakuti zimene Amosi akunena ndi izi: “‘Yeroboamu adzaphedwa ndi lupanga, ndipo Israeli adzapita ndithu ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”
12 Og Amazia sagde til Amos: Du Seer! gak bort, fly du til Judas Land, og æd der Brød, og spaa der!
Ndipo Amaziya anawuza Amosi kuti, “Choka, mlosi iwe! Bwerera ku dziko la Yuda. Uzikalosera kumeneko ndipo anthu a kumeneko azikakudyetsa.
13 Men i Bethel maa du ikke ydermere blive ved at spaa; thi det er Kongens Helligdom, og det er Rigets Hus.
Usanenerenso ku Beteli, chifukwa kumeneko ndi malo opatulika a mfumu ndiponso ndi malo a nyumba yachipembedzo yaufumu.”
14 Da svarede Amos og sagde til Amazia: Jeg er ikke en Profet, og jeg er ikke en Profets Søn, men jeg er en Hyrde og en Mand, som sanker vilde Morbær.
Amosi anayankha Amaziya kuti, “Ine sindine mneneri kapena mwana wa mneneri; koma ndine woweta ziweto, ndiponso mlimi wa nkhuyu.
15 Men Herren tog mig fra Hjorden, og Herren sagde til mig: Gak hen, vær Profet for mit Folk Israel!
Koma Yehova ananditenga ndikuweta nkhosa ndipo anati, ‘Pita ukanenere kwa anthu anga Aisraeli.’
16 Og nu, hør Herrens Ord; du siger: Du maa ikke spaa imod Israel og ikke lade dine Ord dryppe over Isaks Hus.
Tsono imva mawu a Yehova. Iwe ukunena kuti, “‘Usanenere zotsutsa Israeli, ndipo siya kulalikira motsutsa nyumba ya Isake.’”
17 Derfor sasi siger Herren: Din Hustru skal blive en Skøge i Staden, og dine Sønner og dine Døtre skulle falde ved Sværdet, og din Jord skal deles med Maalesnoren, og du selv skal dø i et urent Land, og Israel skal visselig bortføres fra sit Land.
“Tsono zimene akunena Yehova ndi izi: “‘Mkazi wako adzasanduka wachiwerewere mu mzindamu, ndipo ana ako aamuna ndi aakazi adzaphedwa ndi lupanga. Munda wako udzayezedwa ndi chingwe ndi kugawidwa, ndipo iwe mwini udzafera mʼdziko la anthu osapembedza Mulungu. Ndipo Israeli adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”

< Amos 7 >