< Apostelenes gerninger 2 >

1 Og da Pinsefestens Dag kom, vare de alle endrægtigt forsamlede.
Litafika tsiku la chikondwerero cha Pentekosite, onse anali pamodzi.
2 Og der kom pludseligt fra Himmelen en Lyd som af et fremfarende vældigt Vejr og fyldte hele Huset, hvor de sade.
Mwadzidzidzi kunamveka mkokomo kuchokera kumwamba ngati wa mphepo yamphamvu, ndipo inadzaza nyumba yonse imene amakhala.
3 Og der viste sig for dem Tunger som af Ild, der fordelte sig og satte sig paa hver enkelt af dem.
Iwo anaona zinthu zokhala ngati malilime amoto ogawikana ndipo anakhala pa aliyense wa iwo.
4 Og de bleve alle fyldte med den Helligaand, og de begyndte at tale i andre Tungemaal, efter hvad Aanden gav dem at udsige.
Ndipo onse anadzazidwa ndi Mzimu Woyera, nayamba kuyankhula mu ziyankhulo zina, monga Mzimu Woyerayo anawayankhulitsa.
5 Men der var Jøder, bosiddende i Jerusalem, gudfrygtige Mænd af alle Folkeslag under Himmelen.
Ayuda woopa Mulungu ochokera ku mayiko onse a dziko lapansi ankakhala mu Yerusalemu nthawi imeneyi.
6 Da denne Lyd kom, strømmede Mængden sammen og blev forvirret; thi hver enkelt hørte dem tale paa hans eget Maal.
Utamveka mkokomo uja, gulu la anthu linasonkhana. Anthuwo anadabwa chifukwa aliyense anawamva atumwiwo akuyankhula ziyankhulo zosiyanasiyana.
7 Og de forbavsedes alle og undrede sig og sagde: „Se, ere ikke alle disse, som tale, Galilæere?
Mothedwa nzeru anafunsana kuti, “Kodi anthu onse amene akuyankhulawa si Agalileya?
8 Hvor kunne vi da høre dem tale, hver paa vort eget Maal, hvori vi ere fødte,
Nanga bwanji aliyense wa ife akuwamva iwo mu chinenero cha kwawo?
9 Parthere og Medere og Elamiter, og vi, som høre hjemme i Mesopotamien, Judæa og Kappadokien, Pontus og Asien,
Apanti, Amedi ndi Aelami; okhala ku Mesopotamiya, ku Yudeya ndi ku Kapadokiya, ku Ponto ndi ku Asiya,
10 i Frygien og Pamfylien, Ægypten og Libyens Egne ved Kyrene, og vi her boende Romere,
ku Frugiya ndi Pamfiliya, ku Igupto ndi ku madera a ku Libiya kufupi ndi ku Kurene; alendo ochokera ku Roma,
11 Jøder og Proselyter, Kretere og Arabere, vi høre dem tale om Guds store Gerninger i vore Tungemaal?‟
Ayuda ndi otsatira chipembedzo cha Chiyuda onse pamodzi; Akrete ndi Aarabu, ife tonse tikuwamva akuyankhula za ntchito zodabwitsa za Mulungu mu ziyankhulo zathu.”
12 Og de forbavsedes alle og vare tvivlraadige og sagde den ene til den anden: „Hvad kan dette være?‟
Modabwa ndi mothedwa nzeru anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Zimenezi zikutanthauzanji?”
13 Men andre sagde spottende: „De ere fulde af sød Vin.‟
Koma ena anawaseka nati, “Aledzera vinyo watsopano.”
14 Da stod Peter frem med de elleve og opløftede sin Røst og talte til dem: „I jødiske Mænd og alle I, som bo i Jerusalem! dette være eder vitterligt, og laaner Øre til mine Ord!
Koma Petro anayimirira pamodzi ndi atumwi khumi ndi mmodziwo ndipo anakweza mawu ake nayankhula kwa gulu la anthu nati: “Ayuda anzanga, ndi nonse amene muli mu Yerusalemu, mvetsetsani izi ndipo tcherani khutu ku zimene ndikunena.
15 Thi disse ere ikke drukne, som I mene; det er jo den tredje Time paa Dagen;
Kunena zoona, anthu awa sanaledzere ayi, monga momwe mukuganizira, pakuti ino ndi 9 koloko mmawa!
16 men dette er, hvad der er sagt ved Profeten Joel:
Koma izi ndi zimene ananena Mneneri Yoweli kuti:
17 „Og det skal ske i de sidste Dage, siger Gud, da vil jeg udgyde af min Aand over alt Kød; og eders Sønner og eders Døtre skulle profetere, og de unge iblandt eder skulle se Syner, og de gamle iblandt eder skulle have Drømme.
“‘Mulungu akuti, mʼmasiku otsiriza ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse. Ana anu aamuna ndi aakazi adzanenera, anyamata anu adzaona masomphenya, nkhalamba zanu zidzalota maloto.
18 Ja, endog over mine Trælle og over mine Trælkvinder vil jeg i de Dage udgyde af min Aand, og de skulle profetere.
Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi, ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo, ndipo iwo adzanenera.
19 Og jeg vil lade ske Undere paa Himmelen oventil og Tegn paa Jorden nedentil, Blod og Ild og rygende Damp.
Ndipo ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga ndi zizindikiro pa dziko lapansi pano, ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
20 Solen skal forvandles til Mørke og Maanen til Blod, førend Herrens store og herlige Dag kommer.
Dzuwa lidzadetsedwa ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi lisanafike tsiku lalikulu ndi laulemerero la Ambuye.
21 Og det skal ske, enhver, som paakalder Herrens Navn, skal frelses.‟ —
Ndipo aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka.’
22 I israelitiske Mænd! hører disse Ord: Jesus af Nazareth, en Mand, som fra Gud var godtgjort for eder ved kraftige Gerninger og Undere og Tegn, hvilke Gud gjorde ved ham midt iblandt eder, som I jo selv vide,
“Inu Aisraeli mverani mawu awa; Yesu wa ku Nazareti anali munthu amene anaperekedwa kwa inu ndi Mulungu. Ndipo Mulungu anakutsimikizirani zimenezi ndi zamphamvu, zodabwitsa ndi zizindikiro zimene anachita mwa Iye pakati panu, monga inu mukudziwa.
23 ham, som efter Guds bestemte Raadslutning og Forudviden var bleven forraadt, ham have I ved lovløses Haand korsfæstet og ihjelslaaet.
Yesu ameneyu anaperekedwa kwa inu mwa kufuna ndi kudziwiratu kwa Mulungu; ndipo inu mothandizidwa ndi anthu oyipa, munamupha Iye pomupachika pa mtanda.
24 Men Gud oprejste ham, idet han gjorde Ende paa Dødens Veer, eftersom det ikke var muligt, at han kunde fastholdes af den.
Koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa, kumumasula Iye ku zowawa za imfa, chifukwa kunali kosatheka kuti agwiridwe ndi imfa.
25 Thi David siger med Henblik paa ham: „Jeg havde altid Herren for mine Øjne; thi han er ved min højre Haand, for at jeg ikke skal rokkes.
Pakuti Davide ananena za Iye kuti, “‘Ndinaona Ambuye pamaso panga nthawi zonse. Chifukwa Iye ali kudzanja langa lamanja, Ine sindidzagwedezeka.
26 Derfor glædede mit Hjerte sig, og min Tunge jublede, ja, ogsaa mit Kød skal bo i Haab;
Chifukwa chake mtima wanga ndi wokondwa ndipo lilime langa likukondwera; thupi langanso lidzakhala ndi chiyembekezo.
27 thi du skal ikke lade min Sjæl tilbage i Dødsriget, ikke heller tilstede din hellige at se Forraadnelse. (Hadēs g86)
Chifukwa simudzasiya moyo wanga kumalo a anthu akufa, ku manda, kapena kulekerera Woyerayo kuti awole. (Hadēs g86)
28 Du har kundgjort mig Livets Veje; du skal fylde mig med Glæde for dit Aasyn.‟
Inu munandidziwitsa ine njira zamoyo; Inu mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu.’
29 I Mænd, Brødre! Jeg kan sige med Frimodighed til eder om Patriarken David, at han er baade død og begraven, og hans Grav er hos os indtil denne Dag.
“Abale, ine ndikuwuzani motsimikiza kuti kholo lathu Davide anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda, ndipo manda ake alipo lero lino.
30 Da han nu var en Profet og vidste, at Gud med Ed havde tilsvoret ham, at af hans Lænds Frugt skulde en sidde paa hans Trone,
Koma iye anali mneneri ndipo anadziwa kuti Mulungu analonjeza ndi lumbiro kuti adzayika mmodzi wa zidzukulu zake pa mpando waufumu.
31 talte han, forudseende, om Kristi Opstandelse, at hverken blev han ladt tilbage i Dødsriget, ej heller saa hans Kød Forraadnelse. (Hadēs g86)
Davide ataoneratu zimene zinali mʼtsogolo anayankhula za kuuka kwa Khristu, kuti Iye sanasiyidwe mʼmanda, ndipo thupi lake silinawole. (Hadēs g86)
32 Denne Jesus oprejste Gud, hvorom vi alle ere Vidner.
Mulungu wamuukitsa Yesu ameneyu, ndipo ife ndife mboni za zimenezi.
33 Efter at nu han ved Guds højre Haand er ophøjet og af Faderen har faaet den Helligaands Forjættelse, har han udgydt denne, hvilket I baade se og høre.
Khristu anakwezedwa kukhala kudzanja lamanja la Mulungu, nalandira Mzimu Woyera amene Atate anamulonjeza, ndipo watipatsa ife zimene mukuona ndi kumvazi.
34 Thi David for ikke op til Himmelen; men han siger selv: „Herren sagde til min Herre: Sæt dig ved min højre Haand,
Pakuti si Davide anakwera kumwamba koma iye akuti, “‘Ambuye anawuza Ambuye anga kuti: Khala kudzanja langa lamanja
35 indtil jeg faar lagt dine Fjender som en Skammel for dine Fødder.‟
mpaka nditasandutsa adani ako kukhala chopondapo mapazi ako.’
36 Derfor skal hele Israels Hus vide for vist, at denne Jesus, hvem I korsfæstede, har Gud gjort baade til Herre og til Kristus.‟
“Nʼchifukwa chake, Aisraeli onse adziwe ndithu kuti, Yesu amene inu munamupachika, Mulungu wamuyika kukhala Ambuye ndiponso Mpulumutsi.”
37 Men da de hørte dette, stak det dem i Hjertet, og de sagde til Peter og de øvrige Apostle: „I Mænd, Brødre! hvad skulle vi gøre?‟
Anthu atamva zimenezi, anatsutsika kwambiri mu mtima ndipo anati kwa Petro ndi atumwi enawo, “Abale, kodi ife tichite chiyani?”
38 Men Peter sagde til dem: „Omvender eder, og hver af eder lade sig døbe paa Jesu Kristi Navn til eders Synders Forladelse; og I skulle faa den Helligaands Gave.
Petro anawayankha kuti, “Lapani ndipo mubatizidwe aliyense wa inu, mʼdzina la Yesu Khristu kuti machimo anu akhululukidwe. Ndipo mudzalandira mphatso ya Mzimu Woyera.
39 Thi for eder er Forjættelsen og for eders Børn og for alle dem, som ere langt borte, saa mange som Herren vor Gud vil tilkalde.‟
Pakuti lonjezoli ndi lanu ndi ana anu ndiponso la onse amene ali kutali, ndi iwo onse amene Ambuye Mulungu wathu adzawayitane.”
40 Ogsaa med mange andre Ord vidnede han for dem og formanede dem, idet han sagde: „Lader eder frelse fra denne vanartede Slægt!‟
Petro anawachenjeza ndi mawu ena ambiri, ndipo anawadandaulira iwo kuti, “Mudzipulumutse ku mʼbado owonongeka uno.”
41 De, som nu toge imod hans Ord, bleve døbte; og der føjedes samme Dag omtrent tre Tusinde Sjæle til.
Iwo amene anawulandira uthenga wake anabatizidwa ndipo tsiku lomwelo miyoyo pafupifupi 3,000 inawonjezedwa ku gulu lawo.
42 Og de holdt fast ved Apostlenes Lære og Samfundet, Brødets Brydelse og Bønnerne.
Iwo ankasonkhana pamodzi kuphunzitsidwa ndi atumwi, pachiyanjano, pachakudya ndi popemphera.
43 Men der kom Frygt over enhver Sjæl, og der skete mange Undere og Tegn ved Apostlene.
Aliyense ankachita mantha chifukwa cha zodabwitsa ndi zizindikiro zambiri zimene atumwi ankachita.
44 Og alle de troende holdt sig sammen og havde alle Ting fælles.
Okhulupirira onse anali pamodzi ndipo aliyense ankapereka zinthu zake kuti zikhale za onse.
45 Og de solgte deres Ejendom og Gods og delte det ud iblandt alle, efter hvad enhver havde Trang til.
Ankagulitsa minda yawo ndi katundu wawo, ndi kugawira kwa aliyense molingana ndi zosowa zake.
46 Og idet de hver Dag vedholdende og endrægtigt kom i Helligdommen og brød Brødet hjemme, fik de deres Føde med Fryd og i Hjertets Enfold,
Tsiku ndi tsiku ankasonkhana pamodzi pa bwalo la pa Nyumba ya Mulungu. Ankadya pamodzi mʼnyumba zawo mwasangala ndi mtima woona.
47 idet de lovede Gud og havde Yndest hos hele Folket. Men Herren føjede daglig til dem nogle, som lode sig frelse.
Ankayamika Mulungu ndipo anthu onse ankawakomera mtima. Ndipo tsiku ndi tsiku Ambuye ankawonjezera ena pa chiwerengero cha olandira chipulumutso.

< Apostelenes gerninger 2 >