< 2 Samuel 22 >

1 Og David talede Ordene af denne Sang for Herren paa den Dag, Herren havde friet ham af alle hans Fjenders Haand og af Sauls Haand,
Davide anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli.
2 og han sagde: Herren er min Klippe og min Befæstning og den, som befrier mig.
Iye anati, “Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga.
3 Han er Gud, min Klippe, paa hvilken jeg tror, mit Skjold og min Frelses Horn, min Ophøjelse og min Tilflugt, min Frelser, fra Vold har du frelst mig.
Mulungu wanga ndiye thanthwe langa, mʼmene ndimathawiramo, chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa. Iye ndi linga langa, pothawirapo panga ndi mpulumutsi wanga. Munandipulumutsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
4 Jeg vil paakalde Herren, som bør at loves, saa bliver jeg frelst fra mine Fjender.
“Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
5 Thi Dødens Bølger omspændte mig, Belials Bække forfærdede mig.
“Mafunde a imfa anandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
6 Helvedes Reb omgave mig, Dødens Snarer laa foran mig. (Sheol h7585)
Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol h7585)
7 Da jeg var i Angest, raabte jeg til Herren, ja, jeg raabte til min Gud, og han hørte min Røst af sit Tempel og mit Raab med sine Øren.
“Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinapemphera kwa Mulungu wanga. Iye ali mʼnyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika mʼmakutu ake.
8 Og Jorden bævede og rystede, Himmelens Grundvolde bevægedes, og de bævede, thi han var vred.
“Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, maziko a miyamba anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
9 Og der opgik en Røg af hans Næse, og Ild af hans Mund fortærede; gloende Kul brændte ud fra ham.
Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
10 Og han bøjede Himmelen og for ned, og der var Mørkhed under hans Fødder.
Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
11 Og han for paa Keruben og fløj, og han blev set over Vejrets Vinger.
Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
12 Og han satte Mørkhed til Dække trindt omkring sig; der var Vandenes Forsamling og tykke Skyer.
Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, mitambo yakuda ya mlengalenga.
13 Fra Glansen, som var for ham, brændte gloende Kul.
Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera makala amoto alawilawi.
14 Herren tordnede fra Himmelen, og den højeste udgav sin Røst.
Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
15 Og han udskød Pile og adspredte dem; der kom Lyn, og han forfærdede dem.
Iye anaponya mivi yake, nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
16 Da saas Havets Leje, Jordens Grundvolde blottedes ved Herrens Trusel, ved hans Næses Aandes Pust.
Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera, ndipo maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwake.
17 Han udrakte sin Haand fra det høje, han hentede mig, han drog mig af mange Vande.
“Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
18 Han friede mig fra min stærke Fjende, fra mine Hadere, thi de vare mig for stærke.
Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga amene anali amphamvu kuposa ine.
19 De overfaldt mig i min Modgangs Tid; men Herren var min Støtte.
Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
20 Og han udførte mig i det vide Rum; han friede mig, thi han havde Lyst til mig.
Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
21 Herren gengældte mig efter min Retfærdighed, han betalte mig efter mine Hænders Renhed.
“Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
22 Thi jeg har bevaret Herrens Veje, og jeg har ikke handlet ugudeligt imod min Gud.
Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso pa Mulungu wanga.
23 Thi alle hans Domme ere mig for Øje, og hans Skikke, fra dem viger jeg ikke;
Malamulo ake onse ali pamaso panga, sindinasiye malangizo ake.
24 men jeg var fuldkommen for ham og vogtede mig for min Misgerning.
Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
25 Og Herren betalte mig efter min Retfærdighed, efter min Renhed for hans Øjne.
Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi makhalidwe anga abwino pamaso pake.
26 Imod den fromme viser du dig from, imod den trofaste vældige viser du dig trofast.
“Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu, kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
27 Imod den rene viser du dig ren, og imod den forvendte viser du dig vrang.
Kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa anthu achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
28 Og du skal frelse det elendige Folk, og dine Øjne ere over de høje, dem fornedrer du.
Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma maso anu amatsutsana ndi odzikuza ndipo mumawatsitsa.
29 Thi du, Herre, er min Lygte, og Herren skal gøre min Mørkhed klar.
Inu Yehova, ndinu nyale yanga; Yehova wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
30 Thi ved dig stormer jeg igennem Skaren, ved min Gud springer jeg over en Mur.
Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo, ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
31 Guds Vej er fuldkommen, Herrens Tale er lutret; han er alle dem et Skjold, som haabe paa ham.
“Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa iye.
32 Thi hvo er en Gud foruden Herren? og hvo er en Klippe foruden vor Gud?
Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
33 Gud er min Styrke og Kraft, og han letter min Vej fuldkomment.
Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
34 Han gør mine Fødder som Hindernes og skal lade mig staa paa mine Høje.
Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
35 Han lærer mine Hænder til Krigen, og en Kobberbue spændes med mine Arme.
Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
36 Og du giver mig din Frelses Skjold; og idet du ydmyger mig, gør du mig stor.
Inu mundipatsa ine chishango chanu cha chigonjetso; mumawerama kuti mundikweze.
37 Du gør mine Trin vide under mig, og mine Knokler snublede ikke.
Inu mwalimbitsa njira yanga kuti ndiyende bwino, kuti mapazi anga asaterereke.
38 Jeg forfølger mine Fjender og ødelægger dem og vender ikke tilbage, før jeg har gjort Ende paa dem.
“Ine ndinathamangitsa adani anga ndi kuwakantha; sindinabwerere mpaka iwo atawonongedwa.
39 Ja, jeg har gjort Ende paa dem og knuset dem, at de ikke skulle rejse sig; og de faldt under mine Fødder.
Ndinawakantha kotheratu, ndipo sanathe kudzukanso; Iwo anagwera pansi pa mapazi anga.
40 Og du har omgjordet mig med Kraft til Krigen, du skal nedbøje dem under mig, som staa op imod mig.
Inu munandipatsa ine mphamvu yochitira nkhondo; munagwaditsa adani anga pa mapazi anga.
41 Og du har jaget mig mine Fjender paa Flugt, ja mine Hadere, og jeg udrydder dem.
Inu muchititsa kuti adani anga atembenuke ndi kuthawa; ndipo ndinawononga adani anga.
42 De saa sig om, men der var ingen Frelser; til Herren, men han svarede dem ikke.
Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova, koma sanawayankhe.
43 Og jeg støder dem smaa som Jordens Støv, som Dynd paa Gader knuser jeg dem og tramper dem ned.
Ine ndinawaperesa ngati fumbi la pa dziko lapansi; ndinawasinja ndipo ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
44 Og du udfriede mig fra mit Folks Kiv; du bevarede mig til Hedningernes Hoved, et Folk, som jeg ikke kendte, de tjene mig.
“Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa mitundu ya anthu; Inu mwandisunga kuti ndikhale mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
45 Den fremmedes Børn smigre for mig; da deres Øre hørte om mig, adløde de mig.
Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine, amandigonjera.
46 Den fremmedes Børn visne hen, og de gaa omgjordede ud af deres Borge.
Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
47 Herren lever, og lovet være min Klippe, og Gud, min Frelses Klippe, skal ophøjes!
“Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa. Akuzike Mulungu, Thanthwe, Mpulumutsi wanga!
48 Den Gud, som giver mig Hævn, og som nedkaster Folkene under mig,
Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amayika anthu a mitundu yonse pansi pa ulamuliro wanga,
49 og som fører mig ud fra mine Fjender; du ophøjer mig over dem, som staa op imod mig, du redder mig fra Voldsmænd.
amene amandimasula mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
50 Derfor vil jeg bekende dig, Herre! iblandt Hedningerne og synge dit Navn Lov.
Choncho ine ndidzakutamandani Inu Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
51 Han gør sin Frelse stor for sin Konge og gør Miskundhed imod sin Salvede, imod David og imod hans Sæd, evindelig.
“Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake, amaonetsa kukoma mtima kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.”

< 2 Samuel 22 >