< 2 Samuel 16 >

1 Da David var gaaet lidt frem fra Toppen, se, da kom Ziba, Mefiboseths Tjener, imod ham med et Par sadlede Asener, og paa dem vare to Hundrede Brød og hundrede Klaser Rosiner og hundrede Stykker Sommerfrugt og en Flaske Vin.
Davide atapitirira pangʼono pamwamba pa phiri, anakumana ndi Ziba mtumiki wa Mefiboseti akudikira kuti akumane naye. Iye anali ndi abulu a chishalo pa msana ndipo ananyamula malofu a buledi 200, ntchintchi 100 za mphesa zowuma, zipatso za pa nthawi yachilimwe 100 ndi thumba la vinyo.
2 Og Kongen sagde til Ziba: Hvad vil du dermed? og Ziba sagde: Asenerne skulle være for Kongens Hus til at ride paa, og Brødet og Sommerfrugten til at æde for de unge Karle, og Vinen til at drikke for den, som bliver træt i Ørken.
Mfumu inafunsa Ziba kuti, “Nʼchifukwa chiyani wabweretsa izi?” Ziba anayankha kuti, “Abuluwa ndi oti anthu a mʼbanja mwanu akwerepo, buledi ndi zipatso ndi za anthu anu kuti adye, ndipo vinyoyo ndi woti atsitsimutse anthu amene atope mʼchipululu.”
3 Og Kongen sagde: Men hvor er din Herres Søn? og Ziba sagde til Kongen: Se, han blev i Jerusalem; thi han sagde: I Dag skal Israels Hus give mig min Faders Rige igen.
Kenaka mfumu inafunsa kuti, “Kodi chidzukulu cha mbuye wako chili kuti?” Ziba anati kwa iye, “Watsalira ku Yerusalemu chifukwa akuganiza kuti, ‘Lero Aisraeli andibwezera ufumu wa agogo anga.’”
4 Og Kongen sagde til Ziba: Se, alt det, som Mefiboseth har, skal være dit; og Ziba sagde: Jeg nedbøjer mig, lad mig finde Naade for dine Øjne, min Herre Konge!
Ndipo mfumu inati kwa Ziba, “Zonse zimene zinali za Mefiboseti ndi zako tsopano.” Ziba anati, “Ine modzichepetsa ndikukugwandirani, mbuye wanga mfumu, kuti ndipeze chisomo pamaso panu.”
5 Og Kong David kom til Bahurim, og se, der gik en Mand derudfra af Sauls Huses Slægt, hvis Navn var Simei, Geras Søn, som gik ud og vedblev at bande ham.
Mfumu Davide itayandikira Bahurimu, munthu wochokera ku fuko limodzi ndi banja la Sauli anabwera kuchokera mʼmenemo. Dzina lake linali Simei, mwana wa Gera ndipo amatukwana pamene amabwera.
6 Og han slog efter David og efter alle Kong Davids Tjenere med Stene, og alt Folket og alle de vældige vare ved højre og venstre Side af ham.
Iye amagenda Davide miyala ndi akuluakulu onse a mfumu, ngakhale kuti ankhondo onse ndi oteteza Davide anali ali kumanzere ndi kumanja kwake.
7 Og Simei sagde saa, der han bandede: Gak ud, gak ud, du blodgerrige Mand og du Belials Mand!
Potukwana, Simeiyo amati, “Choka iwe, choka iwe, munthu wopha anthu, munthu wachabechabe iwe!
8 Herren har betalt dig alt Sauls Huses Blod, hans, i hvis Sted du er bleven Konge, og Herren har givet Riget i din Søn Absaloms Haand, og se, du er i din Ulykke, thi du er en blodgerrig Mand.
Yehova wakubwezera chifukwa cha magazi onse amene unakhetsa pa nyumba ya Sauli, yemwe iwe ukulamulira mʼmalo mwake. Yehova wapereka ufumu kwa mwana wako Abisalomu. Ndipo ona mathero ako ndi amenewa chifukwa ndiwe munthu wopha anthu!”
9 Da sagde Abisaj, Zerujas Søn, til Kongen: Hvorfor skulde denne døde Hund bande min Herre Kongen? Kære, lad mig gaa over, og jeg vil tage hans Hoved.
Ndipo Abisai mwana wa Zeruya anati kwa mfumu, “Nʼchifukwa chiyani galu wakufa uyu akutukwana mbuye wanga mfumu? Ndiloleni ndipite kuti ndikadule mutu wake.”
10 Men Kongen sagde: Hvad har jeg med eder at gøre, I Zerujas Sønner? naar han bander, og Herren har sagt til ham: Band David! hvo kan da sige: Hvorfor gjorde du saa?
Koma mfumu inati, “Inu ana a Zeruya, kodi ndikuchitireni chiyani? Ngati iye akutukwana chifukwa Yehova wamuwuza kuti, ‘Tukwana Davide,’ angafunse ndani kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?’”
11 Og David sagde til Abisaj og til alle sine Tjenere: Se, min Søn, som er kommen af mit Liv, søger efter mit Liv, og hvi skulde ikke meget mere nu denne Benjaminit gøre det? lader ham være og lader ham bande, thi Herren har sagt det til ham.
Tsono Davide anati kwa Abisai ndi akuluakulu ake onse, “Mwana wanga wobereka ndekha akufuna kundipha. Nanji tsono munthu wa fuko la Benjamini uyu! Musiyeni; mulekeni atukwane pakuti Yehova wachita kumuwuza kuti atero.
12 Maaske Herren skal se til min Elendighed, og Herren skal betale mig godt i Stedet for hans Forbandelse paa denne Dag.
Mwina Yehova adzaona mazunzo anga ndipo adzandibwezera zabwino chifukwa cha kutukwanidwa kumene ndikulandira lero.”
13 Saa gik David og hans Mænd paa Vejen; men Simei gik frem ved Siden af Bjerget tværs over for ham og blev ved at bande og slog med Stene tværs over for ham og støvede med Støvet.
Kotero Davide ndi anthu ake anapitirira kuyenda mu msewu pamene Simei amayenda mʼmbali mwa phiri moyangʼanana naye akutukwana ndi kuponya miyala pamene amayenda nʼkumamutsiranso dothi.
14 Og Kongen kom ind og alt Folket, som var med ham, som vare trætte, og de vederkvægedes der.
Mfumu ndi anthu ake onse anafika kumene amapita atatopa kwambiri. Ndipo kumeneko anapumula.
15 Men Absalom og alt Folket, Israels Mænd, kom til Jerusalem, og Akitofel med ham.
Pa nthawi imeneyi Abisalomu ndi Aisraeli ena onse anabwera ku Yerusalemu, Ahitofele anali naye.
16 Og det skete, der Arkiteren Husaj, Davids Ven, kom til Absalom, da sagde Husaj til Absalom: Kongen leve! Kongen leve!
Tsono Husai Mwariki bwenzi la Davide anapita kwa Abisalomu ndipo anati kwa iye, “Ikhale ndi moyo wautali mfumu! Ikhale ndi moyo wautali mfumu!”
17 Men Absalom sagde til Husaj: Er dette din Miskundhed mod din Ven? hvorfor drog du ikke med din Ven?
Abisalomu anafunsa Husai, “Kodi ichi ndi chikondi chimene ukumuonetsa bwenzi lako? Nʼchifukwa chiyani sunapite ndi bwenzi lako?”
18 Og Husaj sagde til Absalom: Ikke saa; thi hvem Herren og dette Folk og alle Israels Mænd udvælger, hans vil jeg være, og hos ham vil jeg blive.
Husai anati kwa Abisalomu, “Ayi, ndidzakhala wake wa amene Yehova wamusankha, wosankhidwa ndi anthu awa ndi anthu onse a Israeli, ndipo ndidzakhala wake nthawi zonse.
19 Og for det andet, hvem skulde jeg tjene? skulde jeg ikke tjene for hans Søns Ansigt? ligesom jeg tjente for din Faders Ansigt, saa vil jeg være for dit Ansigt.
Kodi ndidzatumikiranso yani? Kodi sinditumikira mwana wa mfumu? Monga momwe ndinatumikira abambo anu, kotero ndidzatumikiranso inu.”
20 Da sagde Absalom til Akitofel: Giver I nu Raad, hvad vi skulle gøre.
Abisalomu anati kwa Ahitofele, “Tiwuze malangizo ako. Kodi tichite chiyani?”
21 Og Akitofel sagde til Absalom: Gak ind til din Faders Medhustruer, som han lod blive tilbage til at bevare Huset, saa skal al Israel høre, at du er bleven forhadt hos din Fader, og alle deres Hænder, som ere hos dig, skulle blive stærke.
Ahitofele anayankha kuti, “Mugone ndi azikazi a abambo anu amene awasiya kuti asamalire nyumba yaufumu. Aisraeli onse adzamva kuti mwachitira abambo anu chinthu chonyansa kotheratu ndipo anthu onse amene ali ndi iwe adzalimbikitsidwa.”
22 Da opsloge de et Telt paa Taget for Absalom, og Absalom gik ind til sin Faders Medhustruer for al Israels Øjne.
Choncho anamangira tenti Abisalomu pa denga la nyumba ndipo iye anagona ndi azikazi a abambo ake Aisraeli onse akuona.
23 Men Akitofels Raad, som han raadede i de Dage, var, ligesom man havde adspurgt Gud om en Ting; saa var alt Akitofels Raad baade for David og for Absalom.
Tsono masiku amenewo malangizo amene Ahitofele amapereka anali ngati mawu ochokera kwa Mulungu. Umu ndi mmene Davide ndi Abisalomu amalandirira malangizo onse a Ahitofele.

< 2 Samuel 16 >