< 2 Samuel 14 >
1 Og Joab, Zerujas Søn, vidste, at Kongens Hjerte var til Absalom.
Yowabu mwana wa Zeruya anadziwa kuti maganizo a mfumu ali pa Abisalomu.
2 Og Joab sendte hen til Thekoa og lod hente en viis Kvinde derfra, og han sagde til hende: Kære, anstil dig sørgende, og før dig i Sørgeklæderne og salv dig ikke med Olie, men vær som en Kvinde, der mange Dage har sørget over en død.
Kotero Yowabu anatuma munthu wina kupita ku Tekowa ndi kukatengako mkazi wanzeru. Yowabu anati kwa mkaziyo, “Ukhale ngati namfedwa. Uvale zovala zaumasiye ndipo usadzole mafuta ena aliwonse. Ukhale ngati mkazi amene wakhala akulira masiku ambiri.
3 Og du skal gaa ind til Kongen og tale til ham paa denne Maade; og Joab lagde Ordene i hendes Mund.
Kenaka upite kwa mfumu ndipo ukayankhule mawu awa.” Ndipo Yowabu anamuwuza mawu oti akanene.
4 Og den thekoitiske Kvinde talede til Kongen og faldt ned til Jorden paa sit Ansigt og nedbøjede sig, og hun sagde: Frels, o Konge!
Mkazi wochokera ku Tekowa uja atapita kwa mfumu anadzigwetsa pansi, napereka ulemu kwa mfumu nati, “Thandizeni mfumu!”
5 Og Kongen sagde til hende: Hvad fattes dig? og hun sagde: Sandelig, jeg er en Enke, og min Mand er død.
Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi chikukusautsa iwe nʼchiyani?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mkazi wamasiye, mwamuna wanga anamwalira.
6 Og din Tjenerinde havde to Sønner, og de kom i Trætte paa Marken, og der var ingen, som kunde tale dem til Rette; da slog den ene den anden og dræbte ham.
Ine wantchito wanu ndinali ndi ana aamuna awiri. Iwo anayamba kumenyana mʼmunda, ndipo panalibe woti awaleretse. Wina anakantha mnzakeyo mpaka kumupha.
7 Og se, den ganske Slægt staar op imod din Tjenerinde og siger: Giv os den hid, som slog sin Broder, saa ville vi dræbe ham for hans Broders Sjæl, hvem han ihjelslog, og ødelægge ogsaa Arvingen; og de ville udslukke min Glød, som er tilovers, at min Mand ikke skal beholde et Navn og nogen overbleven efter sig paa Jorden.
Tsono banja lonse landiwukira ine, wantchito wanu. Iwo akuti, ‘Utipatse mwana amene anakantha mʼbale wakeyo kuti timuphe chifukwa cha moyo wa mʼbale wake amene anaphedwayo. Ife tidzaphanso mlowamʼmalo.’ Anthuwo adzapha mwana wanga amene wanditsalira, ndipo dzina la mwamuna wanga silidzakumbukika pakuti sipadzakhalanso mwana pa banja lathu.”
8 Da sagde Kongen til Kvinden: Gak til dit Hus, og jeg vil give Befaling for dig.
Mfumu inati kwa mkaziyo, “Pitani ku nyumba kwanu ndipo ine ndidzalamula mʼmalo mwanu.”
9 Og den thekoitiske Kvinde sagde til Kongen: Min Herre Konge, Skylden derfor være paa mig og min Faders Hus! men Kongen og hans Trone være skyldfri!
Koma mkazi wochokera ku Tekowayo anati kwa mfumu, “Mbuye wanga mfumu, kulakwa kukhale pa ine ndi banja la abambo anga ndipo mfumu ndi mpando wanu waufumu mukhale osalakwa.”
10 Og Kongen sagde: Den, som taler imod dig, den skal du føre til mig, saa skal han ikke ydermere røre ved dig.
Mfumu inayankha kuti, “Ngati wina aliyense anene kanthu kwa iwe, umubweretse kwa ine, ndipo sadzakuvutitsanso.”
11 Og hun sagde: O Konge! Kære, kom Herren din Gud i Hu, at Blodhævnere skulle ikke blive mange til Fordærvelse, og at de ikke lægge min Søn øde; og han sagde: Saa vist som Herren lever, der skal ikke falde et Haar af din Søn til Jorden.
Mkaziyo anati, “Mfumu ipemphe kwa Yehova Mulungu wake kuti aletse wobwezera imfa asaphenso wina kuti mwana wanga asawonongedwe.” Mfumu inati, “Pali Yehova wamoyo ngakhale tsitsi limodzi la pamutu pa mwana wako silidzathotholedwa.”
12 Da sagde Kvinden: Kære, lad din Tjenerinde tale til min Herre Konge et Ord; og han sagde: Tal.
Kenaka mkaziyo anati, “Lolani kuti wantchito wanu ayankhule mawu kwa inu mbuye wanga mfumu.” Iye anayankha kuti, “Yankhula.”
13 Og Kvinden sagde: Men hvorfor har du tænkt saadant imod Guds Folk? thi idet Kongen har talt saadanne Ord, bliver han selv ligesom skyldig, idet Kongen ikke lader sin udstødte komme tilbage.
Mkaziyo anati, “Nʼchiyani tsono chimene mwaganiza kuchitira zimenezi anthu a Mulungu? Pamene mfumu yanena izi, kodi sikudzitsutsa yokha, pakuti mfumu sinayitanitse mwana amene anamupirikitsa?
14 Thi vi dø visselig og ere som Vandet, der bortflyder paa Jorden, hvilket ikke samles; men Gud tager ikke Livet bort, men tænker over, at den udstødte ikke altid skal være udstødt fra ham.
Koma poti madzi akatayika sawoleka, ndiye tonsefe tiyenera kufa ndithu. Koma Mulungu safuna kuti moyo wa munthu utayike kotero anakonza njira yakuti wopirikitsidwayo asakhale wotayikiratu.
15 Saa er jeg nu kommen til at tale dette Ord til min Herre Kongen, fordi Folket gør mig bange; derfor sagde din Tjenerinde: Kære, jeg vil tale til Kongen, maaske gør Kongen efter sin Tjenerindes Ord.
“Tsopano ine ndabwera kudzanena izi kwa inu mbuye wanga mfumu chifukwa anthu andichititsa mantha. Mdzakazi wanu anaganiza kuti, ‘Ndikayankhula kwa mfumu, mwina adzachita zimene mdzakazi wake adzamupempha.
16 Thi Kongen vil høre det for at redde sin Tjenerinde af den Mands Haand, som vil udslette baade mig og min Søn fra Guds Arv.
Mwina mfumu idzavomereza kupulumutsa mdzakazi wake mʼdzanja la munthu amene akufuna kupha ine pamodzi ndi mwana wanga kutichotsa pa cholowa chimene Mulungu anatipatsa.’
17 Og din Tjenerinde sagde: Min Herre Kongens Ord skal dog være mig til Trøst; thi som en Guds Engel er, saa er min Herre Kongen til at høre det gode og det onde, og Herren din Gud skal være med dig.
“Ndipo tsopano mtumiki wanu akuti, ‘Lolani mawu a mbuye wanga mfumu abweretse mpumulo kwa ine, pakuti mbuye wanga mfumu ali ngati mngelo wa Mulungu pozindikira chabwino ndi choyipa. Yehova Mulungu wanu akhale nanu.’”
18 Og Kongen svarede og sagde til Kvinden: Dølg dog ikke for mig det Ord, som jeg vil spørge dig om; og Kvinden sagde: Min Herre Kongen tale dog.
Kenaka mfumu inati kwa mkaziyo, “Usandibisire chilichonse pondiyankha chimene ndidzakufunsa.” Mkaziyo anati, “Mbuye wanga mfumu yankhulani.”
19 Og Kongen sagde: Er ikke Joabs Haand med dig i alt dette? og Kvinden svarede og sagde: Saa vist som din Sjæl lever, min Herre Konge, der er ingen anden hverken til højre eller venstre af alle dem, som min Herre Kongen har talt om; thi din Tjener Joab bød mig det, og han lagde alle disse Ord i din Tjenerindes Mund.
Mfumu inafunsa kuti, “Kodi zimenezi sukuchita motsogozedwa ndi Yowabu?” Mkaziyo anayankha kuti, “Pali inu wamoyo, mbuye wanga mfumu, palibe munthu angakhotere kumanja kapena kumanzere pa chilichonse chimene mbuye wanga mfumu mwanena. Inde, ndi mtumiki wanu Yowabu amene wandilangiza ine kuchita zimenezi ndipo ndi amene anandipatsa mawu onsewa woti ine mtumiki wanu ndiyankhule.
20 At jeg skulde vende Sagen saaledes, den Gerning har din Tjener Joab gjort; men min Herre er viis efter en Guds Engels Visdom til at vide alle Ting, som ere paa Jorden.
Mtumiki wanu Yowabu anachita zimenezi kuti asinthe mmene zinthu zilili lero. Mbuye wanga muli ndi nzeru ngati za mngelo wa Mulungu. Mumadziwa zonse zimene zikuchitika mʼdziko.”
21 Da sagde Kongen til Joab: Kære, se, du har gjort denne Gerning; saa gak, lad den unge Mand Absalom komme tilbage.
Mfumu inati kwa Yowabu, “Chabwino, ine ndichita zimenezi. Pita kamutenge Abisalomuyo.”
22 Da faldt Joab paa sit Ansigt til Jorden og nedbøjede sig og velsignede Kongen, og Joab sagde: I Dag fornemmer din Tjener, at jeg har fundet Naade for dine Øjne, min Herre Konge, idet Kongen gør efter sine Tjeneres Ord.
Yowabu anawerama pansi kupereka ulemu kwa mfumu. Yowabuyo anati, “Lero mtumiki wanu wadziwa kuti wapeza chifundo pamaso panu, mbuye wanga mfumu, chifukwa mwavomera pempho lakeli.”
23 Saa gjorde Joab sig rede og drog til Gesur og førte Absalom til Jerusalem.
Choncho Yowabu anapita ku Gesuri ndipo anamubweretsa Abisalomu ku Yerusalemu.
24 Men Kongen sagde: Lad ham vende tilbage til sit Hus og ikke se mit Ansigt. Saa vendte Absalom tilbage til sit Hus og saa ikke Kongens Ansigt.
Koma mfumu inati, “Iye apite ku nyumba yake; asaone nkhope yanga.” Kotero Abisalomu anapita ku nyumba yake ndipo sanakumane ndi mfumu.
25 Og der var ikke saa dejlig en Mand i al Israel som Absalom, saa at han blev saare rost, der var ingen Lyde paa ham fra hans Fodsaale og indtil hans Hovedisse.
Mʼdziko lonse la Israeli munalibe munthu amene anayamikidwa chifukwa cha maonekedwe ake wokongola ngati Abisalomu. Kuyambira kumutu mpaka ku mapazi ake, analibe chilema.
26 Og naar han ragede sit Hoved (og det skete, naar hvert Aar var til Ende, at han ragede det, thi det var ham for svart, at han maatte rage det), da vejede hans Hovedhaar to Hundrede Sekel efter Kongens Vægt.
Nthawi ina iliyonse akamameta tsitsi lake, ankameta pamene layamba kumulemera. Akatero amaliyeza, ndipo limalemera makilogalamu awiri pa sikelo yaufumu.
27 Og Absalom bleve fødte tre Sønner og en Datter, og hendes Navn var Thamar, hun var en dejlig Kvinde af Udseende.
Abisalomu anali ndi ana aamuna atatu ndi wamkazi mmodzi. Mwana wamkazi dzina lake linali Tamara, ndipo anali mkazi wokongola kwambiri.
28 Saa blev Absalom to Aar i Jerusalem og saa ikke Kongens Ansigt.
Abisalomu anakhala zaka ziwiri mu Yerusalemu osaonekera kwa mfumu.
29 Og Absalom sendte Bud til Joab for at sende ham til Kongen; men han vilde ikke komme til ham, og han sendte endnu anden Gang, dog vilde han ikke komme.
Kenaka Abisalomu anatumiza mawu kwa Yowabu, kumutuma kuti apite kwa mfumu, koma Yowabu anakana kubwera. Kotero anatumizanso mawu kachiwiri, koma Yowabu anakananso.
30 Da sagde han til sine Tjenere: Ser det Stykke af Joabs Ager ved Siden af min, som han har Byg paa, gaar og sætter Ild derpaa; da satte Absaloms Tjenere Ild paa det Stykke.
Tsono Abisalomu anati kwa antchito ake, “Taonani, munda wa Yowabu uli pafupi ndi wanga ndipo muli barele mʼmenemo. Pitani mukawutenthe mundawo.” Ndipo antchito a Abisalomu anawutentha mundawo.
31 Da stod Joab op og kom til Absalom i Huset og sagde til ham: Hvorfor satte dine Tjenere Ild paa det Stykke, som hører mig til?
Ndipo Yowabu anapita ku nyumba ya Abisalomu ndipo anati kwa iye, “Nʼchifukwa chiyani antchito ako atentha munda wanga?”
32 Og Absalom sagde til Joab: Se, jeg sendte Bud til dig og lod sige: Kom hid, at jeg kan sende dig til Kongen og lade sige: Hvorfor er jeg kommen fra Gesur? det var mig godt, at jeg var der endnu; saa lad mig nu se Kongens Ansigt, men er der en Misgerning hos mig, da slaa han mig ihjel.
Abisalomu anati kwa Yowabu, “Taona, ine ndinatumiza mawu kwa iwe ndipo ndinati, ‘Bwera kuno kuti ndikutume kwa mfumu kukafunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ine ndinabwera kuchokera ku Gesuri? Zikanakhala bwino ndikanakhala komweko!’ Tsono pano ndikufuna kuonana ndi mfumu, ndipo ngati ndili olakwa mfumuyo indiphe.’”
33 Og Joab gik ind til Kongen og gav ham det til Kende, og han kaldte ad Absalom, og han kom ind til Kongen, og han nedbøjede sig paa sit Ansigt til Jorden for Kongens Ansigt, og Kongen kyssede Absalom.
Choncho Yowabu anapita kwa mfumu ndipo anayiwuza zimenezi. Ndipo mfumu inamuyitanitsa Abisalomu, ndipo analowa nawerama kugunditsa nkhope yake pansi pamaso pa mfumu. Tsono mfumu inapsompsona Abisalomu.