< Anden Kongebog 21 >

1 Manasse var tolv Aar gammel, der han blev Konge, og regerede fem og halvtredsindstyve Aar i Jerusalem, og hans Moders Navn var Hefziba.
Manase anakhala mfumu ali ndi zaka khumi ndi ziwiri ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 55. Amayi ake anali Hefiziba.
2 Og han gjorde det, som var ondt for Herrens Øjne, efter de Hedningers Vederstyggeligheder, hvilke Herren havde fordrevet fra Israels Børns Ansigt.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, potsatira mchitidwe wonyansa wa mitundu imene Yehova anayipirikitsa pofika Aisraeli.
3 Og han byggede igen de Høje, som Ezekias, hans Fader, havde ødelagt, og oprejste Altre for Baal og gjorde et Astartebillede, ligesom Akab, Israels Konge, havde gjort, og tilbad al Himmelens Hær og tjente dem.
Iyetu anamanganso malo opembedzera mafano amene Hezekiya abambo ake anawawononga. Anamangira Baala maguwa a nsembe ndi mtengo wa fano la Asera monga anachitira Ahabu mfumu ya Israeli ndipo ankapembedza zolengedwa zonse zamlengalenga.
4 Og han byggede Altre i Herrens Hus, om hvilket Herren havde sagt: Jeg vil sætte mit Navn i Jerusalem.
Anamanga maguwa ansembewa mʼNyumba ya Yehova, mʼmene Yehova ananena kuti, “Mu Yerusalemu ndidzayikamo Dzina langa.”
5 Og han byggede Altre til Himmelens hele Hær i begge Forgaardene til Herrens Hus.
Mʼmabwalo onse awiri a Nyumba ya Yehova, Manase anamangamo maguwa opembedzerapo zinthu zamlengalenga.
6 Og han lod sin Søn gaa igennem Ilden og var en Dagvælger og agtede paa Fugleskrig og beskikkede Spaamænd og Tegnsudlæggere; han gjorde meget ondt for Herrens Øjne til at opirre ham.
Iye anapsereza mwana wake pa moto ngati nsembe, ankachita za matsenga, ankawombeza mawula, ankapita kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ndiponso ankapembedza mizimu. Iyeyo anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova ndipo anakwiyitsa Yehovayo.
7 Og han satte det Astartebillede, som han havde gjort, i det Hus, om hvilket Herren havde sagt til David og til hans Søn Salomo: I dette Hus og i Jerusalem, som jeg udvalgte af alle Israels Stammer, vil jeg sætte mit Navn evindeligt;
Iye anatenga fano losema la Asera limene analipanga ndi kuliyika mʼNyumba ya Yehova, Nyumba imene Yehova ananena kwa Davide ndi mwana wake Solomoni kuti, “Mʼnyumba iyi ndi mu Yerusalemu ndiwo malo amene ndasankha pakati pa mafuko onse a Aisraeli kuyikamo Dzina langa kwamuyaya.
8 og jeg vil ikke ydermere lade Israels Fødder vandre bort fra Landet, som jeg gav deres Fædre, naar de kun holde ved at gøre efter alt det, som jeg har budet dem, og efter hele Loven, som Mose, min Tjener, bød dem.
Sindidzalola kuti Aisraeli achotsedwe mʼdziko lawo limene ndinapatsa makolo awo ngati iwowo adzasamala kuchita zinthu zonse zimene ndinawalamula ndi kusunga malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anawapatsa.”
9 Men de adløde ikke; og Manasse forførte dem til at handle værre end Hedningerne, hvilke Herren havde ødelagt for Israels Børns Ansigt.
Koma anthu sanamvere. Manase anawasocheretsa, kotero kuti anachita zoyipa zambiri kupambana anthu a mitundu ina amene Yehova anawawononga pamene Aisraeli ankafika.
10 Da talte Herren ved sine Tjenere, Profeterne, og sagde:
Yehova anayankhula kudzera mwa atumiki ake, aneneri kuti,
11 Fordi Manasse, Judas Konge, har gjort disse Vederstyggeligheder, saa han har gjort noget værre end alt det, som Amoriterne gjorde, som vare for ham, og fordi han kom ogsaa Juda til at synde med sine stygge Afguder:
“Manase mfumu ya Yuda wachita machimo onyansawa ndipo wachita zoyipa kupambana Aamori amene analipo kale iye asanabadwe ndi kuchimwitsa anthu a ku Yuda ndi mafano ake.
12 Derfor saa sagde Herren Israels Gud: Se, jeg vil føre Ulykke over Jerusalem og Juda, at hvo det hører, for ham skulle begge hans Øren klinge.
Choncho Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Taonani, ndikubweretsa pa Yerusalemu ndi Yuda mavuto akuti aliyense amene adzawamve adzathedwa nzeru.
13 Og jeg vil udstrække Samarias Maalesnor over Jerusalem, samt veje den med Akabs Hus's Vægt, og jeg vil afviske Jerusalem, som den, der afvisker et Fad, afvisker og vender det helt om.
Ndidzalanga Yerusalemu ndi Yuda pogwiritsa ntchito muyeso umene ndinalangira Samariya ndi Ahabu pamodzi ndi nyumba yake. Ndidzayeretsa Yerusalemu monga mmene munthu amachitira popukuta mbale ndipo atayipukuta amayivundikira pansi.
14 Og jeg vil bortstøde det overblevne af min Arv og give dem i deres Fjenders Haand, saa at de skulle blive til Bytte og til Rov for alle deres Fjender,
Ndidzawataya anthu otsala amene ndi cholowa changa ndipo ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo. Adzachotsedwa ndipo adaniwo adzawalanda zinthu zonse
15 fordi de gjorde det, som er ondt for mine Øjne, og opirrede mig fra den Dag, da deres Fædre droge ud af Ægypten, og indtil denne Dag.
chifukwa anachita zoyipa pamaso panga ndipo akhala akundikwiyitsa kuchokera tsiku limene makolo awo anatuluka mu Igupto mpaka lero lino.’”
16 Tilmed udøste Manasse ogsaa saare meget uskyldigt Blod, indtil han fyldte Jerusalem fra den ene Ende til den anden; foruden hans Synd, med hvilken han kom Juda til at synde, til at gøre det onde for Herrens Øjne.
Kuwonjezera apo, Manase anakhetsa kwambiri magazi a anthu osalakwa mpaka magaziwo kuyenderera mu Yerusalemu kuyambira mbali ina mpaka mbali ina, kuphatikiza pa kuchimwitsa Yuda, kotero kuti anthu anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
17 Men det øvrige af Manasses Handeler og alt det, han har gjort, og hans Synd, som han syndede, ere de Ting ikke skrevne i Judas Kongers Krønikers Bog?
Ntchito zina za Manase ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
18 Og Manasse laa med sine Fædre og blev begraven i sit Hus's Have, som var i Ussas Have, og Amon, hans Søn, blev Konge i hans Sted.
Manase anagona ndi makolo ake ndipo anayikidwa mʼmanda mʼmunda wa Uza, ku nyumba yaufumu. Ndipo Amoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
19 Amon var to og tyve Aar gammel, der han blev Konge, og regerede to Aar i Jerusalem; og hans Moders Navn var Mesullemeth, Haruz's Datter fra Jotba.
Amoni anakhala mfumu ali ndi zaka 22 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka ziwiri. Amayi ake anali Mesulemeti mwana wa Haruzi, wochokera ku Yotiba.
20 Og han gjorde det onde for Herrens Øjne, ligesom Manasse, Hans Fader, havde gjort.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira Manase abambo ake.
21 Og han vandrede i al den Vej, som hans Fader havde vandret, og tjente de stygge Afguder, som hans Fader havde tjent, og tilbad dem.
Anatsatira makhalidwe onse a abambo ake. Ankapembedza mafano amene abambo akewo ankawapembedza ndipo ankawagwadira.
22 Og han forlod Herren, sine Fædres Gud, og vandrede ikke i Herrens Vej.
Iyeyo anasiya Yehova Mulungu wa makolo ake ndipo sanayende mʼnjira ya Yehova.
23 Og Amons Tjenere forbandt sig imod ham, og de dræbte Kongen i hans Hus.
Nduna za Amoni zinamuchita chiwembu ndipo zinamupha mʼnyumba yake.
24 Og Folket i Landet ihjelslog alle dem, som havde forbundet sig imod Kong Amon; og Folket i Landet gjorde Josias, hans Søn, til Konge i hans Sted.
Koma anthu a mʼdzikomo anapha onse amene anachitira chiwembu Mfumu Amoni, nayika Yosiya mwana wake kukhala mfumu mʼmalo mwake.
25 Men det øvrige af Amons Handeler, hvad han har gjort, ere de Ting ikke skrevne i Judas Kongers Krønikers Bog?
Ntchito zina za Amoni ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
26 Og man begrov ham i hans Grav, udi Ussas Have, og Josias, hans Søn, blev Konge i hans Sted.
Iye anayikidwa mʼmanda ake mʼmunda wa Uza. Ndipo Yosiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< Anden Kongebog 21 >