< Anden Krønikebog 31 >
1 Og der alt dette var fuldendt, drog al Israel, som var til Stede, ud i Judas Stæder, og de sønderbrøde Støtterne og huggede Astartebillederne itu og nedbrøde Højene og Altrene i hele Juda og Benjamin og i Efraim og i Manasse, indtil de havde fuldendt det; siden vendte alle Israels Børn tilbage, hver til sin Ejendom, til deres Stæder.
Zonse zitatha, Aisraeli onse amene anali kumeneko anapita ku mizinda ya ku Yuda, nakaphwanya miyala yachipembedzo ndi kudula mitengo ya mafano a Asera. Iwo anakawononga malo achipembedzo ndi maguwa ansembe amene anali mʼdziko lonse la Yuda, Benjamini, Efereimu ndi Manase. Atawononga zonsezi, Aisraeli anabwerera ku mizinda yawo ndi ku malo awo.
2 Og Ezekias beskikkede Præsternes og Leviternes Skifter, efter deres Skifter, enhver efter hans Tjenestes Beskaffenhed, saavel for Præsterne som for Leviterne, til at bringe Brændoffer og Takofre, at de skulde tjene og takke og love i Herrens Lejres Porte;
Hezekiya anakhazikitsa magulu a ansembe ndi Alevi, gulu lililonse monga mwa ntchito zawo ngati ansembe kapena Alevi, kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, kutumikira, kuyamikira ndi kuyimba matamando pa zipata za ku malo okhala Yehova.
3 og den Del, Kongen gav af sit Gods, var til Brændofre, til Brændofre om Morgenen og om Aftenen og til Brændofre om Sabbaterne og ved Nymaanederne og Højtiderne, som skrevet er i Herrens Lov.
Kuchokera pa chuma chake, mfumu inapereka nsembe zopsereza za mmawa ndi madzulo ndiponso nsembe zopsereza za pa Chikondwerero cha Masabata, Chikondwerero cha Mwezi Watsopano ndipo inakhazikitsa zikondwerero monga zinalembedwera mʼmalamulo a Yehova.
4 Og han sagde til Folket, til Indbyggerne i Jerusalem, at de skulde give Præsterne og Leviterne deres Del, paa det de kunde holde fast ved Herrens Lov.
Iyo inalamula anthu amene amakhala mu Yerusalemu kupereka gawo lawo kwa ansembe ndi Alevi kuti iwowo adzipereke ku malamulo a Yehova.
5 Og der det Ord kom ud, gave Israels Børn meget af Førstegrøden af Korn, Most og Olie og Honning og af alt, hvad der kom ind af Marken, og de bragte Tiende af alt i Mangfoldighed.
Lamuloli atangolilengeza, Aisraeli anapereka mowolowamanja zipatso zoyamba kucha za tirigu, vinyo watsopano, mafuta ndi uchi ndi zonse zomwe nthaka yawo inabereka. Anabweretsa zochuluka kwambiri, chakhumi cha chilichonse.
6 Og Israels og Judas Børn, som boede i Judas Stæder, de bragte ogsaa Tiende af stort Kvæg og smaat Kvæg og Tiende af de hellige Ting, som vare helligede Herren deres Gud; de bragte dette og lagde Hob ved Hob.
Aisraeli ndi Ayuda amene amakhala mʼmizinda ya Yuda anabweretsanso chakhumi cha ngʼombe zawo ndi nkhosa ndi chakhumi cha zinthu zoyera zoperekedwa kwa Yehova Mulungu wawo, ndipo anaziyika mʼmilumilu.
7 I den tredje Maaned begyndte de at lægge Grund til Hobene, og i den syvende Maaned bleve de færdige med dem.
Anayamba kuchita izi mwezi wachitatu ndipo anatsiriza mwezi wachisanu ndi chiwiri.
8 Og der Ezekias og de Øverste kom og saa Hobene, da velsignede de Herren og hans Folk Israel.
Hezekiya ndi akuluakulu ake atabwera ndi kuona miluyo, anatamanda Yehova ndi kudalitsa anthu ake, Aisraeli.
9 Og Ezekias spurgte Præsterne og Leviterne angaaende Hobene.
Hezekiya anafunsa ansembe ndi Alevi za miluyi;
10 Og Asaria, den Ypperstepræst af Zadoks Hus, sagde til ham: Siden man begyndte med at bringe Gaven til Herrens Hus, have vi ædt og ere blevne mætte, og vi have levnet i Mangfoldighed; thi Herren har velsignet sit Folk, saa at denne Hob er bleven tilovers.
ndipo Azariya, mkulu wa ansembe, ochokera ku banja la Zadoki anayankha kuti, “Kuyambira pamene anthu anayamba kubweretsa zopereka zawo ku Nyumba ya Yehova ife takhala ndi zokwanira kudya ndi zina zambiri zosunga, chifukwa Yehova wadalitsa anthu ake, ndipo mulu umenewu ndiye zotsala.”
11 Da sagde Ezekias, at man skulde indrette Kamre i Herrens Hus, og de indrettede dem.
Hezekiya analamula kuti akonze zipinda zosungiramo za mʼNyumba ya Yehova, ndipo izi zinachitika.
12 Og de bragte Gaven og Tienden og de helligede Ting trolig derind; og Kanania, Leviten, var den første Opsynsmand over dem, og Simei, hans Broder, var den anden.
Ndipo iwo mokhulupirika anabweretsa zopereka, chakhumi ndi mphatso zopatulika. Konaniya Mlevi ndiye amayangʼanira zinthu zimenezi ndipo mʼbale wake Simei ndiye anali wachiwiri wake.
13 Men Jehiel, Asasia og Nahath og Asahel og Jerimoth og Josabad og Eliel og Jismakia og Mabath og Benaja vare Tilsynsmænd under Kanania og Simei, hans Broder, efter Befaling af Kong Ezekias og Asaria, Guds Hus's Fyrste.
Yehieli, Azaziya, Nahati, Asaheli, Yerimoti, Yozabadi, Elieli, Isimakiya, Mahati ndi Benaya anali oyangʼanira motsogozedwa ndi Konaniya ndi Simei, mʼbale wake. Iwowa anasankhidwa ndi mfumu Hezekiya ndi Azariya mkulu woyangʼanira Nyumba ya Mulungu.
14 Og Kore, Jimnas Søn, Leviten, Portneren imod Østen, var sat over de frivillige Gaver til Gud for at uddele Gaven, som bragtes Herren, tillige med de højhellige Ting.
Kore mwana wa Imuna Mlevi, mlonda wa Chipata Chakummawa, amayangʼanira zopereka zaufulu kwa Mulungu, ankagawa zopereka za kwa Yehova ndiponso mphatso zopatulika.
15 Og næst ham var Eden og Minjamin og Jesua og Semaja, Amaria og Sekanja ansatte i Præsternes Stæder paa Tro og Love for at uddele til deres Brødre i Skifterne, til den mindste som til den største,
Edeni, Miniyamini, Yesuwa, Semaya, Amariya, Sekaniya amamuthandiza mokhulupirika mʼmizinda yonse a ansembe kugawira kwa ansembe anzawo monga mwa magulu awo, aakulu ndi aangʼono omwe.
16 undtagen til dem, som vare opførte i Slægtregisteret over Mandkønnet, fra tre Aar gamle og derover, nemlig alle dem, som gik i Herrens Hus til den daglige Gerning, til deres Tjeneste, i hvad de havde at varetage, efter deres Skifter.
Kuwonjezera apa, amagawira ana aamuna a zaka zitatu kapena kupitirira amene mayina awo anali mʼmbiri ya mibado yawo, amene adzalowe mʼNyumba ya Yehova kugwira ntchito za tsiku ndi tsiku za magulu awo, molingana ndi udindo ndi magulu awo.
17 Og Præsterne, som vare opførte i Slægtregisteret efter deres Fædrenehuse, og Leviterne fra tyve Aar gamle og derover, vare paa deres Vagter, i deres Skifter.
Ndipo anazigawa kwa ansembe amene analembetsa mayina awo mwa mbiri ya mabanja awo, chimodzimodzinso Alevi amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirira molingana ndi udindo wawo ndi magulu awo.
18 Og i Slægtregisteret vare opførte alle deres smaa Børn, deres Hustruer og deres Sønner og deres Døtre, den hele Forsamlings; thi de skulde hellige sig til det, som var dem betroet, i Hellighed.
Iwo anaphatikizanso ana onse aangʼono, akazi ndiponso ana aamuna ndi ana aakazi a gulu lonse amene analembedwa mʼmbiri ya mibado yawo iyi, pakuti anakhulupirika pa kudzipatula okha.
19 Og for Arons Børn, Præsterne, som boede paa Markerne til deres Stæder, til hver Stad især, var der Mænd, som vare nævnede ved Navn, som skulde uddele til alt Mandkøn iblandt Præsterne og til alle dem, som vare opførte i Slægtregisteret over Leviterne.
Kunena za ansembe, zidzukulu za Aaroni, amene amakhala mʼminda yozungulira mizinda yawo kapena mzinda wina uliwonse, anthu anasankhidwa mowatchula mayina kuti azipereka magawo kwa munthu wamwamuna aliyense pakati pawo ndiponso kwa onse amene analembedwa mʼmbiri ya mibado ya Alevi.
20 Og paa denne Maade gjorde Ezekias i hele Juda; og han gjorde det, som var godt og ret og sandt for Herrens hans Guds Ansigt.
Izi ndi zimene Hezekiya anachita mu Yuda monse, kuchita zabwino, zolungama ndi zokhulupirika pamaso pa Yehova Mulungu wake.
21 Og i al den Gerning, som han begyndte i Guds Hus's Tjeneste og i Loven og i Budet, idet han søgte sin Gud, handlede han af sit ganske Hjerte og havde Lykke.
Pa chilichonse chimene anachita pa ntchito ya Nyumba ya Mulungu ndi pa kumvera malangizo ndi malamulo, iye anafunafuna Mulungu wake ndipo anagwira ntchito ndi mtima wake wonse. Ndipo zinthu zimamuyendera bwino.