< Anden Krønikebog 18 >

1 Og Josafat havde Rigdom og Ære i Mangfoldighed, og han gjorde Svogerskab med Akab.
Tsono Yehosafati anali ndi chuma chambiri ndi ulemu, ndipo iye anachita mgwirizano wa ukwati ndi Ahabu.
2 Og der nogle Aar vare til Ende, drog han ned til Akab til Samaria, og Akab lod slagte smaat Kvæg og stort Kvæg i Mangfoldighed til ham og til det Folk, som var med ham, og han tilskyndede ham til at drage op til Ramoth i Gilead.
Patapita zaka zina, iye anapita kukacheza kwa Ahabu mu Samariya. Ahabu anaphera iye pamodzi ndi anthu amene anali naye, nkhosa zambiri ndi ngʼombe ndipo anamuwumiriza kuti akathire nawo nkhondo Ramoti Giliyadi
3 Thi Akab, Israels Konge, sagde til Josafat, Judas Konge: Vil du drage med mig til Ramoth i Gilead? Og han sagde til ham: Jeg vil være ligesom du, og mit Folk skal være ligesom dit Folk, og vi ville være med dig i Krigen.
Ahabu mfumu ya Israeli anafunsa Yehosafati mfumu ya Yuda kuti, “Kodi mudzapita nane kukalimbana ndi Ramoti Giliyadi?” Yehosafati anayankha kuti, “Ine ndili ngati inu nomwe, ndi anthu anga ngati anthu anu. Ife tikhala nanu limodzi pa nkhondoyi.”
4 Fremdeles sagde Josafat til Israels Konge: Kære, adspørg i Dag Herrens Ord!
Koma Yehosafati anatinso kwa mfumu ya Israeli, “Choyamba mupemphe nzeru kwa Yehova.”
5 Da samlede Israels Konge Profeterne, fire Hundrede Mænd, og sagde til dem: Skulle vi drage imod Ramoth i Gilead til Krig, eller skal jeg lade være? og de sagde: Drag op, og Gud skal give den i Kongens Haand.
Tsono mfumu ya Israeli inasonkhanitsa aneneri 400 ndipo inawafunsa kuti, “Kodi tipite kukalimbana ndi Ramoti Giliyadi kapena tileke?” Iwo anayankha kuti, “Pitani, pakuti Mulungu adzawupereka mʼdzanja la mfumu.”
6 Men Josafat sagde: Er her ikke endnu en Herrens Profet, at vi kunne spørge ham ad?
Koma Yehosafati anafunsanso kuti, “Kodi kuno kulibe mneneri wina wa Yehova amene ife tingafunsireko?”
7 Og Israels Konge sagde til Josafat: Her er endnu en Mand, ved hvilken man kan adspørge Herren (men jeg hader ham, fordi han spaar ikke godt over mig, men alle sine Dage ondt), det er Mika, Jimas Søn; og Josafat sagde: Kongen sige ikke saa!
Mfumu ya Israeli inayankha Yehosafati kuti, “Alipo munthu mmodzi amene ife kudzera mwa iye titha kufunsira kwa Yehova, koma ndimadana naye chifukwa sandilosera zabwino koma zoyipa nthawi zonse. Iyeyu ndi Mikaya mwana wa Imula.” Yehosafati anayankha kuti, “Mfumu isanene motero.”
8 Da kaldte Israels Konge ad en Kammertjener og sagde: Hent hurtigt Mika, Jimlas Søn!
Choncho mfumu ya Israeli inayitana mmodzi mwa akuluakulu ake ndipo inati, “Kamutengeni Mikaya mwana wa Imula, abwere msanga.”
9 Og Israels Konge og Josafat, Judas Konge, sade hver paa sin Trone, iførte Kongedragt, og de sade paa en fri Plads foran Indgangen til Samarias Port; og alle Profeterne spaaede for deres Ansigt.
Mfumu ya Israeli ndi Yehosafati mfumu ya Yuda, atavala mikanjo yawo yaufumu anali atakhala pa mipando yawo yaufumu pabwalo lopunthira tirigu pa khomo la chipata cha Samariya, pamodzi ndi aneneri onse akunenera pamaso pawo.
10 Og Zedekias, Kna'anas Søn, havde gjort sig Jernhorn og sagde: Saa sagde Herren: Med disse skal du stange Syrerne, indtil de aldeles udryddes.
Tsono Zedekiya mwana wa Kenaana anapanga nyanga zachitsulo ndipo analengeza kuti, “Yehova akuti, ‘Ndi nyanga izi udzagunda Aaramu mpaka atawonongedwa!’”
11 Og alle Profeterne spaaede saaledes og sagde: Drag op til Ramoth i Gilead og vær lykkelig, og Herren skal give den i Kongens Haand.
Aneneri ena onse amanenera chimodzimodzi kuti, “Kathireni nkhondo Ramoti Giliyadi ndipo kapambaneni, pakuti Mulungu adzamupereka mʼdzanja la mfumu.”
12 Og Budet, som var gaaet bort for at kalde Mika, talte til ham, sigende: Se, Profeternes Ord ere som af een Mund gunstige for Kongen; kære, lad dit Ord og være som Ordet af een af dem, og tal gunstigt!
Wauthenga amene anapita kukayitana Mikaya anati kwa iye, “Taonani aneneri ena onse ngati munthu mmodzi akulosera za chipambano cha mfumu. Mawu anunso agwirizane ndi awo ndipo muyankhule zabwino.”
13 Da sagde Mika: Saa vist som Herren lever, det som min Gud siger, det vil jeg tale.
Koma Mikaya anati, “Pali Yehova wamoyo, ine ndidzanena zimene Mulungu wanga andiwuze.”
14 Og han kom til Kongen, og Kongen sagde til ham: Mika, skulle vi drage imod Ramoth i Gilead til Krig, eller skal jeg lade være? Og han sagde: Drager op og værer lykkelige, og de skulle gives i eders Haand.
Iye atafika mfumu inamufunsa kuti, “Mikaya, kodi tipite ku nkhondo kukalimbana ndi Ramoti Giliyadi kapena tileke?” Iye anayankha kuti, “Kathireni nkhondo ndipo kapambaneni, pakuti mzindawo udzaperekedwa mʼdzanja lanu.”
15 Og Kongen sagde til ham: Hvor mange Gange skal jeg besværge dig, at du intet siger mig uden Sandheden i Herrens Navn?
Mfumu inati kwa iye, “Kodi ndikuwuze kangati kuti ulumbire kuti usandiwuze chilichonse koma zoonadi mʼdzina la Yehova?”
16 Da sagde han: Jeg saa al Israel adspredt paa Bjergene som Faar, der ingen Hyrde have; og Herren sagde: Disse have ingen Herre, lad dem vende tilbage, hver til sit Hus med Fred.
Ndipo Mikaya anayankha kuti, “Ine ndinaona Aisraeli atabalalika mʼmapiri monga nkhosa zopanda mʼbusa, ndipo Yehova anati, ‘Anthu awa alibe mbuye wawo. Aliyense apite kwawo mu mtendere!’”
17 Da sagde Israels Konge til Josafat: Har jeg ikke sagt dig: Han spaar mig ikke godt, men ondt?
Mfumu ya Israeli inati kwa Yehosafati, “Kodi ine sindinakuwuzeni kuti sandinenera zabwino koma zoyipa zokhazokha?”
18 Og han sagde: Hører derfor Herrens Ord: Jeg saa Herren sidde paa sin Trone, og al Himmelens Hær staaende ved hans højre og ved hans venstre Side;
Mikaya anapitiriza ndi kunena kuti, “Imvani tsono mawu a Yehova: Ine ndinaona Yehova atakhala pa mpando wake waufumu ndi gulu lonse lakumwamba litayima ku dzanja lake lamanja ndi lamanzere.
19 og Herren sagde: Hvo vil overtale Akab, Israels Konge, at han skal drage op og falde ved Ramoth i Gilead? Og han sagde: Den ene sagde saa, og den anden sagde saa.
Ndipo Yehova anati, ‘Ndani amene adzamunyengerere Ahabu mfumu ya Israeli kuti akathire nkhondo Ramoti Giliyadi ndi kukafera komweko?’ “Wina ananena zina, winanso ananena zina.”
20 Da gik en Aand ud og stod for Herrens Ansigt og sagde: Jeg vil overtale ham; og Herren sagde til ham: Hvormed?
Pomaliza mzimu wina unatuluka ndi kuyima pamaso pa Yehova ndipo unati, “Ine ndikamunyengerera!” Yehova anafunsa kuti, “Ukagwiritsa ntchito njira yanji?”
21 Og han sagde: Jeg vil gaa ud og være en løgnagtig Aand i alle hans Profeters Mund; og han sagde: Du skal overtale ham og ogsaa formaa det; gak ud og gør saaledes!
Mzimuwo unati, “Ine ndidzapita ndi kukhala mzimu wabodza mʼkamwa mwa aneneri ake onse!” Yehova anati, “‘Iwe ukamunyengadi iyeyo. Pita kachite zimenezo.’
22 Og nu se, Herren har givet en løgnagtig Aand i disse dine Profeters Mund; men Herren har talt ondt over dig.
“Choncho Yehova wayika mzimu wabodza mʼkamwa mwa aneneri anuwa. Yehova waneneratu kuti inu mukaona tsoka.”
23 Da gik Zedekias, Kna'anas Søn, frem, og slog Mika paa Kinden og sagde: Hvor er den Vej, ad hvilken Herrens Aand er gaaet bort fra mig til at tale med dig?
Ndipo Zedekiya mwana wa Kenaana anapita pafupi ndi kumenya khofi Mikaya. Zedekiya anafunsa kuti, “Kodi mzimu wochokera kwa Yehova unadzera njira iti pamene unachoka kwa ine kupita kwa iwe?”
24 Og Mika sagde: Se, du skal se det paa den Dag, naar du gaar ind fra et Kammer i et andet for at skjule dig.
Mikaya anayankha kuti, “Udzadziwa pa tsiku limene uzikalowa mʼchipinda chamʼkati kuti ukabisale.”
25 Da sagde Israels Konge: Tager Mika og fører ham tilbage til Amon, Stadens Befalingsmand, og til Joas, Kongens Søn,
Pamenepo mfumu ya Israeli inalamula kuti, “Tengani Mikaya ndipo mupite naye kwa Amoni, wolamulira mzindawo ndi kwa Yowasi mwana wa mfumu,
26 og siger: Saa siger Kongen: Sætter denne i Fængsels Hus og bespiser ham med Trængsels Brød og Trængsels Vand, indtil jeg kommer tilbage med Fred.
ndipo mukanene kuti, ‘Chimene mfumu ikunena ndi ichi; Muyike munthu uyu mʼndende ndipo musamupatse kanthu kalikonse koma buledi ndi madzi pangʼono mpaka nditabwera mwamtendere.’”
27 Og Mika sagde: Dersom du kommer tilbage med Fred, da har Herren ikke talt ved mig; og han sagde: Hører, I Folk alle sammen!
Mikaya anayankhula kuti, “Ngati inu mukabwera mwamtendere, Yehova sanayankhule kudzera mwa ine.” Ndipo anawonjeza kuti, “Anthu nonsenu, mumve zimene ndanenazi.”
28 Saa drog Israels Konge og Josafat, Judas Konge, op imod Ramoth i Gilead.
Choncho mfumu ya Israeli ndi Yehosafati mfumu ya Yuda anapita ku Ramoti Giliyadi.
29 Og Israels Konge sagde til Josafat: Jeg vil forklæde mig og gaa i Kampen, men tag du dine egne Klæder paa; og Israels Konge forklædte sig, og de gik i Kampen.
Mfumu ya Israeli inati kwa Yehosafati, “Ine ndipita ku nkhondo modzibisa koma iwe uvale mikanjo yaufumu.” Kotero mfumu ya Israeli inadzibisa ndipo inapita ku nkhondoko.
30 Men Kongen af Syrien bød de Øverste for Vognene, som han havde, og sagde: I skulle ikke stride imod liden eller stor, uden imod Israels Konge alene.
Tsono mfumu ya Aramu inalamulira olamulira magaleta kuti, “Musamenyane ndi wina aliyense, wamngʼono kapena wamkulu koma mfumu ya Israeli yokha.”
31 Og det skete, der de Øverste for Vognene saa Josafat, da sagde de: Han er Israels Konge; og de omringede ham for at stride; men Josafat raabte, og Herren hjalp ham, og Gud tilskyndede dem til at vende sig fra ham.
Olamulira magaleta ataona Yehosafati, iwo anaganiza kuti, “Mfumu ya Israeli ndi iyi.” Kotero anatembenuka kukamenyana naye koma Yehosafati anafuwula, ndipo Yehova anamuthandiza. Mulungu anawabweza mʼmbuyo,
32 Og det skete, der de Øverste for Vognene saa, at det ikke var Israels Konge, da vendte de tilbage fra ham.
pakuti olamulira magaleta ataona kuti sanali mfumu ya Israeli, anasiya kumuthamangitsa.
33 Og en Mand spændte Buen paa Lykke og Fromme og skød Israels Konge imellem Remmene og Panseret; da sagde han til Køresvenden: Vend din Haand om og før mig ud af Hæren; thi jeg er saaret.
Koma munthu wina anaponya muvi wake mwachiponyeponye ndipo analasa mfumu ya Israeli pakati polumikizira malaya achitsulo. Mfumu inawuza oyendetsa galeta kuti, “Bwerera, undichotse pa nkhondo pano. Ndavulazidwa.”
34 Og Kampen tog til paa den samme Dag, og Israels Konge blev staaende i Vognen over for Syrerne indtil Aftenen; og han døde ved den Tid, da Solen gik ned.
Nkhondo inakula kwambiri tsiku lonse, ndipo mfumu ya Israeli inakhala tsonga mʼgaleta lake kuyangʼanana ndi Aaramu mpaka madzulo. Ndipo pamene dzuwa linkalowa inamwalira.

< Anden Krønikebog 18 >