< 1 Timoteus 4 >

1 Men Aanden siger klarlig, at i kommende Tider ville nogle falde fra Troen, idet de agte paa forførende Aander og paa Dæmoners Lærdomme,
Mzimu akunena momveka bwino kuti mʼmasiku otsiriza anthu ena adzataya chikhulupiriro chawo ndi kutsatira mizimu yonyenga ndi zinthu zophunzitsidwa ndi ziwanda.
2 ved Løgnlæreres Hykleri, som ere brændemærkede i deres egen Samvittighed,
Ziphunzitso zimenezi zimachokera ku chinyengo cha anthu onama, amene chikumbumtima chawo chinamatidwa ndi chitsulo cha moto.
3 som byde, at man ikke maa gifte sig, og at man skal afholde sig fra Spiser, hvilke Gud har skabt til at nydes med Taksigelse af dem, som tro og have erkendt Sandheden.
Iwo amaletsa anthu ukwati ndi kuwalamula kuti asamadye zakudya zina, zimene Mulungu analenga kuti amene anakhulupirira ndi kudziwa choonadi, azidye moyamika.
4 Thi al Guds Skabning er god, og intet er at forkaste, naar det tages med Taksigelse;
Pakuti chilichonse chimene Mulungu analenga ndi chabwino, ndipo chilichonse chisasalidwe, akamachilandira moyamika,
5 thi det helliges ved Guds Ord og Bøn.
pakuti chimayeretsedwa ndi mawu a Mulungu ndi pemphero.
6 Naar du foreholder Brødrene dette, er du en god Kristi Jesu Tjener, idet du næres ved Troens og den gode Læres Ord, den, som du har efterfulgt;
Ngati abale uwalangiza zimenezi, udzakhala mtumiki wabwino wa Khristu Yesu, woleredwa mʼchoonadi cha chikhulupiriro ndi mʼchiphunzitso chabwino chimene wakhala ukutsata.
7 men afvis de vanhellige og kærlingagtige Fabler! Derimod øv dig selv i Gudsfrygt!
Koma upewe nkhani zachabe ndi nthano za amayi okalamba; mʼmalo mwake udziphunzitse kukhala moyo wolemekeza Mulungu.
8 Thi den legemlige Øvelse er nyttig til lidet, men Gudsfrygten er nyttig til alle Ting, idet den har Forjættelse for det Liv, som nu er, og for det, som kommer.
Pakuti kulimbitsa thupi kumapindulitsapo pangʼono, koma moyo woopa Mulungu umapindulitsa pa zonse. Umatilonjeza moyo pa moyo uno ndiponso pa moyo umene ukubwerawo.
9 Den Tale er troværdig og al Modtagelse værd.
Amenewa ndi mawu odalirika ndi oyenera kuwalandira kwathunthu.
10 Thi derfor lide vi Møje og Forhaanelser, fordi vi have sat vort Haab til den levende Gud, som er alle Menneskers Frelser, mest deres, som tro.
Nʼchifukwa chake timagwira ntchito molimbika ndi kuyesetsa, chifukwa tayika chiyembekezo chathu mwa Mulungu wamoyo, amene ndi Mpulumutsi wa anthu onse, koma makamaka wa amene amakhulupirira.
11 Paabyd og lær dette!
Lamulira ndi kuphunzitsa zinthu zimenezi.
12 Lad ingen ringeagte dig for din Ungdoms Skyld, men bliv et Forbillede for dem, som tro, i Tale, i Vandel, i Kærlighed, i Tro, i Renhed!
Usalole kuti wina akupeputse chifukwa ndiwe wachinyamata, koma khala chitsanzo kwa okhulupirira pa mayankhulidwe, pa makhalidwe, pa chikondi, pa chikhulupiriro ndi pa kuyera mtima.
13 Indtil jeg kommer, saa giv Agt paa Oplæsningen, Formaningen, Undervisningen.
Mpaka nditabwera, udzipereke powerenga mawu a Mulungu kwa anthu, kulalikira ndi kuphunzitsa.
14 Forsøm ikke den Naadegave, som er i dig, som blev given dig under Profeti med Haandspaalæggelse af de Ældste.
Usanyozere mphatso yako yomwe inapatsidwa kwa iwe kudzera mʼmawu auneneri pamene gulu la akulu ampingo linakusanjika manja.
15 Tænk paa dette, lev i dette, for at din Fremgang maa være aabenbar for alle.
Uzichita zimenezi mosamalitsa ndi modzipereka kwathunthu, kuti aliyense aone kuti ukupita mʼtsogolo.
16 Giv Agt paa dig selv og paa Undervisningen; hold ved dermed; thi naar du gør dette, skal du frelse baade dig selv og dem, som høre dig.
Samala kwambiri moyo wako ndi ziphunzitso zako. Uzichitabe zimenezi chifukwa ukatero, udzadzipulumutsa ndiponso udzapulumutsa okumvetsera.

< 1 Timoteus 4 >