< 1 Samuel 27 >
1 Og David sagde i sit Hjerte: Jeg omkommer nu en Dag ved Sauls Haand; intet er mig bedre, end at jeg flyr til Filisternes Land, at Saul kan opgive at søge efter mig ydermere i alt Israels Landemærke, og at jeg kan undgaa hans Haand.
Davide anaganiza mu mtima mwake nati, “Tsiku lina ine ndidzaphedwa ndi Sauli. Palibe chabwino ndingachite, koma kuthawira ku dziko la Afilisti. Kotero Sauli adzasiya kundifunafuna mʼdziko lonse la Israeli, ndipo ndidzapulumuka.”
2 Da gjorde David sig rede og gik over, han og seks Hundrede Mand, som vare med ham, til Akis, Maoks Søn, Kongen i Gath.
Choncho Davide ndi anthu 600 amene anali nawo anachoka napita kwa Akisi mwana wa Maoki mfumu ya ku Gati.
3 Og David boede hos Akis i Gath, han og hans Mænd, hver med sit Hus; David og hans to Hustruer: Ahinoam, den Jisreelitiske, og Abigail, Nabals Hustru, den Karmelitiske.
Davide anakhala ndi Akisi ku Gati pamodzi ndi ankhondo ake, aliyense ndi banja lake. Davide ali ndi akazi ake awiri, Ahinoamu wa ku Yezireeli ndi Abigayeli wa ku Karimeli, mkazi wamasiye wa Nabala.
4 Og det blev Saul tilkendegivet, at David var flyet til Gath; da blev han ikke ydermere ved at søge efter ham.
Sauli anamva kuti Davide wathawira ku Gati, ndipo sanamufunefunenso.
5 Og David sagde til Akis: Kære, dersom jeg har fundet Naade for dine Øjne, saa lad dem give mig et Sted i een af Byerne i Landet, at jeg maa blive der; thi hvorfor skal din Tjener bo i den kongelige Stad hos dig?
Kenaka Davide anawuza Akisi kuti, “Ngati ndapeza kuyanja pamaso panu mundipatse malo dera limodzi la dziko lanu kuti ndizikhala kumeneko. Mtumiki wanu adzakhala mu mzinda waufumu chifukwa chiyani?”
6 Da gav Akis ham Ziklag samme Dag; derfor er Ziklag Judas Kongers indtil denne Dag.
Choncho tsiku limenelo Akisi anamupatsa Zikilagi ndipo mzindawo wakhala wa mafumu a Yuda mpaka lero.
7 Og Tallet paa de Dage, i hvilke David boede i Filisternes Land, var eet Aar og fire Maaneder.
Davide anakhala mʼdziko la Afilisti kwa chaka chimodzi ndi miyezi inayi.
8 Saa drog David og hans Mænd op, og de overfaldt Gesuriterne og Girsiterne og Amalekiterne; thi disse boede i Landet, som hørte dem til fra gammel Tid, i Retningen af Schur og indtil Ægyptens Land.
Tsono Davide ndi anthu ake ankapita kukathira nkhondo Agesuri, Agirizi ndi Aamaleki. (Mitundu ya anthu imeneyi kuyambira kale inkakhala mʼdziko la pakati pa Suri ndi Igupto).
9 Og David slog Landet og lod hverken Mand eller Kvinde leve og tog smaat Kvæg og stort Kvæg og Asener og Kameler og Klæder og vendte tilbage til Akis.
Davide ankati akathira nkhondo dera lina, sankasiya munthu wamoyo, mwamuna kapena mkazi, koma ankatenga nkhosa, ngʼombe, abulu, ngamira ndi zovala, pambuyo pake nʼkubwerera kwa Akisi.
10 Naar Akis sagde: Hvor faldt I ind i Dag? da sagde David: Imod Sønden i Juda og imod Sønden mod Jerahmeeliterne og imod Sønden mod Keniterne.
Akisi akafunsa kuti, “Kodi lero unapita kukathira nkhondo kuti?” Davide ankayankha kuti, “Ndinapita kukathira nkhondo kummwera kwa Yuda,” mwinanso ankanena kuti, “Ndinapita ku dziko la Ayerahimeeli” kapenanso ankanena kuti, “Ndinapita ku dziko la Akeni.”
11 Og David lod ikke en Mand eller Kvinde leve, saa at han førte dem til Gath; thi han sagde: At de ikke skulle forkynde noget imod os og sige: Saaledes gjorde David; og saaledes var hans Vis alle de Dage, han boede i Filisternes Land.
Davide sankasiya mwamuna kapena mkazi wamoyo kuti akafotokozere anthu a ku Gati zochitikazo kuopa kuti opulumukawo akhoza kudzanena kuti “Davide watichita zakutizakuti.” Tsono izi ndi zimene Davide ankachita pamene ankakhala mʼdziko la Afilisti.
12 Derfor troede Akis David og sagde: Han har gjort sig forhadt for sit Folk, for Israel, derfor skal han være min Tjener evindelig.
Akisi ankamukhulupirira Davide ndipo ankati mu mtima mwake, “Davide wadzisandutsa munthu woyipa kwambiri pakati pa anthu ake omwe, Aisraeli. Tsono adzakhala mtumiki wanga mpaka kalekale.”