< Første Kongebog 22 >
1 Og de sade stille tre Aar; der var ingen Krig imellem Syrerne og Israel.
Kwa zaka zitatu panalibe nkhondo pakati pa Aramu ndi Israeli.
2 Men det skete i det tredje Aar, da drog Josafat, Judas Konge, ned til Israels Konge.
Koma pa chaka chachitatu, Yehosafati mfumu ya ku Yuda anapita kukacheza ndi mfumu ya ku Israeli.
3 Og Israels Konge sagde til sine Tjenere: Vide I, at Ramoth i Gilead hører os til? og vi tie stille om at tage den tilbage af Syriens Konges Haand!
Mfumu ya ku Israeli nʼkuti itawuza atumiki ake kuti, “Kodi inu simukudziwa kuti Ramoti Giliyadi ndi dera lathu ndipo ife palibe chimene tikuchita kuti tilitenge deralo mʼmanja mwa mfumu ya Aramu?”
4 Derefter sagde han til Josafat: Vil du drage med mig til Krig imod Ramoth i Gilead? og Josafat sagde til Israels Konge: Jeg vil være som du, mit Folk skal være som dit Folk, mine Heste som dine Heste.
Tsono iye anafunsa Yehosafati kuti, “Kodi udzapita nane ku nkhondo ku Ramoti Giliyadi?” Yehosafati anayankha mfumu ya ku Israeli kuti, “Ine ndili monga inu, anthu anga monga anthu anu, akavalo anga monga akavalo anu.”
5 Fremdeles sagde Josafat til Israels Konge: Kære, adspørg i Dag Herrens Ord!
Koma Yehosafati anawuzanso mfumu ya ku Israeli kuti, “Poyamba mupemphe nzeru kwa Yehova.”
6 Da samlede Israels Konge Profeterne, ved fire Hundrede Mænd, og sagde til dem: Skal jeg drage til Krig imod Ramoth i Gilead eller lade det være? og de sagde: Drag op, og Herren skal give den i Kongens Haand.
Choncho mfumu ya Israeli inasonkhanitsa pamodzi aneneri okwanira 400, ndipo inawafunsa kuti, “Kodi ndipite kukathira nkhondo Ramoti Giliyadi, kapena ndileke?” Iwo anayankha kuti, “Pitani, pakuti Ambuye waupereka mzindawo mʼmanja mwa mfumu.”
7 Men Josafat sagde: Er her ikke endnu en Herrens Profet, at vi kunde spørge ham ad?
Koma Yehosafati anafunsa kuti, “Kodi kuno kulibenso mneneri wina wa Yehova kumene ife tingakafunsireko nzeru?”
8 Og Israels Konge sagde til Josafat: Her er endnu een Mand, ved hvem man kan adspørge Herren, men jeg hader ham, fordi han spaar ikke godt over mig, men ondt, det er Mika, Jimlas Søn; og Josafat sagde: Kongen sige ikke saa!
Mfumu ya ku Israeli inayankha Yehosafati kuti, “Alipo munthu mmodzi amene ife tingakafunsire kwa Yehova, koma ndimadana naye chifukwa iyeyo samanenera kanthu kalikonse kabwino ka ine, koma zoyipa nthawi zonse. Dzina lake ndi Mikaya mwana wa Imula.” Yehosafati anayankha kuti, “Mfumu musatero.”
9 Da kaldte Israels Konge ad en af Kammertjenerne og sagde: Hent hurtigt Mika, Jimlas Søn!
Choncho mfumu ya Israeli inayitana mmodzi mwa atumiki ake ndipo inati, “Kayitane Mikaya mwana wa Imula msangamsanga.”
10 Og Israels Konge og Josafat, Judas Konge, sade hver paa sin Trone, iførte Kongedragt, paa en fri Plads ved Indgangen til Samarias Port, og alle Profeterne spaaede for deres Ansigt.
Atavala mikanjo yawo yaufumu, mfumu ya ku Israeli ndi Yehosafati mfumu ya ku Yuda anakhala pa mipando yawo yaufumu pabwalo lopondera tirigu pafupi ndi chipata cha Samariya, pamodzi ndi aneneri onse akunenera pamaso pawo.
11 Og Zedekia, Knaanas Søn, havde gjort sig Jernhorn, og han sagde: Saaledes sagde Herren: Med disse skal du stange Syrerne, indtil de aldeles udryddes.
Tsono Zedekiya mwana wa Kenaana nʼkuti atapanga nyanga zachitsulo ndipo iye ananenera kuti, “Yehova akuti, ‘Ndi nyanga izi, inu mudzagunda nazo Aaramu mpaka iwo atawonongeka.’”
12 Og alle Profeterne spaaede saaledes og sagde: Drag op imod Ramoth i Gilead og vær lykkelig, og Herren skal give den i Kongens Haand.
Aneneri ena onse ananenera zomwezonso. Iwo anati, “Kathireni nkhondo Ramoti Giliyadi ndipo mukapambana, pakuti Yehova adzawupereka mzindawo mʼdzanja la mfumu.”
13 Og Budet, som var gaaet bort for at kalde paa Mika, talte til ham sigende: Kære, se, Profeternes Ord ere som af een Mund gunstige for Kongen; kære, lad dit Ord være ligesom Ordet af en af dem og tal gunstigt!
Wamthenga amene anapita kukayitana Mikaya anamuwuza kuti, “Taonani, aneneri onse monga munthu mmodzi akunenera za kupambana kwa mfumu. Mawu anunso akhale ogwirizana ndi mawu awo, ndipo mukayankhule zabwino.”
14 Da sagde Mika: Saa vist som Herren lever, det som Herren siger mig, det vil jeg tale.
Koma Mikaya anati, “Pali Yehova wamoyo, ine ndikawawuza zokhazo zimene Yehova akandiwuze.”
15 Og han kom til Kongen, og Kongen sagde til ham: Mika! skulle vi drage imod Ramoth i Gilead til Krig eller lade være? Og han sagde til ham: Drag op og vær lykkelig, og Herren skal give den i Kongens Haand.
Atafika, Ahabu anamufunsa kuti, “Mikaya, kodi tipite kukathira nkhondo Ramoti Giliyadi, kapena tileke?” Iye anayankha kuti, “Pitani ndipo mukapambana, pakuti Yehova adzawupereka mzindawo mʼdzanja la mfumu.”
16 Og Kongen sagde til ham: Hvor mange Gange skal jeg besværge dig, at du intet siger mig uden Sandheden i Herrens Navn?
Ahabu anati kwa iye, “Kodi ndikulumbiritse kangati kuti undiwuze zoona zokhazokha mʼdzina la Yehova?”
17 Da sagde han: Jeg saa al Israel adspredt paa Bjergene ligesom Faarene, der ingen Hyrde have; og Herren sagde: Disse have ingen Herre, lad dem vende tilbage hver til sit Hus med Fred!
Pamenepo Mikaya anayankha kuti, “Ndinaona Aisraeli onse atamwazikana pa mapiri ngati nkhosa zopanda mʼbusa, ndipo Yehova anati, ‘Anthu awa alibe mbuye wawo. Aliyense apite kwawo mwamtendere.’”
18 Da sagde Israels Konge til Josafat: Har jeg ikke sagt dig: Han spaar mig ikke godt, men ondt?
Mfumu ya ku Israeli inati kwa Yehosafati, “Kodi ine sindinakuwuzeni kuti ameneyu samanenera kanthu kalikonse kabwino ka ine, koma zoyipa zokhazokha?”
19 Og han sagde: Hør derfor Herrens Ord: Jeg saa Herren sidde paa sin Trone, og al Himmelens Hær staaende hos ham ved hans højre og ved hans venstre Side.
Mikaya anapitiriza kuyankhula nati, “Tsono imvani mawu a Yehova: Ine ndinaona Yehova atakhala pa mpando wake waufumu, gulu lonse la kumwamba litayima ku dzanja lake lamanja ndi ku dzanja lake lamanzere.
20 Og Herren sagde: Hvo vil overtale Akab, at han skal drage op og falde ved Ramoth i Gilead? og den ene sagde saa, og den anden sagde saa.
Ndipo Yehova anati, ‘Kodi ndani amene akamukope Ahabu kuti akathire nkhondo Ramoti Giliyadi, nʼkukafera komweko?’” “Wina anapereka maganizo ena ndipo winanso maganizo ena.
21 Da gik en Aand ud og stod for Herrens Ansigt og sagde: Jeg vil overtale ham; og Herren sagde til ham: Hvormed?
Potsirizira, mzimu wina unabwera ndi kuyima pamaso pa Yehova ndipo unati, ‘Ine ndidzamukopa.’”
22 Og han sagde: Jeg vil gaa ud og være en løgnagtig Aand i alle hans Profeters Mund; og han sagde: Du skal overtale ham, ja ogsaa formaa det; gak ud og gør saa!
Yehova anafunsa kuti, “Ukamukopa bwanji?” Mzimuwo unati, “Ndidzapita ndi kukakhala mzimu wabodza pakamwa pa aneneri ake onse.” Yehova anati, “‘Iwe udzamukopadi. Pita kachite zomwezo.’
23 Og nu, se, Herren har givet en løgnagtig Aand i alle disse dine Profeters Mund; men Herren har talt ondt over dig.
“Ndipo tsopano taonani, Yehova wayika mzimu wabodza mʼkamwa mwa aneneri anu onsewa. Yehova waneneratu kuti mukaona mavuto.”
24 Da gik Zedekia, Knaanas Søn, frem og slog Mika paa Kinden og sagde: Hvorledes? er Herrens Aand gaaet over fra mig for at tale med dig?
Pamenepo Zedekiya mwana wa Kenaana anapita pafupi namenya Mikaya patsaya. Iye anafunsa Mikaya kuti, “Kodi mzimu wa Yehova unadzera njira iti pamene umatuluka mwa ine kuti uziyankhula ndi iwe?”
25 Og Mika sagde: Se, du skal se det paa den Dag, naar du gaar ind fra et Kammer til et andet for at skjule dig.
Mikaya anayankha kuti, “Udzaona pa tsiku limene uzikalowa mʼchipinda chamʼkati kuti ukabisale.”
26 Da sagde Israels Konge: Tag Mika og før ham tilbage til Amon, Stadens Befalingsmand, og til Joas, Kongens Søn.
Pamenepo mfumu ya ku Israeli inalamula kuti, “Mugwireni Mikaya ndipo mubwerere naye kwa Amoni mkulu wa mzinda, ndi kwa Yowasi mwana wa mfumu
27 Og du skal sige: Saa siger Kongen: Sætter denne i Fængsels Hus og bespiser ham med Trængsels Brød og Trængsels Vand, indtil jeg kommer med Fred.
ndipo mukanene kuti, ‘Chimene mfumu ikunena ndi ichi; Muyikeni mʼndende munthu uyu ndipo musamupatse chakudya china koma buledi ndi madzi pangʼono mpaka nditabwerera mwamtendere.’”
28 Og Mika sagde: Dersom du kommer tilbage med Fred, da har Herren ikke talt ved mig; og han sagde: Hører, I Folk alle sammen!
Mikaya ananena kuti, “Ngati mudzabwerera mwamtendere, Yehova sanayankhule kudzera mwa ine.” Ndipo iye anapitiriza kunena kuti, “Gwiritsitsani mawu angawa, anthu inu nonse!”
29 Saa drog Israels Konge og Josafat, Judas Konge, op imod Ramoth i Gilead.
Choncho mfumu ya ku Israeli ndi Yehosafati mfumu ya ku Yuda anapita ku Ramoti Giliyadi.
30 Og Israels Konge sagde til Josafat: Jeg vil forklæde mig og saa gaa i Kampen, men tag du dine egne Klæder paa; og Israels Konge forklædte sig og gik i Slaget.
Mfumu ya ku Israeli inawuza Yehosafati kuti, “Ine ndidzalowa mu nkhondoyi modzibisa, koma inu muvale zovala zanu zaufumu.” Choncho mfumu ya ku Israeli inadzibisa ndi kupita ku nkhondo.
31 Men Kongen af Syrien bød sine to og tredive øverste for Vognene og sagde: I skulle ikke stride imod liden eller stor, uden imod Israels Konge alene.
Tsono mfumu ya ku Aramu nʼkuti italamulira anthu ake 32 olamulira magaleta kuti, “Musamenyane ndi wina aliyense, wamngʼono kapena wamkulu, koma mfumu ya ku Israeli.”
32 Og det skete, der de øverste for Vognene saa Josafat, da sagde de: Han er visselig Israels Konge, og de bøjede af for at stride imod ham. Da raabte Josafat.
Olamulira magaleta ataona Yehosafati, ankaganiza kuti, “Ndithu iyi ndiye mfumu ya ku Israeli.” Choncho anabwerera kukamenyana naye, koma Yehosafati atafuwula,
33 Og det skete, der de øverste for Vognene saa, at han ikke var Israels Konge, da vendte de tilbage fra ham.
olamulira akavalo anaona kuti sanali mfumu ya ku Israeli ndipo analeka kumuthamangitsa.
34 Og en Mand spændte Buen paa Lykke og Fromme og skød Israels Konge mellem Remmene og Panseret; da sagde denne til sin Køresvend: Vend din Haand om og før mig ud af Hæren; thi jeg er saaret.
Koma munthu wina anaponya muvi wake mwachiponyeponye ndi kulasa mfumu ya ku Israeli polumikizira malaya ake odzitetezera. Mfumu inawuza woyendetsa galeta lake kuti, “Tembenuka ndipo undichotse pa nkhondo pano pakuti ndalasidwa.”
35 Og Kampen tog til paa den samme Dag, og Kongen blev holdt staaende i Vognen over for Syrerne, og han døde om Aftenen, og Blodet flød af Saaret midt i Vognen.
Nkhondo inakula kwambiri tsiku limenelo, ndipo mfumu inakhala tsonga mʼgaleta lake moyangʼanana ndi Aaramu. Magazi ake ankayenderera pansi kuchokera mʼgaleta, ndipo pa nthawi ya madzulo inamwalira.
36 Og man udraabte igennem Lejren, der Solen gik ned, og sagde: Hver gaa til sin Stad og hver til sit Land!
Pamene dzuwa linkalowa, kunamveka mfuwu wa nkhondo kuti, “Munthu aliyense apite ku mzinda wa kwawo, aliyense apite ku dziko la kwawo!”
37 Saa døde Kongen og blev ført til Samaria, og de begrove Kongen i Samaria.
Ndipo mfumu ija inafa, nabwera nayo ku Samariya, ndipo anayika mʼmanda kumeneko.
38 Og man skyllede Vognen ved Samarias Dam; og Hundene slikkede hans Blod, hvor Skøgerne badede sig, efter Herrens Ord, som han havde talt.
Anatsuka galeta lija pa dziwe la ku Samariya (pamene ankasamba akazi achiwerewere) ndipo agalu ananyambita magazi a mfumuyo, monga momwe Yehova ananenera.
39 Men det øvrige af Akabs Handeler, og alt det han gjorde, og om det Elfenbens Hus, som han byggede, og om alle Stæderne, som han byggede, er det ikke skrevet i Israels Kongers Krønikers Bog?
Tsono ntchito zina za Ahabu, kuphatikiza zonse anazichita, nyumba yaufumu imene anamanga yokutidwa ndi minyanga ya njovu, mizinda yotetezedwa, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?
40 Og Akab laa med sine Fædre, og Ahasia, hans Søn, blev Konge i hans Sted.
Ahabu anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Ahaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
41 Og Josafat, Asas Søn, blev Konge over Juda i Akabs, Israels Konges, fjerde Aar.
Yehosafati, mwana wa Asa anakhala mfumu ya ku Yuda chaka chachinayi cha Ahabu mfumu ya ku Israeli.
42 Josafat var fem og tredive Aar gammel, der han blev Konge, og regerede fem og tyve Aar i Jerusalem, og hans Moders Navn var Asuba, Silhis Datter.
Yehosafati anali wa zaka 35 pamene analowa ufumu, ndipo analamulira ku Yerusalemu zaka 25. Amayi ake anali Azuba mwana wa Silihi.
43 Og han vandrede i alle sin Fader Asas Veje og veg ikke derfra, men gjorde det, som var ret for Herrens Øjne.
Pa zinthu zonse, Yehosafati anayenda mʼnjira za Asa abambo ake ndipo sanachite zotsutsana ndi machitidwe a abambo ake. Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova. Komabe, malo azipembedzo sanawawononge, ndipo anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
44 Dog bleve Højene ikke borttagne; Folket ofrede endnu og gjorde Røgelse paa Højene.
Yehosafati anakhala mwamtendere ndi mfumu ya ku Israeli.
45 Og Josafat holdt Fred med Israels Konge.
Ntchito zake zina za Yehosafati, zinthu zimene anachita ndi zamphamvu zimene anaonetsa, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Yuda?
46 Men det øvrige af Josafats Handeler og hans Magt, hvilken han skaffede sig, og hvorledes han har stridt, er det ikke skrevet i Judas Kongers Krønikers Bog?
Iye anachotsa mʼdzikomo amuna onse ochita zachiwerewere mwa chipembedzo amene anatsalira pa nthawi ya ulamuliro wa Asa, abambo ake.
47 Og de øvrige af Skørlevnerne, som vare blevne tilbage fra Asas, hans Faders, Dage, borttog han af Landet.
Nthawi imeneyo kunalibe mfumu ku Edomu, amene ankalamulira anali munthu woyikidwa ndi mfumu ya ku Yuda.
48 Og der var ingen Konge i Edom; men en Befalingsmand var Konge.
Yehosafati anapanga sitima zapamadzi zopita ku Ofiri kukatenga golide, koma sitimazo sizinayende chifukwa zinawonongeka ku Ezioni Geberi.
49 Og Josafat havde ti Tharsisskibe, som skulde drage til Ofir efter Guld; men de droge ikke derhen, thi Skibene bleve sønderslagne i Ezion-Geber.
Nthawi imeneyo Ahaziya mwana wa Ahabu anawuza Yehosafati kuti, “Anthu anga ayende pa madzi pamodzi ndi anthu anu,” koma Yehosafati anakana.
50 Da sagde Ahasia, Akabs Søn, til Josafat: Lad mine Tjenere fare med dine Tjenere paa Skibene; men Josafat vilde ikke.
Ndipo Yehosafati anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Ndipo Yoramu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
51 Og Josafat laa med sine Fædre og blev begraven med sine Fædre i Davids, sin Faders, Stad; og Joram, hans Søn, blev Konge i hans Sted.
Ahaziya mwana wa Ahabu anakhala mfumu ya ku Israeli ku Samariya mʼchaka cha 17 cha Yehosafati mfumu ya ku Yuda, ndipo analamulira Israeli zaka ziwiri.
52 Ahasia, Akabs Søn, blev Konge over Israel i Samaria udi Josafats, Judas Konges, syttende Aar og var Konge over Israel to Aar.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, chifukwa anayenda mʼnjira za abambo ndi amayi ake komanso mʼnjira za Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa Israeli.
53 Og han gjorde det, som ondt var for Herrens Øjne, og vandrede i sin Faders Vej og i sin Moders Vej og i Jeroboams, Nebats Søns, Vej, hans, som kom Israel tir at synde. Og han tjente Baal og tilbad ham og opirrede Herren, Israels Gud, alt ligesom hans Fader gjorde.
Potumikira ndi kupembedza Baala, iye anakwiyitsa Yehova Mulungu wa Israeli, monga momwe anachitira abambo ake.