< Første Kongebog 20 >
1 Og Benhadad, Kongen i Syrien samlede hele sin Hær, og der var to og tredive Konger med ham og Heste og Vogne; og han drog op og belejrede Samaria og stred imod den.
Tsono Beni-Hadadi mfumu ya ku Aramu inasonkhanitsa magulu ake onse a ankhondo. Iye pamodzi ndi mafumu 32, akavalo awo ndi magaleta awo, anapita kukawuzungulira mzinda wa Samariya ndi kuwuthira nkhondo.
2 Og han sendte Bud til Akab, Israels Konge, til Staden.
Iye anatuma amithenga ake mu mzindamo kwa Ahabu mfumu ya Israeli, kukanena kuti,
3 Og han lod ham sige: Saa siger Benhadad: Dit Sølv og dit Guld, det er mit, og dine smukkeste Hustruer og Børn, de ere mine.
“Beni-Hadadi akuti, ‘Siliva wako ndi golide wako ndi wanga, ndipo akazi ako okongola ndi ana ako ndi anganso.’”
4 Og Israels Konge svarede og sagde: Efter dine Ord skal det være, min Herre Konge! jeg er din og alt det, jeg har.
Mfumu ya Israeli inayankha kuti, “Monga mmene mwanenera, mbuye wanga mfumu, ine pamodzi ndi zonse zomwe ndili nazo ndi zanu.”
5 Derefter kom Budene igen og sagde: Saa siger Benhadad: Efterdi jeg sendte til dig og lod sige: Du skal give mig dit Sølv og dit Guld og dine Hustruer og dine Børn:
Amithenga aja anabwereranso kwa Ahabu ndipo anamuwuza kuti, “Beni-Hadadi akuti, ‘Ine ndinakulamula kuti undipatse siliva wako ndi golide wako, akazi ako ndi ana ako.
6 Saa vil jeg sende mine Tjenere til dig i Morgen paa denne Tid, og de skulle ransage i dit Hus og i dine Tjeneres Huse, og det skal ske, alt det, som er lysteligt for dine Øjne, skulle de lægge i deres Hænder og tage det bort.
Koma mawa nthawi ngati yomwe ino ndidzatuma atumiki anga kudzafufuza mʼnyumba yako yaufumu ndi nyumba za akuluakulu ako. Iwo adzatenga chilichonse chimene umachidalira ndi kupita nacho.’”
7 Da kaldte Israels Konge ad alle Landets ældste og sagde: Kære, mærker og ser, at denne søger det, som ondt er; thi han sendte til mig om mine Hustruer og om mine Børn og om mit Sølv og om mit Guld, og jeg har ikke nægtet ham det.
Pamenepo mfumu ya Israeli inayitanitsa akuluakulu a mʼdzikomo niwawuza kuti, “Taonani momwe munthuyu akufunira kutibweretsera mavuto! Atatumiza mawu oti ndimupatse akazi anga ndi ana anga, siliva wanga ndi golide wanga, ine sindinamukanize.”
8 Da sagde alle de ældste og alt Folket til ham: Du skal ikke adlyde og ikke samtykke.
Akuluakulu onse ndi anthu onse anayankha kuti, “Musamumvere kapena kuvomereza zofuna zake.”
9 Da sagde han til Benhadads Bud: Siger min Herre Kongen: Alt det, du sendte til din Tjener første Gang om, vil jeg gøre, men denne Gerning kan jeg ikke gøre, og Budene gik og bragte ham Svar igen.
Tsono Ahabu anayankha amithenga a Beni-Hadadi kuti, “Kamuwuzeni mbuye wanga mfumu kuti, ‘Mtumiki wanu adzachita zonse zimene munazifuna nthawi yoyamba ija, koma izi mwazifunazi sindingazikwanitse.’” Iwo anachoka nakapereka yankho kwa Beni-Hadadi.
10 Da sendte Benhadad til ham og lod sige: Guderne gøre mig nu og fremdeles saa og saa, om Støvet af Samaria skal blive nok til, at alt Folket, som er i Følge med mig, skal kunne føre hver en Haandfuld derfra.
Pamenepo Beni-Hadadi anatumizanso uthenga wina kwa Ahabu kuti, “Milungu indilange koopsa, ngati mu Samariya mudzakhale fumbi loti nʼkudzaza dzanja la aliyense wa anthu anga.”
11 Da svarede Israels Konge og sagde: Siger: Den, som ombinder Bæltet, skal ikke rose sig som den, der løser det.
Mfumu ya Israeli inayankha kuti, “Kamuwuzeni kuti, ‘Mwamuna mnzako nʼpachulu, nʼkulinga utakwerapo.’”
12 Og det skete, der han hørte dette Ord, medens han drak, han og Kongerne i Teltene, da sagde han til sine Tjenere: Sætter an; og de satte an imod Staden.
Beni-Hadadi anamva uthenga umenewu pamene iye ankamwa ndi mafumu anzake mʼmatenti awo, ndipo analamula anthu ake kuti, “Konzekerani kukathira nkhondo.” Choncho anakonzekera kukathira nkhondo mzindawo.
13 Og se, en Profet gik frem til Akab, Israels Konge, og sagde: Saa sagde Herren: Har du set hele denne store Hob? se, jeg vil give den i Dag i din Haand, at du skal fornemme, at jeg er Herren.
Ndipo taonani, mneneri wina anabwera kwa Ahabu mfumu ya Israeli nadzalengeza kuti, “Yehova akuti, ‘Kodi ukuchiona chigulu chachikulu cha ankhondochi? Taona, ndikuchipereka chimenechi lero mʼdzanja lako, ndipo pamenepo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
14 Og Akab sagde: Ved hvem? og han sagde: Saa siger Herren: Ved Landshøvdingenes Drenge; og han sagde: Hvem skal begynde Striden? og han sagde: Du.
Ahabu anafunsa kuti, “Koma ndani adzachita zimenezi?” Mneneri anayankha kuti, “Yehova akuti, ‘Adzachita zimenezi ndi asilikali a nduna za mʼzigawo.’” Ndipo iye anafunsa kuti, “Kodi ndani adzayambe nkhondoyi?” Mneneriyo anayankha kuti, “Ndinu.”
15 Saa talte han Landshøvdingenes Drenge, og de vare to Hundrede og to og tredive; og efter dem talte han hele Folket, alle Israels Børn, syv Tusinde.
Choncho Ahabu anawerenga asilikali achinyamata a nduna za mʼzigawo ndipo onse analipo 232. Ndipo anawerenganso ankhondo a ku Israeli ndipo onse analipo 7,000.
16 Og de droge ud om Middagen; og Benhadad drak og var drukken i Teltene, han og Kongerne, nemlig de to og tredive Konger, som hjalp ham.
Iwo ananyamuka nthawi yamasana pamene Beni-Hadadi ndi mafumu 32 othandizana naye ankamwa mpaka kuledzera mʼmatenti awo.
17 Og Landshøvdingenes Drenge droge først ud; og Benhadad sendte nogle hen, og de gave ham til Kende og sagde: Der drager Mænd ud fra Samaria.
Asilikali achinyamata a nduna za mʼzigawo ndiwo amene anayamba kupita ku nkhondo. Nthawi imeneyi Beni-Hadadi nʼkuti atatumiza anthu oti akazonde, amene anadzafotokoza kuti, “Anthu ankhondo akubwera kuchokera ku Samariya.”
18 Og han sagde: Dersom de ere uddragne for Freds Skyld, saa griber dem levende, og dersom de ere uddragne for Krigs Skyld, saa griber dem levende!
Iye anati, “Kaya akubwera mwamtendere kapena mwankhondo, muwagwire amoyo.”
19 Da de vare uddragne af Staden, nemlig Landshøvdingenes Drenge og Hæren, som fulgte dem:
Choncho asilikali achinyamata a nduna za mʼzigawo anatuluka mu mzinda, gulu lankhondo lili pambuyo pawo.
20 Da sloge de hver sin Mand, og Syrerne flyede, og Israel forfulgte dem; og Benhadad, Kongen af Syrien, undkom paa en Hest med Rytterne.
Ndipo aliyense wa iwo anapha munthu wake. Ataona izi, Aaramu anathawa Aisraeli ali pambuyo pawo kuwapirikitsa. Koma Beni-Hadadi mfumu ya ku Aaramu anathawa atakwera pa kavalo pamodzi ndi ankhondo ena okweranso pa akavalo.
21 Og Israels Konge drog ud og slog Heste og Vogne og slog Syrerne med et stort Slag.
Mfumu ya Israeli inapita chitsogolo ndi kugwira akavalo ndi magaleta ndipo Aaramu ambiri anaphedwa.
22 Da gik Profeten frem til Israels Konge og sagde til ham: Gak, forstærk dig, og vid og se, hvad du skal gøre; thi naar Aaret er omme, vil Kongen af Syrien drage op imod dig.
Zitachitika izi, mneneri wina anabwera kwa mfumu ya Israeli ndipo anati, “Mulimbike ndipo muganize bwino zoti mudzachite, chifukwa chaka chikudzachi mfumu ya Aramu idzakuthiraninso nkhondo.”
23 Og Kongen af Syriens Tjenere sagde til ham: Deres Guder ere Bjergenes Guder, derfor ere de stærkere end vi; men lader os stride imod dem paa det jævne Land; hvad gælder det, om vi ikke skulle blive stærkere end de?
Nthawi imeneyi, akuluakulu a mfumu ya Aramu anamulangiza kuti, “Milungu ya anthu a ku Israeli ndi milungu ya mʼmapiri. Nʼchifukwa chake anali ndi mphamvu zotipambana ife. Koma ngati tidzamenyana nawo ku chigwa, ndithudi ife tidzakhala ndi mphamvu kuposa iwo.
24 Og gør denne Gerning: Tag Kongerne bort, hver fra sin Plads, og sæt Statholdere i deres Sted!
Inu chitani izi: chotsani mafumu onse pa maudindo awo ndipo mʼmalo mwawo muyikemo atsogoleri a ankhondo.
25 Og tæl dig en Hær, som denne Hær var, som er falden for dig, og Heste som de Heste og Vogne som de Vogne, og lader os stride imod dem paa det jævne Land; hvad gælder det, om vi ikke skulle blive stærkere end de? og han adlød deres Røst og gjorde saa.
Musonkhanitsenso gulu lankhondo lofanana ndi lomwe linaphedwa lija, akavalo monga omwe anaphedwa aja, ndi magaleta monga omwe anawonongedwa aja, kuti tikamenyane ndi Israeli ku chigwa. Pamenepo, ife tidzapambana iwowo.” Beni-Hadadi anagwirizana nawo ndipo anachita momwemo.
26 Og det skete, der Aaret var omme, da talte Benhadad Syrerne og drog op til Afek, til Krigen imod Israel.
Chaka chinacho Beni-Hadadi anasonkhanitsa Aaramu, napita ku Afeki kukamenyana ndi Israeli.
27 Og Israels Børn bleve talte og forsynede, og de droge imod dem; og Israels Børn lejrede sig imod dem som to smaa Gedehjorde; men Syrerne havde opfyldt Landet.
Aisraeli atasonkhananso, napatsidwa zakudya zawo anapita kukakumana nawo. Aisraeli anamanga misasa yawo moyangʼanana ndi Aaramu ndipo ankaoneka ngati timagulu tiwiri ta mbuzi, pomwe Aaramu anali atakuta dera lonselo.
28 Og der kom en Guds Mand frem og talte til Israels Konge og sagde: Saa sagde Herren: Fordi Syrerne have sagt: Herren er Bjergenes Gud og ikke Dalenes Gud, derfor har jeg givet hele denne store Hob i din Haand, for at I skulle fornemme, at jeg er Herren.
Munthu wa Mulungu anabwera, nawuza mfumu ya Israeli kuti, “Yehova akuti, ‘Popeza Aaramu akuganiza kuti Yehova ndi mulungu wa ku mapiri, osati wa ku zigwa, Ine ndidzapereka chigulu chonsechi kwa iwe, ndipo iwe udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
29 Og disse lejrede sig over for dem syv Dage, og det skete paa den syvende Dag, da begyndte Slaget, og Israels Børn sloge Syrerne, hundrede Tusinde Fodfolk paa een Dag.
Kwa masiku asanu ndi awiri anakhala moyangʼanana mʼmisasa yawo, ndipo pa tsiku lachisanu ndi chiwiri nkhondo inayambika. Aisraeli anapha Aaramu okwana 100,000 tsiku limodzi lokha.
30 Og de, som bleve tilovers, flyede til Afek ind i Staden, og Muren faldt paa syv og tyve Tusinde Mænd, som vare blevne tilovers; og Benhadad flyede og kom i Staden, fra et Kammer til et andet.
Ena onse otsala anathawira ku Afeki, kumene khoma linagwera anthu 27,000. Ndipo Beni-Hadadi anathawira mu mzinda, nakabisala mʼchipinda chamʼkati.
31 Da sagde hans Tjenere til ham: Kære, se, vi have hørt, at Israels Konger ere naadige Konger; kære, lader os lægge Sække om vore Lænder og Reb om vore Hoveder og gaa ud til Israels Konge, maaske han lader din Sjæl leve.
Atumiki ake anamuwuza kuti, “Taonani, ife tamva kuti mafumu a fuko la Israeli ndi achifundo. Tiyeni tipite kwa mfumu ya ku Israeli titavala ziguduli mʼchiwuno mwathu ndi kumanga zingwe mʼmakosi mwathu. Mwina iye sakakuphani.”
32 Og de bandt Sække om deres Lænder og Reb om deres Hoveder, og de kom til Israels Konge og sagde: Benhadad, din Tjener siger: Kære, lad min Sjæl leve; og han sagde: Lever han endnu? han er min Broder.
Atavala ziguduli mʼchiwuno mwawo ndi kumanga zingwe mʼmakosi mwawo, anapita kwa mfumu ya ku Israeli ndipo anayiwuza kuti, “Mtumiki wanu Beni-Hadadi akunena kuti, ‘Chonde loleni kuti ndikhale moyo.’” Mfumu inayankha kuti, “Kodi iye akanali ndi moyo? Iye ujatu ndi mʼbale wanga.”
33 Og Mændene udlagde sig det til det gode og skyndte sig med at faa ham til at sige, om det var hans Alvor, og de sagde: Benhadad er din Broder; og han sagde: Gaar ind, henter ham hid; da gik Benhadad ud til ham, og han lod ham stige op paa Vognen.
Anthuwo ankaganiza kuti mawuwo anali abwino ndipo anavomereza mawuwa mofulumira. Iwo anati, “Inde, Beni-Hadadi ndi mʼbale wanu!” Mfumu inati, “Pitani kamutengeni.” Beni-Hadadi atatuluka, Ahabu anamukweza mʼgaleta lake.
34 Og Benhadad sagde til ham: Jeg vil give dig igen de Stæder, som min Fader tog fra din Fader, og du maa anlægge dig Gader i Damaskus, ligesom min Fader anlagde i Samaria; og jeg, sagde Akab, vil med den Pagt lade dig fare. Saa gjorde han en Pagt med ham og lod ham fare.
Beni-Hadadi anawuza Ahabu kuti, “Ndidzabweza mizinda imene abambo anga analanda abambo anu. Ndipo mutha kumanga nyumba zanu zamalonda mu Damasiko, monga anachitira abambo anga ku Samariya.” Ahabu anati, “Chifukwa cha mgwirizano umenewu, ine ndidzakumasula.” Choncho anachita naye mgwirizano, ndipo anamulola kuti apite.
35 Og en Mand af Profeternes Børn sagde til sin Næste ved Herrens Ord: Kære, slaa mig; men Manden vægrede sig ved at slaa ham.
Molamulidwa ndi Yehova, mmodzi mwa ana a aneneri anawuza mnzake kuti, “Chonde, menye ndi chida chako,” koma mnzakeyo anakana.
36 Da sagde han til ham: Fordi du ikke adlød Herrens Røst, se, da skal en Løve slaa dig, naar du gaar fra mig; og han gik fra ham, og en Løve traf ham og slog ham.
Choncho mneneriyo anati, “Chifukwa sunamvere Yehova, ukangochoka pano, mkango ukupha.” Ndipo munthuyo atangochoka pamenepo, mkango unamupeza ndi kumupha.
37 Og han traf en anden Mand og sagde: Kære, slaa mig; og Manden slog ham haardt og saarede ham.
Mneneriyo anapeza munthu wina ndipo anamuwuza kuti, “Chonde, menye.” Choncho munthuyo anamumenya ndi kumuvulaza.
38 Da gik Profeten og stod for Kongen paa Vejen og gjorde sig ukendelig med et Klæde over sine Øjne.
Pamenepo mneneriyo anapita nakayima pa msewu kudikirira mfumu. Iye anadzibisa nakulunga nsalu nkhope yake.
39 Og det skete, da Kongen drog forbi, at han raabte til Kongen og sagde: Din Tjener var dragen ud midt i Krigen, og se, en Mand veg af Vejen og førte en Mand til mig og sagde: Forvar denne Mand; dersom han savnes, da skal dit Liv være i Stedet for hans Liv, eller du skal betale et Centner Sølv.
Mmene mfumu inkadutsa pamenepo, mneneriyo anafuwula kwa mfumuyo kuti, “Ine mtumiki wanu ndinalowa pakati pa nkhondo, ndipo munthu wina anabwera kwa ine atatenga mmodzi mwa anthu ogwidwa pa nkhondo, nandiwuza kuti, ‘Sunga munthu uyu. Ngati asowa, ndiye kuti ndidzakupha, kapena udzalipira ndalama 3,000 za siliva.’
40 Og det skete, der din Tjener havde at gøre her og der, da var han ikke mere der; og Israels Konge sagde til ham: Saa er din Dom, du har selv fældet den.
Pamene ine mtumiki wanu ndinali wotanganidwa apa ndi apa, munthuyo anasowa.” Mfumu ya Israeli inati, “Chimenechi ndiye chilango chako. Iwe wadziweruza wekha.”
41 Da skyndte han sig og tog Klædet bort fra sine Øjne, og Israels Konge kendte ham, at han var en af Profeterne.
Pamenepo mneneriyo anachotsa msangamsanga nsalu yomwe anakulunga pa nkhope yake, ndipo mfumu ya Israeli inamuzindikira kuti ndi mmodzi mwa aneneri.
42 Og han sagde til ham: Saa sagde Herren: Fordi du slap den Mand, som jeg har sat i Band, af din Haand, da skal din Sjæl være i Stedet for hans Sjæl, og dit Folk i Stedet for hans Folk.
Iye anawuza mfumu kuti, “Yehova akuti, ‘Chifukwa chakuti mwamasula munthu amene Ine ndinati ndi woyenera kuphedwa, inuyo ndi amene mudzaphedwe mʼmalo mwa iyeyo, anthu anu mʼmalo mwa anthu ake.’”
43 Saa drog Israels Konge til sit Hus, ilde tilfreds og vred; og han kom til Samaria.
Mwachisoni ndi mokwiya, mfumu ya Israeli inapita ku nyumba yake yaufumu ku Samariya.