< Første Krønikebog 24 >
1 Men for Arons Børn vare Skifterne disse: Arons Sønner vare Nadab og Abihu, Eleasar og Ithamar.
Magulu a ana a Aaroni anali awa: Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
2 Men Nadab og Abihu døde for deres Faders Ansigt, og de havde ingen Børn; og Eleasar og Ithamar gjorde Præstetjeneste.
Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe.
3 Og David tillige med Zadok af Eleasars Børn og Akimelek af Ithamars Børn inddelte dem til deres Embede i deres Tjeneste.
Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira.
4 Og der blev flere fundne af Eleasars Børn, som vare Øverster for Mændene, end af Ithamars Børn, da de delte dem; af Eleasars Børn var der seksten Øverster for deres Fædrenehuse, men af Ithamars Børn for deres Fædrenehuse var der otte.
Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara.
5 Og de inddelte dem efter Lodkastning, disse med hine; thi der havde været Helligdommens Fyrster og Guds Fyrster saavel af Eleasars Børn som af Ithamars Børn.
Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.
6 Og Semaja, Nethaneels Søn, Skriveren, en af Leviterne, opskrev dem i Paasyn af Kongen og Fyrsterne, og Zadok, Præsten, og Akimelek, Abjathars Søn, og Øversterne for Fædrenehusene blandt Præsterne og Leviterne; et Fædrenehus blev udtrukket for Eleasar, et andet blev skiftevis udtrukket for Ithamar.
Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.
7 Den første Lod kom ud for Jojarib, den anden for Jedaja,
Maere woyamba anagwera Yehoyaribu, achiwiri anagwera Yedaya,
8 den tredje for Harim, den fjerde for Seorim,
achitatu anagwera Harimu, achinayi anagwera Seorimu,
9 den femte for Malkia, den sjette for Mijamin,
achisanu anagwera Malikiya, achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,
10 den syvende for Hakkoz, den ottende for Abia,
achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi, achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,
11 den niende for Jesua, den tiende for Sekania,
achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa, a khumi anagwera Sekaniya,
12 den ellevte for Eljasib, den tolvte for Jakim,
a 11 anagwera Eliyasibu, a 12 anagwera Yakimu,
13 den trettende for Hufa, den fjortende for Jesebab,
a 13 anagwera Hupa, a 14 anagwera Yesebeabu,
14 den femtende for Bilga, den sekstende for Immer,
a 15 anagwera Biliga, a 16 anagwera Imeri,
15 den syttende for Hesir, den attende for Hafizez,
a 17 anagwera Heziri, a 18 anagwera Hapizezi,
16 den nittende for Petakia, den tyvende for Ezekiel,
a 19 anagwera Petahiya, a 20 anagwera Ezekieli,
17 den en og tyvende for Jakin, den to og tyvende for Gamul,
a 21 anagwera Yakini, a 22 anagwera Gamuli,
18 den tre og tyvende for Delaja, den fire og tyvende for Maaseja.
a 23 anagwera Delaya, ndipo a 24 anagwera Maaziya.
19 Disses Embedsgerning var det at gaa ind i Herrens Hus, som deres Vis var, efter deres Faders, Arons, Anvisning, saaledes som Herren, Israels Gud havde budt ham.
Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.
20 Og hvad de øvrige af Levis Børn angaar, da var der af Amrams Sønner Subael, af Subaels Sønner Jedeja.
Za zidzukulu zina zonse za Levi: Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli; kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.
21 Hvad Rehabia angaar, da var af Rehabias Sønner Jissija den første.
Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake: Mtsogoleri anali Isiya.
22 Af Jizehariterne var der Selomoth, af Selomoths Sønner var der Jahath;
Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti; kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.
23 og Jerijas Sønner: Amaria var den anden, Jehasiel den tredje, Jekameam den fjerde.
Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.
24 Af Ussiels Sønner var der Mika, af Mikas Sønner var der Samir.
Mwana wa Uzieli: Mika; kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.
25 Jissija var Mikas Broder; af Jissijas Sønner var der Sakaria.
Mʼbale wa Mika: Isiya; kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.
26 Meraris Sønner vare: Maheli og Musi, Børn af hans Søn Jasia.
Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Mwana wa Yaaziya: Beno.
27 Meraris Børn af hans Søn Jasia vare baade Skoam og Sakur og Ibri.
Ana a Merari: Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.
28 Af Maheli var der Eleasar, og han havde ingen Sønner.
Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.
29 Hvad Kis angaar, Kis's Sønner vare Jeramel.
Kuchokera kwa Kisi: Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.
30 Og Musis Sønner vare: Maheli og Eder og Jerimoth; disse ere Leviternes Børn efter deres Fædres Hus.
Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti. Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo.
31 Ogsaa de kastede Lod ligesom deres Brødre, Arons Børn, i Paasyn af Kong David og Zadok og Akimelek, og Øversterne for Fædrenehusene iblandt Præsterne og Leviterne, Øversten for Fædrenehuset saavel som hans yngste Broder.
Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.