< Første Krønikebog 19 >

1 Og det skete derefter, at Nahas, Ammons Børns Konge, døde, og hans Søn blev Konge i hans Sted.
Patapita nthawi Nahasi mfumu ya Aamoni inamwalira, ndipo mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
2 Da sagde David: Jeg vil gøre Miskundhed imod Hanon, Nahas Søn, thi hans Fader gjorde Miskundhed imod mig; og David sendte Bud at lade ham trøste over hans Fader, og Davids Tjenere kom til Ammons Børns Land, til Hanon, for at trøste ham.
Davide anaganiza kuti, “Ine ndidzachitira chifundo Hanuni mwana wa Nahasi chifukwa abambo ake anandichitira zabwino.” Choncho Davide anatumiza anthu kuti akamupepesere kwa Hanuni chifukwa cha imfa ya abambo ake. Anthu amene Davide anawatuma atafika kwa Hanuni mʼdziko la Aamoni kudzamupepesa,
3 Da sagde Ammons Børns Fyrster til Hanon: Mon David i dine Øjne ærer din Fader ved det han sender dig Trøstere? mon hans Tjenere ikke ere komne til dig for at udforske og at omstyrte og at udspejde Landet?
atsogoleri a ankhondo a Aamoni anawuza Hanuni kuti, “Kodi mukuganiza kuti Davide akupereka ulemu kwa abambo anu potumiza anthuwa kwa inu kudzapepesa? Kodi anthuwa sanawatumize kuti adzaone dziko lathu ndi kuchita ukazitape ndi cholinga chofuna kuwulanda?”
4 Da tog Hanon Davids Tjenere og lod dem rage og skar Halvdelen af deres Klæder indtil Skrævet og lod dem fare.
Choncho Hanuni anagwira anthu amene Davide anawatuma aja ndipo anawameta ndi kudula zovala zawo pakati mʼchiwuno mpaka matako kuonekera ndipo anawabweza kwawo.
5 Og nogle gik og gave David det til Kende om de Mænd; da sendte han dem et Bud i Møde, thi Mændene vare saare forhaanede, og Kongen lod sige: Bliver i Jeriko, indtil eders Skæg vokser, og kommer da tilbage!
Munthu wina atafika ndi kufotokozera Davide za anthuwo, iye anatuma amithenga kukakumana nawo, chifukwa anali ndi manyazi kwambiri. Mfumu inati, “Mukhale ku Yeriko mpaka ndevu zanu zitakula, ndipo kenaka mubwere kuno.”
6 Der Ammons Børn saa, at de havde gjort sig forhadte for David, da sendte Hanon og Ammons Børn tusinde Centner Sølv for at leje sig fra Mesopotamien og fra Syria-Maaka og fra Zoba Vogne og Ryttere.
Aamoni atazindikira kuti amukwiyitsa kwambiri Davide, Hanuni ndi Aamoni anatumiza siliva wolemera makilogalamu 34,000 kuti akalipirire magaleta ndi okwerapo ake a ku Mesopotamiya; Aramu-Maaka ndi Zoba.
7 Og de lejede sig to og tredive Tusinde Vognkæmpere og Kongen af Maaka og hans Folk, og de kom og lejrede sig lige for Medba; og Ammons Børn samlede sig fra deres Stæder og kom til Striden.
Iwo analipira magaleta okwanira 32,000, pamodzi ndi mfumu ya ku Maaka ndi ankhondo ake. Amenewa anabwera ndi kudzamanga misasa yawo pafupi ndi Medeba. Nawonso Aamoni anabwera kuchokera ku mizinda yawo ndipo anapita kukachita nkhondo.
8 Der David hørte det, da udsendte han Joab og de vældiges hele Hær.
Davide atamva zimenezi, anatumiza Yowabu ndi gulu lonse la ankhondo amphamvu.
9 Og Ammons Børn droge ud og opstillede deres Slagorden foran Indgangen til Staden, men Kongerne, som vare komne, stillede særskilt paa Marken.
Aamoni anatuluka ndi kukhala mʼmizere ya nkhondo pa chipata cha mzinda wawo, pamene mafumu amene anabwera nawo anali kwa wokha, ku malo wopanda mitengo.
10 Der Joab saa, at Krigen truede ham for og bagfra, da udvalgte han nogle af alle de udvalgte i Israel og opstillede sig imod Syrerne.
Yowabu ataona kuti kunali mizere ya ankhondo kutsogolo kwake ndi kumbuyo kwake; iye anasankha ena mwa ankhondo a Israeli odziwa kuchita bwino nkhondo ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aaramu.
11 Og det øvrige Folk gav han under sin Broder Abisajs Haand, og de opstillede sig imod Ammons Børn.
Iye anayika ankhondo ena otsalawo mʼmanja mwa Abisai mʼbale wake ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aamoni.
12 Og han sagde: Dersom Syrerne blive mig for stærke, da skal du være mig til Hjælp; men dersom Ammons Børn blive dig for stærke, da vil jeg hjælpe dig.
Yowabu anati, “Ngati Aaramu andipose mphamvu, iwe ubwere udzandipulumutse; koma ngati Aamoni akupose mphamvu, ine ndidzabwera kudzakupulumutsa.
13 Vær frimodig, og lader os vise os frimodige for vort Folk og for vor Guds Stæder; men Herren gøre, hvad som godt er for hans Øjne.
Limba mtima ndipo timenyane nawo mopanda mantha chifukwa cha anthu athu ndi mizinda ya Mulungu wathu. Yehova achite chomukomera pamaso pake.”
14 Da drog Joab frem og det Folk, som var hos ham, til Striden imod Syrerne; og disse flyede for hans Ansigt.
Choncho Yowabu ndi ankhondo amene anali naye anapita kukamenyana ndi Aaramu, ndipo iwo anathawa pamaso pake.
15 Der Ammons Børn saa, at Syrerne flyede, da flyede de og for Abisaj, hans Broders, Ansigt, og kom til Staden; og Joab kom til Jerusalem.
Aamoni atazindikira kuti Aaramu akuthawa, iwo anathawanso pamaso pa Abisai mʼbale wake ndi kulowa mu mzinda. Motero Yowabu anabwerera ku Yerusalemu.
16 Og der Syrerne saa, at devare slagne for Israels Ansigt, da sendte de Bud og lode de Syrer, som vare paa hin Side Floden, rykke ud, og Sofak, Hadad-Esers Stridshøvedsmand, anførte dem.
Aaramu ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anatumiza amithenga kukayitana Aaramu amene anali ku tsidya la Mtsinje, pamodzi ndi mtsogoleri wa ankhondo wa Hadadezeri, Sofaki akuwatsogolera.
17 Der det blev David tilkendegivet, da samlede han hele Israel og drog over Jordanen, og han kom til dem og stillede sig imod dem, og David stillede sig i Slagorden imod Syrerne, og de strede med ham.
Davide atawuzidwa zimenezi, iye anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kuwoloka Yorodani. Iyeyo anapita kukakumana nawo ndipo anakhala mʼmizere yankhondo moyangʼanana ndipo iwo anamenyana naye.
18 Men Syrerne flyede for Israels Ansigt, og David ihjelslog af Syrerne syv Tusinde Vognkæmpere og fyrretyve Tusinde Fodfolk, ligeledes dræbte han Sofak, Stridshøvedsmanden.
Koma iwo anathawa pamaso pa Aisraeli, ndipo Davide anapha anthu okwera pa magaleta 7,000 ndi ankhondo oyenda pansi 40,000. Iye anaphanso Sofaki, mtsogoleri wawo wankhondo.
19 Der Hadad-Esers Tjenere saa, at de vare slagne for Israels Ansigt, da gjorde de Fred med David og tjente ham; og Syrerne vilde ikke ydermere hjælpe Ammons Børn.
Mafumu amene ali pansi pa Hadadezeri ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anachita mtendere ndi Davide ndipo anakhala pansi pa ulamuliro wake. Motero Aaramu anaopa kuthandizanso Aamoni.

< Første Krønikebog 19 >