< Pieseò 5 >

1 Přišelť jsem do zahrady své, sestro má choti, sbírám mirru svou i vonné věci své, jím plást svůj i med svůj, pijí víno své a mléko své. Jezte, přátelé, píte a hojně se napíte, moji milí.
Ndalowa mʼmunda mwanga, iwe mlongo wanga, iwe mkwatibwi wanga; ndasonkhanitsa mure wanga ndi zokometsera zakudya zanga. Ndadya uchi wanga pamodzi ndi zisa zake zomwe; ndamwa vinyo wanga ndi mkaka wanga. Abwenzi Idyani abwenzi anga, imwani; Inu okondana, imwani kwambiri.
2 Spávámť, a však srdce mé bdí. Hlas milého mého, tlukoucího: Otevři mi, sestro má, přítelkyně má, holubičko má, upřímá má; nebo hlava má plná jest rosy, a kadeře mé krůpějí nočních.
Ndinagona tulo koma mtima wanga unali maso. Tamverani, bwenzi langa akugogoda: “Nditsekulire, mlongo wanga, bwenzi langa, nkhunda yanga, wangwiro wanga. Mutu wanga wanyowa ndi mame, tsitsi langa lanyowa chifukwa cha nkhungu ya usiku.”
3 Svlékla jsem sukni svou, kterakž ji obleku? Umyla jsem nohy své, což je mám káleti?
Ndavula kale zovala zanga, kodi ndizivalenso? Ndasamba kale mapazi anga kodi ndiwadetsenso?
4 Milý můj sáhl rukou svou skrze dvéře, a vnitřnosti mé pohnuly se ve mně.
Bwenzi langa anapisa dzanja lake pa chibowo cha pa chitseko; mtima wanga unagunda chifukwa cha iye.
5 I vstala jsem, abych otevřela milému svému, a aj, z rukou mých kapala mirra, i z prstů mých, mirra tekutá na rukovětech závory.
Ndinanyamuka kukamutsekulira wachikondi wangayo, ndipo manja anga anali noninoni ndi mure, zala zanga zinali mure chuchuchu, pa zogwirira za chotsekera.
6 Otevřelať jsem byla milému svému, ale milý můj již byl ušel, a pominul. Duše má byla vyšla, když on promluvil. Hledala jsem ho, ale nenašla jsem ho; volala jsem ho, ale neozval se mi.
Ndinamutsekulira wachikondi wanga, koma nʼkuti wachikondi wangayo atachoka; iye anali atapita. Mtima wanga unafumuka chifukwa cha kuchoka kwake. Ndinamuyangʼanayangʼana koma sindinamupeze. Ndinamuyitana koma sanandiyankhe.
7 Nalezše mne strážní, kteříž chodí po městě, zbili mne, ranili mne, vzali i rouchu mou se mne strážní zdí městských.
Alonda anandipeza pamene ankayendera mzindawo. Anandimenya ndipo anandipweteka; iwo anandilanda mwinjiro wanga, alonda a pa khoma aja!
8 Zavazuji vás přísahou dcery Jeruzalémské, jestliže byste našly milého mého, co jemu povíte? Že jsem nemocná milostí.
Inu akazi a ku Yerusalemu ndithu ndikukupemphani, mukapeza wokondedwa wangayo, kodi mudzamuwuza chiyani? Muwuzeni kuti ine ndadwala nacho chikondi.
9 Což má milý tvůj mimo jiné milé, ó nejkrásnější z žen? Co má milý tvůj nad jiné milé, že nás tak přísahou zavazuješ?
Iwe wokongola kuposa akazi onsewa, kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana wina aliyense bwanji? Kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana ena onse chotani kuti uzichita kutipempha motere?
10 Milý můj jest bílý a červený, znamenitější nežli deset tisíců jiných.
Wokondedwa wangayo ndi wowala kwambiri ndi wathanzi pakati pa anthu 1,000.
11 Hlava jeho jako ryzí zlato, vlasy jeho kadeřavé, černé jako havran.
Mutu wake ndi golide woyengeka bwino; tsitsi lake ndi lopotanapotana, ndiponso lakuda bwino ngati khwangwala.
12 Oči jeho jako holubic nad stoky vod, jako v mléce umyté, stojící v slušnosti.
Maso ake ali ngati nkhunda mʼmbali mwa mitsinje ya madzi, ngati nkhunda zitasamba mu mkaka, zitayima ngati miyala yamtengowapatali.
13 Líce jeho jako záhonkové vonných věcí, jako květové vonných věcí; rtové jeho jako lilium prýštící mirru tekutou.
Masaya ake ali ngati timinda ta mbewu zokometsera zakudya zopatsa fungo lokoma. Milomo yake ili ngati maluwa okongola amene akuchucha mure.
14 Ruce jeho prstenové zlatí, vysazení kamením drahým jako postavcem modrým; břicho jeho stkvělost slonové kosti zafiry obložené.
Manja ake ali ngati ndodo zagolide zokongoletsedwa ndi miyala yamtengowapatali. Thupi lake ndi losalala ngati mnyanga wanjovu woyikamo miyala ya safiro.
15 Hnátové jeho sloupové mramoroví, na podstavcích zlata nejčistšího založení; oblíčej jeho jako Libán, výborný jako cedrové.
Miyendo yake ili ngati mizati yamwala, yokhazikika pa maziko a golide. Maonekedwe ake ali ngati Lebanoni, abwino kwambiri ngati mkungudza.
16 Ústa jeho přesladká, a všecken jest přežádostivý. Takovýť jest milý můj, takový jest přítel můj, ó dcery Jeruzalémské.
Milomo yake ndi yosangalatsa kwambiri; munthuyo ndi wokongola kwambiri! Uyu ndiye wachikondi wanga ndi bwenzi langa, inu akazi a ku Yerusalemu.

< Pieseò 5 >