< Žalmy 99 >
1 Hospodin kraluje, užasněte se národové; sedí nad cherubíny, pohniž se země.
Yehova akulamulira, mitundu ya anthu injenjemere; Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi, dziko lapansi ligwedezeke.
2 Hospodin na Sionu veliký, a vyvýšený jest nade všecky lidi.
Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova; Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.
3 Oslavujte jméno tvé veliké a hrozné, nebo svaté jest.
Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri, Iye ndi woyera.
4 Moc zajisté králova miluje soud; ty jsi ustanovil práva, soud a spravedlnost v Jákobovi ty konáš.
Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera; mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.
5 Vyvyšujte Hospodina Boha našeho, a sklánějte se u podnoží noh jeho, svatýť jest.
Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mulambireni pa mapazi ake; Iye ndi woyera.
6 Mojžíš a Aron mezi kněžími jeho, a Samuel mezi vzývajícími jméno jeho; volávali k Hospodinu, a on je vyslýchal.
Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake, Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake; iwo anayitana Yehova ndipo Iyeyo anawayankha.
7 V sloupu oblakovém mluvíval k nim; kteřížto když ostříhali svědectví jeho, i ustanovení jim vydal.
Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo; iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.
8 Hospodine Bože náš, tys je vyslýchal, Bože, bývals jim milostiv, i když jsi je trestal pro výstupky jejich.
Inu Yehova Mulungu wathu, munawayankha iwo; Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka, ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.
9 Vyvyšujte Hospodina Boha našeho, a sklánějte se na hoře svaté jeho; neboť jest svatý Hospodin Bůh náš.
Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mumulambire pa phiri lake loyera, pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.