< Žalmy 83 >
1 Píseň a žalm Azafův. Bože, neodmlčujž se, nečiň se neslyše, aniž se upokojuj, ó Bože silný.
Nyimbo. Salimo la Asafu. Inu Mulungu musakhale chete; musangoti phee, Mulungu musangoti duu.
2 Nebo aj, nepřátelé tvoji se bouří, a ti, kteříž tě v nenávisti mají, pozdvihují hlavy.
Onani adani anu akuchita chiwawa, amene amadana nanu autsa mitu yawo.
3 Chytře tajné rady proti lidu tvému skládají, a radí se proti těm, kteréž ty skrýváš,
Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu; Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.
4 Říkajíce: Poďte, a vyhlaďme je, ať nejsou národem, tak aby ani zpomínáno nebylo více jména Izraelova.
Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”
5 Jednomyslněť se na tom spolu snesli, i smlouvou se proti tobě zavázali,
Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu; Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:
6 Stánkové Idumejští a Izmaelitští, Moábští a Agarenští,
Matenti a Edomu ndi Aismaeli, Mowabu ndi Ahagiri,
7 Gebálští a Ammonitští, a Amalechitští, Filistinští s obyvateli Tyrskými.
Agebala, Aamoni ndi Aamaleki, Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.
8 Ano i Assyrští spojili se s nimi, jsouce na ruku synům Lotovým. (Sélah)
Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo kupereka mphamvu kwa ana a Loti. (Sela)
9 Učiniž jim jako Madianským, jako Zizarovi, a jako Jabínovi při potoku Císon,
Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani, monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.
10 Kteříž jsou do konce vyhlazeni v Endor, a učiněni hnůj země.
Amene anawonongedwa ku Endori ndi kukhala ngati zinyalala.
11 Nalož s nimi a s vůdci jejich jako s Gorébem, jako s Zébem, jako s Zebahem, a jako s Salmunou, se všemi knížaty jejich.
Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,
12 Neboť jsou řekli: Uvažme se dědičně v příbytky Boží.
amene anati, “Tiyeni tilande dziko la msipu la Mulungu.”
13 Můj Bože, učiň to, ať jsou jako chumelice, a jako stéblo před větrem.
Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga, ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.
14 Jakož oheň spaluje les, a jako plamen zapaluje hory,
Monga moto umatentha nkhalango, kapena malawi a moto kuyatsa phiri,
15 Tak ty je vichřicí svou stihej, a bouří svou ohrom je.
kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho, ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.
16 Naplň tváře jejich zahanbením, tak aby hledali jména tvého, Hospodine.
Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.
17 Nechať se hanbí a děsí na věčné časy, a ať potupu nesou a zahynou.
Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse; awonongeke mwa manyazi.
18 A tak ať poznají, že ty, kterýž sám jméno máš Hospodin, jsi nejvyšší nade vší zemí.
Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova, ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.