< Žalmy 79 >

1 Žalm Azafovi. Bože, vtrhli pohané do dědictví tvého, poškvrnili chrámu svatosti tvé, obrátili Jeruzalém v hromady.
Salimo la Asafu. Inu Mulungu, anthu a mitundu ina alowerera mʼcholowa chanu; ayipitsa Nyumba yanu yoyera, asandutsa Yerusalemu kukhala bwinja.
2 Dali těla mrtvá služebníků tvých za pokrm ptákům nebeským, těla svatých tvých šelmám zemským.
Iwo anapereka mitembo ya atumiki anu kwa mbalame zamlengalenga ngati chakudya, matupi a oyera mtima anu kwa zirombo za dziko lapansi.
3 Vylili krev jejich jako vodu okolo Jeruzaléma, a nebyl, kdo by je pochovával.
Akhetsa magazi monga madzi kuzungulira Yerusalemu yense, ndipo palibe wina woti ayike mʼmanda anthu akufa.
4 Vydáni jsme v pohanění sousedům našim, v posměch a žert těm, kteříž jsou vůkol nás.
Ife ndife chinthu chonyozeka kwa anansi athu, choseketsa ndi cholalatiridwa kwa iwo amene atizungulira.
5 Až dokud, ó Hospodine? Na věky-liž se hněvati budeš, a hořeti bude jako oheň horlení tvé?
Mpaka liti Inu Yehova? Kodi mudzakwiya mpaka muyaya? Kodi mpaka liti nsanje yanu idzayaka ngati moto?
6 Vylí hněv svůj na národy, kteříž tě neznají, a na království, kteráž jména tvého nevzývají.
Khuthulirani ukali wanu pa anthu a mitundu ina amene sakudziwani Inu, pa maufumu amene sayitana pa dzina lanu;
7 Neboť jsou sežrali Jákoba, a obydlí jeho v poustku obrátili.
pakuti iwo ameza Yakobo ndi kuwononga dziko lawo.
8 Nezpomínejž nám dřevních nepravostí našich, rychle ať předejdou nás milosrdenství tvá, neboť jsme velmi znuzeni.
Musatilange chifukwa cha machimo a makolo athu chifundo chanu chibwere msanga kukumana nafe, pakuti tili ndi chosowa chachikulu.
9 Pomoz nám, ó Bože spasení našeho, pro slávu jména svého; vytrhni nás, a buď milostiv hříchům našim pro jméno své.
Tithandizeni Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, chifukwa cha ulemerero wa dzina lanu; tipulumutseni ndi kutikhululukira machimo athu chifukwa cha dzina lanu.
10 Proč mají říkati pohané: Kdež jest Bůh jejich? Budiž znám mezi pohany, před očima našima, skrze pomstu krve služebníků svých, kteráž jest vylita.
Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akuti, “Ali kuti Mulungu wawo?” Ife tikuona, zidziwike pakati pa anthu a mitundu ina kuti mumabwezera chilango chifukwa cha magazi amene anakhetsedwa a atumiki anu.
11 Vstupiž před oblíčej tvůj lkání vězňů, a podlé velikosti síly své zanechej ostatků k smrti oddaných.
Kubuwula kwa anthu a mʼndende kufike pamaso panu; ndi mphamvu ya dzanja lanu muwasunge amene aweruzidwa kuti aphedwe.
12 A odplať sousedům našim sedmernásobně do lůna jejich za pohanění, kteréž jsou tobě činili, ó Pane.
Mubwezere kwa anansi athu kasanu nʼkawiri kunyoza kumene ananyoza Inu Ambuye.
13 My pak, lid tvůj a ovce pastvy tvé, slaviti tě budeme na věky; od národu do pronárodu vypravovati budeme chválu tvou.
Pamenepo ife anthu anu, nkhosa za pabusa panu, tidzakutamandani kwamuyaya, kuchokera mʼbado ndi mʼbado tidzafotokoza za matamando anu.

< Žalmy 79 >