< Žalmy 66 >

1 Přednímu z kantorů, píseň žalmu. Plésej Bohu všecka země.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
2 Zpívejte žalmy k slávě jména jeho, ohlašujte slávu a chválu jeho.
Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
3 Rcete Bohu: Jak hrozný jsi v skutcích svých! Pro velikost síly tvé lháti budou tobě nepřátelé tvoji.
Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
4 Všecka země skláněti se tobě a prozpěvovati bude, žalmy zpívati bude jménu tvému. (Sélah)
Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
5 Poďte a vizte skutky Boží, jak hrozný jest v správě při synech lidských.
Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
6 Obrátil moře v suchost, řeku přešli nohou po suše, tuť jsme se veselili v něm.
Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
7 Panuje v síle své nade vším světem, oči jeho spatřují národy, zpurní nebudou míti zniku. (Sélah)
Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
8 Dobrořečte národové Bohu našemu, a ohlašujte hlas chvály jeho.
Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
9 Zachoval při životu duši naši, aniž dopustil, aby se poklesla noha naše.
Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
10 Nebo jsi nás zpruboval, ó Bože, přečistil jsi nás, tak jako přečištěno bývá stříbro.
Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
11 Uvedl jsi nás byl do leči, krutě jsi bedra naše ssoužil,
Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
12 Vsadils člověka na hlavu naši, vešli jsme byli do ohně i do vody, a však jsi nás vyvedl do rozvlažení.
Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
13 A protož vejdu do domu tvého s zápalnými obětmi, a plniti tobě budu sliby své,
Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
14 Kteréž vyřkli rtové moji, a vynesla ústa má, když jsem byl v ssoužení.
Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
15 Zápaly tučných beranů obětovati budu tobě s kaděním, volů i kozlů nastrojím tobě. (Sélah)
Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
16 Poďte, slyšte, a vypravovati budu, kteříž se koli bojíte Boha, co jest učinil duši mé.
Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
17 Ústy svými k němu jsem volal, a vyvyšoval jsem ho jazykem svým.
Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
18 Bychť byl patřil k nepravosti srdcem svým, nebyl by vyslyšel Pán.
Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
19 Ale vyslyšelť Bůh, a pozoroval hlasu modlitby mé.
koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
20 Požehnaný Bůh, kterýž neodstrčil modlitby mé, a milosrdenství svého ode mne neodjal.
Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!

< Žalmy 66 >