< Žalmy 65 >

1 Přednímu z kantorů žalm, Davidova píseň. Na tobě přestávati sluší, ó Bože, tebe na Sionu chváliti, a tu tobě slib vyplňovati.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Nyimbo. Matamando akudikira Inu Mulungu mu Ziyoni; kwa inu malumbiro athu adzakwaniritsidwa.
2 Tu k tobě modlitbu vyslýchajícímu všeliké tělo přicházeti bude.
Inu amene mumamva pemphero, kwa inu anthu onse adzafika.
3 Mnohé nepravosti, kteréž se zmocnily nás, a přestoupení naše ty očistíš.
Pamene tinathedwa nzeru ndi machimo, Inu munakhululukira mphulupulu zathu.
4 Blahoslavený, kohož vyvoluješ, a přivodíš, aby obýval v síňcích tvých. Tuť nasyceni budeme dobrým domu tvého, v svatyni chrámu tvého.
Odala iwo amene inu muwasankha ndi kuwabweretsa pafupi kukhala mʼmabwalo anu! Ife tadzazidwa ndi zinthu zabwino za mʼNyumba mwanu, za mʼNyumba yanu yoyera.
5 Předivné věci podlé spravedlnosti nám mluvíš, Bože spasení našeho, naděje všech končin země i moře dalekého,
Mumatiyankha ife ndi ntchito zodabwitsa zachilungamo, Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, chiyembekezo cha mathero onse a dziko lapansi ndi cha nyanja zomwe zili kutali kwambiri,
6 Kterýž upevňuješ hory mocí svou, silou jsa přepásán,
amene munapanga mapiri ndi mphamvu zanu, mutadziveka nokha ndi mphamvu.
7 Kterýž skrocuješ zvuk moře, ječení vlnobití jeho, i bouření se národů,
Amene munakhalitsa bata nyanja kukokoma kwa mafunde ake, ndi phokoso la anthu a mitundu ina.
8 Tak že se báti musejí obyvatelé končin zázraků tvých, kteréž nastáváním jitra a večera k plésání přivodíš.
Iwo amene akukhala kutali amaopa zizindikiro zozizwitsa zanu; kumene dzuwa limatulukira ndi kumene dzuwa limalowera. Inu mumafuna nyimbo zachimwemwe.
9 Navštěvuješ zemi a svlažuješ ji, hojně ji obohacuješ. Potok Boží naplňován bývá vodami, i nastrojuješ obilé jejich, když ji tak spravuješ.
Inu mumasamalira dziko lapansi ndi kulithirira; Inuyo mumalilemeretsa kwambiri. Mtsinje wa Mulungu ndi wodzaza ndi madzi kuti upereke tirigu kwa anthu, pakuti Inu munakhazikitsa zimenezi.
10 Záhony její svlažuješ, brázdy její snižuješ, dešti ji obměkčuješ, a zrostlinám jejím požehnání dáváš.
Mwadzaza nthaka yake ndi madzi ndi kusalaza migula yake, mwayifewetsa ndi mvula yamawawa ndi kudalitsa mbewu zake.
11 Korunuješ rok dobrotivostí svou, a šlepěje tvé kropí tučností;
Inu mumaveka chaka ndi zinthu zochuluka, ndipo ngolo zanu zimasefukira ndi zinthu zochuluka.
12 Skropují pastviště po pustinách, tak že i pahrbkové plésáním přepasováni bývají.
Malo a udzu a mʼchipululu amasefukira; mapiri avekedwa ndi chisangalalo.
13 Přiodíny bývají roviny dobytkem, a údolí přistřína obilím, tak že radostí prokřikují, a prozpěvují.
Madambo akutidwa ndi zoweta ndi zigwa zavekedwa ndi tirigu; izo pamodzi zikufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe.

< Žalmy 65 >