< Žalmy 6 >

1 Přednímu kantoru na neginot, k nízkému zpěvu, žalm Davidův. Hospodine, netresci mne v hněvě svém, ani v prchlivosti své kárej mne.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide. Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, kapena kundilanga mu ukali wanu.
2 Smiluj se nade mnou, Hospodine, neboť jsem zemdlený; uzdrav mne, Hospodine, nebo ztrnuly kosti mé.
Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka; Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.
3 Ano i duše má předěšena jest náramně, ty pak, Hospodine, až dokavad?
Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu. Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?
4 Navratiž se, Hospodine, a vytrhni duši mou; spomoz mi pro milosrdenství své.
Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse; pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
5 Nebo mrtví nezpomínají na tebe, a v hrobě kdo tě bude oslavovati? (Sheol h7585)
Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda? (Sheol h7585)
6 Ustávám v úpění svém, ložce své každé noci svlažuji, slzami svými postel svou smáčím.
Ine ndatopa ndi kubuwula; usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.
7 Sškvrkla se zámutkem tvář má, sstarala se příčinou všech nepřátel mých.
Maso anga atupa chifukwa cha chisoni; akulephera kuona chifukwa cha adani anga.
8 Odstuptež ode mne všickni činitelé nepravosti; neboť jest vyslyšel Hospodin hlas pláče mého.
Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa, pakuti Yehova wamva kulira kwanga.
9 Vyslyšel Hospodin pokornou modlitbu mou, Hospodin modlitbu mou přijal.
Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo; Yehova walandira pemphero langa.
10 Nechažť se zastydí a předěsí zřejmě všickni nepřátelé moji, nechažť jsou zpět obráceni a rychle zahanbeni.
Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha; adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.

< Žalmy 6 >