< Žalmy 50 >

1 Žalm Azafovi. Bůh silný, Bůh Hospodin mluvil, a přivolal zemi od východu slunce i od západu jeho.
Salimo la Asafu. Wamphamvuyo, Yehova Mulungu, akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.
2 Z Siona v dokonalé kráse Bůh zastkvěl se.
Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri Mulungu akuwala.
3 Béřeť se Bůh náš, a nebude mlčeti; oheň před ním vše zžírati bude, a vůkol něho vichřice náramná.
Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete; moto ukunyeketsa patsogolo pake, ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho
4 Zavolal nebes s hůry i země, aby soudil lid svůj, řka:
Iye akuyitanitsa zamumlengalenga ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.
5 Shromažďte mi svaté mé, kteříž smlouvu se mnou učinili při obětech.
Mundisonkhanitsire okhulupirika anga, amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.
6 I budou vypravovati nebesa spravedlnost jeho; nebo sám Bůh soudce jest. (Sélah)
Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake, pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.
7 Slyš, lide můj, a buduť mluviti, Izraeli, a buduť tebou osvědčovati. Já zajisté Bůh, Bůh tvůj jsem.
Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula, iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa; ndine Mulungu, Mulungu wako.
8 Nechci tě obviňovati z příčiny obětí tvých, ani zápalů tvých, že by vždycky přede mnou nebyli.
Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako, kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.
9 Nevezmuť z domu tvého volka, ani z chlévů tvých kozlů.
Ine sindikufuna ngʼombe yayimuna kuchokera mʼkhola lako kapena mbuzi za mʼkhola lako,
10 Nebo má jest všecka zvěř lesní, i hovada na tisíci horách.
pakuti nyama iliyonse yakunkhalango ndi yanga ndiponso ngʼombe za ku mapiri ochuluka.
11 Já znám všecko ptactvo po horách, a zvěř polní před sebou mám.
Ine ndimadziwa mbalame iliyonse mʼmapiri ndiponso zolengedwa zonse zakutchire ndi zanga.
12 Zlačním-li, nic tobě o to nedím; nebo můj jest okršlek zemský i plnost jeho.
Ndikanakhala ndi njala sindikanakuwuzani, pakuti dziko lonse ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndi zanga.
13 Zdaliž jídám maso z volů, a pijím krev kozlovou?
Kodi ndimadya nyama ya ngʼombe zazimuna kapena kumwa magazi a mbuzi?
14 Obětuj Bohu obět chvály, a plň Nejvyššímu své sliby;
“Pereka nsembe zachiyamiko kwa Mulungu, kwaniritsa malonjezo ako kwa Wammwambamwamba.
15 A vzývej mne v den ssoužení, vytrhnu tě, a ty mne budeš slaviti.
Ndipo undiyitane pa tsiku lako la masautso; Ine ndidzakulanditsa, ndipo udzandilemekeza.”
16 Sic jinak bezbožníku praví Bůh: Což tobě do toho, že ty vypravuješ ustanovení má, a béřeš smlouvu mou v ústa svá,
Koma kwa woyipa, Mulungu akuti, “Kodi uli ndi mphamvu yanji kuti uzinena malamulo anga kapena kutenga pangano langa pa milomo yako?
17 Poněvadž jsi vzal v nenávist kázeň, a zavrhl jsi za sebe slova má.
Iwe umadana ndi malangizo anga ndipo umaponyera kumbuyo kwako mawu anga.
18 Vidíš-li zloděje, hned s ním běžíš, a s cizoložníky díl svůj máš.
Ukaona wakuba umamutsatira, umachita maere ako pamodzi ndi achigololo
19 Ústa svá pouštíš ke zlému, a jazyk tvůj skládá lest.
Umagwiritsa ntchito pakamwa pako pa zinthu zoyipa ndipo umakonza lilime lako kuchita chinyengo.
20 Usazuješ se, a mluvíš proti bratru svému, a na syna matky své lehkost uvodíš.
Nthawi zonse umayankhula motsutsana ndi mʼbale wako ndipo umasinjirira mwana wa amayi ako enieni.
21 To jsi činil, a já mlčel jsem. Měl-liž jsi ty se domnívati, že já tobě podobný budu? Nýbrž trestati tě budu, a představímť to před oči tvé.
Wachita zimenezi ndipo Ine ndinali chete; umaganiza kuti ndine wofanana nawe koma ndidzakudzudzula ndipo ndidzakutsutsa pamaso pako.
22 Srozumějtež tomu již aspoň vy, kteříž se zapomínáte na Boha, abych snad nepochytil, a nebyl by, kdo by vytrhl.
“Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:
23 Kdož obětuje obět chvály, tenť mne uctí, a tomu, kdož napravuje cestu svou, ukáži spasení Boží.
Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza, ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse chipulumutso cha Mulungu.”

< Žalmy 50 >